< Mark 6 >

1 And he went forth from thence, and cometh into his own city, —and his disciples follow him.
Yesu anachoka kumeneko napita ku mudzi kwawo, pamodzi ndi ophunzira ake.
2 And, when it was Sabbath, he began to be teaching in the synagogue, and, the greater part, as they heard, were being struck with astonishment, saying—Whence hath this man these things?—and—What the wisdom which hath been given to this man?—and—Such mighty works as these, through his hands, are coming to pass!
Tsiku la Sabata litafika, anayamba kuphunzitsa mʼsunagoge, ndipo ambiri amene anamumva anadabwa. Iwo anafunsa kuti, “Kodi munthu uyu anazitenga kuti zimenezi? Kodi ndi nzeru yotani imene munthu ameneyu wapatsidwa, kuti Iye akuchitanso zodabwitsa!
3 Is not, this, the carpenter? the son of Mary, the brother of James and Joses and Judas and Simon? And are not his sisters here with us?—and they were finding cause of stumbling in him.
Kodi uyu si mpalamatabwa uja? Kodi uyu si mwana wa Mariya ndi mʼbale wa Yakobo, Yose, Yudasi ndi Simoni? Kodi alongo ake si ali ndi ife?” Ndipo anakhumudwa naye.
4 And Jesus was saying unto them—A prophet is not without honour, save in his own city and among his kinsfolk, and in his house;
Yesu anawawuza kuti, “Mneneri amalemekezedwa kulikonse kupatula kwawo, ndi pakati pa abale ake ndi a mʼbanja mwake.”
5 and he could not, there, do so much as a single mighty work, —save, on a few sick, he laid his hands and cured them.
Sanachite zodabwitsa kumeneko, koma anangosanjika manja pa odwala ochepa ndi kuwachiritsa.
6 And he marvelled because of their unbelief. And he was going round the villages in a circuit, teaching.
Ndipo Iye anadabwa chifukwa chakusowa chikhulupiriro kwawo. Pamenepo Yesu anayenda mudzi ndi mudzi kuphunzitsa.
7 And he calleth near the twelve, and began to be sending them forth two and two, —and was giving them authority over the impure spirits:
Atayitana khumi ndi awiriwo, Iye anawatuma awiriawiri ndipo anawapatsa ulamuliro pa mizimu yoyipa.
8 and charged them that they should take, nothing, for a journey, save a staff only, —no bread, no satchel, no copper, for the belt;
Zomwe anawalangiza ndi izi: “Musatenge kanthu ka paulendo koma ndodo yokha; osatenga buledi, thumba, kapena ndalama.
9 but having bound on light sandals, and not to put on, two tunics;
Muvale nsapato koma osatenga malaya apadera.
10 and he was saying unto them—Wheresoever ye shall enter into a house, there, abide, until ye go forth from thence;
Pamene mulowa mʼnyumba mukakhale momwemo kufikira mutachoka mʼmudzimo.
11 And, whatsoever place shall not welcome you nor hearken unto you, when ye are going forth from thence, shake off the dust that is under you feet, for a witness against them.
Ndipo ngati pa malo ena sakakulandirani kapena kukumverani, sasani fumbi la kumapazi anu pamene mukuchoka, kuti ukhale umboni wowatsutsa.”
12 And they went forth and made proclamation, in order that men should repent;
Anatuluka kupita kukalalikira kuti anthu atembenuke mtima.
13 and, many demons, were they casting out, —and were anointing with oil, many sick, and were curing them.
Anatulutsa ziwanda zambiri ndi kudzoza mafuta odwala ambiri ndi kuwachiritsa.
14 And King Herod heard, —for, famous, had become his name; and he was saying—John the Immerser hath arisen from among the dead, and, for this cause, are the powers working mightily in him;
Mfumu Herode anamva zimenezi, pakuti dzina la Yesu linali litadziwika kwambiri. Ena amati, “Yohane Mʼbatizi waukitsidwa kwa akufa, ndipo nʼchifukwa chake mphamvu zochita zodabwitsa zinkagwira ntchito mwa Iye.”
15 But, others, were saying—It is Elijah, and, others were saying—A prophet, like one of the prophets!
Ena anati, “Iye ndi Eliya.” Enanso anati, “Ndi mneneri, ofanana ndi mmodzi wa aneneri akale.”
16 But, when Herod heard, he was saying—He whom I beheaded—John, the same, hath been raised.
Koma Herode atamva zimenezi anati, “Yohane, munthu amene ndinamudula mutu, waukitsidwa kuchokera kwa akufa.”
17 For, Herod himself, had sent and secured John and bound him in prison, for the sake of Herodias the wife of Philip his brother, —for, her, had he married,
Pakuti Herode iye mwini analamula kuti amumange Yohane ndi kumuyika mʼndende. Anachita izi chifukwa cha Herodia, mkazi wa mʼbale wake Filipo, amene iye anamukwatira.
18 For John had been saying to Herod—It is not allowed thee, to have, the wife of thy brother.
Pakuti Yohane ankanena kwa Herode kuti, “Sikololedwa kwa inu kuti mukwatire mkazi wa mʼbale wanu.”
19 And, Herodias, was cherishing [a grudge] against him, and wishing, to slay him, —and could not;
Ndipo Herodia anamusungira Yohane chidani ndipo anafuna kumupha, koma sanathe kutero,
20 for, Herod, stood in fear of John, knowing him to be a man righteous and holy, —and was keeping him safe; and, when he heard him, he paid earnest heed, and, with pleasure, used to listen to him.
chifukwa Herode anaopa Yohane ndipo anamuteteza, podziwa kuti iye anali munthu wolungama ndi woyera mtima. Herode akamamva Yohane, ankathedwa nzeru; komabe amakonda kumumvetsera.
21 And, an opportune day arriving, when Herod on his birthday made a feast for his nobles, and for the rulers of thousands and for the first men of Galilee,
Pomaliza mpata unapezeka. Pa tsiku lokumbukira kubadwa kwake, Herode anakonzera phwando akuluakulu ake, akulu a ankhondo ndi anthu odziwika a mu Galileya.
22 when the daughter of this very Herodias came in and danced, she pleased Herod and those reclining together, and, the king, said unto the damsel—Ask me what thou wilt, and I will give it thee;
Mwana wamkazi wa Herodia atabwera ndi kudzavina, anakondweretsa Herode ndi alendo ake a pa mphwandopo. Mfumu inati kwa mtsikanayo, “Undipemphe chilichonse chimene ukuchifuna, ndipo ndidzakupatsa.”
23 and he took an oath to her—Whatsoever thou shalt ask me, I will give thee, unto half my kingdom.
Ndipo analonjeza ndi lumbiriro kuti, “Chilichonse chimene upempha ndidzakupatsa, ngakhale theka la ufumu wanga.”
24 And, going out, she said unto her mother—What shall I ask? and she said—The head of John the Immerser;
Iye anatuluka nati kwa amayi ake, “Kodi ndikapemphe chiyani?” Iye anamuyankha kuti, “Mutu wa Yohane Mʼbatizi.”
25 And, coming in straightway, with hast, unto the king, she asked, saying—I desire, that, forthwith, thou give me, upon a charger, the head of John the Immerser.
Nthawi yomweyo mtsikana uja anafulumira kupita komwe kunali mfumu ndi pempho lake: “Ndikufuna kuti mundipatse pomwe pano mutu wa Yohane Mʼbatizi mʼmbale.”
26 And, though the king was, very grieved, yet, by reason of the oaths, and of them who were reclining, he would not refuse her.
Mfumu inamva chisoni chachikulu, koma chifukwa cha lumbiro lake ndi alendo ake a pa mphwandolo, sanafune kumukaniza.
27 And the king, straightway, sending off a guard, gave orders to bring his head.
Nthawi yomweyo iye anatumiza yemwe anali ndi ulamuliro wonyonga anthu kuti abweretse mutu wa Yohane. Munthuyo anapita, nakadula mutu wa Yohane mʼndende,
28 And, departing, he beheaded him in the prison, and brought his head upon a charger, and gave it unto the damsel—and, the damsel, gave it unto her mother.
nabweretsa mutuwo mʼmbale. Anawupereka kwa mtsikanayo, ndipo iye anakapereka kwa amayi ake.
29 And, hearing of it, his disciples went and took away his corpse, and laid it in a tomb.
Atamva izi, ophunzira a Yohane anabwera nadzatenga mtembo ndi kukawuyika mʼmanda.
30 And the apostles gather themselves together unto Jesus, and reported unto him all things, as many as they had done, and as many as they had taught.
Atumwi anasonkhana mozungulira Yesu namufotokozera zonse zomwe anachita ndi kuphunzitsa.
31 And he saith unto them—Come, ye yourselves, apart, into a desert place, and rest yourselves a little. For they who were coming and they who were going were many, and, not even to eat, were they finding fitting opportunity.
Popeza kuti panali anthu ambiri amene amabwera ndi kumapita, analibe mpata wakuti adye, ndipo Iye anawawuza kuti, “Tiyeni kuno kumalo achete kuti tikapume.”
32 And they departed, in the boat, into a desert place, apart.
Ndipo anachoka okha pa bwato napita kumalo a okhaokha.
33 And many saw them going away, and took note of it, and, afoot, from all the cities, ran they together thither, —and outwent them.
Koma ambiri amene anawaona akuchoka anawazindikira ndipo anathamanga wapansi kuchokera mʼmidzi yonse nakayambirira kufika.
34 And, coming forth, he saw, a great multitude, and was moved with compassion towards them, because they were like sheep having no shepherd, and he began to be teaching them many things.
Yesu atafika ku mtunda ndi kuona gulu lalikulu la anthu, anamva nawo chisoni chifukwa anali ngati nkhosa zopanda mʼbusa. Ndipo anayamba kuwaphunzitsa zinthu zambiri.
35 And, already, a late hour, having arrived, his disciples came unto him and were saying, A desert, is the place, and it is, already, a late hour:
Pa nthawi iyi nʼkuti dzuwa litapendeka, ndipo ophunzira ake anabwera kwa Iye nati, “Kuno ndi kuthengo, ndipo ano ndi madzulo.
36 dismiss them, that, departing into the surrounding hamlets and villages, they may buy themselves something to eat.
Awuzeni anthuwa azipita ku midzi ndi madera ozungulira, kuti akadzigulire kanthu kakuti adye.”
37 But, he, answering said to them—Ye, give them, to eat. And they say unto him—Shall we depart and buy two hundred denaries’ worth of loaves, and give them to eat?
Koma Iye anayankha kuti, “Apatseni kanthu koti adye.” Iwo anati kwa Iye, “Apa pafunika ndalama za miyezi isanu ndi itatu zomwe munthu amalandira! Kodi tipite kukagwiritsa ntchito ndalama zotere kugulira buledi kuti tiwapatse adye?”
38 And, he, saith unto them—How many loaves, have ye? Go, see! And, getting to know, they say—Five, and, two fishes.
Iye anawafunsa kuti, “Muli ndi malofu a buledi angati? Pitani mukaone.” Ataona anati kwa Iye, “Asanu ndi nsomba ziwiri.”
39 And he gave them orders, that all should be made recline, in parties, upon, the green grass.
Pamenepo Yesu anawalamulira kuti awakhazike anthu pansi mʼmagulu pa msipu obiriwira.
40 And they fell back, in companies, by hundreds and by fifties.
Ndipo anakhala pansi mʼmagulu a anthu 100 ndi gulu la anthu makumi asanu.
41 And, taking the five loaves, and the two fishes, looking up into heaven, he blessed, and brake up the loaves, and began giving unto the disciples, that they might set before them, and, the two fishes, divided he, unto all.
Atatenga malofu a buledi asanu ndi nsomba ziwiri, nayangʼana kumwamba, Iye anayamika nagawa malofu a bulediwo. Kenaka anawapatsa ophunzira ake kuti awapatse anthu. Ndipo anagawanso nsomba ziwirizo kwa onse.
42 And they did all eat, and were filled.
Onse anadya ndipo anakhuta,
43 And they took up broken pieces, twelve baskets, full measure, and from the fishes.
ndipo ophunzira ake anatola buledi ndi nsomba zotsalira zokwanira madengu khumi ndi awiri.
44 And they who did eat the loaves were, five thousand men.
Chiwerengero cha amuna amene anadya chinali 5,000.
45 And, straightway, constrained he his disciples to enter into the boat, and be going forward to the other side, unto Bethsaida, —while, he, was dismissing the multitude.
Nthawi yomweyo Yesu anawuza ophunzira ake kuti alowe mʼbwato ndi kuti atsogole kupita ku Betisaida, pamene Iye ankawuza anthu kuti azipita.
46 And, bidding them farewell, he departed into the mountain to pray.
Atawasiya, Iye anakwera ku phiri kukapemphera.
47 And, when, evening, came, the boat was in the midst of the sea, and, he alone, on the land.
Pofika madzulo, bwato linali pakati pa nyanja, ndipo Iye anali yekha pa mtunda.
48 And, seeing them distressed in the rowing, for the wind was against them, about the fourth watch of the night, he cometh unto them, walking upon the sea, —and was wishing to pass by them.
Iye anaona ophunzira ake akuvutika popalasa bwato, chifukwa mphepo imawomba mokumana nawo. Pa nthawi ya mʼbandakucha Iye anafika kwa iwo akuyenda pa nyanja. Anali pafupi kuwapitirira,
49 But, they, seeing him, upon the sea, walking, supposed that it was an apparition, and cried out aloud;
koma atamuona Iye akuyenda pa nyanja, anaganiza kuti anali mzukwa. Iwo anafuwula,
50 for, all, saw him, and were troubled. But, he, straightway, talked with them, and saith unto them—Take courage! it is, I—be not afraid!
pakuti onse anamuona ndipo anachita mantha. Nthawi yomweyo Iye anawayankhula nati, “Limbani mtima! Ndine. Musachite mantha.”
51 And he went up unto them, into the boat, —and the wind lulled. And, exceedingly, within themselves, were they astonished;
Ndipo Iye anakwera mʼbwato pamodzi nawo, ndipo mphepo inaleka. Iwo anadabwa kwambiri,
52 for they understood not by the loaves, —but their, heart, had been, hardened.
popeza sanazindikire zimene zinachitika pa malofu a buledi; pakuti mitima yawo inali yowuma.
53 And crossing over unto the land, they came unto Gennesaret, and cast anchor near.
Atawoloka, anafika ku Genesareti nayima pa dooko.
54 And, when they had, come forth, out of the boat, straightway, recognizing him,
Atangotuluka mʼbwato, anthu anamuzindikira Yesu.
55 the people ran round the whole of that country, and began to be carrying round, upon couches, them who were sick, wherever they heard that he was.
Anathamanga uku ndi uko mʼdera lonse nakanyamula odwala pa machira kupita nawo kulikonse kumene anamva kuti kuli Iye.
56 And, wheresoever he was entering into villages, or into cities, or into hamlets, in the marketplaces, laid they the sick, and were beseeching him, that, only the fringe of his mantle, they might touch, and, as many soever as touched it, were being made well.
Ndipo kulikonse kumene anapita, ku midzi, mʼmizinda ndi madera a ku midzi, iwo anayika odwala mʼmalo a mʼmisika. Iwo anamupempha kuti awalole kuti akhudze ngakhale mphonje za mkanjo wake, ndipo onse amene anamukhudza anachira.

< Mark 6 >