< Leviticus 6 >

1 And Yahweh spake unto Moses, saying—
Yehova anawuza Mose kuti,
2 When any person, shall sin, and shall commit a trespass against Yahweh, —and shall withhold something of the truth from his neighbour in respect of a deposit, or a pledge or anything plundered, or shall use extortion with his neighbour;
“Ngati munthu wina aliyense achimwa, nachita zinthu mosakhulupirika kwa Yehova chifukwa cha kunyenga mnzake pokana kumubwezera zimene anamusungitsa, kapena kumubera kapenanso kumulanda,
3 or shall find something lost and shall withhold something of the truth therein, and shall swear to a falsehood, —as regardeth a single thing of all that a son of earth may do, to commit sin thereby;
kapena ndi kunama kuti sanatole chinthu chimene chinatayika, kapena kulumbira mwachinyengo pa chinthu chilichonse chimene munthu akachita amachimwa nacho,
4 and so it shall come about that he shall commit sin and then become aware of his guilt, then shall he return the plunder which he had plundered, or the extortion which he had extorted, or the deposit that was deposited with him, —or the lost thing which he hath found:
ndi wopalamula ndithu, ndipo ayenera kubweza zimene anabazo, zimene analanda mwachinyengozo, zimene anamusungitsazo, zimene anatolazo
5 or in anything as to which he hath been swearing to a falsehood, then shall he make it good in the principal thereof, and the fifth part thereof, shall he add thereunto, —to whomsoever it belongeth, to him, shall he give it in the day he becometh aware of his guilt;
kapena zimene analumbira monyengazo. Pa tsiku limene apezeke kuti wapalamuladi, iye ayenera kumubwezera mwini wake zinthu zonsezi ndi kuwonjezerapo chimodzi mwa zigawo zisanu zilizonse.
6 but, his guilt-bearer, itself, shall he bring in unto Yahweh, —a ram without defect out of the flock by thine estimate as a guilt-bearer, unto the priest.
Pambuyo pake apereke kwa Yehova nsembe yopalamula. Nsembe yake ikhale nkhosa yayimuna yopanda chilema ndipo mtengo wake wogwirizana ndi nsembe yopepesera machimo.
7 So shall the priest put a propitiatory-covering over him before Yahweh, and it shall be forgiven him, —on account of any one thing, of all which one might do, so as to become guilty therein.
Kenaka wansembe achite mwambo wopepesera tchimo la munthuyo pamaso pa Yehova, ndipo adzakhululukidwa chilichonse chomwe anachita kuti akhale wopalamula.”
8 And Yahweh spake unto Moses saying:
Yehova anawuza Mose kuti,
9 Command Aaron and his sons, saying, This is the law of the ascending-sacrifice, —the same, is the ascending-sacrifice, which is upon the hearth, upon the altar, all the night until the morning, —and the fire of the altar, shall be kept burning therein.
“Lamula Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Lamulo la nsembe yopsereza ndi ili: Nsembe yopserezayo izikhala pa moto pa guwa usiku wonse mpaka mmawa, ndipo moto wa paguwapo uzikhala ukuyaka nthawi zonse.
10 So then the priest shall put on his upper garment of linen, and, breeches of linen, shall he put on over his flesh, then shall he take up the fat-ashes, whereto the fire consumeth the ascending-sacrifice on the altar, —and shall put them beside the altar.
Tsono wansembe avale mkanjo wake wa nsalu yofewa ndi yosalala. Mʼkati avalenso kabudula wofewa, wosalala. Pambuyo pake atenge phulusa la nyama imene yatenthedwa pa guwa lansembe paja ndi kulithira pambali pa guwa lomwelo.
11 Then shall he put off his garments, and put on other garments, —and shall carry forth the fat-ashes unto the outside of the camp, unto a clean place,
Akatero avule zovala zakezo ndi kuvala zovala zina. Kenaka atulutse phulusalo ndi kukaliyika pa malo woyeretsedwa kunja kwa chithando.
12 And, the fire on the altar, shall be kept burning therein, it shall not be suffered to go out, but the priest shall kindle up thereon pieces of wood, morning by morning, —and shall set in order thereupon the ascending-sacrifice, and shall make a perfume thereon with the fat-pieces of the peace-offerings:
Moto wa pa guwa uzikhala ukuyaka nthawi zonse, usamazime. Mmawa uliwonse wansembe aziwonjezerapo nkhuni pa motopo ndi kukonza nsembe yopsereza, ndi kutentha mafuta a nsembe yachiyanjano pamenepo.
13 fire, shall continually be kept burning on the altar, it shall not be suffered to go out.
Moto uzikhala ukuyaka pa guwa nthawi zonse ndipo usazimepo.
14 And, this, is the law of the meal-offering, —the sons of Aaron shall bring it near before Yahweh, unto the front of the altar.
“‘Lamulo la nsembe yachakudya ndi ili: ana a Aaroni azibwera nayo nsembeyo pamaso pa Yehova, patsogolo pa guwa.
15 Then shall one lift up therefrom a handful of the fine meal of the meal-offering, and of the oil thereof, and all the frankincense which is upon the meal-offering, —and shall make a perfume at the altar, an altar-flame of a satisfying odour, shall the memorial thereof be, unto Yahweh.
Wansembe mmodzi atapeko dzanja limodzi la ufa wosalala wa nsembe yachakudya ija kuti ukhala ufa wachikumbutso ndi mafuta pamodzi ndi lubani yense amene ali pa nsembe ya chakudyacho, ndipo azitenthe pa guwa kuti zilandiridwe ndi Yehova mʼmalo mwa nsembe yonse kuti zikhale nsembe ya fungo lokomera Yehova.
16 And the remainder thereof, shall Aaron and his sons eat, —as unleavened cakes, shall it be eaten, in a holy place, within the court of the tent of meeting, shall they eat it.
Aaroni ndi ana ake azidya zimene zatsala koma azidya zopanda yisiti ku malo wopatulika, ku bwalo la tenti ya msonkhano.
17 It shall not be baked into anything leavened, as their portion, have I given it, from among the altar-flames of Yahweh, —most holy, it is, like the sin-bearer, and like the guilt-bearer,
Poziphika asathire yisiti. Ndawapatsa zotsalazo kuti zikhale gawo lawo la nsembe zanga zopsereza. Zonsezi ndi zopatulika kwambiri monga nsembe yopepesera tchimo ndiponso nsembe yopepesera machimo.
18 Any male among the sons of Aaron may eat it, an age-abiding statute to your generations from among the altar-flames of Yahweh, —every one that toucheth them shall be hallowed.
Mwana aliyense wamwamuna wa Aaroni azidyako za nsembe zopsereza zopereka kwa Yehova. Ndi gawo lake lokhazikika la chopereka chopsereza kwa Yehova pa mibado yanu yonse. Chilichonse chimene chidzakhudza nsembezo chidzakhala chopatulika.’”
19 And Yahweh spake unto Moses, saying—
Yehova anawuzanso Mose kuti,
20 This, is the oblation of Aaron and his sons, which they shall bring near unto Yahweh in the day when he is anointed, The tenth of an ephah of fine meal, as a continual meal-offering, —half thereof in the morning, and half thereof in the evening;
“Nsembe imene Aaroni ndi ana ake ayenera kupereka kwa Yehova pa tsiku limene wansembe akudzozedwa ndi iyi: ufa wosalala kilogalamu imodzi ngati chopereka chachakudya cha nthawi zonse. Azipereka theka limodzi mmawa ndipo theka linalo madzulo.
21 on a pan, with oil, shall it be made when well mingled, shalt thou bring it in, —in baked portions, as a meal-offering in pieces, shalt thou bring it near as a satisfying odour unto Yahweh.
Ipangidwe ndi mafuta pa chiwaya ndipo ubwere nayo ili yosakaniza bwino, yophikidwa mitandamitanda monga amachitira ndi nsembe yachakudya. Iphikidwe moti itulutse fungo lokomera Yehova.
22 And the priest that is anointed in his stead from among his sons, shall prepare it, —[it is] an age-abiding statute, that unto Yahweh, shall a perfume, of the entire gift, be made:
Mwana wa fuko la Aaroni amene adzadzozedwe kukhala wansembe kulowa mʼmalo mwa Aaroni ndiye amene azidzakonza ndi kupereka nsembeyi kwa Yehova nthawi zonse monga kunalembedwera.
23 yea, every meal-offering of a priest, shall be, entire—it shall not be eaten.
Nsembe iliyonse yachakudya ya wansembe izitenthedwa kwathunthu, isamadyedwe.”
24 And Yahweh spake unto Moses, saying—
Yehova anawuza Mose kuti
25 Speak unto Aaron and unto his sons, saying, This, is the law of the sin-bearer. In the place where the ascending-sacrifice is slain, shall the sin-bearer be slain, before Yahweh, most holy, it is.
“Uza Aaroni ndi ana ake kuti, ‘Malamulo a nsembe ya tchimo ndi awa: Nsembeyi iziphedwa pamaso pa Yehova pa malo pamene mumaphera nsembe yopsereza popeza ndi nsembe yopatulika.
26 The priest who maketh it a sin-bearer, shall eat it, —in a holy place, shall it be eaten, in the court of the tent of meeting.
Wansembe amene apereke nsembeyi adyere ku malo wopatulika ndiye kuti mʼbwalo la tenti ya msonkhano.
27 Every one who toucheth the flesh thereof, shall be hallowed; and when one sprinkleth some of the blood thereof upon a garment, that whereon it was sprinkled, shalt thou wash in a holy place.
Chilichonse chimene chidzakhudza nsembeyo chidzakhala chopatulika, ndipo ngati magazi ake agwera pa chovala, muchape chovalacho pa malo opatulika.
28 But, the earthen vessel wherein it is boiled, shall be broken, —or, if, in a vessel of bronze, it hath been boiled, then shall the vessel be scoured and rinsed in water.
Mʼphika wadothi umene aphikira nyamayo auphwanye. Koma ngati yaphikidwa mu mʼphika wa mkuwa, awukweche ndi kuwutsukuluza ndi madzi.
29 Any male among the priests may eat thereof, —most holy, it is.
Munthu wamwamuna aliyense wa mʼbanja la wansembe angathe kuyidya popeza nsembeyi ndi yopatulika kwambiri.
30 But, no sin-bearer whereof any of the blood is taken into the tent of meeting to make a propitiatory-covering in the sanctuary, shall be eaten, —with fire, shall it be consumed.
Koma nsembe yopepesera tchimo imene magazi ake amabwera nawo mu tenti ya msonkhano kudzachita mwambo wopepesera tchimo ku malo opatulika isadyedwe, mʼmalo mwake itenthedwe.’”

< Leviticus 6 >