< Jeremiah 43 >

1 And it came to pass, when Jeremiah had made an end of speaking unto all the people all the words of Yahweh their God, with which Yahweh their God had sent him unto them, —even all these words,
Yeremiya atatsiriza kuwawuza anthuwo mawu onse a Yehova Mulungu wawo, amene Yehova anamutuma kuti akawawuze,
2 then spake Azariah son of Hoshaiah, and Johanan son of Kareah, and all the proud men, —saying unto Jeremiah—Falsely, art thou speaking, Yahweh our God hath not sent thee to say, Ye shall not enter Egypt to sojourn there;
Azariya mwana wa Hosayia ndi Yohanani mwana wa Kareya pamodzi ndi anthu onse odzikuza anawuza Yeremiya kuti, “Ukunama iwe! Yehova Mulungu wathu sanakutume kuti unene kuti, ‘Musapite ku Igupto kukakhala kumeneko.’
3 but Baruch son of Neriah, is goading thee on against us, —that he may deliver us into the hand of the Chaldeans, to put us to death, or take us away captive to Babylon.
Koma ndi Baruki mwana wa Neriya amene akukulimbikitsa kuti utiletse zopita ku Igupto ndi kuti mʼmalo mwake tidzipereke mʼmanja mwa Ababuloni, kuti iwo atiphe kapena kutitenga ukapolo ku Babuloni.”
4 So Johanan son of Kareah, and all the captains of the forces and all the people, hearkened not, unto the voice of Yahweh, —by remaining in the land of Judah;
Motero Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo pamodzi ndi anthu onse sanamvere lamulo la Yehova loti akhale mʼdziko la Yuda.
5 but Johanan son of Kareah and all the captains of the forces took all the remnant of Judah, who had returned, out of all the nations whither they had been driven to sojourn in the land of Judah:
Mʼmalo mwake, Yohanani mwana wa Kareya ndi atsogoleri onse a ankhondo anatenga anthu onse otsala a ku Yuda amene anabwera kudzakhala mʼdziko la Yuda kuchokera ku mayiko onse kumene anabalakirako.
6 both the men and the women and the children, and the daughters of the king, and every soul that Nebuzaradan chief of the royal executioners had left, with Gedaliah son of Ahikam son of Shaphan, —and Jeremiah the prophet, and Baruch son of Neriah;
Mʼgulu la anthu otengedwalo munali amuna onse, akazi ndi ana, ana aakazi a mfumu, ndiponso anthu amene Nebuzaradani mtsogoleri wa asilikali olonda mfumu anawasiya kwa Gedaliya mwana wa Ahikamu, mdzukulu wa Safani pamodzinso ndi mneneri Yeremiya ndi Baruki mwana wa Neriya.
7 and entered the land of Egypt, for they hearkened not unto the voice of Yahweh, —yea entered as far as Tahpanhes.
Kotero anthuwo analowa mʼdziko la Igupto chifukwa anakana kumvera Yehova, nakafika ku Tapanesi.
8 Then came the word of Yahweh unto Jeremiah, in Tahpanhes, saying:
Ndipo Yehova anayankhula ndi Yeremiya ku Tapanesi kuti,
9 Take in thy hand great stones and hide them in the mortar that is in the brickyard which is at the entrance of the house of Pharaoh in Tahpanhes, —before the eyes of the men of Judah.
“Tenga miyala inayi yayikulu ndipo uyikwirire mʼdothi pa chiwundo cha polowera ku nyumba yaufumu ya Farao ku Tapanesi. Uchite zimenezi Ayuda onse akuona.
10 Then shalt thou say unto them—Thus, saith Yahweh of hosts, God of Israel—Behold me! sending and fetching Nebuchadrezzar king of Babylon, my servant, and I will set his throne over these stones which I have hid, —and he shall spread his canopy over them.
Ndipo uwawuze kuti, ‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Ndidzayitana mtumiki wanga Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, ndipo adzakhazika mpando wake waufumu pa miyala imene ndayikwirira apayi. Iye adzafunyulula tenti yake yaufumu pa miyala imeneyi.
11 And when he entereth, then will he smite the land of Egypt and deliver Him who is for death to death and Him who is for captivity to captivity, and Him who is for the sword to the sword.
Iye adzabwera kudzathira nkhondo Igupto. Iwo oyenera kufa ndi mliri adzafa ndi mliri, iwo oyenera kutengedwa ukapolo adzatengedwa ukapolo, ndipo iwo oyenera kufa ndi lupanga adzafa ndi lupanga.
12 So will I kindle a fire in the houses of the gods of Egypt, and he shall burn them and carry them away Captive, —and shall wrap the land of Egypt about him, just as a shepherd, wrappeth about, him his garment, and shall go forth from thence in peace;
Adzayatsa moto mʼnyumba zopembedzera milungu ya Igupto. Adzayeretsa dziko la Igupto monga momwe mʼbusa amayeretsera chovala chake pochotsamo nsabwe. Pambuyo pake adzachoka mʼdziko la Igupto mwa mtendere.
13 And he shall break in pieces the pillars of Beth-shemesh, which is in the land of Egypt, —And the houses of the gods of Egypt, shall he burn with fire.
Ku Iguptoko adzagwetsa zipilala zachipembedzo za ku nyumba yopembedzera mulungu wa dzuwa. Adzatentha ndi moto nyumba za milungu ya ku Igupto.’”

< Jeremiah 43 >