< Jeremiah 38 >
1 And, when Shephatiah son of Mattan and Gedaliah son of Pashhur and Jucal son of Shelemiah, and Pashhur son of Malchiah, heard the words which Jeremiah was speaking unto all the people saying:
Sefatiya mwana wa Matani, Gedaliya mwana wa Pasi-Huri, Yukali mwana wa Selemiya, ndi Pasi-Huri mwana wa Malikiya anamva zimene Yeremiya ankawuza anthu onse kuti,
2 Thus saith Yahweh, He that remaineth in this city shall die, by sword by famine, or by pestilence, —whereas, he that goeth forth unto the Chaldeans, shall live, so shall he have his life for a spoil, and shall live.
“Yehova akuti, ‘Aliyense amene akhale mu mzinda muno adzafa ndi nkhondo njala kapena mliri. Koma aliyense amene atatuluke kukadzipereka kwa Ababuloni adzapulumutsa moyo wake; iyeyo adzakhala ndi moyo.
3 Thus, saith Yahweh, —This city shall surely be given, into the hand of the force of the king of Babylon, and he shall capture it.
Mzinda uno udzaperekedwa ndithu kwa gulu lankhondo la mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulande.’”
4 Then said the princes unto the king, —Let this man we pray thee, be put to death, for in this way, is he weakening the hands of the men of war who are left in this, city, and the hands of all the people, by speaking unto them such words as these; for, this man, is not seeking prosperity for this people but misfortune.
Tsono akuluakuluwo anawuza mfumu kuti, “Munthu uyu ayenera kuphedwa. Iye akutayitsa mtima asilikali pamodzi ndi anthu onse amene atsala mu mzinda muno, chifukwa cha zimene akuwawuza. Munthu ameneyu sakufunira zabwino anthuwa koma chiwonongeko chawo.”
5 Then said King Zedekiah, —Lo! he is in your hand; for the king is not one who is able to do anything against you.
Mfumu Zedekiya anayankha kuti, “Munthuyu ali mʼmanja mwanu. Ine sindingakuletseni chimene mukufuna kumuchitira.”
6 Then took they Jeremiah and cast him into the dungeon of Malchiah son of the king, which was in the guard-court, and they let Jeremiah down with ropes, —now, in the dungeon, was no water only mire, so Jeremiah sank in the mire.
Choncho iwo anatenga Yeremiya nakamuponya mʼchitsime cha Malikiya, mwana wa mfumu, chimene chinali mʼbwalo la alonda. Iwo anamutsitsira mʼdzenjemo ndi chingwe. Munalibe madzi koma matope okhaokha, ndipo Yeremiya anamira mʼmatopewo.
7 When Ebed-melech the Ethiopian one of the eunuchs, he being in the house of the king, heard that they had delivered Jeremiah into the dungeon, —the king being seated in the gate of Benjamin,
Koma Ebedi-Meleki, Mkusi, mmodzi mwa anthu ofulidwa ogwira ntchito mʼnyumba ya mfumu, anamva kuti Yeremiya anamuponya mʼchitsime. Nthawi imeneyo nʼkuti mfumu ili ku chipata cha Benjamini.
8 then went forth Ebed-melech out of the house of the king, and spake unto the king, saying:
Ebedi-Meleki anatuluka ku nyumba ya mfumu kukayiwuza kuti,
9 My lord, O King! wickedly, have these men done all that they have done to Jeremiah the prophet, whom indeed they have cast into the dungeon, —since he would have died where he was because of the famine, for there is no bread any longer, in the city.
“Mbuye wanga mfumu, zimene anthu awa amuchitira mneneri Yeremiya ndi zoyipa kwambiri. Iwo amuponya mʼchitsime, ndipo adzafa ndi njala chifukwa buledi watha mu mzinda muno.”
10 Then the king commanded Ebed-melech the Ethiopian saying, —Take with thee from hence thirty men, and lift Jeremiah the prophet out of the dungeon before he die.
Tsono mfumu inalamula Ebedi-Meleki, Mkusi, kuti, “Tenga anthu makumi atatu, ndipo mukamutulutse mʼchitsimemo mneneri Yeremiya asanafe.”
11 So Ebed-melech took the men with him, and went into the house of the king under the treasury, and took thence pieces of cast-off clothes, and old rags, —and let them down unto Jeremiah in the dungeon with the ropes.
Pamenepo Ebedi-Meleki anatenga anthuwo, napita nawo ku nyumba ya mfumu ya pansi pa chipinda chosungiramo chuma. Kumeneko anakatengako sanza ndipo anatsitsira sanzazo ndi chingwe mʼchitsime mʼmene munali Yeremiya.
12 Then said Ebed-melech the Ethiopian unto Jeremiah, —Put, I pray thee the pieces of cast-off clothes and the old rags under thine arm-joints, under the ropes, And Jeremiah did so,
Ebedi-Meleki, Mkusi, anawuza Yeremiya kuti, “Ika sanzazo mkwapa mwako kuti zingwe zingakupweteke.” Yeremiya anachitadi zimenezi,
13 Then drew they Jeremiah with the ropes, and lifted him up out of the dungeon, —and Jeremiah remained in the guard-court.
ndipo anamukoka ndi zingwe ndi kumutulutsa mʼchitsimecho. Ndipo Yeremiya anakhalabe ku bwalo la alonda.
14 Then King Zedekiah sent and fetched Jeremiah the prophet unto him, in the third entrance, which is in the house of Yahweh, —and the king said unto Jeremiah—I am going to ask thee a thing, do not hide anything from me.
Tsiku lina Mfumu Zedekiya anayitana mneneri Yeremiya ndipo anabwera naye ku chipata chachitatu cha Nyumba ya Yehova. Mfumu inawuza Yeremiya kuti, “Ndikufuna kukufunsa kanthu kena, ndipo usandibisire chilichonse.”
15 Then said Jeremiah unto Zedekiah, When I tell thee, wilt thou not, surely put me to death? And when I counsel thee, thou wilt not hearken unto me.
Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Ndikakuyankhani, kodi simundipha? Ngakhaletu ine nditakulangizani, inu simudzandimvera.”
16 So King Zedekiah aware unto Jeremiah secretly saying, —By the life of Yahweh who made for us, this soul, I will in no wise put thee to death, Neither will I deliver thee into the hand of these men who are seeking thy life.
Koma Mfumu Zedekiya mwachinsinsi inalumbira kwa Yeremiya kuti, “Pali Yehova wamoyo, amene amatipatsa moyo, sindidzakupha ngakhalenso kukupereka kwa amene akufuna kukuphawa.”
17 Then said Jeremiah unto Zedekiah—Thus, saith Yahweh God of hosts, God of Israel—If thou wilt, indeed go forth, unto the princes of the king of Babylon, then shall thine own soul live, and, this city, shall not be burned with fire, —but thou shalt live, thou and thy house.
Pamenepo Yeremiya anati kwa Zedekiya, “Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti, ‘Ngati mutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mudzakhala ndi moyo ndipo mzinda uno sadzawutentha, inu pamodzi ndi banja lanu mudzakhala ndi moyo.
18 But, if thou wilt not go forth unto the princes of the king of Babylon, then shall this city be delivered into the hand of the Chaldeans, and they shall burn it with fire, and, thou, shalt not escape out of their hand.
Koma ngati simutuluka kukadzipereka kwa ankhondo a mfumu ya ku Babuloni, mzinda uno udzaperekedwa kwa Ababuloni ndipo adzawutentha; inuyo simudzapulumuka mʼdzanja mwawo.’”
19 Then said King Zedekiah unto Jeremiah: I am afraid of the Jews who have fallen away unto the Chaldeans, lest they deliver me, into their hand, and they maltreat me.
Mfumu Zedekiya inati kwa Yeremiya, “Ine ndikuopa Ayuda amene anathawira kale kwa Ababuloni, pakuti mwina Ababuloniwo adzandipereka kwa Ayudawo ndipo iwowo adzandizunza.”
20 But Jeremiah said, They shall not deliver!—Hearken I pray thee unto the voice of Yahweh in what I am speaking unto thee, that it may be well with thee and thy soul live.
Yeremiya anayankha kuti, “Ngati mumvera Yehova ndi kuchita zimene ndakuwuzani, ndiye kuti zinthu zidzakuyenderani bwino. Inu simudzaphedwa.
21 But if thou art refusing to go forth, this, is the thing which Yahweh hath shewed me: —
Koma mukakana kudzipereka, chimene Yehova wandiwululira ndi ichi:
22 behold, then, all the women that are left in the house of the king of Judah, brought forth unto the princes of the king of Babylon, —and, those very women, saying, The men thou wast wont to salute, have goaded thee on and prevailed upon thee, —Thy foot having sunk in the mire, they have turned away back.
Akazi onse amene atsala mʼnyumba ya mfumu ya Yuda adzaperekedwa kwa akuluakulu a mfumu ya ku Babuloni. Akazi amenewo adzakuwuzani kuti, “‘Abwenzi ako okhulupirika aja anakusokeretsa, ndipo anakugonjetsa. Poti tsopano miyendo yako yazama mʼmatope; abwenzi ako aja akusiya.’
23 Yea thou shalt behold all thy wives and thy children brought forth unto the Chaldeans, and thou, shalt not escape out of their hand, —but by the hand of the king of Babylon, shalt thou be taken, and, this city, shall be burned with fire.
“Akazi pamodzi ndi ana anu adzaperekedwa kwa Ababuloni. Inuyo simudzapulumuka mʼmanja mwawo koma mfumu ya ku Babuloni idzakugwirani; mzinda uno adzawutentha.”
24 Then said Zedekiah unto Jeremiah—Do not let, any man, know of these words, and thou shalt not die.
Pamenepo Zedekiya anati kwa Yeremiya, “Usawuze munthu wina aliyense zimene takambiranazi, ukatero udzaphedwa.
25 But, when the princes hear that I have spoken with thee and they come in unto thee and say unto thee—Do tell us we pray thee what thou didst speak unto the king, do not hide it from us so will we not put thee to death, —and what spake the king unto, thee?
Akuluakulu akamva kuti ndinayankhula nawe ndipo akabwera kwa iwe nʼkudzakufunsa kuti, ‘Tiwuze zimene unanena kwa mfumu ndi zimene mfumu inanena kwa iwe; usatibisire, ukatero tidzakupha,’
26 Then shalt thou say unto them, —I was causing my supplication to fall prostrate before the king, —that he would not cause me to return to the house of Jonathan, to die there.
udzawawuze kuti, ‘Ine ndimapempha mfumu kuti isandibwezerenso ku nyumba ya Yonatani kuti ndikafere kumeneko.’”
27 Then came in all the princes unto Jeremiah and asked him, and he told them according to all these words which the king, had commanded, —so they turned in silence from him, for the matter, had not been reported.
Akuluakulu onse anabweradi kwa Yeremiya kudzamufunsa. Iye anawayankha monga momwe mfumu inamulamula. Choncho palibe amene ananenanso kanthu, pakuti palibe amene anamva zomwe anakambirana ndi mfumu.
28 So Jeremiah remained in the guard-court, until the day when Jerusalem, was captured; thus it fell out when Jerusalem, was captured.
Ndipo Yeremiya anakhalabe mʼbwalo la alonda mpaka tsiku limene mzinda wa Yerusalemu unalandidwa.