< Psalms 111 >

1 Praise ye Yah! I will give thanks unto Yahweh, with a whole heart, in the circle of the upright and the assembly.
Tamandani Yehova. Ndidzathokoza Yehova ndi mtima wanga wonse mʼbwalo la anthu olungama mtima ndi pa msonkhano.
2 Great are the works of Yahweh, sought out, by all who find pleasure therein.
Ntchito za Yehova nʼzazikulu; onse amene amakondwera nazo amazilingalira.
3 Honourable and majestic, is his doing, and, his righteousness, standeth for aye.
Zochita zake ndi za ulemerero ndi zaufumu, ndipo chilungamo chake ndi chosatha.
4 A memorial, hath he made by his wonders, Gracious and compassionate, is Yahweh.
Iye wachititsa kuti zodabwitsa zake zikumbukirike; Yehova ndi wokoma mtima ndi wachifundo.
5 Food, hath he given to them who revere him, He will remember, age-abidingly, his covenant.
Amapereka chakudya kwa amene amamuopa Iye; amakumbukira pangano lake kwamuyaya.
6 The might of his works, hath he declared to his people, that he may give them the inheritance of the nations.
Waonetsa anthu ake mphamvu ya ntchito zake, kuwapatsa mayiko a anthu a mitundu ina.
7 The works of his hands, are faithful and just, Firm are all his precepts;
Ntchito za manja ake ndi zokhulupirika ndi zolungama; malangizo ake onse ndi odalirika.
8 Upheld to futurity, to times age-abiding, done in faithfulness and equity.
Malamulo ndi okhazikika ku nthawi za nthawi, ochitidwa mokhulupirika ndi molungama.
9 Ransom, hath he sent to his people, He hath commanded, to times age-abiding, his covenant, Holy and reverend, is his Name.
Iyeyo amawombola anthu ake; anakhazikitsa pangano lake kwamuyaya dzina lake ndi loyera ndi loopsa.
10 The beginning of wisdom, is the reverence of Yahweh, Good discretion, have all that do them, His praise, endureth for aye.
Kuopa Yehova ndicho chiyambi cha nzeru; onse amene amatsatira malangizo ake amamvetsa bwino zinthu. Iye ndi wotamandika mpaka muyaya.

< Psalms 111 >