< Joshua 4 >

1 And it came to pass, when all the nation had made an end of passing over the Jordan, that Yahweh slake unto Joshua, saying:
Anthu onse atatha kuwoloka Yorodani, Yehova anati kwa Yoswa,
2 Take unto you, from among the people, twelve men, one man severally from each tribe;
“Sankha amuna khumi ndi awiri, mmodzi pa fuko lililonse.
3 and command ye them, saying, Take you up from hence, out of the midst of the Jordan, from the place where stood the feet of the priests with firm footing, twelve stones; —and carry them over with you, and lay them down in the lodging-place where ye shall lodge, tonight.
Tsono uwalamule kuti, ‘Tengani miyala khumi ndi iwiri pakati penipeni pa mtsinje wa Yorodani, pamalo pamene ansembe anayimirirapo. Miyalayo muwoloke nayo ndi kudzayitula pamalo pamene mukagone usiku uno.’”
4 So Joshua called unto the twelve men whom he had made ready, from among the sons of Israel, —one man severally out of each tribe;
Choncho Yoswa anayitana amuna khumi ndi awiri amene anawasankha aja kuchokera pakati pa Aisraeli, mmodzi pa fuko lililonse,
5 and Joshua said unto them: Pass ye over, before the ark of Yahweh your God, into the midst of the Jordan, —and lift ye up, each man one stone upon his shoulder, according to the number of the tribes of the sons of Israel:
ndipo anawawuza kuti, “Lowani pakati pa mtsinje wa Yorodani, patsogolo pa Bokosi la Yehova Mulungu wanu. Ndipo aliyense wa inu atenge mwala pa phewa lake, monga mwa chiwerengero cha mafuko a Aisraeli,
6 that this may be a sign in your midst, —for your sons will ask in time to come, saying, What mean these stones to you?
kuti ikhale chizindikiro kwa inu. Mʼtsogolo muno ana anu akamadzakufunsani kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
7 Then shall ye say unto them—That the waters of the Jordan, were cut off, from before the ark of the covenant of Yahweh, when it passed into the Jordan, the waters of the Jordan, were cut off. So shall these stones become a memorial unto the sons of Israel, unto times age-abiding.
Muzidzawawuza kuti, ‘Madzi a Yorodani analeka kuyenda pamene Bokosi la Chipangano la Yehova linkawoloka mtsinjewo. Miyala iyi idzakhala chikumbutso kwa anthu a Israeli kwa muyaya.’”
8 And the sons of Israel did so, as Joshua commanded, and took up twelve stones out of the midst of the Jordan, as spake Yahweh unto Joshua, according to the number of the tribes of the sons of Israel, —and carried them with them unto the place where they lodged, and laid them down there.
Aisraeli anachitadi monga Yoswa anawalamulira. Iwo ananyamula miyala khumi ndi iwiri kuchokera pakati pa Yorodani, fuko lililonse la Israeli mwala wake, monga Yehova analamulira Yoswa. Miyalayo anapita nayo ku misasa yawo nakayikhazika kumeneko.
9 Twelve stones also, did Joshua set up in the midst of the Jordan, in the place where stood the feet of the priests who were bearing the ark of the covenant, —and they have remained there until this day.
Yoswa anayimika miyala khumi ndi iwiri imene inali pakati pa Yorodani pamalo pamene ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anayimapo. Ndipo miyalayo ili pamalo pomwepo mpaka lero lino.
10 Now, the priests who were bearing the ark, continued standing in the midst of the Jordan, until everything was finished which Yahweh commanded Joshua, to speak unto the people, according to all that Moses commanded Joshua, —the people therefore hasted, and passed over.
Ansembe onyamula Bokosi lija anayimirirabe pakati pa Yorodani mpaka zonse zimene Yehova analamulira Yoswa kuti awuze anthu zinatha. Zimenezi zinali monga momwe Mose anamufotokozera Yoswa. Tsono anthu anawoloka mtsinjewo mofulumira.
11 And so it was, as soon as all the people had made an end of passing over, —then passed over the ark of Yahweh, and the priests, in presence of the people.
Anthu atatha kuwoloka, ansembe anatsogolera anthuwo atanyamula Bokosi la Yehova.
12 Also the sons of Reuben and the sons of Gad and the half tribe of Manasseh, passed over, armed, before the sons of Israel, —as Moses had spoken unto them:
Anthu a fuko la Rubeni, Gadi ndi theka la fuko la Manase anawoloka patsogolo pa Aisraeli ali ndi zida, monga momwe Mose anawalamulira.
13 about forty thousand, equipped for the war, passed over before Yahweh, to battle, into the waste plains of Jericho.
Asilikali pafupifupi 40,000 anawoloka napita kukayima mʼchigwa cha Yeriko kukonzekera nkhondo.
14 On that day, did Yahweh magnify Joshua in the eyes of all Israel, —and they revered him, as they revered Moses, all the days of his life.
Zimene Yehova anachita tsiku limeneli zinapatsa anthu mtima wolemekeza Yoswa. Ndipo anamulemekeza masiku onse a moyo wake, monga momwe analemekezera Mose.
15 Then spake Yahweh unto Joshua, saying:
Kenaka Yehova anati kwa Yoswa,
16 Command the priests who are bearing the ark of testimony, —that they come up out of the Jordan.
“Lamula ansembe onyamula Bokosi la Chipanganowo kuti atuluke mu Yorodani.”
17 So Joshua commanded the priests, saying, —Come ye up out of the Jordan.
Choncho Yoswa anawalamuladi ansembe aja kuti atuluke mu Yorodani muja.
18 And it came to pass, when the priests who were bearing the ark of the covenant of Yahweh came up out of the midst of the Jordan, and the soles of the feet of the priests were withdrawn unto the dry ground, then returned the waters of the Jordan unto their place, and went, as before, over all his banks.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova aja atangotuluka mu mtsinje muja nʼkuponda powuma, madzi a mu Yorodani anayambanso kuyenda ngati poyamba mpaka kumasefukira.
19 So, the people, came up out of the Jordan, on the tenth of the first month, —and encamped in Gilgal, at the eastern end of Jericho.
Aisraeli anawoloka Yorodani tsiku lakhumi la mwezi woyamba ndipo anakamanga misasa yawo ku Giligala mbali ya kummawa kwa Yeriko.
20 And, these twelve stones which they took out of the Jordan, did Joshua set up, in Gilgal.
Ku Giligala, Yoswa anayimikako miyala khumi ndi iwiri imene anayitenga mu Yorodani ija.
21 Then spake he unto the sons of Israel, saying, —When your sons shall ask, in time to come, of their fathers, saying, —What mean these stones?
Ndipo iye anati kwa Aisraeli, “Mʼtsogolo muno pamene adzukulu anu adzafunsa makolo awo kuti, ‘Kodi miyala iyi ikutanthauza chiyani?’
22 then shall ye let your sons know, saying, —On dry ground, came Israel over this Jordan;
Muzidzawawuza kuti, ‘Aisraeli anawoloka Yorodani pansi pali powuma.’
23 in that Yahweh your God dried up the waters of the Jordan, from before you, until ye had passed over, —as Yahweh your God had done unto the Red Sea, which he dried up from before us, until we had passed over:
Pakuti Yehova Mulungu wanu ndiye anawumitsa Yorodani pamaso panu mpaka inu mutawoloka. Yehova Mulungu wanu anaphwetsa madzi a Yorodani monga mmene anachitira ndi Nyanja Yofiira mpaka ife tinawoloka powuma.
24 that all the peoples of the earth might know the hand of Yahweh, that, firm, it is; that they might revere Yahweh your God, all the days.
Iye anachita zimenezi kuti anthu onse pa dziko lapansi adziwe kuti dzanja la Yehova ndi lamphamvu, ndi kuti inu muziopa Yehova Mulungu wanu masiku onse.”

< Joshua 4 >