< Proverbs 12 >

1 He that loveth correction, loveth knowledge, but, he that hateth reproof, is brutish.
Munthu amene amakonda mwambo amakonda kudziwa zinthu, koma amene amadana ndi chidzudzulo ndi wopusa.
2 A good man, obtaineth favour from Yahweh, but, a man of wicked devices, will he condemn.
Munthu wabwino amapeza kuyanja pamaso pa Yehova, koma Yehova amatsutsa munthu wochita chinyengo.
3 A son of earth, shall not be established, by lawlessness, but, the root of the righteous, shall not be disturbed.
Munthu sangakhazikike bwino pochita zoyipa, koma maziko a anthu olungama sadzatekeseka.
4 A virtuous woman, is the crown of her husband, but, a veritable decay in his bones, is she that causeth shame.
Mkazi wakhalidwe labwino ali ngati chipewa chaufumu kwa mwamuna wake, koma mkazi wochititsa manyazi ali ngati chilonda cha mafinya kwa mwamuna wake.
5 The plans of the righteous, are just, but, the counsels of the lawless, are deceitful.
Maganizo a anthu olungama ndi owongoka, koma malangizo a anthu oyipa ndi achinyengo.
6 The words of the lawless, are—of lying in wait for blood, but, the mouth of the upright, shall deliver them.
Mawu a anthu oyipa ndi ophetsa, koma mawu a anthu olungama amapulumutsa.
7 Overthrown are the lawless and they are not, but, the house of the righteous, shall stand.
Anthu oyipa amagonjetsedwa ndipo amayiwalika, koma nyumba ya anthu olungama idzakhalabe.
8 In proportion to his prudence, is a man, to be praised, but, the perverse in heart, shall be an object of contempt.
Munthu amatamandidwa malinga ndi nzeru zake, koma anthu amitima yokhota amanyozedwa.
9 Better slighted, and have a servant, than to honour oneself, and come short of bread.
Nʼkwabwino kukhala munthu wonyozeka koma wodzigwirira ntchito nʼkukhala ndi zonse zofunika, kuposa kukhala wodzikuza koma ulibe ndi chakudya chomwe.
10 A righteous man, regardeth the desire of his beast, but, the compassions of the lawless, are cruel.
Munthu wolungama amasamalira moyo wa ziweto zake, koma chifundo cha munthu woyipa ndi chakhanza.
11 He that tilleth his land, shall be filled with food, but, he that runneth after worthless men, lacketh sense.
Wolima mʼmunda mwake mwakhama adzakhala ndi chakudya chochuluka, koma wotsata zopanda pake alibe nzeru.
12 A lawless man craveth the prey of the wicked, but, the root of the righteous, is enduring.
Munthu woyipa amalakalaka zofunkha za anthu oyipa, koma mizu ya anthu olungama imabereka zipatso.
13 By the transgression of the lips, is the wicked man, ensnared, but the righteous, cometh out of distress.
Munthu woyipa amakodwa mu msampha wa mayankhulidwe ake oyipa; koma munthu wolungama amatuluka mʼmavuto.
14 Of the fruit of a man’s mouth, shall he be satisfied with good, and, the dealing of the hands of a son of earth, shall be paid back to him.
Munthu amakhala ndi zabwino zambiri chifukwa cha mawu ake ndipo ntchito zimene munthu agwira ndi manja ake zimamupindulira.
15 The way of the foolish, is right in his own eyes, but, he that hearkeneth to counsel, is wise.
Zochita za chitsiru mwini wakeyo amaziona ngati zabwino, koma munthu wanzeru amamvera malangizo.
16 A foolish man, on the [same] day, letteth his vexation be known, but, he that concealeth an affront, is prudent.
Mkwiyo wa chitsiru umadziwika nthawi yomweyo, koma munthu wanzeru sasamala kunyozedwa.
17 He that whispereth faithfulness, declareth righteousness, but, a false witness, is a fraud.
Woyankhula zoona amapereka umboni woona, koma mboni yabodza imafotokoza zonama.
18 There is who babbleth, as with thrusts of a sword, but, the tongue of the wise, hath healing.
Munthu woyankhula mosasamala mawu ake amalasa ngati lupanga, koma mawu a munthu wanzeru amachiritsa.
19 A lip that is faithful, shall be firm to futurity, but, only for a twinkling, is the tongue that is false.
Mawu woona amakhala mpaka muyaya koma mawu abodza sakhalitsa.
20 Deceit, is in the heart of contrivers of mischief, but, to the counsellors of peace, shall be joy.
Mʼmitima ya anthu amene amakonza zoyipa muli chinyengo; koma anthu olimbikitsa za mtendere amakhala ndi chimwemwe.
21 Unseemly to the righteous, is any trouble, but, the lawless, are full of misfortune.
Palibe choyipa chimene chimagwera munthu wolungama, koma munthu woyipa mavuto samuthera.
22 An abomination to Yahweh, are lips that are false, but, he that dealeth faithfully, is his delight.
Pakamwa pa bodza pamamunyansa Yehova, koma amakondwera ndi anthu oyankhula zoona.
23 A prudent man, concealeth knowledge, but, the heart of dullards, proclaimeth folly.
Munthu wochenjera amabisa nzeru zake, koma munthu wopusa amaonetsa uchitsiru wake poyera.
24 The hand of the diligent, shall bear rule, but, the indolent, shall come under tribute.
Ogwira ntchito mwakhama adzalamulira, koma aulesi adzakhala ngati kapolo.
25 When anxiety is in the heart of a man, one may bow him down, but, a good word, maketh him glad.
Nkhawa imakhala ngati katundu wolemera mu mtima mwa munthu, koma mawu abwino amamusangalatsa.
26 The righteous man guideth his neighbour, but, the way of the lawless, leadeth them astray.
Munthu wolungama amatsogolera mnansi wake, koma ntchito za anthu oyipa zimawasocheretsa.
27 Indolence, roasteth not, his own game, but, the substance of a man, is precious, when he is diligent.
Munthu waulesi sapeza chimene akufuna, koma munthu wakhama amapeza chuma chamtengo wapatali.
28 In the way of righteousness, is life, and, in the path thereof, immortality,
Mʼnjira yachilungamo muli moyo; koma njira ya munthu woyipa imafikitsa ku imfa.

< Proverbs 12 >