< Numbers 20 >

1 Then came the sons of Israel the whole assembly, into the desert of Zin in the first month, and the people dwelt in Kadesh, —and Miriam died there, and was buried there.
Pa mwezi woyamba gulu lonse la Aisraeli linafika ku chipululu cha Zini, ndipo anakhala ku Kadesi. Miriamu anafera kumeneko ndipo anayikidwa mʼmanda.
2 And there was no water for the assembly, —so they gathered together against Moses and against Aaron.
Kunalibe madzi woti anthu onse ndi kumwa, choncho anthuwo anasonkhana motsutsana ndi Mose ndi Aaroni.
3 And the people contended with Moses, —and spake saying, Would then we had died when our brethren died, before Yahweh!
Anakangana ndi Mose kuti, “Kunali bwino ifenso tikanangofa pamene abale athu anafa pamaso pa Yehova!
4 Wherefore then hast thou brought the convocation of Yahweh into this desert, —to die there, we, and our cattle?
Chifukwa chiyani unabweretsa gulu la Yehova mʼchipululu muno, kuti ife ndi ziweto zathu tife kuno?
5 And wherefore did ye cause us to come up out of Egypt, to bring us into this wretched place?—not a place of seeds, and figs, and vines and pomegranates, even water, is there none to drink.
Nʼchifukwa chiyani unatitulutsa mʼdziko la Igupto ndi kutibweretsa kumalo woyipa ano? Kuno kulibe tirigu kapena nkhuyu, mphesa kapena makangadza. Ndipo kuno kulibenso madzi akumwa!”
6 And Moses and Aaron went in from the presence of the multitude unto the entrance of the tent of meeting, and fell upon their faces, —and the glory of Yahweh appeared unto them.
Mose ndi Aaroni anachoka mu msonkhano ndi kupita pa khomo la tenti ya msonkhano, nagwa pansi chafufumimba ndipo ulemerero wa Yehova unaonekera.
7 Then spake Yahweh unto Moses, saying:
Yehova anati kwa Mose,
8 Take the staff and gather together the assembly, thou, and Aaron thy brother, then shall ye speak unto the cliff before their eyes and it shall give forth its waters, —so shalt thou bring forth unto them water, out of the cliff, and shalt cause the assembly, and their cattle to drink.
“Tenga ndodo, ndipo iwe ndi mʼbale wako Aaroni musonkhanitse anthu onse pamodzi. Uyankhule ndi thanthwe ilo iwo akuona ndipo lidzatulutsa madzi ake. Udzatulutsa madzi mʼthanthwe limeneli kuti anthu onse ndi ziweto zawo amwe.”
9 And Moses took the staff from before Yahweh, —as he commanded him.
Choncho Mose anatenga ndodo pamaso pa Yehova monga momwe anamulamulira.
10 And Moses and Aaron gathered together the convocation before the cliff, —and he said unto them: Hear I pray you ye rebels! Out of this cliff, must we bring forth for you water?
Mose ndi Aaroni anasonkhanitsa anthuwo pamodzi ku thanthwelo ndipo Mose anawawuza kuti, “Tamverani osamvera inu, kodi tikupatseni madzi kuchokera ku thanthwe ili?”
11 And Moses lifted high his hand and smote the cliff with his staff, twice, —and there came forth water in abundance, and the assembly and their cattle, did drink.
Choncho Mose anatukula dzanja lake ndi kumenya thanthwelo kawiri ndi ndodo yake ndipo madzi ambiri anatuluka mwamphamvu, ndipo anthu ndi ziweto zawo anamwa.
12 Then said Yahweh unto Moses and unto Aaron, Because ye believed not in me, to hallow me in the eyes of the sons of Israel, therefore, shall ye not bring in this convocation into the land which I have given unto them.
Koma Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni, “Chifukwa chakuti simunandikhulupirire ndiponso simunandilemekeze monga Woyera pamaso pa Aisraeli, simudzalowetsa anthuwa mʼdziko limene ndikupereka kwa iwo.”
13 The same, were the waters of Meribah [that is "Contention"] in that the sons of Israel contended with Yahweh, —and so he hallowed himself among them.
Awa anali madzi a ku Meriba, kumene Aisraeli anakangana ndi Yehova ndiponso kumene Yehovayo anadzionetsa yekha kuti ndi Woyera pakati pawo.
14 And Moses sent messengers from Kadesh, unto the king of Edom, —Thus, saith thy brother Israel, Thou thyself, knowest all the distress which befell us;
Mose anatumiza amithenga kuchokera ku Kadesi kupita kwa mfumu ya ku Edomu, kukanena kuti, “Mʼbale wako Israeli akunena izi: Inuyo mukudziwa za mavuto onse amene anatigwera.
15 and how our fathers went down to Egypt, and we abode in Egypt, many days, and that the Egyptians ill-treated us, and our fathers;
Makolo athu anapita ku Igupto ndipo tinakhala kumeneko zaka zambiri. Aigupto anatizunza pamodzi ndi makolo athuwo,
16 and we made outcry unto Yahweh, and he heard our voice, and sent a messenger, and brought us forth out of Egypt, —lo! then, we, are in Kadesh, a city at the extremity of thy boundary,
koma titalirira Yehova, Iyeyo anamva kulira kwathuko ndipo anatitumizira mngelo amene anatitulutsa ku Igupto.” “Taonani, tsopano tili pano pa Kadesi, mzinda wa mʼmalire a dziko lanu.
17 Let us, we pray thee, pass through thy land—we will not pass through field or vineyard, nor will we drink the waters of a well, —by the king’s road, will we go—we will turn neither to the right hand nor to the left, until we get through thy boundary.
Chonde mutilole tidutse mʼdziko lanu. Sitidzera mʼminda yanu kapena mu mpesa wanu, kapenanso kumwa madzi mʼchitsime chilichonse. Tidzayenda kutsata msewu waukulu wa mfumu ndipo sitidzapatukira ku dzanja lamanja kapena lamanzere mpaka titadutsa malire a dziko lanu.”
18 And Edom said unto him, Thou shalt not pass through my land, —lest with the sword, I come out to meet thee.
Koma Edomu anayankha kuti, “Musadutse kuno: Mukangoyesera tidzabwera ndi kumenyana nanu ndi lupanga.”
19 And the sons of Israel said unto him—By the highway, will we go up, and if thy waters, we should drink—I, and my cattle then would I give the price thereof, —only—it is nothing!—with my feet, would I pass through.
Aisraeli anayankha kuti, “Tidzayenda motsata msewu waukulu. Ndipo ngati ife kapena ziweto zathu tidzamwa madzi anu tidzalipira. Tikungofuna tidutse nawo, palibenso china.”
20 And he said, Thou shalt not pass through. And Edom came out to meet him, with a strong people, and with a firm hand.
Koma Edomu anayankhanso kuti, “Musadutse.” Kenaka Edomu anatuluka ndi gulu lankhondo lalikulu komanso lamphamvu.
21 Thus did Edom refuse to give Israel passage through his boundary, —and Israel turned away from him.
Edomu anakaniza Israeli kuti adutse mʼdziko lake, choncho Israeli anabwerera.
22 Then set they forward from Kadesh, —and the sons of Israel. all the assembly, came in to Mount Hor.
Gulu lonse la Aisraeli linachoka ku Kadesi ndipo linafika ku phiri la Hori.
23 Then spake Yahweh unto Moses and unto Aaron in Mount Hor, —near the boundary of the land of Edom saying:
Ali pa phiri la Hori, pafupi ndi malire a Edomu, Yehova anati kwa Mose ndi Aaroni,
24 Aaron shall be withdrawn unto his kinsfolk, for he shall not enter into the land. which I have given unto the sons of Israel, —because ye spurned my bidding, at the waters of Meribah.
“Aaroni adzakakhala ndi anthu a mtundu wake, sadzalowa mʼdziko limene ndapereka kwa Aisraeli, chifukwa nonse munandiwukira motsutsana ndi malamulo anga ku madzi a ku Meriba.
25 Take thou Aaron, and Eleazar his son, —and bring them up Mount Hor;
Tenga Aaroni ndi mwana wake wamwamuna Eliezara ndipo ukwere nawo ku phiri la Hori.
26 and strip thou Aaron of his garments, and put them upon Eleazar his son, —and, Aaron, shall be withdrawn and shall die there.
Uvule Aaroni zovala zake ndipo umuveke mwana wake Eliezara, pakuti Aaroni adzafera komweko, ndipo adzakakhala ndi anthu a mtundu wake.”
27 And Moses did as Yahweh commanded, —and they went up into, Mount Hor, in sight of all the assembly.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira: Anapita ku phiri la Hori gulu lonse likuona.
28 And Moses stripped Aaron of his garments and put them upon Eleazar his son, and Aaron died there, in the top of the mount, —and Moses and Eleazar came down out of the mount.
Pamenepo Mose anavula Aaroni zovala zake ndi kuveka mwana wake Eliezara. Aaroni anafa kumeneko pamwamba pa phirilo. Koma Mose ndi Eliezara anatsika ku phiriko,
29 And all the assembly saw that Aaron was dead; and they bewailed Aaron thirty days, even all the house of Israel.
ndipo pamene anthu onse anamva kuti Aaroni wafa, nyumba yonse ya Israeli inamulira Aaroniyo masiku makumi atatu.

< Numbers 20 >