< Jeremiah 1 >

1 The words of Jeremiah son of Hilkiah, —of the priests who were in Anathoth, in the land of Benjamin:
Mawu a Yeremiya mwana wa Hilikiya, mmodzi mwa ansembe a ku Anatoti, mʼdziko la Benjamini.
2 unto whom came the word of Yahweh, in the days of Josiah son of Amon king of Judah, —in the thirteenth year of his reign;
Mawuwa Yehova anayankhula naye mʼchaka cha 13 cha ulamuliro wa Yosiya mwana wa Amoni mfumu ya Yuda.
3 it came also in the days of Jehoiakim son of Josiah, king of Judah, unto the end of the eleventh year of Zedekiah son of Josiah king of Judah, —as far as the carrying away of Jerusalem captive, in the fifth month.
Yehova anayankhulanso naye pa nthawi yonse ya ulamuliro wa Yehoyakimu mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, mpaka mwezi wachisanu wa chaka cha 11 cha ufumu wa Zedekiya mwana wa Yosiya mfumu ya Yuda, pamene anthu a ku Yerusalemu anapita ku ukapolo.
4 So then, the word of Yahweh came unto me, saying:
Yehova anayankhula nane kuti,
5 Before I formed thee at thy birth, I took knowledge of thee, And before thy nativity, I hallowed thee, —A prophet to the nations, I appointed thee.
“Ndisanakuwumbe mʼmimba mwa amayi ako ndinali nditakudziwa kale, iwe usanabadwe ndinali nditakupatula kale; ndinakuyika kuti ukhale mneneri kwa anthu a mitundu yonse.”
6 Then said I—Ah! My Lord Yahweh! Lo! I know not how to speak, —For a child, am I!
Ine ndinati, “Haa! Ambuye Yehova, ine sinditha kuyankhula; popeza ndikanali wamngʼono.”
7 Then said Yahweh unto me, Do not say, A child, am, I,—For against whomsoever I send thee, shalt thou go, And whatsoever I command thee, shalt thou speak:
Koma Yehova anandiwuza kuti, “Usanene kuti, ‘Ndikanali wamngʼono’ popeza udzapita kwa munthu aliyense kumene ndidzakutuma ndi kunena chilichonse chimene ndidzakulamulira.
8 Be not afraid of their faces, For with thee, am I, to deliver thee Declareth Yahweh.
Usawaope, pakuti Ine ndili nawe, ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.
9 Then Yahweh put forth his hand, and touched my mouth, —and Yahweh said unto me, Lo! I have put my words in thy mouth.
Pamenepo Yehova anatambalitsa dzanja lake nakhudza pakamwa panga, nandiwuza kuti, “Taona, tsopano ndayika mawu anga mʼkamwa mwako.
10 See! I have set thee in charge this day, over the nations and over the kingdoms, To uproot and to break down, and to destroy and to tear in pieces, —To build and to plant.
Lero ndakusankha kuti ukhale ndi ulamuliro pa mitundu ya anthu ndi pa maufumu awo kuti uzule ndi kugwetsa, uwononge ndi kugumula, kuti uwamange ndi kudzala.”
11 Moreover the Word of Yahweh came unto me saying, What canst thou see Jeremiah? And I said, A twig of an almond-tree, can I see.
Yehova anandifunsa kuti, “Yeremiya, kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona nthambi ya mtengo wa mtowo.”
12 Then said Yahweh unto me—Thou hast rightly seen, —for keeping watch, am I over my word to perform it.
Yehova anandiwuza kuti, “Waona bwino, chifukwa Ine ndikuonetsetsa kuti mawu angawa akwaniritsidwe.”
13 And the word of Yahweh came unto me a second time saying, What canst thou see? And I said, A boiling caldron, can I see, with, the front thereof, on the North.
Yehova anandifunsanso kachiwiri kuti, “Kodi ukuona chiyani?” Ine ndinayankha kuti, “Ndikuona mʼphika wa madzi owira, ndipo wagudukira kuno kummwera.”
14 Then said Yahweh unto me, —Out of the North, shall break forth calamity, against all the inhabitants of the land.
Yehova anandiwuza kuti, “Mavuto a anthu onse okhala mʼdziko lino adzachokera kumpoto.
15 For behold me! calling for all the families of the kingdoms of the North, Declareth Yahweh, —and they shall come, and set every one his throne at the opening of the gates of Jerusalem and against all her walls round about, and against all the cities of Judah!
Ine ndikuyitana anthu onse a ku maufumu a kumpoto,” akutero Yehova. “Mafumu awo adzabwera ndipo aliyense adzakhazika mpando wake waufumu polowera pa zipata za Yerusalemu; iwo adzabwera ndi kuzungulira makoma ake ndiponso midzi yonse ya dziko la Yuda.
16 Then will I pronounce my judgments against them, concerning all their wickedness, —in that they have forsaken me and have burned incense unto other gods, and have bowed down to the works of their own hands,
Ndidzatulutsa mlandu wanga ndi iwo chifukwa cha zoyipa zimene anachita pondisiya Ine. Iwo anakafukiza lubani kwa milungu ina, ndi kupembedza zimene anapanga ndi manja awo.
17 Thou, therefore, shalt gird thy loins, and arise, and speak unto them, all that, I, command thee, —be not dismayed because of them, lest I dismay thee before their face.
“Koma iwe Yeremiya konzeka! Nyamuka ndipo ukawawuze zonse zimene ndakulamulira. Usachite nawo mantha, kuopa kuti Ine ndingakuchititse mantha iwo akuona.
18 I, therefore—lo! I have set thee to-day as a fortified city, and as a pillar of iron and as walls of bronze, over all the land, —against the kings of Judah, against her princes, against her priests and against the people of the land.
Taona, lero ndakupanga kukhala ngati mzinda wotetezedwa, ngati mzati wachitsulo ndiponso ngati makoma a mkuwa kuti usaopsedwe ndi munthu aliyense wa mʼdzikomo; kaya ndi mafumu a Yuda, akuluakulu ake, ansembe ake, kapena munthu wamba wa mʼdzikomo.
19 And they will fight against thee but shall not prevail against thee, —for with thee, am I, Declareth Yahweh, to deliver thee.
Iwo adzalimbana nawe koma sadzakugonjetsa, popeza Ine ndili nawe ndipo ndidzakupulumutsa,” akutero Yehova.

< Jeremiah 1 >