< Proverbs 2 >
1 My son, if thou wilt receive my sayings, and, my commandments, wilt treasure up by thee;
Mwana wanga, ngati ulandira mawu anga ndi kusunga malamulo anga mu mtima mwako,
2 So that thou direct, unto wisdom, thine ear, bend thy heart, unto understanding;
ndiponso kutchera khutu lako ku nzeru ndi kuyikapo mtima pa kumvetsa zinthu;
3 Yea if, for understanding, thou cry aloud, for knowledge, utter thy voice;
ngati upempha kuti uzindikire zinthu inde kupempha ndi mtima wonse kuti ukhale womvetsa zinthu,
4 If thou seek her as silver, and, like hid treasure, thou search for her,
ngati ufunafuna nzeruyo ngati siliva ndi kuyisakasaka ngati chuma chobisika,
5 Then, shalt thou understand the reverence of Yahweh, and, the knowledge of God, shalt thou find.
ndiye udzamvetsa bwino tanthauzo la kuopa Yehova; ndipo udzapezanso tanthauzo la kumudziwa Yehova.
6 For, Yahweh, giveth wisdom, out of his mouth, knowledge and understanding;
Pakuti Yehova ndiye amapereka nzeru, ndipo mʼkamwa mwake mumachokera chidziwitso ndi kumvetsa zinthu.
7 Yea he treasureth, for the upright, safety, A shield [is he] to them who walk in integrity,
Anthu olungama zinthu zimawayendera bwino chifukwa Yehova amakhala nawo. Paja Yehova ndiye chishango cha amene amayenda mwangwiro,
8 To him that observeth the paths of justice, yea, the way of his men of lovingkindness, he doth guard.
pakuti ndiye mlonda wa njira zolungama. Iye amasamala mayendedwe a anthu ake okhulupirika.
9 Then, shalt thou understand righteousness and justice, and equity—every noble course.
Choncho udzamvetsa tanthauzo la ungwiro, chilungamo, kusakondera ndi njira iliyonse yabwino.
10 When wisdom entereth thy heart, and, knowledge, to thy soul, is sweet,
Pakuti nzeru idzalowa mu mtima mwako, kudziwa zinthu kudzakusangalatsa.
11 Discretion, shall watch over thee, understanding, shall preserve thee: —
Kuganizira bwino za mʼtsogolo kudzakusunga; kumvetsa zinthu bwino kudzakuteteza.
12 To rescue thee from the way of the wrongful, from the man that speaketh perverse things;
Nzeru idzakupulumutsa ku mayendedwe oyipa, kwa anthu amabodza,
13 From them who forsake the paths of rectitude, to walk in the ways of darkness;
amene amasiya njira zolungama namayenda mʼnjira zamdima,
14 Who rejoice to do wrong, exult in the perversities of the wrongful;
amene amakondwera pochita zoyipa namasangalala ndi kuyipa kwa ntchito zawo zonyansa.
15 Whose paths, are twisted, and they are tortuous in their tracks:
Amenewa ndi anthu a njira zawo zokhotakhota, ndipo makhalidwe awo ndi achinyengo.
16 To rescue thee, from the woman that is a stranger, from the female unknown, who with her speeches seduceth;
Nzeruyo idzakupulumutsanso kwa mkazi wachigololo; kwa mkazi wachilendo woyankhula moshashalika,
17 Who forsaketh the friend of her youth, and, the covenant of her God, hath forgotten;
amene wasiya mwamuna wa chitsikana wake ndi kuyiwala pangano limene anachita pamaso pa Mulungu wake.
18 For she hath appointed, unto death, her house, and unto the shades, her courses;
Pakuti nyumba yake imatsetserekera ku imfa; njira zake zimamufikitsa ku manda.
19 None who go in unto her, come back, neither attain they unto the paths of life:
Opita kwa iye palibe ndi mmodzi yemwe amabwerera kapena kupezanso njira zamoyo.
20 To the end that thou walk in the way of good men, and, the paths of the righteous, that thou observe.
Choncho iwe uziyenda mʼnjira za anthu abwino, uzitsata njira za anthu ochita chilungamo.
21 For, the upright, shall abide on the earth, —and, the men of integrity, shall remain therein;
Pakuti anthu olungama ndiwo ati adzakhale mʼdziko ndipo anthu angwiro ndiwo ati adzakhazikike mʼmenemo;
22 But, the lawless, out of the earth, shall be cut off, and, traitors, shall they tear away therefrom.
Koma anthu oyipa adzachotsedwa mʼdzikomo, ndipo anthu onyenga adzachotsedwamo.