< Numbers 28 >

1 And Yahweh spake unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Command the sons of Israel, and thou shalt say unto them, —My offering, my food for my altar-flames my satisfying odour, shall ye take heed to offer unto me in its season,
“Lamula Aisraeli kuti, ‘Onetsetsani kuti mukupereka kwa Ine pa nthawi yoyikika, chopereka cha chakudya chotentha pa moto monga fungo lokoma kwa Ine.’
3 Therefore shalt thou say to them. This, is the altar-flame, which ye shall offer unto Yahweh, —he-lambs a year old, without defect, two daily, as a continual ascending-sacrifice.
Awuze kuti, ‘Nsembe ya chakudya imene muzipereka pa moto kwa Yehova tsiku ndi tsiku ndi iyi: Ana ankhosa a chaka chimodzi awiri, wopanda chilema.
4 The one lamb, shalt thou offer in the morning, —and the other lamb, shalt thou offer between the two evenings;
Mmawa muzipereka mwana wankhosa mmodzi ndipo winayo madzulo.
5 also the tenth of an ephah of fine meal for a meal-offering, —overflowed with beaten oil the fourth of a hin:
Muziperekanso kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi lita imodzi ya mafuta a olivi.
6 a continual ascending-sacrifice, —which was offered in Mount Sinai, as a satisfying odour an altar-flame unto Yahweh.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku imene analamula pa phiri la Sinai kuti ikhale fungo lokoma, nsembe yopsereza pa moto yopereka kwa Yehova.
7 Also the drink-offering thereof the fourth of a hin for each lamb, —in a holy place, shall it be poured out as a libation of strong drink unto Yahweh.
Chopereka chachakumwa chikhale lita imodzi yachakumwa chaukali pa nkhosa iliyonse. Muzithira pamalo opatulika, kupereka kwa Yehova.
8 And, the other lamb, shalt thou offer between the two evenings; like the meal-offering of the morning, and like the drink-offering thereof, shalt thou offer, an altar flame a satisfying odour unto Yahweh.
Muzipereka mwana wankhosa winayo madzulo, pamodzi ndi chopereka chachakudya monga poyamba paja ndi chopereka chachakumwa monga mmawa. Ichi ndi chopereka chachakudya, fungo lokoma kwa Yehova.’”
9 But, on the sabbath day, two he-lambs a year old without defect, and two-tenths of fine meal as a meal-offering, overflowed with oil and the drink-offering thereof:
“‘Pa tsiku la Sabata, muzipereka nsembe ana ankhosa awiri a chaka chimodzi wopanda chilema, pamodzi ndi chopereka chachakumwa ndi chopereka chachakudya chokwana makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta.
10 the ascending-sacrifice of a sabbath, on its own sabbath, —besides the continual ascending-sacrifice and the drink-offering thereof.
Iyi ndi nsembe yopsereza ya pa Sabata iliyonse, kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake chachakumwa.’”
11 And in the beginnings of your months, shall ye bring near an ascending-sacrifice unto Yahweh, two choice bullocks and one ram, seven he-lambs a year old without defect;
“Pa tsiku loyamba la mwezi uliwonse muzipereka kwa Yehova nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi, ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi, onse wopanda chilema.
12 and three-tenths of fine meal, as a meal-offering, overflowed with oil, to each bullock, —and two-tenths of fine-meal as a meal-offering, overflowed with oil, to each ram;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; ndi nkhosa yayimuna, chopereka cha chakudya cha makilogalamu awiri a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta;
13 and a tenth, severally, of fine meal as a meal-offering, overflowed with oil, to each lamb, —an ascending-sacrifice, a satisfying odour, an altar-flame unto Yahweh.
ndipo pa mwana wankhosa aliyense, chopereka cha ufa wa kilogalamu imodzi ya ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, izi ndi za nsembe yopsereza, fungo lokoma, nsembe yotentha pa moto ya kwa Yehova.
14 And as their drink-offerings, half a hin, shall be to a bullock and the third of a hin to a ram, and the fourth of a hin to a lamb, of wine, —This, is the ascending-sacrifice of a month in its month, for the months of the year.
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pakhale chopereka cha chakumwa cha malita awiri a vinyo; ndipo pa nkhosa yayimuna, lita limodzi ndi theka, ndipo pa mwana wankhosa, lita limodzi. Iyi ndi nsembe yopsereza ya mwezi ndi mwezi yoperekedwa pa mwezi watsopano mʼkati mwa chaka.
15 Also one he-goat as a sin-bearer unto Yahweh, —besides the continual ascending-sacrifice, shall it be offered, with the drink-offering thereof.
Powonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse ndi chopereka chake cha chakumwa, mbuzi yayimuna imodzi iperekedwe kwa Yehova ngati nsembe yopepesera machimo.
16 And, on the first month on the fourteenth day of the month, shall be a passover unto Yahweh;
“‘Pa tsiku la 14 la mwezi woyamba muzichita Paska wa Yehova.
17 and, on the fifteenth day of this month, a festival, —seven days, unleavened cakes, shall be eaten.
Pa tsiku la 15 la mwezi womwewo pazikhala chikondwerero. Muzidya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri.
18 On the first day, a holy convocation, —no laborious work, shall ye do;
Pa tsiku loyamba muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
19 but ye shall bring near—as an altar-flame—an ascending-sacrifice unto Yahweh, —two choice bullocks and one ram, —and seven he-lambs a year old, without defect, must they be for you;
Koma muzipereka kwa Yehova nsembe yotentha pa moto, nsembe yopsereza ya ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa yayimuna imodzi ndi ana ankhosa asanu ndi awiri aamuna a chaka chimodzi, onsewo wopanda chilema.
20 and, for their meal-offering, fine meal, overflowed with oil, —three-tenths for a bullock, and two-tenths for a ram, shall ye offer;
Pamodzi ndi ngʼombe yayimuna iliyonse, muzikonza chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta; makilogalamu awiri pa nkhosa yayimuna iliyonse.
21 a tenth, severally, shalt thou offer for each lamb, —for the seven lambs;
Kilogalamu imodzi pa mwana wankhosa aliyense mwa ana ankhosa asanu ndi awiri aja.
22 also one he-goat for bearing sin, to put a propitiatory-covering over you:
Muziphatikizapo mbuzi yayimuna monga nsembe yopepesera machimo anu.
23 in addition to the ascending-sacrifice of the morning, which is for the continual ascending-sacrifice, shall ye offer these.
Muzikonza zimenezi nthawi zonse, powonjezera pa nsembe yopsereza ya mmawa.
24 Like these, shall ye offer, daily, for seven days, as the food of the altar-flame of a satisfying odour, unto Yahweh, —besides the continual ascending-sacrifice, shall it be offered, with the drink-offering thereof.
Motere muzikonza chakudya cha nsembe yopsereza ya tsiku ndi tsiku pa masiku asanu ndi awiri ngati fungo lokomera Yehova. Zimenezi ziziperekedwa kuwonjezera pa nsembe yopsereza ya nthawi zonse pamodzi ndi nsembe yachakumwa.
25 And on the seventh day, shall ye have, a holy convocation, —no laborious work, shall ye do.
Pa tsiku lachisanu ndi chiwiri muzichita msonkhano wopatulika ndipo musamagwire ntchito iliyonse.
26 And on the day of firstfruits when ye bring near a new meal-offering unto Yahweh, in your weeks, a holy convocation shall there be unto you, no laborious work, shall ye do;
“‘Pa tsiku la zipatso zoyambirira kucha, pamene mukupereka chopereka cha chakudya chatsopano kwa Yehova, pa nthawi ya chikondwerero cha Masabata, muzichita msonkhano wopatulika ndipo musagwire ntchito zolemetsa.
27 but ye shall bring near as an ascending-sacrifice, for a satisfying odour unto Yahweh, two choice bullocks one ram, —seven he-lambs a year old;
Muzipereka nsembe zopsereza za ana angʼombe aamuna awiri, nkhosa imodzi yayimuna ndi ana ankhosa aamuna asanu ndi awiri a chaka chimodzi monga fungo lokomera Yehova.
28 also their meal-offering, fine meal, overflowed with oil, —three-tenths for each bullock, two-tenths for the one ram;
Pa ngʼombe yayimuna iliyonse pazikhala chopereka cha chakudya cha makilogalamu atatu a ufa wosalala wosakaniza ndi mafuta, pa nkhosa yayimuna iliyonse makilogalamu awiri.
29 a tenth severally, for each lamb, —of the seven lambs;
Ndipo pa mwana wankhosa aliyense mwa asanu ndi awiri aja, kilogalamu imodzi.
30 one young he-goat, —for putting a propitiatory-covering over you:
Muziperekanso mbuzi yayimuna imodzi kuti izikhala nsembe yopepesera machimo anu.
31 in addition to, the continual ascending-sacrifice, with the meal-offering thereof, shall ye offer them, —without defect, shall they be for you, with their drink-offerings.
Muzipereka zimenezi pamodzi ndi zopereka za zakumwa ndi nsembe yake ya chakudya. Onetsetsani kuti nyamazo zilibe chilema.

< Numbers 28 >