< Numbers 17 >
1 Then spake Yahweh unto Moses, saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
2 Speak unto the sons of Israel and take of them one staff each for an ancestral house of all their princes, by their ancestral houses, twelve staves, —each man’s name, shalt thou write upon his staff;
“Yankhula ndi Aisraeli ndipo akupatse ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse. Ulembe dzina la munthu aliyense pa ndodo yake.
3 and, Aaron’s name, shalt thou write upon the staff of Levi, —for, one staff, shall there be for the head of their ancestral house.
Pa ndodo ya Levi ulembepo dzina la Aaroni, chifukwa pafunika ndodo imodzi ya mtsogoleri pa fuko lililonse.
4 Then shalt thou lay them up in the tent of meeting, —before the testimony, where I meet with you.
Uyike ndodozo mu tenti ya msonkhano, kutsogolo kwa Bokosi la Umboni, kumene ndimakumana nawe.
5 So shall it come to pass, that, the man whom I shall choose, his staff, shall bud, —so will I cause to cease from against me the murmurings of the sons of Israel, wherewith they, are murmuring against you.
Ndodo ya munthu amene ndamusankha idzachita maluwa potero ndidzaletsa madandawulo osatha a Aisraeli otsutsana nawe.”
6 And Moses spake unto the sons of Israel and every one of their princes gave unto him, a staff apiece, for each prince, by their ancestral houses, twelve staves, —and the staff of Aaron, was in the midst of their staves.
Choncho Mose anayankhula ndi Aisraeli, ndipo atsogoleri awo anapereka ndodo khumi ndi ziwiri, imodzi kuchokera kwa mtsogoleri wa fuko lililonse ndipo ndodo ya Aaroni inali pakati pa ndodo zawozo.
7 So Moses laid up the staves before Yahweh, —in the tent of the testimony.
Mose anayika ndodozo pamaso pa Yehova mu tenti ya msonkhano.
8 And it came to pass, on the morrow, that Moses entered into the tent of the testimony; and lo! the staff of Aaron for the house of Levi, had budded, —yea it had brought forth buds and bloomed blossoms, and borne ripe almonds.
Pa tsiku lotsatira Mose analowa mu tenti ya msonkhanoyo ndipo anaona kuti ndodo ya Aaroni, yomwe inkayimira fuko la Levi, sinangophuka masamba chabe, komanso inachita maluwa nʼkubala zipatso za alimondi.
9 So then Moses brought forth all the staves, from before Yahweh, unto all the sons of Israel, —and they saw and took, each man his own staff.
Choncho Mose anatulutsa ndodo zonse pamaso pa Yehova napita nazo kwa Aisraeli onse. Iwowo anaziona ndipo munthu aliyense anatenga ndodo yake.
10 And Yahweh said unto Moses—Put back the rod of Aaron, before the testimony, to be kept as a sign unto such as are perverse, —that thou mayest bring to an end their murmurings against me that they die not.
Yehova anawuza Mose kuti, “Bwezera ndodo ya Aaroni patsogolo pa Bokosi la Umboni, kuti chikhale chizindikiro cha kuwukira kwawo. Zimenezi zidzathetsa kudandaula kwawo kotsutsana nane, kuopa kuti angafe.”
11 Thus did Moses, —as Yahweh commanded him, so, did he.
Mose anachita monga Yehova anamulamulira.
12 Then spake the sons of Israel unto Moses saying: Lo! we have breathed our last—we are lost, we are, all, lost:
Aisraeli anati kwa Mose, “Tikufa! Tatayika, tonse tatayika!
13 whosoever draweth near—draweth near—unto the habitation of Yahweh, dieth, —are we ever to have made an end of breathing our last?
Aliyense woyandikira chihema adzafa. Kodi ndiye kuti tonse tikufa?”