< Job 21 >

1 Then responded Job, and said: —
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 Hear ye patiently my words, and let this be your consolation:
“Mvetserani bwino mawu anga; ichi chikhale chitonthozo changa chochokera kwa inu.
3 Suffer me, that, I, may speak, and, after I have spoken, thou canst mock!
Ndiloleni ndiyankhule ndipo ndikatha kuyankhula munditonzetonze.
4 Did, I, unto man, make my complaint? Wherefore, then, should my spirit not be impatient?
“Kodi ine ndikudandaulira munthu? Tsono ndilekerenji kupsa mtima?
5 Turn round to me, and be astonished, and lay hand on mouth!
Ndipenyeni ndipo mudabwe; mugwire dzanja pakamwa.
6 When I call to mind, then am I dismayed, and there seizeth my flesh a shuddering: —
Ndikamaganiza zimenezi ndimachita mantha kwambiri; thupi langa limanjenjemera.
7 Wherefore do, lawless men, live, advance in years, even wax mighty in power?
Chifukwa chiyani anthu oyipa amakhalabe ndi moyo, amakalamba ndi kusanduka amphamvu?
8 Their seed, is established in their sight, along with them, yea their offspring, before their eyes;
Amaona ana awo akukhazikika pamodzi nawo, zidzukulu zawo zikukula bwino iwo akuona.
9 Their houses, are at peace, without dread, neither is, the rod of GOD, upon them;
Mabanja awo amakhala pa mtendere ndipo sakhala ndi mantha; mkwapulo wa Mulungu suwakhudza nʼkomwe.
10 His bull, covereth, and causeth not aversion, His cow safely calveth, and casteth not her young;
Ngʼombe zawo zazimuna sizilephera kubereketsa; ngʼombe zawo zazikazi sizipoloza.
11 They send forth—like a flock—their young ones, and, their children, skip about for joy;
Amatulutsa ana awo ngati gulu la nkhosa; makanda awo amavinavina pabwalo.
12 They rejoice aloud as [with] timbrel and lyre, and make merry to the sound of the pipe;
Amayimba nyimbo pogwiritsa ntchito matambolini ndi azeze; amakondwa pakumva kulira kwa chitoliro.
13 They complete, in prosperity, their days, and, in a moment to hades, they sink down. (Sheol h7585)
Zaka zawo zimatha ali mu ulemerero ndipo amatsikira ku manda mwamtendere. (Sheol h7585)
14 Yet they said unto GOD, Depart from us, and, In the knowledge of thy ways, find we no pleasure.
Koma anthuwo amawuza Mulungu kuti, ‘Tichokereni!’ Ife tilibe chikhumbokhumbo chofuna kudziwa njira zanu.
15 What is the Almighty, that we should serve him? Or what shall we profit, that we should urge him?
Kodi Wamphamvuzonseyo ndani kuti timutumikire? Ife tipindula chiyani tikamapemphera kwa Iyeyo?
16 Lo! not in their own hand, is their welfare, The counsel of lawless men, is far from me!
Komatu ulemerero wawo suli mʼmanja mwawo, koma ine ndimakhala patali ndi uphungu wa anthu oyipa.
17 How oft, the lamp of the lawless, goeth out, and their calamity, cometh upon them, Sorrows, apportioneth he in his anger;
“Koma nʼkangati kamene nyale ya anthu oyipa imazimitsidwa? Nʼkangati kamene tsoka limawagwera? Nʼkangati kamene Mulungu amawakwiyira ndi kuwalanga?
18 They become as straw before the wind, and as chaff, which the storm stealeth away.
Nʼkangati kamene iwo amakhala ngati phesi lowuluka ndi mphepo, ngati mungu wowuluzika ndi kamvuluvulu?
19 Shall, GOD, reserve, for his children, his sorrow? Let him recompense him so that he may know it;
Paja amati, ‘Mulungu amalanga ana chifukwa cha machimo abambo awo.’ Koma Mulungu amabwezera chilango munthuyo, kuti adziwe kuti Mulungu amalangadi.
20 His own eyes, shall see his misfortune, and, the wrath of the Almighty, shall he drink.
Mulole kuti adzionere yekha chilango chake, kuti alawe ukali wa Wamphamvuzonse.
21 For what shall be his pleasure in his house after him, when, the number of his months, is cut in twain?
Nanga kodi amalabadira chiyani zabanja lake limene walisiya mʼmbuyo, pamene chiwerengero cha masiku ake chatha?
22 Is it, to GOD, one can teach knowledge, seeing that, he, shall judge, them who are on high?
“Kodi alipo wina amene angaphunzitse Mulungu nzeru, poti Iye amaweruza ngakhale anthu apamwamba?
23 This, man dieth, in the very perfection of his prosperity, wholly tranquil and secure;
Munthu wina amamwalira ali ndi mphamvu zonse, ali pa mtendere ndi pa mpumulo,
24 His veins, are filled with nourishment, and, the marrow of his bones, is fresh;
thupi lake lili lonenepa, mafupa ake ali odzaza ndi mafuta.
25 Whereas, this other man, dieth, in bitterness of soul, and hath never tasted good fortune:
Munthu wina amamwalira ali wowawidwa mtima, wosalawapo chinthu chabwino chilichonse.
26 Together, in the dust, they lie down, and, the worm, spreadeth a covering over them.
Olemera ndi osauka omwe amamwalira ndi kuyikidwa mʼmanda ndipo onse amatuluka mphutsi.
27 Lo! I know your plans, and the devices, wherewith ye would do me violence!
“Ndikudziwa bwino zimene mukuganiza, ziwembu zanu zomwe mukuti mundichitire.
28 For ye say, Where is the house of the noble-minded? And where the dwelling-tent of the lawless?
Inu mukuti, ‘Kodi nyumba ya mkulu uja ili kuti, matenti amene munkakhala anthu oyipa aja ali kuti?’
29 Have ye not asked the passers-by in the way? And, their signs, can ye not recognise?
Kodi munawafunsapo anthu amene ali pa ulendo? Kodi munaganizirapo zimene iwo amanena?
30 That, to the day of calamity, is the wicked reserved, to the day of indignant visitation, are they led.
Zakuti munthu woyipa amasungidwa chifukwa cha tsiku la tsoka, kuti amapulumutsidwa chifukwa cha tsiku la ukali wa Mulungu?
31 Who can declare—to his face—his way? And, what, he, hath done, who shall recompense to him?
Kodi ndani amadzudzula munthu wochimwayo? Ndani amamubwezera zoyipa zimene anachita?
32 Yet, he, to the graves, is borne, and, over the tomb, one keepeth watch;
Iye amanyamulidwa kupita ku manda ndipo anthu amachezera pa manda ake.
33 Pleasant to him are the mounds of the torrent-bed, —and, after him, doth every man march, as, before him, there were without number.
Dothi la ku chigwa limamukomera; anthu onse amatsatira mtembo wake, ndipo anthu osawerengeka amakhala patsogolo pa chitanda chakecho.
34 How then should ye comfort me with vanity, since, as for your replies, there lurketh, [in them] treachery?
“Nanga inu mudzanditonthoza bwanji ine ndi mawu anu opandapakewo palibe chimene chatsala kuti muyankhe koma mabodza basi!”

< Job 21 >