< Joshua 3 >
1 So then Joshua rose early in the morning, and they brake up from The Acacias and came as far as the Jordan, he and all the sons of Israel, —and they lodged there before they passed over.
Yoswa ndi Aisraeli onse anadzuka mmamawa nanyamuka ku Sitimu kupita ku Yorodani. Iwo anagona kumeneko asanawoloke mtsinje wa Yorodaniwo.
2 And it came to pass, after three days, that the officers went through the midst of the camp,
Patatha masiku atatu, atsogoleri anayendera misasa yonse,
3 and commanded the people saying, When ye see the ark of the covenant of Yahweh your God, and, the priests the Levites, bearing it, ye also, shall break up out of your place, and come after it.
kulangiza anthu kuti, “Mukaona ansembe a Chilevi atanyamula Bokosi la Chipangano la Yehova Mulungu wanu, inu munyamuke pa malo ano ndi kumalitsatira.
4 Yet shall there be, a distance, between you and it, about two thousand cubits by measure, —do not come near unto it that ye may get to know the way by which ye must go, for ye have not passed this way, heretofore.
Potero mudzadziwa njira yoti mudzere, popeza simunayendepo njira ino nʼkale lomwe. Koma musaliyandikire. Pakati pa inu ndi bokosilo pakhale mtunda pafupifupi kilomita imodzi.”
5 Then said Joshua unto the people, Hallow yourselves, —for, to-morrow, will Yahweh do in your midst, wonderful things.
Yoswa anawuza anthu kuti, “Dzipatuleni tsono pakuti mawa Yehova adzachita zodabwitsa pakati panu.”
6 And Joshua spake unto the priests, saying, Take ye up the ark of the covenant, and pass on before the people. So they took up the ark of the covenant, and went on before the people.
Mmawa mwake Yoswa ananena kwa ansembe kuti, “Nyamulani Bokosi la Chipangano muwoloke ndipo mukhale patsogolo pa anthu.” Motero iwo analinyamula ndi kupita patsogolo pawo.
7 Then said Yahweh unto Joshua: This day, will I begin to magnify thee in the eyes of all Israel, —who shall know, that, as I was with Moses, I will be with thee.
Ndipo Yehova anati kwa Yoswa, “Lero Ine ndidzayamba kukukweza pamaso pa Aisraeli onse kuti adziwe kuti ndili nawe monga ndinalili ndi Mose.
8 Thou, therefore, shalt command the priests who am bearing the ark of the covenant, saying, —When ye are come as far as the edge of the waters of the Jordan, in the Jordan, shall ye stand.
Ansembe amene akunyamula Bokosi la Chipangano uwalamule kuti, ‘Mukafika ku mtsinje wa Yorodani mulowe mu mtsinjemo ndi kuyima mʼmphepete.’”
9 Then said Joshua, unto the sons of Israel, —Draw near hither, and hear ye the words of Yahweh your God.
Yoswa anati kwa Aisraeli, “Bwerani pano mudzamve mawu a Yehova Mulungu wanu.
10 And Joshua said, Hereby, shall ye know, that a Living GOD is in your midst, —and that he will, certainly dispossess, from before you, the Canaanite and the Hittite, and the Hivite and the Perizzite, and the Girgashite, and the Amorite, and the Jebusite.
Umu ndi mmene mudzadziwira kuti Mulungu wamoyo ali pakati panu. Inu mukamadzapita patsogolo Iye adzathamangitsa Akanaani, Ahiti, Ahivi, Aperezi, Agirigasi, Aamori ndi Ayebusi.
11 Lo! the ark of the covenant of the Lord of all the earth, is about to pass before you into the Jordan.
Pamenepo, Bokosi la Chipangano la Mbuye wa dziko lonse lapansi lidzawoloka mu Yorodani patsogolo panu.
12 Now, therefore, take you twelve men, out of the tribes of Israel, —one man severally for each tribe;
Musankhe amuna khumi ndi awiri kuchokera ku fuko lililonse la Israeli.
13 and it shall be, when the soles of the feet of the priests who are bearing the ark of Yahweh, Lord of all the earth, do rest, in the waters of the Jordan, the waters of the Jordan, shall be cut off, the waters that are coming down from above, —and shall stand in one mound.
Mapazi a ansembe onyamula Bokosi la Yehova, Mbuye wa dziko lapansi, akadzangoponda mu Yorodani, madzi ake onse ochokera ku mtunda adzaleka kuyenda ndipo adzayima ngati chipupa.”
14 And it came to pass, when the people set out from their tents, to cross the Jordan, —with the priests, bearing the ark of the covenant before the people,
Tsono Aisraeli anachoka ku misasa yawo kukawoloka mtsinje wa Yorodani. Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano ndiwo anatsogolera anthuwo.
15 then, as the bearers of the ark came as far as the Jordan, and, the feet of the priests who were bearing the ark, were dipped in the edge of the waters, —the Jordan being full over all his banks, all the days of harvest,
Nyengo imeneyi inali yokolola ndipo mtsinje wa Yorodani umakhala wodzaza. Komabe, ansembe onyamula Bokosi la Chipangano anafika ku Yorodani, ndipo atangoponda mʼmadzimo,
16 that the waters which were coming down from above, stood—rose up in one mound, a great way off, by the city Adam, which is beside Zarethan, and, they which were going down to the sea of the waste plain, the salt sea, failed—were cut off, —and, the people, passed over, right against Jericho.
madzi ochokera ku mtunda anasiya kuyenda. Madzi a Yorodani ochokera ku mtunda anawunjikana pamodzi ngati khoma lalitali pa mtunda wautali ndithu ndi mzinda wa Adama chapafupi ndi mzinda wa Zaretani. Madzi othamangira ku nyanja ya Araba, ngakhalenso amene amachokera kuti Nyanja ya Mchere amathera pamenepo. Choncho anthu anawoloka tsidya lina moyangʼanana ndi Yeriko.
17 And the priests who were bearing the ark of the covenant of Yahweh, stood on dry ground, in the midst of the Jordan, with firm footing, —while all Israel were passing over on dry ground, until all the nation had made an end of passing over the Jordan.
Ansembe onyamula Bokosi la Chipangano la Yehova anali chiyimire powuma, pakati pa Yorodani pamene Aisraeli amawoloka mpaka gulu lonse linamaliza kuwoloka powuma.