< Nehemiah 6 >

1 And it came to pass, when it was reported to Sanballat and Tobiah and to Geshem the Arabian and to the rest of our enemies, that I had built the wall, and there was left therein no breach, —though, up to that time, the doors, had I not set up in the gates,
Pamenepo Sanibalati, Tobiya, Gesemu Mwarabu ndi adani athu anamva kuti ndatsiriza ntchito yomanganso khoma ndi kuti palibe mpata umene watsala ngakhale kuti pa nthawi imeneyi ndinali ndisanayike zitseko pa zipata.
2 that Sanballat and Geshem sent unto me, saying, Come! and let us meet together in the villages, in the valley of Ono, —But, they, were plotting to do me harm.
Sanibalati ndi Gesemu, ananditumizira uthenga uwu: “Bwerani tidzakumane pa mudzi wina ku chigwa cha Ono.” Koma iwo anakonzekera kuti akandichite chiwembu kumeneko.
3 So I sent unto them messengers, saying, A great work, am, I, doing, and cannot come down, —wherefore should the work cease whilst I leave it, and come down unto you?
Choncho ine ndinatuma amithenga ndi yankho ili: “Ine ndikugwira ntchito yayikulu kuno ndipo sindingathe kubwera kumeneko. Kodi ntchito iyime pofuna kuti ndibwere kumeneko?”
4 Yet they sent unto me, according to this message, four times, —and I replied to them according to this answer.
Ananditumizira uthenga umodzimodzi omwewu kanayi ndipo ndinawayankha chimodzimodzi.
5 Then Sanballat sent unto me, according to this message, a fifth time, by his young man, —with an open letter, in his hand:
Tsono kachisanu, Sanibalati anatumiza wantchito wake ndi kalata yosamata.
6 wherein was written—Among the nations, it is reported, and, Gashmu, saith it, that, thou and the Jews, are plotting to rebel, for which cause, thou art building the wall, —and, thou, art to become their king, according to these words.
Mu kalatamo munali mawu akuti, “Pali mphekesera pakati pa mitundu ya anthu, ndiponso Gesemu akunena zomwezo kuti inu ndi Ayuda onse mufuna kuwukira boma. Nʼchifukwa chake mukumanga khoma. Mphekeserazo zikutinso inu mukufuna kudzakhala mfumu yawo.
7 Moreover also, prophets, hast thou set up to make proclamation concerning thee in Jerusalem, saying, He hath become king in Judah! Now, therefore, will it he reported to the king, according to these words. Now, therefore, come, and let us take counsel together.
Mwayikanso kale aneneri amene adzalengeza za iwe mu Yerusalemu kuti ‘Mu Yuda muli mfumu!’ Tsono nkhani iyi imveka ndithu kwa mfumu. Choncho bwerani kuti tidzakambirane.”
8 Then sent I unto him, saying, Nothing hath been done, according to these words, which thou art saying, —but, out of thine own heart, art thou feigning them.
Ine ndinatumiza yankho ili: “Pa zimene mukunenazo, palibe chimene chinachitikapo. Inu mukungozipeka mʼmutu mwanu.”
9 For, they all, were seeking to put us in fear, saying, Their hands will slacken from the work, and it will not be accomplished. Now, therefore, strengthen thou my hands!
Apa adani athu onsewa ankangofuna kutiopseza. Iwo ankaganiza kuti “Tichita mantha ndi kuleka kugwira ntchito.” Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu ndilimbitseni mtima.”
10 When, I, came into the house of Shemaiah, son of Delaiah, son of Mehetabel, he, being shut in, he said, Let us meet together in the house of God, in the midst of the temple, and let us close the doors of the temple, for they are coming to slay thee, yea, by night, are they coming to slay thee.
Tsiku lina ndinapita ku nyumba ya Semaya mwana wa Delaya mwana wa Mehatabeli. Tsono anandiwuza kuti, “Tiyeni tikakumanire ku Nyumba ya Mulungu. Tikabisale mʼmenemo ndi kutseka zitseko chifukwa akubwera kudzakuphani. Ndithu usiku uno akubwera kudzakuphani.”
11 Then said I, Should, such a man as I, flee? Who then, being such as I, would enter the temple to save his life? I will not enter.
Koma ndinayankha kuti, “Kodi munthu ngati ine nʼkuthawa? Kapena munthu wofanana ndi ine nʼkupita ku Nyumba ya Mulungu kuti apulumutse moyo wake? Ayi, ine sindipita!”
12 Then perceived I, that lo! it was, not God, who had sent him, —though, a prophecy, he had spoken concerning me, but, Tobiah and Sanballat, had hired him:
Ndinazindikira kuti Mulungu sanamutume koma kuti anayankhula mawu oloserawa motsutsana nane chifukwa Tobiya ndi Sanibalati anamulemba ntchitoyi.
13 to this end, hired, he was, to the end that I might be afraid and do so, and might sin, —and it might serve them for an evil report, to the end they might bring reproach upon me.
Iye analembedwa ntchitoyi ndi cholinga choti ine ndichite mantha, ndithawe. Ndikanatero ndiye kuti ndikanachimwira Yehova ndiponso iwowo akanandiyipitsira mbiri yanga ndi kumandinyoza.
14 Have remembrance, O my God, of Tobiah and of Sanballat, according to these their doings, —moreover also, of Noadiah the prophetess, and of the rest of the prophets, who would have put me in fear.
Tsono ndinapemphera kuti, “Inu Mulungu wanga, kumbukirani Tobiya ndi Sanibalati chifukwa cha zimene achita. Kumbukiraninso mneneri wamkazi Nowadiya ndi aneneri amene akhala akufuna kundiopseza.”
15 So the wall was finished, on the twenty-fifth of Elul, —in fifty-two days.
Ndipo khoma linatsirizidwa kumanga pa tsiku la 25 la mwezi wa Eluli. Linamangidwa pa masiku okwana 52.
16 And it came to pass, when all our enemies heard, and all the nations that were round about us saw, that they fell greatly in their own eyes, and took knowledge that, from God, had this work been wrought.
Adani athu onse atamva izi, mitundu yonse ya anthu yozungulira inachita mantha ndi kuchita manyazi. Iwo anazindikira kuti ntchitoyo inachitika ndi thandizo la Mulungu wathu.
17 Moreover, in those days, were the nobles of Judah busy with their letters which were going unto Tobiah, —and those of Tobiah were coming unto them;
Komanso masiku amenewo anthu olemekezeka a ku Yuda ankalemberana naye makalata ambiri ndi Tobiyayo,
18 for, many in Judah, had taken an oath to him, because he was in marriage affinity with Shecaniah son of Arah, —and, Jehohanan his son, had taken the daughter of Meshullam, son of Berechiah.
pakuti anthu ambiri a ku Yuda anali atalumbira kale kuti adzagwira naye ntchito popeza anali mkamwini wa Sekaniya mwana wa Ara, ndipo mwana wake Yehohanani anakwatira mwana wamkazi wa Mesulamu mwana wa Berekiya.
19 Moreover, his good deeds, were they telling before me, and, my affairs, were they carrying out to him, —letters, did Tobiah send to put me in fear.
Kuwonjezera apo, anthu ankasimba za ntchito zake zabwino ine ndili pomwepo ndipo anakamuwululira mawu anga. Choncho Tobiyayo ankatumiza makalata ondiopseza.

< Nehemiah 6 >