< Psalms 128 >

1 A Song of Ascents. How happy is every one that revereth Yahweh, who walketh in his ways!
Nyimbo yoyimba pokwera ku Yerusalemu. Odala ndi onse amene amaopa Yehova, amene amayenda mʼnjira zake.
2 The labour of thine own hands, surely thou shalt eat. How happy thou, and well for thine!
Udzadya chipatso cha ntchito yako; madalitso ndi chuma zidzakhala zako.
3 Thy wife, like a fruitful vine, within the recesses of thy house, —Thy children, like plantings of olive-trees, round about thy table.
Mkazi wako adzakhala ngati mpesa wobereka mʼkati mwa nyumba yako; ana ako adzakhala ngati mphukira za mitengo ya olivi kuzungulira tebulo lako.
4 Lo! thus, shall be blessed the man who revereth Yahweh.
Ameneyu ndiye munthu wodalitsidwa amene amaopa Yehova.
5 Yahweh will bless thee, out of Zion, —and behold thou the welfare of Jerusalem, all the days of thy life!
Yehova akudalitse kuchokera mʼZiyoni masiku onse a moyo wako; uwone zokoma za Yerusalemu,
6 And behold thou thy children’s children, —Prosperity on Israel!
ndipo ukhale ndi moyo kuti udzaone zidzukulu zako. Mtendere ukhale ndi Israeli.

< Psalms 128 >