< Numbers 3 >

1 Now, these, were the pedigrees of Aaron and Moses, —in the day when Yahweh spake with Moses in Mount Sinai.
Iyi ndi mbiri ya banja la Aaroni ndi Mose pa nthawi yomwe Yehova anayankhula ndi Mose pa phiri la Sinai.
2 And these, are the names of the sons of Aaron—the firstborn Nadab, —and Abihu, Eleazar, and Ithamar.
Mayina a ana aamuna a Aaroni anali Nadabu, woyamba kubadwa, Abihu, Eliezara ndi Itamara.
3 These, are the names of the sons of Aaron, the priests that were anointed, —who were installed to minister as priests.
Amenewa ndi mayina a ana aamuna a Aaroni, ansembe odzozedwa omwe anapatulidwa kuti azitumikira ngati ansembe.
4 But Nadab and Abihu died before Yahweh when they brought near strange fire before Yahweh in the desert of Sinai, and sons, had they none, —so then Eleazar and Ithamar ministered as priests, in the presence of Aaron their father.
Koma Nadabu ndi Abihu, anagwa nafa pamaso pa Yehova pamene ankapereka nsembe ndi moto wachilendo pamaso pa Yehova mʼchipululu cha Sinai. Iwowo analibe ana aamuna. Choncho Eliezara ndi Itamara ndiwo amene ankatumikira ngati ansembe nthawi imene Aaroni abambo awo anali moyo.
5 Then spake Yahweh unto Moses, saying—
Yehova anati kwa Mose,
6 Bring near the tribe of Levi, and thou shalt cause it to stand before Aaron the priest, —so shall they wait upon him;
“Bweretsa fuko la Levi ndipo ulipereke kwa Aaroni wansembe kuti lizimutumikira.
7 so shall they keep his charge, and the charge of all the assembly, before the tent of meeting, —to do the laborious work of the habitation;
Azigwira ntchito yothandiza iyeyo ndi gulu lonse ku tenti ya msonkhano pogwira ntchito ya ku Chihema.
8 so shall they have charge of all the furniture of the tent of meeting, even the charge of the sons of Israel, —to do the laborious work of the habitation.
Azisamalira zipangizo zonse za mu tenti ya msonkhano, ndipo azigwirira ntchito Aisraeli potumikira mu tenti.
9 Thus shalt thou give the Levites unto Aaron and unto his sons, —given, given, they are unto him, from among the sons of Israel;
Pereka Alevi kwa Aaroni ndi kwa ana ake aamuna. Amenewa ndiwo Aisraeli amene aperekedwa kwa iye kwathunthu.
10 but unto Aaron, and unto his sons, shalt thou give oversight, so shall they keep charge of their priesthood, —and, the stranger who cometh near, shall be put to death.
Usankhe Aaroni ndi ana ake aamuna kuti azitumikira pa ntchito ya unsembe. Koma wina aliyense woyandikira malo opatulika aphedwe.”
11 Then spake Yahweh unto Moses, saying—
Yehova anawuzanso Mose kuti,
12 I, therefore, lo! I have taken the Levites out of the midst of the sons of Israel, instead of every firstborn that a mother beareth, from among the sons of Israel, —so shall the Levites be mine;
“Pakati pa Aisraeli onse ndatenga Alevi kulowa mʼmalo mwa mwana wamwamuna aliyense woyamba kubadwa kwa amayi a Chiisraeli. Alevi ndi anga,
13 for, mine, is every firstborn, in the day when I smote every firstborn in the land of Egypt, I hallowed unto myself every firstborn in Israel, both of man and of beast, —mine, did they become, and belong unto me, Yahweh.
pakuti ana onse oyamba kubadwa ndi anga. Nditakantha ana onse oyamba kubadwa mu Igupto, ndinadzipatulira ndekha mwana aliyense woyamba kubadwa mu Israeli, wa munthu ndi nyama. Azikhala anga. Ine ndine Yehova.”
14 Then spake Yahweh unto Moses, in the desert of Sinai, saying: —
Yehova anawuza Mose mʼchipululu cha Sinai kuti,
15 Number thou the sons of Levi, by their ancestral houses, by their families, —every male, from one month old and upwards, shalt thou number them.
“Werenga Alevi monga mwa mabanja awo ndi mafuko awo. Werenga mwamuna aliyense kuyambira wa mwezi umodzi kapena kupitirirapo.”
16 So then Moses numbered them according to the bidding of Yahweh, —as he was commanded.
Choncho Mose anawawerenga potsatira zomwe Yehova anamulamulira.
17 And these were the sons of Levi, by their names, —Gershon, and Kohath, and Merari.
Mayina a ana aamuna a Levi ndi awa: Geresoni, Kohati ndi Merari.
18 And these, the names of the sons of Gershon by their families, —Libni and Shimei.
Mayina a ana a Geresoni potsata mabanja awo ndi awa: Libini ndi Simei.
19 And, the sons of Kohath, by their families Amram, and Izhar, Hebron and Uzziel.
Ana a Kohati potsata mabanja awo ndi awa: Amramu, Izihari, Hebroni ndi Uzieli.
20 And the sons of Merari by their families, Mahli and Mushi. These, are they—the families of the Levites by their ancestral houses.
Ana a Merari potsata mabanja awo ndi awa: Mali ndi Musi. Amenewa ndiwo anali mabanja a Alevi monga mwa makolo awo.
21 To, Gershon, belonged the family of the Libnites, and the family of the Shimeites, —these, are they—the families of the Gershonites.
Kwa Geresoni kunali banja la Alibini, banja la Asimei. Amenewa ndiwo anali mabanja a Ageresoni.
22 They who were numbered of them in the counting of every male, from one month old, and upwards, —they who were num-bered of them, were seven thousand and five hundred.
Chiwerengero cha amuna onse amene anawawerenga a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 7,500.
23 the families of the Gershonites, to the rear of the habitation, were to encamp, westward.
Mabanja a Ageresoni azimanga misasa yawo kumadzulo, kumbuyo kwa Chihema.
24 And, the prince of the ancestral house of the Gershonites, was Eliasaph son of Lael.
Mtsogoleri wa mabanja a Ageresoni anali Eliyasafu mwana wa Laeli.
25 And, the charge, of the sons of Gershon, was over the tent of meeting, the habitation, and the tent, —the covering thereof, and the screen for the entrance of the tent of meeting;
Ntchito imene Ageresoni anapatsidwa ku tenti ya msonkhano inali yosamalira Chihema ndi tenti, pamodzi ndi zophimbira zake, katani ya pa khomo la ku tenti ya msonkhano,
26 and the hangings of the court, and the screen for the entrance of the court which was near the habitation and near the altar, round about, —and the cords thereof, as to all the laborious work thereof.
ndi makatani wotchinga bwalo, katani ya pa chipata cholowera ku bwalo lozungulira Chihema ndi guwa lansembe, zingwe ndi zonse zokhudzana ndi ntchito yawo.
27 And to Kohath, belonged the family of the Amramites and the family of the Izharites, and the family of the Hebronites, and the family of the Uzzielites, —these, are they—the families of the Kohathites.
Kwa Kohati kunali mabanja a Amramu, Aizihara, Ahebroni ndi Auzieli. Awa ndiye anali mabanja a Akohati.
28 In, the counting of every male, from one month old and upwards, there were eight thousand and six hundred, to keep the charge of the sanctuary.
Chiwerengero cha amuna onse a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 8,600. Akohati ankagwira ntchito yosamalira malo wopatulika.
29 The, families of the sons of Kohath, were to encamp, —on the side of the habitation, south-ward.
Mabanja a ana a Kohati ankamanga misasa yawo kummwera kwa Chihema.
30 And the prince of the ancestral house of the families of the Kohathites, was Elizaphan, son of Uzziel.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Kohati anali Elizafani mwana wa Uzieli.
31 And their charge, was—the ark and the table and the lampstand and the altars, and the utensils of the sanctuary wherewith they were to minister, —and the screen, as to all the laborious work thereof.
Iwo ankagwira ntchito yosamalira Bokosi la Chipangano, tebulo, choyikapo nyale, maguwa, zipangizo za kumalo wopatulika zimene ansembe ankagwiritsa ntchito, katani, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito.
32 And the prince of the princes of the Levites, was Eleazar, son of Aaron the priest, —to have the oversight of them that were to keep the charge of the sanctuary.
Mtsogoleri wamkulu wa Alevi anali Eliezara mwana wa Aaroni wansembe. Iye anasankhidwa kukhala woyangʼanira omwe ankasamalira malo wopatulika.
33 To Merari, belonged the family of the Mahlites, and the family of the Mushites, —these, are they—the families of Merari.
Kwa Merari kunali banja la Mali ndi banja la Musi. Amenewa ndiye anali mabanja a Amerari.
34 And they who were numbered of them in the counting of every male, from one month old and upwards, were six thousand, and two hundred.
Chiwerengero cha amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 6,200.
35 And the prince of the ancestral house of the families of Merari, was Zuriel son of Abihail, —on the side of the habitation, were they to encamp northward.
Mtsogoleri wa magulu a mabanja a Amerari anali Zuriyeli mwana wa Abihaili. Iwo ankamanga misasa yawo kumpoto kwa Chihema.
36 And the oversight of the charge of the sons of Merari, was—the boards of the habitation, and the bars thereof and the pillars thereof and the sockets thereof, —and all the furniture thereof, as to all the laborious work thereof;
Amerari anapatsidwa ntchito yosamalira mitengo ya chihema, nsichi zake, mizati yake, matsinde ake, ndi zida zake zonse, ndi zonse zomwe ankagwiritsa ntchito,
37 also the pillars of the court round about and their sockets, —and their pins and their cords.
pamodzi ndi mizati yozungulira bwalo ndi matsinde ake, zikhomo za chihema ndi zingwe zake.
38 But, they who were to encamp before the habitation eastwards before the tent of meeting, towards sunrise, were Moses and Aaron and his sons. to keep the charge of the sanctuary, as the charge of the sons of Israel and, the stranger that came near, was to be put to death.
Mose ndi Aaroni ndi ana ake aamuna ankamanga misasa yawo kummawa kwa chihema, kuyangʼana kotulukira dzuwa, kutsogolo kwa tenti ya msonkhano. Anali ndi ntchito yosamalira malo wopatulika mʼmalo mwa Aisraeli. Aliyense woyandikira malo wopatulika ankayenera kuphedwa.
39 All they who were numbered of the Levites whom Moses [and Aaron] numbered at the bidding of Yahweh by their families, —every male, from one month old and upwards, were two-and-twenty thousand.
Alevi onse amene Mose ndi Aaroni anawawerenga potsatira lamulo la Yehova monga mwa magulu a mabanja awo, amuna onse kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo anali 22,000.
40 And Yahweh said unto Moses: Number thou every firstborn male belonging to the sons of Israel, from one month old and upwards, —and reckon up the number of their names;
Yehova anawuza Mose kuti, “Werenga ana onse aamuna oyamba kubadwa mu Israeli, omwe ali ndi mwezi umodzi kapena kupitirirapo ndipo ulembe mndandanda wa mayina awo.
41 then shalt thou take the Levites for me, me Yahweh, instead of every firstborn among the sons of Israel, —also the cattle of the Levites, instead of every firstling among the cattle of the sons of Israel.
Unditengere Alevi onse mʼmalo mwa ana oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso ziweto zazimuna za Alevi mʼmalo mwa ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa za Aisraeli. Ine ndine Yehova.”
42 So then Moses numbered, as Yahweh commanded him, —every firstborn among the sons of Israel.
Choncho Mose anawerenga ana aamuna onse oyamba kubadwa a Aisraeli monga momwe Yehova anamulamulira.
43 And it was so—that all the firstborn of the males in the counting of names from one month old and upwards of such as were numbered of them, —were two-and-twenty thousand, two hundred and seventy-three.
Chiwerengero chonse cha ana aamuna oyamba kubadwa kuyambira a mwezi umodzi kapena kupitirirapo chinali 22, 273.
44 Then spake Yahweh unto Moses, saying: —
Ndipo Yehova anawuzanso Mose kuti,
45 Take the Levites, instead of all the firstborn among the sons of Israel, and the cattle of the Levites, instead of their cattle, —so shall the Levites belong unto me, me Yahweh;
“Tenga Alevi mʼmalo mwa ana aamuna oyamba kubadwa onse a Aisraeli, ndiponso zoweta zonse za Alevi mʼmalo mwa zoweta za Aisraeli. Alevi ndi anga. Ine ndine Yehova.
46 and as the ransom of the two hundred and seventy-three, —who are more than the Levites, of the firstborn of the sons of Israel,
Pofuna kuwombola ana aamuna 273 oyamba kubadwa a Aisraeli amene anaposa chiwerengero cha aamuna a fuko la Levi,
47 thou shalt take five shekels apiece by the poll, —by the shekel of the sanctuary, shalt thou take it, twenty gerahs to the shekel;
utenge masekeli asanu pa munthu aliyense. Masekeliwo akhale ofanana ndi masekeli a ku malo wopatulika, kumene sekeli imodzi imakwanira magera makumi awiri.
48 and shalt give the silver to Aaron and to his sons, —as the ransom of them that are in excess over them.
Ndalama zimenezi uzipereke kwa Aaroni ndi ana ake aamuna kuti ukhale mtengo woombolera Aisraeli woonjezerawo.”
49 So Moses took the redemption silver from them who were in excess over them who were redeemed by the Levites:
Choncho Mose anatenga ndalama zowombolera zija kuchokera kwa Aisraeli amene chiwerengero chawo chinaposa chiwerengero cha omwe anawomboledwa ndi Alevi.
50 from the firstborn of the sons of Israel, took he the silver, —a thousand three hundred and sixty-five shekels, by the shekel of the sanctuary,
Anatenga masekeli a siliva okwana 1,365 molingana ndi masekeli a ku malo opatulika, kuchokera kwa ana aamuna oyamba kubadwa a Aisraeli.
51 And Moses gave the redemption silver to Aaron and to his sons at the bidding of Yahweh, —As Yahweh commanded Moses.
Mose anapereka ndalama zowombolera zija kwa Aaroni ndi ana ake aamuna monga mwa mawu amene Yehova analamulira.

< Numbers 3 >