< Job 14 >
1 Man that is born of a woman, is of few days, and full of trouble:
“Munthu wobadwa mwa amayi amakhala masiku owerengeka ndipo ndi odzaza ndi mavuto okhaokha.
2 As a flower, he cometh forth—and fadeth, He fleeth also as a shadow, and continueth not.
Amaphuka ngati duwa ndipo kenaka amafota; amathawa ngati mthunzi ndipo sakhalitsa.
3 And yet upon such a one as this, hast thou opened thine eye? And, him, wouldst thou bring into judgment with thee?
Kodi munthu wotereyo nʼkumuyangʼanitsitsa? Kodi mungamubweretse pamaso panu kuti mumuzenge mlandu?
4 Who can bring a clean thing out of an unclean? Not one!
Ndani angatulutse chabwino mʼchoyipa? Palibe ndi mmodzi yemwe!
5 If determined am his days, the number of his months, is with thee, Fixed times for him, thou hast appointed and he cannot go beyond.
Masiku a munthu ndi odziwikiratu; munakhazikitsa chiwerengero cha miyezi yake ndipo munamulembera malire amene sangathe kuwalumpha.
6 Look sway from him, that he may rest, Till he shall pay off, as a hireling, his day.
Choncho Inu mumufulatire ndipo mumuleke apumule kufikira atakondwera nawo moyo ngati munthu waganyu.
7 Though there is—for a tree—hope, —if it should be cut down, that, again, it will grow, and, the tender branch thereof, will not cease;
“Mtengo uli nacho chiyembekezo: ngati wadulidwa, udzaphukiranso ndipo nthambi zake sizidzaleka kuphukira.
8 If its root, should become old in the earth, and, in the dust, its stock should die:
Mizu yake ingathe kukalamba mʼnthaka ndipo chitsa chake nʼkuwola pa dothi,
9 Through the scent of water, it may break forth, and produce branches like a sapling,
koma pamene chinyontho chafika udzaphukira ndipo udzaphuka nthambi ngati mtengo wanthete.
10 Yet, man, dieth, and is prostrate, Yea the son of earth doth cease to breathe, and where is he?
Koma munthu amafa nayikidwa mʼmanda, amapuma mpweya wotsiriza ndipo kutha kwake nʼkomweko.
11 Waters, have failed from, the sea, and, a river, may waste and dry up;
Monga madzi amaphwera mʼnyanja kapena monga mtsinje umaphwera nuwuma,
12 So, a man, hath lain down, and shall not arise, until there are no heavens, they shall not awake, nor be roused up out of their sleep.
momwemonso munthu amagona ndipo sadzukanso; mpaka zamlengalenga zidzathe, anthu sadzauka kapena kudzutsidwa ku tulo tawo.
13 Oh that, in hades, thou wouldst hide me! that thou wouldst keep me secret, until the turn of thine anger, that thou wouldst set for me a fixed time, and remember me: (Sheol )
“Aa, Inu mukanangondibisa mʼmanda ndi kundiphimba kuti ndisaoneke mpaka mkwiyo wanu utapita! Achikhala munandiyikira nthawi, kuti pambuyo pake mundikumbukirenso. (Sheol )
14 If a man die, can he live again? All the days of my warfare, would I wait, until my relief should come: —
Munthu akafa, kodi adzakhalanso ndi moyo? Masiku anga onse a moyo wovutikawu ndidzadikira mpaka itafika nthawi yomasulidwa.
15 Thou shouldst call, and, I, would answer thee, —For the work of thine own hand, thou shouldst long.
Inu mudzandiyitane ndipo ndidzakuyankhani; inu mudzafunitsitsa kuona cholengedwa chimene munachipanga ndi manja anu.
16 For, now, my steps, thou countest, Thou wilt not pass over my sin:
Ndithudi pamenepo mudzayangʼana mayendedwe anga koma simudzalondola tchimo langa.
17 Sealed up in a bag, is my transgression, and thou hast glued over mine iniquity.
Zolakwa zanga zidzakulungidwa mʼthumba; inu mudzaphimba tchimo langa.
18 But, in very deed, a mountain falling, will lie prostrate, or, a rock moved out of its place:
“Koma monga phiri limakokolokera ndi kuswekasweka ndipo monga thanthwe limasunthira kuchoka pa malo ake,
19 Stones, have been hollowed out by waters, the floods thereof wash away the dust of the earth, and, the hope of mortal man, thou hast destroyed:
monganso madzi oyenda amaperesera miyala ndipo madzi othamanga amakokololera nthaka, momwemonso Inu mumawononga chiyembekezo cha munthu.
20 Thou dost overpower him utterly, and he departeth, Disfiguring his face, so, hast thou sent him away.
Inu mumamugonjetsa kamodzinʼkamodzi ndipo munthuyo nʼkutheratu; Inu mumasintha maonekedwe a nkhope yake ndipo mumamutaya kutali.
21 His sons, come to honour, and he knoweth it not, Or they are brought low, and he perceiveth it not of them.
Ana ake akamalemekezedwa, iyeyo sazidziwa zimenezo; akamachititsidwa manyazi iye saziona zimenezo.
22 But, his flesh, for himself, is in pain, and, his soul, for himself, doth mourn.
Iye amangomva zowawa za mʼthupi lake ndipo amangodzilirira yekha mwini wakeyo.”