< Jeremiah 20 >

1 And when Pashhur son of Immer, the priest, who also was deputy-overseer in the house of Yahweh, heard that Jeremiah had prophesied these things,
Wansembe Pasuri mwana wa Imeri, woyangʼanira wamkulu wa Nyumba ya Yehova, anamva Yeremiya akulosera zinthu zimenezi.
2 then Pashhur smote Jeremiah the prophet, —and put him in the stocks that were in the upper gate of Benjamin, which was in the house of Yahweh.
Tsono iye analamula kuti mneneri Yeremiyayo amenyedwe ndi kuyikidwa mʼndende pa Chipata chakumtunda kwa Benjamini ku Nyumba ya Yehova.
3 And it came to pass on the morrow, when Pashhur brought forth Jeremiah out of the stocks, —that Jeremiah said unto him—Not Pashhur, hath Yahweh called thy name, But Magor-missaviv["Terror-round-about"].
Mmawa mwake, Pasuri anatulutsa Yeremiya mʼndende, ndipo Yeremiyayo anamuwuza kuti, “Pasuri, Yehova sadzakutchulanso dzina lako kuti Pasuri koma Zoopsa pa Mbali Zonse.
4 For, Thus, saith Yahweh—Behold me! making thee a ["magor" i. e. a] terror to thyself and to all who love thee, and they shall fall by the sword of their enemies, thine own eyes also, beholding, And all Judah, will I deliver into the hand of the king of Babylon, and he will carry them captive to Babylon and smite them with the sword.
Pakuti Yehova akuti, ‘Ndidzakusandutsa choopsa kwa mwiniwakewe ndi kwa abwenzi ako onse; iweyo ukuona. Anthu a ku Yuda ndidzawapereka onse mʼmanja mwa mfumu ya ku Babuloni. Ena adzatengedwa ukapolo ku Babuloni ndipo ena adzaphedwa pa nkhondo.
5 And I will deliver up—All the wealth of this city, and All her labour, and All her precious things, —And all the treasures of the kings of Judah, will I deliver up into the hands of their enemies, and they will make of them a prey, and take them, and carry them into Babylon.
Ndidzapereka kwa adani awo chuma chonse cha mu mzinda uno, phindu lonse la ntchito yake, zinthu zake zonse za mtengowapatali ndiponso katundu yense wa mafumu a ku Yuda. Iwo adzazitenga monga zinthu zolanda ku nkhondo ndi kupita nazo ku Babuloni.
6 And, thou, Pashhur and all who are dwelling in thy house, shall go into captivity, —Yea into Babylon, shalt thou enter And there, shalt thou die And there, shalt thou be buried Thou and all who love thee, to whom thou hast prophesied falsely.
Ndipo iwe, Pasuri, pamodzi ndi onse a pa banja pako mudzapita ku ukapolo ku Babuloni. Mudzafera kumeneko ndi kuyikidwa mʼmanda, iweyo pamodzi ndi abwenzi ako amene unawalosera zabodza.’”
7 Thou didst persuade me, O Yahweh and I was persuaded, Thou didst lay firm hold on me and didst prevail, —I am become a mockery, all the day, Every one, is laughing at me.
Inu Yehova, mwandinamiza, ndipo ndinapusadi; Inu ndi wamphamvu kuposa ine ndipo munandipambana. Anthu akundinyoza tsiku lonse. Aliyense akundiseka kosalekeza.
8 For, as often as I speak, I make outcry, Violence and wasting, I proclaim, —Yea the word of Yahweh hath become to me a reproach and derision all the day
Nthawi iliyonse ndikamayankhula, ndimafuwula kunena kuti, ziwawa kuno! Tikuwonongeka! Mawu anu Yehova andisandutsa chinthu chonyozeka ndipo ndimachitidwa chipongwe tsiku lonse.
9 Therefore I say—I will not mention him Neither will I speak any more in his name, But then it becometh in my heart as a fire that burneth, Shut up in my bones, —And I am weary of restraint and cannot refrain.
Koma ndikanena kuti, “Sindidzalalikiranso za Iye kapena kuyankhulanso mʼdzina lake,” mawu anu amayaka ngati moto mu mtima mwanga, amakhaladi ngati moto wotsekeredwa mʼmafupa anga. Ndapirira kusunga mawu anu mu mtima mwanga osawatulutsa, koma sindingathe kupirirabe.
10 Because I have heard the whispering of many—"A terror round about!" Tell ye [say they], that we may tell of him, All the men I am wont to salute do watch for my halting, —Peradventure he will be persuaded, and we shall prevail over him, and take our vengeance upon him.
Ndimamva anthu ambiri akunongʼona kuti, “Zoopsa ku mbali zonse! Kamunenezeni! Tiyeni tikamuneneze!” Onse amene anali abwenzi anga akuyembekezera kuti ndigwa pansi, akumanena kuti, “Mwina mwake adzanyengedwa; tidzamugwira ndi kulipsira pa iye.”
11 But, Yahweh, is with me, as a mighty one striking terror, For this cause, shall my persecutors stumble and not prevail, —They have turned very pale, For they have not prospered, Confusion age-abiding, it shall not be forgotten!
Koma Yehova ali nane, ndiye wankhondo wamphamvu. Nʼchifukwa chake ondizunza adzalephera ndipo sadzandipambana. Adzachita manyazi kwambiri chifukwa sadzapambana. Manyazi awo sadzayiwalika konse.
12 But O Yahweh of hosts—Testing the righteous Beholding the affections and the heart, —Let me see thine avenging upon them, For unto thee, have I laid bare my cause.
Inu Yehova Wamphamvuzonse, Inu amene mumayesa anthu molungama ndipo mupenya za mu mtima mwa munthu. Ndiloleni kuti ndione kuti mwalipsira adani anga popeza ndapereka mlandu wanga kwa Inu.
13 Sing ye to Yahweh! Praise ye Yahweh! For he hath delivered the soul of the needy, out of the hand of evildoers.
Imbirani Yehova! Mutamandeni Yehova! Iye amapulumutsa wosauka mʼmanja mwa anthu oyipa.
14 Accursed, be the day on which I was born, —The day when my mother bare me, let it not be blessed!
Litembereredwe tsiku limene ndinabadwa! Tsiku limene amayi anga anandibereka lisatamandidwe!
15 Accursed, be the man who carried tidings to my father saying, There is born to thee a man-child!
Wotembereredwa munthu amene anapita kukasangalatsa abambo anga ndi uthenga woti: “Kwabadwa mwana wamwamuna!”
16 Making him very glad: Yea let that man be—as the cities which Yahweh overthrew and repented not, —And let him hear An outcry in the morning, and A war-shout at broad noon!
Munthu ameneyo akhale ngati mizinda imene Yehova anayiwononga mopanda chisoni. Amve mfuwu mmawa, phokoso la nkhondo masana.
17 Because I was not slain from the womb, —Nor did my mother become my grave, Nor was her womb great for ever!
Chifukwa sanandiphere mʼmimba, kuti amayi anga asanduke manda anga, mimba yawo ikhale yayikulu mpaka kalekale.
18 Wherefore was it—That from the womb, I came forth, to see labour and pain; and That in shame should my days be consumed!
Kodi ndinabadwira mavuto ndi chisoni kuti moyo wanga ukhale wamanyazi wokhawokha?

< Jeremiah 20 >