< Jeremiah 32 >

1 The word which came unto Jeremiah from Yahweh, in the tenth year of Zedekiah king of Judah, —the same, was the eighteenth year of Nebuchadrezzar;
Yehova anayankhula ndi Yeremiya mʼchaka chakhumi cha Zedekiya mfumu ya Yuda, chimene chinalinso chaka cha 18 cha ulamuliro wa Nebukadinezara.
2 and, then, the forces of the king of Babylon were besieging Jerusalem, —and, Jeremiah the prophet, had been shut up in the guard-court, which was in the house of the king of Judah;
Pa nthawi imeneyi nʼkuti ankhondo a mfumu ya ku Babuloni atazinga Yerusalemu, ndipo mneneri Yeremiya ndiye anamutsekera mʼbwalo la alonda mʼnyumba yaufumu ya ku Yuda.
3 whom Zedekiah king of Judah, had shut up, saying, —Why art thou prophesying, saying, —Thus, saith Yahweh, Behold me! giving up this city into the hand of the king of Babylon, and he shall capture it;
Tsono Zedekiya mfumu ya Yuda nʼkuti itamutsekera mʼmenemo, ndipo inati, “Nʼchifukwa chiyani ukulosera motero? Iwe ukunena kuti, ‘Yehova akuti: Ndidzapereka mzinda uno kwa mfumu ya ku Babuloni, ndipo idzawulanda.
4 and, Zedekiah king of Judah! shall not be delivered out of the hand of the Chaldeans, —for he shall be wholly given up, into the hand of the king of Babylon, and shall speak—the mouth of the one to the mouth of the other, and the eyes of the one into the eyes of the other, shall look;
Zedekiya mfumu ya Yuda sidzapulumuka mʼmanja mwa Ababuloni, koma idzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni. Adzayankhula naye ndi kuonana naye maso ndi maso.
5 and into Babylon, shall he lead Zedekiah and, there, shall he remain, until I visit him, Declareth Yahweh, —though ye fight with the Chaldeans, ye shall not prosper?
Zedekiya adzatengedwa kupita naye ku Babuloni, kumene adzakhale mpaka nditamukhawulitsa, akutero Yehova. Ngakhale iye adzamenyane ndi Babuloni, koma sadzapambana.’”
6 And Jeremiah said, —The word of Yahweh came unto me saying:
Yeremiya anati, “Yehova wandiwuza kuti:
7 Lo! Hanameel son of Shallum thine uncle, hath come unto thee saying, —Buy thee my field that is in Anathoth, for, thine, is the right of redemption to buy it.
Taonani, Hanameli mwana wa Salumu, amalume ako akubwera ndipo adzakuwuza kuti, ‘Gula munda wanga wa ku Anatoti, chifukwa iwe ndiwe mʼbale wanga ndipo ndiwe woyenera kuwuwombola.’”
8 So Hanameel son of mine uncle, came unto me, according to the word of Yahweh into the guard-court, and said unto me, Buy, I pray thee my field that is in Anathoth which is in the land of Benjamin, for, thine, is the right of inheritance, and, thine, the redemption, —buy it for thyself. So I knew, that the word of Yahweh, it was.
Ndipo monga momwe Yehova ananenera, Hanameli, msuweni wanga anabweradi ku bwalo la alonda ndipo anati, “Gula munda wanga wa ku Anatoti mʼdziko la Benjamini. Popeza ndiwe woyenera kuwugula ndi kukhala wako, gula munda umenewu kuti ukhale wako.” “Ine ndinadziwa kuti amenewa anali mawu a Yehova aja;
9 And I bought the field from Hanameel son of mine uncle that was in Anathoth, —and weighed him the silver, seventeen shekels, was the silver;
choncho ndinagula munda wa ku Anatoti kwa Hanameli msuweni wanga, ndipo ndinamupatsa masekeli asiliva 17.
10 and I wrote in the scroll and sealed it, and took in attestation witnesses, —and weighed the silver in the balances.
Ndinasayina panganolo ndikulimata pamaso pa mboni, kenaka ndinayeza ndalama zasilivazo pa sikelo.”
11 Then took I the scroll of purchase, both that which was sealed—the title and the conditions—and that which was open;
Pambuyo pake ndinatenga makalata anga a pangano, imodzi yomatidwa mʼmene munali malamulo onse a panganolo ndi ina yosamatidwa.
12 and gave the scroll of purchase unto Baruch son of Neriah son of Mahseiah, in the sight of Hanameel mine uncle[’s son], and in the sight of the witnesses who subscribed the scroll of purchase, —in the sight of all the Jews who were sitting in the guard-court.
Ndinapereka makalatawo kwa Baruki mwana wa Neriya, mdzukulu wa Maseya pamaso pa Hanameli msuweni wanga, pamaso pa mboni zimene zinasayina panganoli ndiponso pamaso pa Ayuda onse okhala mʼbwalo la alonda.
13 Then charged I Baruch in their sight saying:
“Ndinamulangiza Baruki pamaso pa onsewo kuti,
14 Thus, saith Yahweh of hosts, God of Israel, Take thou these scrolls, this scroll of purchase even that which is sealed, and this scroll that is open, and put them in an earthen vessel, —that they may remain many days,
‘Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Tenga makalata awa a umboni wapangano, iyi yokhala ndi chizindikiro ndi yopanda chizindikiro, uwasunge mʼmbiya kuti akhale nthawi yayitali.
15 For Thus, saith Yahweh of hosts, God of Israel: Again, shall houses and fields and vineyards, be bought, in this land.
Pakuti Yehova Wamphamvuzonse, Mulungu wa Israeli akuti: Anthu adzagulanso nyumba, minda ndi mitengo yamphesa mʼdziko lino.’”
16 Then prayed I unto Yahweh, —after I had delivered the scroll of purchase unto Baruch son of Neriah, saying: —
Nditamupatsa makalata a panganowa Baruki mwana wa Neriya, ndinapemphera kwa Yehova:
17 Alas! My Lord, Yahweh! Lo! thou thyself, didst make the heavens, and the earth, by thy great might, and by thine outstretched arm, —There is nothing, too wonderful for thee:
“Aa, inu Ambuye Yehova, munalenga dziko lakumwamba ndi dziko lapansi. Munazilenga ndi dzanja lanu lamphamvu ndipo palibe chokulakani.
18 Executing lovingkindness unto thousands, But recompensing the iniquity of fathers, into the bosom of their children, after them, Thou GOD, the great the mighty, Yahweh of hosts, is his name:
Mumaonetsa chikondi chanu kwa anthu osawerengeka koma mumalanga ana chifukwa cha machimo a makolo awo. Inu ndinu Mulungu Wamkulu ndi Wamphamvu. Dzina lanu ndinu Yehova Wamphamvuzonse.
19 Great in counsel, and mighty in deed, —Whose eyes are open on all the ways of the sons of men, to give unto every one, According to his ways, and According to the fruit of his doings:
Zolinga zanu ndi zazikulu ndipo zochita zanu ndi zamphamvu. Maso anu amaona zonse zimene anthu amachita. Mumapereka mphotho kwa munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndi ntchito zake.
20 Who didst set signs and wonders, in the land of Egypt, unto this day, and in Israel and among mankind, —And didst make for thyself a name as at this day;
Inu munachita zizindikiro zozizwitsa ku Igupto, ndipo mwakhala mukuzichita mpaka lero, pakati pa Aisraeli ndiponso pakati pa anthu onse. Choncho mwadzitchukitsa mpaka lero lino.
21 And didst bring forth thy people Israel out of the land of, Egypt, With signs and with wonders, and With a strong hand, and With an outstretched arm, and With great terror;
Munatulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto ndi dzanja lanu lamphamvu pochita zizindikiro zozizwitsa ndi zodabwitsa zimene zinaopseza adani anu.
22 And didst give unto them this land, which thou hadst sworn to their fathers to give unto them, —a land flowing with milk and honey;
Munawapatsa dziko lino limene munalonjeza mwalumbiro kulipereka kwa makolo awo, dziko loyenda mkaka ndi uchi.
23 And they came in and took possession of it But hearkened not unto thy voice Nor in thy law, did they walk, Nought of what thou hadst commanded them to do, did they do, —And so thou hast caused to befall them all this calamity.
Iwo analowa nʼkulitenga kukhala lawo, koma sanamvere Inu kapena kutsatira lamulo lanu; ndipo sanachite zomwe munawalamula. Choncho inu mwawagwetsera masautso onsewa.”
24 Lo! the earthworks! they have entered the city, to capture it, And the city, hath been given into the hand of the Chaldeans, who are fighting against it, because of the sword and the famine and the pestilence, —And so what thou didst speak, hath come to pass, And there thou art looking on!
“Onani momwe adani azingira ndi mitumbira yankhondo mzindawu kuti awulande ndipo akuwuthira nkhondo. Chifukwa cha lupanga, njala ndi mliri. Mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni anthu atafowoka ndi nkhondo, njala ndi mliri. Zimene munkanena zija zachitikadi monga mukuzionera tsopano.
25 Yet, thou thyself, saidst unto me, O My Lord, Yahweh, Buy thee the field for silver And take in attestation, witnesses, —Whereas, the city, hath been given into the hand of the Chaldeans!
Ngakhale mzindawu udzaperekedwa kwa Ababuloni, komabe Inu Ambuye Yehova, munandiwuza kuti, ‘Gula munda ndi siliva ndipo upereke ndalamazo pali mboni.’”
26 Then came the word of Yahweh, unto Jeremiah, saying: —
Tsono Yehova anawuza Yeremiya kuti,
27 Lo! I, am Yahweh, God of all flesh, —For me, is any thing too wonderful?
“Taonani, Ine ndine Yehova, Mulungu wa anthu onse. Kodi chilipo chinthu choti Ine nʼkundikanika?
28 Therefore, Thus, saith Yahweh, —Behold me! giving this city into the hand of the Chaldeans, and into the hand of Nebuchadrezzar king of Babylon, and he shall capture it;
Nʼchifukwa chake ine Yehova ndikuti: Ndidzawupereka mzinda uno kwa Nebukadinezara mfumu ya ku Babuloni, amene adzawulanda.
29 And the Chaldeans, who are fighting against this city, Shall enter, and Shall set this city on fire, and Shall consume it, —With the houses on whose roofs they burned incense to Baal and poured out drink-offerings to other gods, that they might provoke me to anger;
Ndipo Ababuloni amene akuwuthira nkhondo mzinda uno adzalowa ndi kuwutentha; adzatentha ndi kugwetsa nyumba zimene pa denga pake anthu ankandipsetsa mtima pofukiza lubani kwa Baala ndi popereka chopereka cha chakumwa kwa milungu ina.
30 For the sons of Israel and the sons of Judah have been nothing but doers of wickedness in my sight from the days of their youth, —For the sons of Israel have been doing nothing but provoke me to anger by the workmanship of their hands, Declareth Yahweh;
“Aisraeli ndi Ayuda akhala akuchita zoyipa zokhazokha pamaso panga kuyambira ubwana wawo. Kunena zoona Aisraeli akumandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa, akutero Yehova.
31 For According to mine anger, and According to mine indignation, hath been to me this city, from the day when they built it even unto this day, —that I should pull it down from before my face:
Kuyambira tsiku limene mzindawu unamangidwa mpaka lero, wakhala ukuwutsa mkwiyo wanga ndi ukali wanga. Nʼchifukwa chake ndiyenera kuwuchotsa pamaso panga.
32 because of all the wickedness of the sons of Israel and the sons of Judah, which they have done to provoke me to anger, they, their kings their princes, their priests, and their prophets, and the men of Judah, and the inhabitants of Jerusalem:
Aisraeli ndi Ayuda, anthu a ku Yuda ndi a ku Yerusalemu, mafumu awo, nduna zawo, ansembe ndi aneneri awo anandikwiyitsa ndi ntchito zawo zoyipa.
33 Thus have they turned unto me the back, and not the face, —Though I instructed them, betimes, instructing them, Yet have they not been hearkening, to receive correction;
Anandifulatira ndipo ngakhale ndinakhala ndikuwaphunzitsa kawirikawiri, sanamve kapena kuphunzirapo kanthu.
34 But have set their abominations in the house on which my name hath been called, to defile it;
Iwo anayika mafano awo onyansa mʼnyumba imene imadziwika ndi dzina langa ndipo anayipitsa.
35 And have built the high places of Baal, which are in the valley of Ben-hinnom, To cause their sons and their daughters to pass through unto Molech, Which I commanded them not Neither came it up on my heart, That they should do this horrible thing, —Causing, Judah, to sin!
Anamanga malo opembedzerapo Baala mʼChigwa cha Hinomu kuti aziperekapo ana awo aamuna ndi aakazi ngati nsembe kwa Moleki. Ine sindinawalamulire kutero, ndipo sindinaganizepo nʼkomwe kuti iwo angachite chinthu chonyansa chotero, ndi kuchimwitsa anthu a ku Yuda.
36 Now therefore, because of this, —Thus, saith Yahweh, God of Israel, —Concerning this city, whereof ye are saying, It hath been delivered into the hand of the king of Babylon, by sword, and by famine and by pestilence:
“Anthu ponena za mzindawu akuti udzaperekedwa kwa mfumu ya ku Babuloni mwa nkhondo, njala ndi mliri, koma Yehova Mulungu wa Israeli akuti,
37 Behold me! gathering them out of all the lands whither I have driven them—In mine anger and In mine indignation and In great vexation, —And I will cause them to return into this place, And will make them dwell, securely;
Ine ndidzawasonkhanitsadi anthuwa kuchokera ku mayiko onse kumene ndinawapirikitsira ndili wokwiya ndi waukali kwambiri. Ndidzabwera nawo ku malo ano ndipo ndidzawalola kukhala mwamtendere.
38 And they shall become my people, —And, I, will become their God;
Iwo adzakhala anthu anga, ndipo Ine ndidzakhala Mulungu wawo.
39 And I will give them one heart, and one way, That they may revere me, all the days, —For the good of them and of their children after them;
Ndidzawapatsa mtima umodzi ndi khalidwe limodzi kotero kuti azidzandiopa nthawi zonse ndipo iwo pamodzi ndi zidzukulu zawo zinthu zidzawayendera bwino.
40 And I will solemnise to them an age-abiding covenant, That I will not turn away from following them, to do them good, —But the reverence of myself, will I put in their heart, so that they shall not turn away from me.
Ndidzachita nawo pangano losatha: sindidzaleka kuwachitira zabwino, ndipo ndidzawapatsa mtima woti azidzandiopa, kuti asadzandisiyenso.
41 And I will rejoice over them, to do them good, —And will plant them in this land in truth, with all my heart and with all my soul.
Ndidzakondwera powachitira zabwino, ndipo ndidzawakhazikitsa ndithu mʼdziko lino ndi mtima wanga wonse ndi moyo wanga wonse.
42 For, Thus, saith Yahweh, Like as I have brought upon this people all this great calamity, So, am I bringing upon them all the good that I am speaking concerning them.
“Yehova akuti: Monga momwe ndinagwetsera masautso aakulu onsewa pa anthuwa, momwemonso ndidzawapatsa zinthu zonse zabwino zimene ndinawalonjeza.
43 Therefore shall fields be bought in this land, —whereof ye are saying, It is, a desolation, Without man or beast, It hath been given into the hand of the Chaldeans:
Adzagulanso minda mʼdziko muno, limene inu mukuti, ‘Ndi dziko losiyidwa, lopanda anthu kapena nyama, pakuti linaperekedwa kwa Ababuloni.’
44 Fields—for silver, shall men buy, And write in scrolls And seal them, And take in attestation, witnesses, In the land of Benjamin, and In the places round about Jerusalem, and In the cities of Judah, and In the cities of the hill country, and In the cities of the lowland and In the cities of the South, —For I will cause them of their captivity to return Declareth Yahweh.
Adzagula minda ndi ndalama zasiliva, ndipo achita pangano, ndi kumata pamaso pa mboni. Izi zidzachitika mʼdziko la Benjamini, ku malo ozungulira Yerusalemu, mʼmizinda ya Yuda, mʼmizinda ya ku mapiri, mʼmizinda ya kuchigwa ndi yakummwera ku Negevi. Zoona, ndidzabwezera ufulu wawo, akutero Yehova.”

< Jeremiah 32 >