< Job 16 >
1 Then responded Job, and said: —
Pamenepo Yobu anayankha kuti,
2 I have heard many such things, Wearisome comforters, are ye all!
“Ndinamvapo zambiri monga zimenezi; nonsenu ndinu anthu osatha kutonthoza mtima mnzanu.
3 Is there to be an end to windy words? Or what so strongly exciteth thee, that thou must respond?
Kodi mawu anu ochulukawo adzatha? Kodi chikukuvutani nʼchiyani kuti muzingoyankhula mawu otsutsawa?
4 I also, like you, could speak, —If your soul were in the place of my soul, I could string together words against you, and could therewith shake over you my head.
Inenso ndikanatha kuyankhula monga inu, inuyo mukanakhala monga ndilili inemu; Ine ndikanatha kuyankhula mawu omveka bwino kutsutsana nanu ndi kukupukusirani mutu wanga.
5 I could make you determined, by my mouth, and then my lip-solace should restrain you.
Ndipo mawu a pakamwa panga akanakulimbikitsani; chitonthozo chochokera pa milomo yanga chikanachepetsa ululu wanu.
6 Though I do speak, unassuaged is my stinging pain, —And, if I forbear, of what am I relieved?
“Koma ine ndikati ndiyankhule ululu wanga sukuchepa; ndipo ndikati ndikhale chete, ululu wanga sukuchokabe.
7 But, now, hath he wearied me, thou hast destroyed all my family;
Ndithudi, Inu Mulungu mwanditha mphamvu; mwawononga banja langa lonse.
8 And, having captured me, it hath served, as a witness; and so my wasting away hath risen up against me, in my face, it answereth.
Inu mwandimanga ndipo kundimangako kwakhala umboni; kuwonda kwanga kwandiwukira ndipo kukuchita umboni wonditsutsa.
9 His anger, hath torn and persecuted me, He hath gnashed upon me with his teeth, Mine adversary, hath sharpened his eyes for me.
Mulungu amabwera kwa ine mwankhanza ndipo amadana nane, amachita kulumira mano; mdani wanga amandituzulira maso.
10 They have gaped upon me with their mouth, With reproach, have they smitten my cheek, Together, against me, have they closed their ranks.
Anthu amatsekula pakamwa pawo kundikuwiza; amandimenya pa tsaya mwachipongwe ndipo amagwirizana polimbana nane.
11 GOD doth abandon me to him that is perverse, and, into the hands of the lawless, he throweth me headlong.
Mulungu wandipereka kwa anthu ochita zoyipa ndipo wandiponyera mʼmanja mwa anthu oyipa mtima.
12 At ease, was I when he shattered me, Yea he seized me by my neck, and dashed me in pieces, then set me up for himself as a mark:
Ine ndinali pamtendere, koma Mulungu ananditswanya; anandigwira pa khosi ndi kundiphwanya. Iye anandisandutsa choponyera chandamale chake;
13 His archers came round against me, He clave asunder my reins, and spared not, He poured out, on the earth, my gall:
anthu ake oponya mauta andizungulira. Mopanda kundimvera chisoni, Iye akulasa impsyo zanga ndipo akutayira pansi ndulu yanga.
14 He made a breach in me, breach upon breach, He ran upon me, like a mighty man.
Akundivulaza kawirikawiri, akuthamangira pa ine monga munthu wankhondo.
15 Sackcloth, sewed I on my skin, and rolled—in the dust—my horn:
“Ndasokerera chiguduli pa thupi langa ndipo ndayika mphamvu zanga pa fumbi.
16 My face, is reddened from weeping, and, upon mine eyelashes, is the death-shade: —
Maso anga afiira ndi kulira, ndipo zikope zanga zatupa;
17 Though no violence was in my hands, and, my prayer, was pure.
komatu manja anga sanachite zachiwawa ndipo pemphero langa ndi lolungama.
18 O earth! do not cover my blood, and let there be no place for mine outcry.
“Iwe dziko lapansi, usakwirire magazi anga; kulira kwanga kofuna thandizo kusalekeke!
19 Even now, lo! in the heavens, is my witness,
Ngakhale tsopano mboni yanga ili kumwamba; wonditchinjiriza pa mlandu wanga ali komweko.
20 And, he that voucheth for me is on high. My friends are, they who scorn me, Unto GOD, hath mine eye shed tears: —
Wondipembedzera ndi bwenzi langa, pamene maso anga akukhuthula misozi kwa Mulungu;
21 That one might plead, for a man, with GOD, —Even a son of man, for his friend!
iye, mʼmalo mwanga, amamudandaulira Mulungu monga munthu amadandaulira bwenzi lake.
22 When, a few years, come, then, by a path by which I shall not return, shall I depart.
“Pakuti sipapita zaka zambiri ndisanayende mʼnjira imene sindidzabwerera.”