< Jeremiah 51 >

1 Thus, saith Yahweh—Behold me! stirring up against Babylon, And against the inhabitants of the centre of them who rise up against me, —A wind that destroyeth;
Yehova akuti, “Taonani, ndidzadzutsa mphepo yowononga kuti iwononge Babuloni pamodzi ndi anthu a ku Lebi Kamai.
2 And I will send to Babylon winnowers, And they shall winnow her, And shall empty her land, —For they are against her round about in the day of calamity.
Ndidzatuma alendo ku Babuloni kudzamupeta ndi kuwononga dziko lake kotheratu. Iwo adzalimbana naye ku mbali zonse pa tsiku la masautso ake.
3 Let not the archer tread his bow, Nor lift himself up in his coat of mail, —And do not spare her young men, Devote to destruction all her host.
Okoka uta musawalekerere kapena wonyadira chovala chawo chankhondo. Musawasiye anyamata ake kuti akhale ndi moyo; koma muwononge ankhondo ake kotheratu.
4 So shall they fall wounded in the land of Chaldea, —Yea thrust through, in her streets,
Adzavulazidwa ndi kufera mʼdziko la Babuloni lomwelo ndi mʼmisewu yawo yomwe.
5 For Israel and Judah have not been widowed Of their God, Of Yahweh of hosts, —But, their land, hath been filled with punishment for guilt from the Holy One of Israel
Pakuti Yuda ndi Israeli sanasiyidwe ngati amasiye ndi Mulungu wawo, Yehova Wamphamvuzonse, koma ngakhale dziko la Babuloni ndi lodzaza ndi machimo pamaso pa Woyerayo wa Israeli.
6 Flee out of the midst of Babylon And deliver ye every man his own life, Be not cut off in her punishment, —For it is Yahweh’s, time of avenging, A recompense, is he repaying unto her.
“Thawaniko ku Babuloni! Aliyense apulumutse moyo wake! Musawonongeke naye pamodzi chifukwa cha machimo ake. Imeneyi ndi nthawi yoti Yehova amulange; Yehova adzamulipsira.
7 A cup of gold, was Babylon in the hand of Yahweh, Making drunk all the earth, —Of her wine, have the nations drunk, For this cause have the nations been acting as men who are mad.
Babuloni anali ngati chikho cha golide mʼdzanja la Yehova; kuti aledzeretse dziko lonse lapansi. Mitundu yambiri ya anthu inamwa vinyo wake; nʼchifukwa chake tsopano inachita misala.
8 Suddenly, hath Babylon fallen and been broken, —Howl ye over her Fetch balsam for her pain, Peradventure she shall be healed!
Babuloni wagwa mwadzidzidzi ndi kusweka. Mulireni! Mfunireni mankhwala opha ululu wake; mwina iye nʼkuchira.”
9 We would have healed Babylon, but she is not healed, Leave her and let us go every one to his own land, —For her judgment, reacheth unto the heavens, And mounteth as far as the skies.
Ena anati, “‘Ife tinayesa kumupatsa mankhwala Babuloni, koma sanachire; tiyeni timusiye ndipo aliyense apite ku dziko la kwawo, pakuti mlandu wake wafika mpaka mlengalenga, wafika mpaka kumwamba.’
10 Yahweh hath brought forth our righteousnesses, —Come and let us relate in Zion the work of Yahweh our God.
“‘Yehova waonetsa poyera kuti ndife osalakwa; tiyeni tilengeze mu Ziyoni zimene Yehova Mulungu wathu wachita.’
11 Polish the arrows, Lay hold of the shields, —Yahweh hath roused the spirit of the kings of the Medes, For against Babylon, his purpose is, to destroy her, —For it is, The avenging of Yahweh, The avenging of his temple.
“Yehova wadzutsa mitima ya mafumu a Amedi, popeza cholinga chake ndi kuwononga Babuloni. Motero adzalipsira Ababuloni chifukwa chowononga Nyumba yake. Ndiye Yehova akuti, ‘Nolani mivi, tengani zishango.’
12 Against the walls of Babylon, Lift ye up a standard, Strengthen ye the watch, Station the watchmen, Make ready the ambuscades, —For Yahweh hath both planned and also performed that which he had spoken against the inhabitants of Babylon.
Kwezani mbendera yankhondo kuti muwononge malinga a Babuloni! Limbitsani oteteza, ikani alonda pa malo awo, konzekerani kulalira. Pakuti Yehova watsimikiza ndipo adzachitadi zomwe ananena za anthu a ku Babuloni.
13 O thou who dwellest upon many waters, Who aboundest in treasures, —Come hath thine end! The measure of thine unrighteous gain!
Inu muli ndi mitsinje yambiri ndi chuma chambiri. Koma chimaliziro chanu chafika, moyo wanu watha.
14 Yahweh of hosts hath sworn, by his own soul: Surely I have filled thee with men as with locusts, And they have answered against thee with a shout.
Yehova Wamphamvuzonse analumbira pali Iye mwini kuti: Ndidzakutumizira adani ochuluka ngati dzombe, kuti adzakuthire nkhondo ndipo adzafuwula kuonetsa kuti apambana.
15 He that Made the earth in his might, Established the world in his wisdom, —And in his understanding, stretched out the heavens
“Yehova analenga dziko lapansi ndi mphamvu zake; Iye anapanga dziko lonse ndi nzeru zake ndipo anayala thambo mwaluso lake.
16 By the voice that he uttered, there was a tumult of waters in the heavens, And he caused vapours to ascend from the end of the earth, —Lightnings for the rain, made he, And brought forth wind out of his treasures.
Iye akayankhula, kumamveka mkokomo wamadzi akumwamba. Iyeyo amabweretsa mitambo kuchokera ku malekezero a dziko lapansi. Amabweretsa mphenzi pamodzi ndi mvula ndi kutulutsa mphepo yamkuntho kumalo kumene amasungira.
17 Every son of earth had become too brutish to know, —Every goldsmith, hath been put to shame, by a graven image, —For a falsehood, is his molten image Seeing there is no breath in them:
“Anthu onse ndi opusa ndiponso opanda nzeru; mmisiri aliyense wosula golide akuchita manyazi ndi mafano ake. Mafano akewo ndi abodza; alibe moyo mʼkati mwawo.
18 Vanity, they are, A handiwork of mockeries, —In the time of their visitation, shall they perish.
Mafanowo ndi achabechabe, zinthu zosekedwa nazo. Pamene anthuwo azidzaweruzidwa mafanowo adzawonongedwa.
19 Not like these, is the portion of Jacob, For the fashioner of all things, is he! And the portion of his inheritance, —Yahweh of hosts, is his name.
Koma Yehova amene ndi Cholowa cha Yakobo sali ngati mafanowo. Iyeyu ndi Mlengi wa zinthu zonse, kuphatikizapo mtundu umene anawusankha kuti ukhale anthu ake. Dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
20 A war-club, art thou for me, Weapons of war; Therefore will I Beat down with thee—nations, and Destroy with thee—kingdoms;
“Iwe Babuloni ndi ndodo yanga, chida changa chankhondo. Ndi iwe ndimaphwanya mitundu ya anthu, ndi iwe ndimawononga maufumu,
21 and Beat down with thee—the horse and his rider, —and Beat down with thee—the chariot and its rider;
ndi iwe ndimaphwanya kavalo ndi wokwerapo, ndi iwe ndimaphwanya galeta ndi woyendetsa wake.
22 and Beat down with thee—man and woman, and Beat down with thee—elder and youth, and Beat down with thee—young man and virgin;
Ndi iwe ndimaphwanya mwamuna ndi mkazi, ndi iwe ndimaphwanya nkhalamba ndi wachinyamata, ndi iwe ndimaphwanya mnyamata ndi namwali.
23 and Beat down with thee—the shepherd and his flock, and Beat down with thee—the plowman and his yoke; —and Beat down with thee—governors and deputies:
Ndi iwe ndimaphwanya mʼbusa ndi ziweto, ndi iwe ndimaphwanya mlimi ndi ngʼombe, ndi iwe ndimaphwanya abwanamkubwa ndi atsogoleri a ankhondo.
24 So will I recompense to Babylon, And to all the inhabitants of Chaldea, All their wickedness which they have committed against Zion before your eyes, —Declareth Yahweh.
“Inu mukuona ndidzalanga Babuloni ndi onse amene amakhala mʼdziko la Babuloni chifukwa cha zolakwa zonse anachita ku Ziyoni,” akutero Yehova.
25 Behold me! against thee, O destroying mountain Declareth Yahweh, That destroyest all the earth, —Therefore will I stretch out my hand over thee, And roll thee down from the crags, And make of thee a burning mountain:
“Taonani, ndikukuzenga mlandu, iwe phiri lowononga, amene umawononga dziko lonse lapansi,” akutero Yehova. “Ndidzatambalitsa dzanja langa pofuna kukulanga, kukugubuduzira pansi kuchokera pa matanthwe ako, ndi kukusandutsa kukhala phiri lopserera.
26 So shall they not fetch from thee A stone for a corner nor A stone for a foundation, —For desolations age-abiding, shalt thou become Declareth Yahweh.
Palibe ngakhale ndi mwala wako umodzi umene anthu adzawutenga kuti awugwiritse ntchito kumangira nyumba, chifukwa iwe udzakhala chipululu mpaka muyaya,” akutero Yehova.
27 Set ye up an ensign in the earth Blow ye a horn among the nations Hallow against her—nations, Summon against her the kingdoms of Ararat Minni, and Ashkenaz, —Set in charge against her a marshal, Bring up cavalry like hairy locusts:
“Kwezani mbendera ya nkhondo mʼdziko! Lizani lipenga pakati pa mitundu ya anthu! Konzekeretsani mitundu ya anthu kuti ikamuthire nkhondo; itanani maufumu awa: Ararati, Mini ndi Asikenazi kuti adzamuthire nkhondo. Ikani mtsogoleri wankhondo kuti amenyane naye; tumizani akavalo ochuluka ngati magulu a dzombe.
28 Hallow against her—nations, With the kings of Media, With her governors and all her deputies, —And with all the land of his dominion:
Konzekeretsani mitundu ya anthu. Amenewa ndiwo mafumu a Amedi, abwanamkubwa awo, atsogoleri a ankhondo, ndiponso ankhondo a mayiko amene amawalamulira, kuti idzathire nkhondo Babuloni.
29 Then did the land tremble and was in pain, —For the plans of Yahweh, had been established against Babylon, To make the land of Babylon an astonishment, without inhabitant.
Dziko likunjenjemera ndi kunthunthumira, chifukwa zidzachitikadi zimene Yehova wakonzera Babuloni; kusakaza dziko la Babuloni kuti musapezeke wokhalamo.
30 The heroes of Babylon have ceased to fight They have remained in the strongholds, Parched is their might, They have become women, —They have set fire to her habitations, Broken are her bars!
Ankhondo a ku Babuloni aleka kuchita nkhondo; iwo angokhala mʼmalinga awo. Mphamvu zawo zatheratu; ndipo akhala ngati akazi. Malo ake wokhala atenthedwa; mipiringidzo ya zipata zake yathyoka.
31 Runner to meet runner, shall they run, And teller to meet teller, -To tell the king of Babylon, That captured is his city at the end!
Othamanga akungopezanapezana, amithenga akungotsatanatsatana kudzawuza mfumu ya ku Babuloni kuti alande mzinda wake wonse.
32 and The fords, have been seized, and The reeds, have they burned with fire; and The men of war, are dismayed!
Madooko onse alandidwa, malo onse obisalamo alonda atenthedwa ndi moto, ndipo ankhondo onse asokonezeka.”
33 For, thus, saith Yahweh of hosts, God of Israel, The daughter of Babylon, is like a threshing, floor at the time of treading her: Yet a little, and the time of harvest shall overtake her.
Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, “Babuloni wokongola uja wakhala ngati malo opunthirapo tirigu pa nthawi yake yopuntha tirigu; A ku Yerusalemu akuti, Posachedwapa nthawi yake yomukolola ifika.”
34 Nebuchadrezzar king of Babylon—Hath devoured me Hath vexed me, Hath set me down as an empty vessel, He hath swallowed me like a sea-monster, He hath filled his belly with my dainties, —He hath driven me away!
A ku Yerusalemu akuti, “Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni watiwononga, watiphwanya, ndi kutitaya ngati mbiya yopanda kanthu. Watimeza ngati ngʼona, wakhuta ndi zakudya zathu zokoma, kenaka nʼkutilavula.”
35 The violence done to me and to my flesh, be upon Babylon! Shall the inhabitress of Zion say, —Yea, my blood, be upon the inhabitant of Chaldea! Shall Jerusalem say.
Anthu a ku Ziyoni anene kuti, “Zankhanza zimene anatichitira ife ziwabwerere Ababuloni.” Anthu okhala mu Yerusalemu anene kuti, “Magazi athu amene anakhetsedwa akhale pa amene akukhala ku Babuloni.”
36 Therefore, Thus, saith Yahweh, Behold me! pleading thy cause, So then I will execute the avenging of thee; And will dry up her sea, And make dry her spring:
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Taona, ndidzakumenyera nkhondo ndi kukulipsirira; ndidzawumitsa nyanja yake ndipo akasupe ake adzaphwa.
37 Thus shall Babylon become—Heaps A habitation of jackals An astonishment, and A hissing, Without inhabitant.
Motero Babuloni adzasanduka mulu wa nyumba zogumuka, malo okhala nkhandwe, malo ochititsa mantha ndi onyozedwa, malo wopanda aliyense wokhalamo.
38 Together, like wild lions, shall they roar, —They have growled like lions’ whelps.
Anthu ake onse adzabangula ngati mkango, adzadzuma ngati ana amkango.
39 When they are heated, I will spread their banquets, And let them drink that they may become uproarious, So shall they sleep an age-abiding sleep and not wake, —Declareth Yahweh.
Ngati achita dyera ndiye ndidzawakonzera madyerero ndi kuwaledzeretsa, kotero kuti adzasangalala, kenaka nʼkugona tulo mpaka muyaya ndipo sadzadzukanso,” akutero Yehova.
40 I will bring them down As fat lambs to slaughter, —As rams with he-goats.
“Ine ndidzawatenga kuti akaphedwe ngati ana ankhosa onenepa, ngati nkhosa zazimuna ndi mbuzi.
41 How hath Sheshach, been captured! How hath the praise of all the earth been seized! How hath Babylon become an astonishment among the nations!
“Ndithu Babuloni walandidwa, mzinda umene dziko lonse lapansi limanyadira wagwidwa! Taonani, mmene Babuloni wasandukira chinthu chochititsa mantha pakati pa mitundu ya anthu!
42 The sea, hath gone up over Babylon, —With the multitude of its rolling waves, is she covered.
Nyanja yakwera ndi kumiza Babuloni; mafunde ake okokoma aphimba Babuloni.
43 Her cities have become, an astonishment, A land parched up, and a waste plain, —A land wherein shall no man dwell, Nor pass through them a son of the earth-born!
Mizinda yake yasanduka bwinja, dziko lowuma ndi lachipululu, dziko losakhalamo wina aliyense, dziko losayendamo munthu aliyense.
44 So will I bring punishment upon Bel in Babylon, And will bring forth what he hath swallowed out of his mouth, And the nations shall stream unto him no more, —Even the wall of Babylon hath fallen!
Ndidzalanga Beli mulungu wa Ababuloni, ndidzamusanzitsa zimene anameza. Mitundu ya anthu sidzapitanso kwa iye. Malinga a Babuloni agwa.
45 Come ye forth out of her midst O my people, And deliver ye every man his own life, —Because of the glow of the anger of Yahweh.
“Tulukani mʼBabuloni anthu anga! Pulumutsani miyoyo yanu! Thawani mkwiyo woopsa wa Yehova.
46 And let not your heart be timid, nor be ye afraid, Because of the report that is reported in the earth When there shall come in one year, the report And after that in another year, the report, With violence in the earth, and ruler upon ruler.
Musataye mtima kapena kuchita mantha pamene mphekesera zikumveka mʼdziko mwanu. Chaka ndi chaka pamabuka mphekesera za ziwawa mʼdziko lapansi, ndiponso yakuti mfumu yakuti ikuthira nkhondo mfumu ina.
47 Therefore, lo! days coming when I will bring punishment upon the images of Babylon, And all her land, shall turn pale, —Yea, all her wounded, shall fall in her midst.
Pakuti taonani, nthawi ikubwera ndithu pamene ndidzalanga mafano a ku Babuloni; dziko lake lonse lidzachita manyazi ndi ophedwa ake onse adzakhala ngundangunda pakati pake.
48 Then shall shout over Babylon—heavens and earth and all who are therein, —For out of the North, shall come to her the spoilers Declareth Yahweh.
Pamenepo kumwamba ndi dziko lapansi ndi zonse zili mʼmenemo zidzayimba mokondwa chifukwa cha kugwa kwa Babuloni. Anthu owononga ochokera kumpoto adzamuthira nkhondo,” akutero Yehova.
49 Not only hath Babylon, caused the fall of the slain of Israel, —By Babylon, also have fallen the slain of all the earth.
“Babuloni anapha anthu ambiri pa dziko lapansi. Tsono, nawo anthu a ku Babuloni ayenera kuphedwa chifukwa anapha anthu a ku Yerusalemu.
50 Ye that have escaped the sword, depart do not stand still, —Remember, from afar Yahweh, Let, Jerusalem, come up on your heart: -
Inu amene munapulumuka ku nkhondo ya Babuloni, chokani pano ndipo musazengereze! Kumbukirani Yehova ngakhale muli ku mayiko akutali, ganizirani za Yerusalemu.”
51 We have turned pale for we have heard a reproach, Confusion, hath covered our faces, —For aliens have entered upon the hallowed places of the house of Yahweh!
Inu mukuti, “Tikuchita manyazi, chifukwa tanyozedwa ndipo nkhope zathu zili ndi manyazi, chifukwa anthu achilendo alowa malo opatulika a Nyumba ya Yehova.”
52 Therefore, lo! days are coming, Declareth Yahweh, When I will bring punishment upon her images; And throughout all her land, shall the pierced one groan.
Nʼchifukwa chake Yehova akuti, “Masiku akubwera pamene ndidzalanga mafano ake, ndipo mʼdziko lake lonse anthu ovulala adzabuwula.
53 Though Babylon should mount the heavens, And though she should fortify her strong high-place, From me, should come spoilers unto her Declareth Yahweh.
Ngakhale Babuloni atadzikweza mpaka mlengalenga ndi kulimbitsa nsanja zake, ndidzatuma anthu owononga kudzamenyana naye,” akutero Yehova.
54 A voice of outcry from Babylon! And a great crash from the land of the Chaldeans!
“Imvani mfuwu wolira kuchokera ku Babuloni. Imvani phokoso lachiwonongeko chachikulu kuchokera mʼdziko la Babuloni.
55 For, Yahweh, is spoiling Babylon, And will destroy out of her the loud voice, —Though their waves have roared like many waters, Been uttered the loud boast of their voice.
Pakuti Yehova akuwononga Babuloni, ndipo akuthetsa phokoso lake lalikulu. Mfuwu wa adani ukumveka ngati mkokomo wa madzi ambiri. Phokoso lawo likunka likwererakwerera.
56 For there hath come upon her—upon Babylon—a spoiler, And captured are their heroes And broken are their bows, —For, a GOD of recompenses, is Yahweh, He will surely repay.
Pakuti wowononga wafika kudzamenyana ndi Babuloni, ankhondo ake agwidwa, ndipo mauta awo athyoka. Paja Yehova ndi Mulungu wobwezera chilango; adzabwezera kwathunthu.
57 Then will I make drunk—Her princes and her wise men, Her governors, and her deputies and her heroes, And they shall sleep an age-abiding sleep, and not wake, —Declareth the King, Yahweh of hosts, is his name.
Ndidzaledzeretsa akuluakulu ake pamodzi ndi anzeru ake, abwanamkubwa ake, atsogoleri a ankhondo pamodzinso ndi ankhondo; adzagona kwamuyaya osadzukanso,” akutero Mfumu, amene dzina lake ndi Yehova Wamphamvuzonse.
58 Thus, saith Yahweh of hosts—The broad walls of Babylon, shall be laid utterly bare, And, her lofty gates, with fire, shall be burned, —And peoples shall labour for emptiness, And populations, for the fire, shall weary themselves.
Yehova Wamphamvuzonse akuti, “Malinga aakulu a Babuloni adzasalazidwa ndipo zipata zake zazitali zidzatenthedwa; mitundu ya anthu inangogwira ntchito pachabe. Anthu anatopa ndi kumanga zimene tsopano zikupsa ndi moto.”
59 The word which Jeremiah the prophet commanded Seraiah son of Neriah son of Mahseiah, when he went with Zedekiah king of Judah into Babylon, in the fourth year of his reign, —now Seraiah, was travelling-marshal.
Zedekiya mfumu ya Yuda inali ndi phungu wake wamkulu amene dzina lake linali Seraya mwana wa Neriya chidzukulu cha Maseya. Mʼchaka chachinayi cha ulamuliro wake, Zedekiya anapita ndi Seraya ku Babuloni. Tsono mneneri Yeremiya anamupatsirako uthenga Serayayo.
60 So Jeremiah wrote all the calamity which was to come unto Babylon in one scroll; even all these words which have been written against Babylon.
Yeremiya anali atalemba mʼbuku za masautso onse amene adzafike pa Babuloni ndi zina zonse zokhudza Babuloni.
61 Then said Jeremiah unto Seraiah, —When thou comest into Babylon, then shalt thou look out and read all these words;
Yeremiya anawuza Seraya kuti, “Ukakafika ku Babuloni, ukaonetsetse kuti wawawerengera anthu onse mawu onsewa.
62 and thou shalt say—O Yahweh! thou, thyself, hast spoken against this place to cut it off, That there be in it no inhabitant Neither man nor beast, —But desolations age-abiding, shall it become!
Ndipo ukanene kuti, ‘Inu Yehova, mwanena kuti mudzawononga malo ano, kotero kuti simudzatsala munthu kapena nyama mʼdziko muno; lidzakhala chipululu mpaka muyaya.’
63 And it shall be when thou hast made an end of reading this scroll, that thou shalt bind thereunto a stone, and cast it in the midst of the Euphrates,
Ukakatha kuwerenga bukuli, ukalimangirire ku mwala ndipo ukaliponye pakati pa mtsinje wa Yufurate.
64 Then shalt thou say, —In like manner, shall Babylon sink and not rise Because of the calamity which I am about to bring thereupon: So shall they perish. Thus far, are, the words of Jeremiah.
Ndipo ukanene kuti, ‘Umu ndi mmene adzamirire Babuloni ndipo sadzadzukanso chifukwa cha masautso amene adzamugwere.’” Mawu a Yeremiya athera pamenepa.

< Jeremiah 51 >