< Job 41 >
1 Canst thou draw out the Crocodile with a fish-hook? Or, with a cord, canst thou fasten down his tongue?
“Kodi ungathe kukoka ngʼona ndi mbedza ya nsomba kapena kukanikiza lilime lake pansi ndi chingwe?
2 Wilt thou put a rush-cord on his nose? or, with a thorn, wilt thou pierce his jaw?
Kodi ungathe kumanga chingwe mʼmphuno mwake, kapena kubowola nsagwada zake ndi mbedza?
3 Will he multiply unto thee supplications, or will he speak unto thee softly?
Kodi ngʼonayo idzakupempha kuti uyichitire chifundo? Kodi idzakuyankhula ndi mawu ofatsa?
4 Will he solemnise a covenant with thee? Wilt thou take him for a life-long servant?
Kodi idzachita nawe mgwirizano kuti uyisandutse kapolo wako mpaka muyaya?
5 Wilt thou sport with him, as with a little bird? Or wilt thou bind him, for thy maidens?
Kodi udzasewera nayo ngati mbalame, kapena kuyimangirira kuti atsikana ako asewere nayo?
6 Shall the companions bargain over him? or will they part him among the traders?
Kodi anthu adzayitsatsa malonda? Nanga amalondawo nʼkugawanagawana nyama yake kuti akagulitse?
7 Wilt thou fill, with darts, his skin? or, with fish-spears, his head?
Kodi chikopa chake ungathe kuchilasa ndi zisonga, kapena kubowola mutu wake ndi nthungo zophera nsomba?
8 Lay thou upon him thy hand, remember the battle—no more!
Ukayiputa udziwe kuti pali nkhondo, ndipo iweyo sudzabwereranso.
9 Lo! any hope of him, hath been found deceptive, Even at the sight of him, shall not one be overwhelmed?
Chiyembekezo choti nʼkuyigonjetsa ndi chabodza; kungoyiona kokha, ndithu iwe kumangodzigwera wekha.
10 None so bold, that he will rouse him! Who then is he that, before me, can stand?
Palibe wolimba mtima kuti ndi kuyiputa. Ndani angalimbe mtima kulimbana ndi Ine?
11 Who hath forestalled me, that I may repay him? Under all the heavens, mine it is!
Kodi ndani anandipatsa kanthu kuti ndimubwezere? Zonse za pansi pa thambo ndi zanga.
12 I will not pass by in silence his parts, or the matter of strength, or the grace of his armour.
“Sindidzaleka kuyankhula za ziwalo zake za chirombocho, za mphamvu zake ndiponso za maonekedwe a thupi lake.
13 Who hath removed his outer garment, through his double row of teeth, who would enter?
Ndani angasende chikopa chake? Ndani angayiyandikire kuti abowole chikopa chake cholimbacho?
14 The doors of his face, who hath opened? The circles of his teeth, are a terror!
Ndani angatsekule kukamwa kwake, pakamwa pamene pazunguliridwa ndi mano ochititsa mantha?
15 A pride, are his arched sides, closed up, with a firm seal;
Kumsana kwake kuli mizere ya mamba onga zishango zolumikizanalumikizana;
16 One to another, they join, and, air, cannot enter between them;
Mambawo ndi olukanalukana kotero kuti mpweya sungathe kulowa pakati pake.
17 Each to its fellow, they cleave, they grasp each other, and cannot be parted;
Ndi olumikizanalumikizana; ndi omatirirana kwambiri kotero kuti sangathe kulekana.
18 His sneezings, flash forth light, and, his eyes, are like the eyelashes of the dawn;
Kuyetsemula kwake kumatulutsa mbaliwali; maso ake amawala ngati kuwala kwa mʼbandakucha.
19 Out of his mouth, torches dart forth, sparks of fire, escape;
Mʼkamwa mwake mumatuluka nsakali zamoto ndipo mumathetheka mbaliwali zamoto.
20 Out of his nostrils, proceedeth smoke, like a blown pot and rushes;
Mʼmphuno mwake mumatuluka utsi ngati wa mʼnkhali yowira yomwe ili pa moto wa bango.
21 His breath, setteth coals ablaze, and, a flame, out of his mouth, proceedeth;
Mpweya wake umayatsa makala, ndipo malawi amoto amatuluka mʼkamwa mwake.
22 In his neck, lodgeth strength, and, before him, danceth dismay;
Mphamvu zake zili mʼkhosi mwake; aliyense wokumana nayo amangoti njenjenje ndi mantha.
23 The dewlaps of his flesh, cleave together, hardened upon him, they cannot be moved;
Minyewa ya thupi lake ndi yolumikizana ndipo ndi yokhwima kwambiri ndi yolimba.
24 His heart, is hardened like a stone, yea hardened, like the nether millstone;
Pachifuwa pake ndi powuma ngati mwala, ndi pa gwaa, ngati mwala wamphero.
25 At his rising up, mighty men are afraid, by reason of terror, they are beside themselves:
Ngʼonayo ikangovuwuka, ndi anthu amphamvu omwe amaopa; amabwerera mʼmbuyo, kuthawa.
26 As for him that assaileth him, the sword availeth not, spear, dart, or coat of mail:
Ngakhale ikanthidwe ndi lupanga, lupangalo silichita kanthu, ngakhale mkondo, muvi ndi nthungo, zonse zimalephera.
27 He counteth iron as broken straw, and bronze as rotten wood:
Chitsulo imachiyesa ngati phesi chabe ndi mkuwa ngati chikuni chowola.
28 The arrow, will not make him flee, Into chaff, are sling-stones changed by him:
Muvi sungathe kuyithawitsa, miyala imene ayilasa nayo imangoyinyenyanyenya.
29 As a straw, is a club accounted, and he laugheth at the whir of the javelin;
Zibonga zimakhala ngati ziputu; imangoseka pamene akuyibaya ndi nthungo.
30 His underparts, are points of potsherd, a pointed threshing roller spreadeth out upon the slime:
Mamba a ku mimba kwake ali ngati chopunthira chakunthwa ndipo imasiya mkukuluzi mʼmatope ngati galeta lopunthira tirigu.
31 He causeth to boil, as a cauldron, the raging deep, the sea, he maketh like a brewing vessel:
Imagadutsa madzi ozama ngati madzi a mʼnkhali, imachititsa nyanja kuti iwire ngati mbiya yoyengera mafuta.
32 After him, he lighteth up a path, one might think the resounding deep to be hoary!
Kumbuyo kwake imasiya nthubwitubwi zambee, kotero kuti munthu angaganize kuti nyanja yachita imvi.
33 There is not—upon the dust—his like, that hath been made to be without fear;
Pa dziko lapansi palibe china chofanana nacho, nʼcholengedwa chopanda mantha.
34 Every thing lofty, he beholdeth, he, is king over all ravenous beasts.
Chimanyoza nyama zina zonse; icho chija ndi mfumu ya nyama zonse.”