< Matthew 26 >

1 And it came to pass, when Jesus ended all these words, he said unto his disciples:
Yesu atamaliza kuyankhula zonsezi, anati kwa ophunzira ake,
2 Ye know that, after two days, the passover, taketh place, —and, the Son of Man, is to be delivered up, to be crucified.
“Monga mukudziwa, kwatsala masiku awiri kuti Paska ifike ndipo Mwana wa Munthu adzaperekedwa kuti apachikidwe.”
3 Then, were gathered together, the High-priests and the Elders of the people, into the court of the High-priest who was called Caiaphas;
Pamenepo akulu a ansembe ndi akuluakulu anasonkhana ku nyumba ya mkulu wa ansembe dzina lake Kayafa,
4 and they took counsel together, in order that, Jesus, by guile, they might secure, and slay.
ndipo anapangana kuti amugwire Yesu mobisa ndi kumupha.
5 They were saying, however: Not during the feast, lest, an uproar, arise among the people.
Ndipo anati, “Osati nthawi yaphwando chifukwa pangabuke chipolowe pakati pa anthu.”
6 But, Jesus, happening to be in Bethany, in the house of Simon the leper,
Yesu ali ku Betaniya mʼnyumba Simoni Wakhate,
7 there came unto him a woman, holding an alabaster-jar of costly perfume, and she poured it down upon his head, as he was reclining.
mayi wina anabwera kwa Iye ndi botolo la mafuta onunkhira a mtengowapatali, amene anathira pa mutu pake Iye akudya pa tebulo.
8 And the disciples, seeing it, were greatly displeased, saying—To what end, this loss?
Ophunzira ataona izi anayipidwa nafunsa kuti, “Chifukwa chiyani akuwononga chotere?
9 For this could have been sold for much, and given to the destitute.
Mafuta amenewa akanatha kugulitsidwa pa mtengo waukulu, ndipo ndalama zake zikanaperekedwa kwa osauka.”
10 But Jesus, taking note, said unto them—Why vex ye the woman? for, a seemly work, hath she wrought for me;
Yesu podziwa izi anawawuza kuti, “Chifukwa chiyani mukumuvutitsa mayiyu? Wandichitira Ine chinthu chabwino.
11 For, always, the destitute, have ye with you, —but, me, not always, have ye;
Osauka mudzakhala nawo nthawi zonse, koma simudzakhala ndi Ine nthawi zonse.
12 For, she, pouring this perfume upon my body, so as to prepare me for burial, did it.
Pamene wathira mafuta onunkhirawa pa thupi langa, wachita izi kukonzekera kuyikidwa kwanga mʼmanda.
13 Verily, I say unto you—Wheresoever this glad-message shall be proclaimed in all the world, also what she did, will be told, as a memorial of her.
Zoonadi, ndikuwuzani kuti kulikonse kumene Uthenga Wabwinowu udzalalikidwa ku dziko lonse lapansi, zimene wachitazi zidzanenedwanso pomukumbukira.”
14 Then, went one of the twelve, the one called Judas Iscariot, unto the High-priests,
Pamenepo mmodzi wa khumi ndi awiriwo wotchedwa Yudasi Isikarioti anapita kwa akulu a ansembe
15 and said—What are ye willing to give unto me? and, I, unto you, will deliver him up. And they appointed him thirty pieces of silver.
nafunsa kuti, “Kodi mundipatsa chiyani ngati nditamupereka Iye kwa inu?” Pamenepo anamuwerengera ndalama zokwanira masiliva makumi atatu.
16 And, from that time, was he seeking a favourable opportunity that he might, deliver him up.
Kuyambira pamenepo Yudasi anafunafuna nthawi yabwino yoti amupereke Yesu.
17 And, on the first of the days of unleavened bread, the disciples came unto Jesus, saying—Where wilt thou, that we make ready for thee to eat the passover?
Pa tsiku loyamba laphwando la buledi wopanda yisiti, ophunzira anabwera kwa Yesu ndi kumufunsa kuti, “Kodi mukufuna tikakonze kuti malo odyera Paska?”
18 And, he, said—Go your way into the city, unto such-a-one, and say to him, The teacher, saith, My season, is, near, with thee, will I keep the passover, with my disciples.
Iye anayankha kuti, “Pitani mu mzinda kwa munthu wakutiwakuti ndipo kamuwuzeni kuti, ‘Aphunzitsi akuti, nthawi yanga yoyikidwa yayandikira. Ine ndidzadya phwando la Paska ndi ophunzira anga ku nyumba kwako.’”
19 And the disciples did, as Jesus directed them, and made ready the passover.
Pamenepo ophunzira ake anachita monga momwe Yesu anawawuzira ndipo anakonza Paska.
20 And, when, evening, came, he was reclining with the twelve [disciples];
Kutada, Yesu ndi ophunzira ake khumi ndi awiriwo anakhala pa tebulo nʼkumadya.
21 and, as they were eating, he said—Verily, I say unto you, One from among you, will deliver me up.
Akudya, Iye anati, “Zoonadi, ndikuwuzani kuti mmodzi wa inu adzandipereka.”
22 And, being exceedingly grieved, they began to be saying to him, each one—Can it be, I, Lord?
Iwo anamva chisoni kwambiri ndipo anayamba kuyankhulana naye mmodzimmodzi nati, “Kodi nʼkukhala ine Ambuye?”
23 And, he, answering, said—He who hath dipped with me his hand in the bowl, the same, will deliver me up.
Yesu anayankha nati, “Iye amene akusunsa mʼmbale pamodzi ndi Ine, yemweyo adzandipereka.
24 The Son of Man, indeed, goeth his way, according as it is written concerning him, —But alas! for that man, through whom the Son of Man, is being delivered up: Well, had it been for him, if, that man, had not been born!
Mwana wa Munthu adzaphedwa monga mmene kunalembedwera za Iye. Koma tsoka kwa munthu amene apereka Mwana wa Munthu! Kukanakhala bwino kwa iye akanapanda kubadwa.”
25 And Judas, who was delivering him up, answering, said—Can it be, I, Rabbi? He saith unto him—Thou, hast said.
Ndipo Yudasi amene anamupereka Iye anati, “Monga nʼkukhala ine Aphunzitsi?” Yesu anayankha nati, “Iwe watero.”
26 And, as they were eating, Jesus, taking a loaf and blessing, brake, —and, giving to his disciples, said—Take, eat! This, is, my body.
Pamene ankadya, Yesu anatenga buledi, nayamika ndipo anamunyema nagawira ophunzira ake nanena kuti, “Tengani, idyani; ili ndi thupi langa.”
27 And, taking a cup, and giving thanks, he gave unto them, saying—Drink of it, all of you;
Kenaka anatenga chikho, nayamika nachipereka kwa iwo nati, “Imwani nonsenu.
28 For, this, is my blood of the covenant, which, for many, is to be poured out, for remission of sins.
Awa ndi magazi anga a pangano amene akhetsedwa chifukwa cha ambiri kuti akhululukidwe machimo.
29 Moreover, I say unto you—In nowise, will I drink, henceforth, of this produce of the vine, until that day, whensoever I shall drink it with you, new, in the kingdom of my Father.
Ndikuwuzani kuti sindidzamwanso kuchokera ku chipatso cha mtengo wa mpesa kuyambira lero mpaka tsiku ilo pamene ndidzamwenso mwatsopano ndi inu mu ufumu wa Atate anga.”
30 And, having sung praise, they went forth unto the Mount of Olives.
Atayimba nyimbo, anatuluka kupita ku phiri la Olivi.
31 Then, Jesus saith unto them—All ye, will find cause of stumbling in me, during this night; for it is written, I will smite the shepherd, and, the sheep of the flock, will be scattered abroad;
Pamenepo Yesu anawawuza kuti, “Usiku omwe uno inu nonse mudzandithawa, pakuti kwalembedwa: “‘Kantha mʼbusa, ndipo nkhosa zidzabalalika.’
32 But, after my arising, I will go before you into Galilee.
Koma ndikadzauka, ndidzatsogola kupita ku Galileya.”
33 Now Peter, answering, said unto him—Though, all, shall find cause of stumbling in thee, I, shall never find cause of stumbling.
Petro anayankha nati, “Ngakhale onsewa atakuthawani, ine ndekha ayi.”
34 Jesus saith unto him: Verily, I say unto thee—During this night, before a cock crow, Thrice, wilt thou deny me.
Yesu anayankha nati, “Zoonadi, ndikukuwuza kuti usiku omwe uno, asanalire tambala, udzandikana Ine katatu.”
35 Peter saith unto him: Even though it be needful for me, with thee to die, in nowise, will I deny thee. Likewise, all the disciples also, said.
Koma Petro ananenetsa nati, “Ngakhale kutakhala kufa nanu pamodzi, sindidzakukanani.” Ndipo ophunzira onse ananena chimodzimodzi.
36 Then Jesus cometh with them, into a place called Gethsemane, —and he saith unto his disciples, Sit ye here, while I go yonder and pray.
Kenaka Yesu anapita ku malo otchedwa Getsemani, ndipo anawawuza kuti, “Khalani pano pamene Ine ndikukapemphera apo.”
37 And, taking with him, Peter and the two sons of Zebedee, he began to be grieved and to be in great distress.
Anatenga Petro ndi ana awiri a Zebedayo, ndipo anayamba kumva chisoni ndi kuvutika mu mtima.
38 Then, saith he unto them: Encompassed with grief, is my soul, unto death: Abide ye here, and be watching with me.
Pamenepo anawawuza kuti, “Moyo wanga uli ndi chisoni chofa nacho. Khalani pano ndipo dikirani pamodzi ndi Ine.”
39 And, going forward a little, he fell upon his face, offering prayer, and saying—My Father! If it is possible, let this cup pass from me, —Nevertheless, not as, I, will, but as, thou, wilt.
Atapita patsogolo pangʼono, anagwa pansi chafufumimba napemphera kuti, “Atate anga, ngati ndikotheka, chikho ichi chichotsedwe kwa Ine. Koma osati monga mmene ndifunira, koma monga mufunira Inu.”
40 And he cometh unto his disciples, and findeth them sleeping, and said unto Peter—Thus, powerless are ye, one hour, to watch with me?
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nawapeza ali mtulo. Iye anafunsa Petro kuti, “Kodi anthu inu, simukanakhala maso pamodzi ndi Ine kwa ora limodzi lokha?
41 Be watching and praying, that ye may not enter into temptation: The spirit, indeed, is, eager, but, the flesh, weak.
Khalani maso ndi kupemphera kuti musagwe mʼmayesero. Mzimu ukufuna koma thupi ndi lofowoka.”
42 Again, a second time, departing he prayed, saying: My Father! If it is impossible for this to pass, except I, drink, it, Accomplished, be, thy will.
Anachokanso nakapemphera kachiwiri kuti, “Atate anga, ngati chikhochi sichingandichoke, mpaka nditamwa, kufuna kwanu kuchitike.”
43 And coming, he, again, found them sleeping, for their eyes had become heavy.
Atabweranso anawapeza ali mtulo chifukwa zikope zawo zinalemedwa ndi tulo.
44 And, leaving them, he, again, departed, and prayed a third time, the same word, saying again.
Choncho anawasiya napitanso kukapemphera kachitatu nanenanso chimodzimodzi.
45 Then, cometh he unto the disciples, and saith unto them, —Ye are sleeping what time remaineth, and taking your rest: Lo! the hour hath drawn near, and, the Son of Man, is being delivered up into the hands of sinners.
Kenaka anabwera kwa ophunzira ake nati kwa iwo, “Kodi mukanagonabe ndi kupumula? Taonani, ora layandikira ndipo Mwana wa Munthu akuperekedwa mʼmanja mwa ochimwa.
46 Arise! let us be going, —Lo! he that delivereth me up, hath drawn near.
Imirirani, tiyeni tizipita! Wondipereka Ine wafika!”
47 And, while, yet, he was speaking, lo! Judas, one of the twelve, came, and, with him, a large multitude, with swords and clubs, from the High-priests and Elders of the people.
Akuyankhula choncho, Yudasi mmodzi mwa khumi ndi awiriwo anafika. Pamodzi ndi iye panali gulu lalikulu la anthu ali ndi mikondo ndi zibonga otumidwa ndi akulu a ansembe ndi akuluakulu.
48 And, he who was delivering him up, gave them a sign, saying—Whomsoever I shall kiss, he, it is, —secure him.
Womuperekayo anawawuziratu chizindikiro anthuwo kuti, “Amene ndidzapsompsona ndi iyeyo; mugwireni.”
49 And, straightway, coming unto Jesus, he said—Joy to thee! Rabbi, and eagerly kissed him.
Pamenepo Yudasi anapita kwa Yesu nati, “Moni, Aphunzitsi!” Ndipo anapsompsona Iye.
50 But, Jesus, said unto him—Friend! wherefore art thou here? Then, coming forward, they thrust their hands upon Jesus, and secured him.
Yesu anayankha kuti, “Bwenzi langa, chita chimene wabwerera.” Pamenepo anthuwo anabwera patsogolo namugwira Yesu ndi kumumanga.
51 And lo! one of those with Jesus, stretching forth his hand, grasped his sword, and smiting the servant of the High-priest, cut off his ear.
Pa chifukwa ichi, mmodzi wa anzake a Yesu anagwira lupanga lake, nalisolola ndi kutema wantchito wa mkulu wa ansembe, nadula khutu lake.
52 Then, Jesus saith unto him—Put back thy sword into its place, for, all they who take a sword, by a sword, shall perish.
Yesu anati kwa iye, “Bwezera lupanga lako mʼchimake, chifukwa onse amene amapha ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
53 Or thinkest thou that I cannot call upon my Father, and he will set near me, even now, more than twelve legions of messengers?
Kodi mukuganiza kuti sindingathe kupempha Atate anga ndipo nthawi yomweyo nʼkundipatsa magulu a angelo oposa khumi ndi awiri?
54 How then should the Scriptures be fulfilled, that, thus, it must needs come to pass?
Koma nanga malemba akwaniritsidwa bwanji amene akuti ziyenera kuchitika motere?”
55 In that hour, said Jesus unto the multitudes: As against a robber, came ye forth, with swords and clubs, to arrest me? Daily in the temple, used I to sit teaching, and ye secured me not;
Pa nthawi yomweyo Yesu anati kwa gululo, “Kodi ndine mtsogoleri wa anthu owukira kuti mwabwera ndi malupanga ndi zibonga kudzandigwira? Tsiku ndi tsiku ndimakhala mʼNyumba ya Mulungu kuphunzitsa, koma simunandigwire.
56 But, this, hath, wholly, come to pass, that, the Scriptures of the prophets, may be fulfilled. Then, the disciples, all forsaking him, fled.
Koma zonsezi zachitika kuti zolembedwa ndi aneneri zikwaniritsidwe.” Pamenepo ophunzira anamusiya nathawa.
57 And, they who secured Jesus, led him away unto Caiaphas the High-priest, where the Scribes and the Elders gathered themselves together.
Iwo amene anamugwira Yesu anamutengera kwa Kayafa, mkulu wa ansembe, kumene aphunzitsi amalamulo ndi akuluakulu anasonkhana.
58 Now, Peter, was following him afar off, unto the court of the High-priest, —and, entering within, was sitting with the attendants, to see the end.
Koma Petro anamutsatira Iye patali, mpaka ku bwalo la mkulu wa ansembe. Analowa nakhala pansi pamodzi ndi alonda kuti aone zotsatira.
59 Now, the High-priests and all the High-council, were seeking false-witness against Jesus, that they might, put him to death;
Akulu a ansembe ndi akulu olamulira Ayuda amafunafuna umboni wonama wofuna kuphera Yesu.
60 and found not any, though many came forward as false-witnesses. At length, however, there came forward, two,
Koma sanathe kupeza uliwonse, angakhale kuti mboni zambiri zabodza zinapezeka. Pomalizira mboni ziwiri zinabwera patsogolo.
61 and said: This, man said—I am able to pull down the shrine of God, and, in three days, to, build, it.
Ndipo zinati, “Munthu uyu anati, ‘Ndikhoza kupasula Nyumba ya Mulungu ndi kuyimanganso mʼmasiku atatu.’”
62 And the High-priest, arising, said unto him—Nothing, answerest thou? What are these, against thee bearing witness?
Pamenepo mkulu wa ansembe anayimirira nati kwa Yesu, “Kodi suyankha? Kodi umboni umenewu ndi otani umene anthu awa akupereka kukutsutsa Iwe?”
63 But, Jesus, was silent. And, the High-priest, said unto him: I put thee on oath, by the Living God, that, to us, thou say—Whether, thou, art the Christ, the Son of God.
Koma Yesu anakhalabe chete. Mkulu wa ansembe anati kwa Iye, “Ndikulamulira Iwe ndi lumbiro pamaso pa Mulungu wa Moyo: utiwuze ife ngati ndiwe Khristu Mwana wa Mulungu.”
64 Jesus saith unto him: Thou, hast said; Moreover, I say unto you—Hereafter, ye will see the Son of Man, sitting on the right hand of power, and coming upon the clouds of heaven.
Yesu anayankha nati, “Mwanena ndinu. Koma ndikunena kwa inu nonse: mʼtsogolomo mudzaona Mwana wa Munthu atakhala kudzanja lamanja la Wamphamvuzonse ndipo akubwera ndi mitambo ya kumwamba.”
65 Then, the High-priest rent asunder his garments, saying—He hath spoken profanely! What further need have we, of witnesses? Lo! now, ye have heard the profanity!
Pamenepo mkulu wa ansembe anangʼamba zovala zake nati, “Wanyoza Mulungu! Tifuniranji mboni zina? Taonani, tsopano mwamva mwano wake.
66 How, to you, doth it seem? And, they, answering, said: Guilty of death, he is.
Mukuganiza bwanji?” Iwo anayankha kuti, “Ayenera kuphedwa!”
67 Then, spat they into his face, and buffeted him; and, others, struck him smartly,
Kenaka anamulavulira kumaso namumenya ndi zibakera. Ena anamumenya makofi.
68 saying—Prophesy unto us, O Christ! Who is he that struck thee?
Ndipo anati, “Tanenera kwa ife, Khristu. Wakumenya ndani?”
69 Now, Peter, was sitting without, in the court; and there came unto him a certain female servant, saying—Thou also, wast with Jesus, the Galilaean.
Tsopano Petro anakhala ku bwalo la nyumbayo, ndipo mtsikana wantchito anabwera kwa iye nati, “Iwenso unali ndi Yesu wa ku Galileya.”
70 But, he, denied before all, saying—I know not what thou sayest.
Koma iye anakana pamaso pawo nati, “Sindikudziwa chimene ukunena.”
71 And, when he went out into the porch, another female saw him, and said unto them who were there—This, one was with Jesus the Nazarene.
Kenaka anachoka kupita ku khomo la mpanda, kumene mtsikana wina anamuonanso nawuza anthu nati, “Munthu uyu anali ndi Yesu wa ku Nazareti.”
72 And, again, he denied, with an oath—I know not the man.
Iye anakananso molumbira kuti, “Sindimudziwa munthuyu!”
73 And, after a little, the by-standers, coming forward, said unto Peter: Truly, thou also, art, from among them, for, thy very speech, maketh thee, manifest.
Patapita kanthawi pangʼono, amene anayimirira pamenepo anapita kwa Petro nati, “Zoonadi, ndiwe mmodzi wa iwo, popeza mayankhulidwe ako akukuwulula.”
74 Then, began he to be cursing and swearing—I know not the man! And, straightway, a cock crowed.
Pamenepo anayamba kudzitemberera ndipo analumbira kwa iwo nati, “Sindimudziwa munthu ameneyo!” Nthawi yomweyo tambala analira.
75 And Peter was put in mind of the declaration of Jesus, of his having said—Before a cock crow, thrice, wilt thou utterly deny me; and, going forth outside, he wept bitterly.
Ndipo Petro anakumbukira mawu amene Yesu anayankhula kuti, “Tambala asanalire, udzandikana Ine katatu.” Ndipo anatuluka panja nakalira kwambiri.

< Matthew 26 >