< Jeremiah 17 >
1 The sin of Judah, is written With a stylus of iron, With the point of a diamond: It is engraved Upon the tablet of their heart, And upon the horns of your altars;
“Tchimo la Yuda lazokotedwa ndi cholembera cha chitsulo, lalembedwa ndi msonga ya mwala wadayimondi. Uchimowo walembedwa pa mitima yawo ndiponso pa nyanga za maguwa awo.
2 So long as their sons remember their altars, and their Sacred Stems, By the green tree, —Upon the high hills,
Ngakhale ana awo amakumbukira maguwa awo ndi zoyimiritsa ngati zifanizo za mulungu wawo Asera, pa tsinde la mitengo ya masamba ambiri, pa mapiri aatali mʼdzikomo.
3 O my mountain in the field Thy substance all thy treasures, for a prey, will I give: Thy high places for sin, within all thy bounds.
Chuma chanu ndiponso katundu wanu yense ndidzazipereka kwa ofunkha kuti zikhale dipo lawo chifukwa cha machimo ochitika mʼdziko lonse.
4 So shalt thou even of thyself, suffer to rest the inheritance which I gave thee, Seeing that I will cause thee to serve thine enemies, in the land which thou knowest not; For, a fire, have ye kindled in mine anger, Unto times age-abiding, shall it burn.
Mudzataya dziko limene ndinakupatsani kuti likhale cholowa chanu. Ndidzakusandutsani akapolo otumikira adani anu mʼdziko limene inu simukulidziwa, chifukwa mwabutsa mkwiyo wanga ngati moto, ndipo udzayaka mpaka muyaya.”
5 Thus, saith Yahweh Accursed is the man—Who trusteth in a son of earth, And hath made flesh his arm, —And whose heart from Yahweh, turneth aside:
Yehova akuti, “Ndi wotembereredwa munthu amene amadalira munthu mnzake, amene amatsamira pa munthu mnzake kuti amuthandize pamene mtima wake wafulatira Yehova.
6 Therefore shall he become as a shrub in the waste plain, Neither shall he perceive when good cometh, But shall inhabit Parched places in a wilderness, A land of salt that cannot be dwelt in.
Munthuyo adzakhala ngati chitsamba mʼchipululu; iye sadzapeza zabwino. Adzakhala mʼchipululu mopanda madzi, mʼdziko lamchere limene munthu sangathe kukhalamo.
7 Blessed is the man Who trusteth in Yahweh, To whom Yahweh is his ground of confidence;
“Koma ndi wodala munthu amene amadalira Yehova, amene amatsamira pa Iye.
8 For he shall become like a tree planted by waters, And, by a stream, shall he send out his roots, Neither shall he perceive when heat cometh, But, his leaf shall continue green: Even in a year of dearth, shall he not be anxious, Neither shall he cease from bearing fruit.
Adzakhala ngati mtengo wodzalidwa mʼmphepete mwa madzi umene umatambalitsa mizu yake mʼmbali mwa mtsinje. Mtengowo suopa pamene kukutentha; masamba ake amakhala obiriwira nthawi zonse. Suchita mantha pa chaka cha chilala ndipo sulephera kubereka chipatso.”
9 Deceitful is the heart above all things And, dangerously wayward, —Who can know it?
Mtima wa munthu ndi wonyenga kupambana zinthu zonse ndipo kuyipa kwake nʼkosachizika. Ndani angathe kuwumvetsa?
10 I—Yahweh, Searching the heart, Testing the affections; And giving to every man According to his way, According to the fruit of his doings.
“Ine Yehova ndimafufuza mtima ndi kuyesa maganizo, ndimachitira munthu aliyense molingana ndi makhalidwe ake ndiponso moyenera ntchito zake.”
11 As a partridge gathereth eggs she did not lay, [So] is he that maketh riches but not with justice, —In the midst of his days, shall he leave them, And in his latter end, prove to have been base.
Munthu amene amapeza chuma mwachinyengo ali ngati nkhwali imene imafungatira mazira amene sinayikire. Pamene ali pakatikati pa moyo wake, chumacho chidzamuthera, ndipo potsiriza adzasanduka chitsiru.
12 A throne of glory, exalted from the beginning, hath been the place of our sanctuary.
Nyumba yathu yopemphereramo ili ngati mpando waufumu waulemerero wokhazikitsidwa pa phiri lalitali chiyambire.
13 Thou hope of Israel Yahweh, All who forsake thee, shall turn pale, —Yea, all who depart from me, in the ground, shall be written, For they have forsaken a fountain of living water, even Yahweh.
Inu Yehova, chiyembekezo cha Israeli, onse amene amakusiyani adzachita manyazi. Iwo amene amakufulatirani mayina awo adzafafanizika ngati olembedwa pa fumbi chifukwa anakana Yehova, kasupe wa madzi amoyo.
14 Heal thou me O Yahweh, that I may be healed, Save me that I may be saved, —For, my praise, thou art!
Inu Yehova, chiritseni, ndipo ndidzachira; pulumutseni ndipo ndidzapulumuka, chifukwa ndinu amene ndimakutamandani.
15 Lo! they, are saying unto me, —Where is the word of Yahweh? Pray thee let it come to pass!
Anthu akumandinena kuti, “Mawu a Yehova ali kuti? Zichitiketu lero kuti tizione!”
16 But as for me, I have neither forced myself away from tending the flock after thee, Nor yet for the woeful day, have I longed—thou, knowest, —That which came out of my lips, before thy face, was uttered.
Ine sindinakuwumirizeni kuti muwalange. Mukudziwa kuti ine sindilakalaka tsiku la tsoka. Zonse zimene ndinayankhula Inu mukuzidziwa.
17 Do not thou become to me a terror, —My refuge, art thou, in the day of calamity.
Musandichititse mantha; ndinu pothawira panga pa tsiku la mavuto.
18 Let my persecutors, turn pale, but let not me, turn pale, Let, them, be terrified, but let not, me, be terrified, —Bring thou upon them a day of calamity, And with a double fracture, destroy them.
Ondizunza anga achite manyazi, koma musandichititse manyazi; iwo achite mantha kwambiri, koma ine mundichotsere manthawo. Tsiku la mavuto liwafikire; ndipo muwawononge kotheratu.
19 Thus, said Yahweh unto me—Go and stand in the gate of the sons of the people, through which the kings of Judah enter in, and through which they come out, —also in all the gates of Jerusalem.
Yehova anandiwuza kuti, “Pita ukayime pa chipata chodzerapo anthu, chimene mafumu a ku Yuda amalowerapo ndi kutulukirapo. Ukayimenso pa zipata zina zonse za Yerusalemu.
20 Then shalt thou say unto them—Hear ye the word of Yahweh Ye kings of Judah and all Judah, And all ye inhabitants of Jerusalem, —who enter in through these gates:
Ukawawuze kuti, ‘Imvani mawu a Yehova, inu mafumu onse a ku Yuda ndi anthu onse a ku Yuda ndi inu nonse okhala mu Yerusalemu amene mumatulukira pa zipata izi.’
21 Thus, saith Yahweh, Take heed unto your souls, —And do not bear any burden on the sabbath day, Nor bring it in through the gates of Jerusalem, —
Yehova akuti: samalani kuti pa tsiku la Sabata musanyamule katundu kapena kulowa naye pa zipata za Yerusalemu.
22 Neither shall ye take forth any burden out of your houses on the sabbath day, Nor any manner of work, shall ye do, —But ye shall hallow the sabbath day, As I commanded your fathers.
Musalowetse katundu mʼnyumba zanu kapena kugwira ntchito pa tsiku la Sabata, koma mulipatule tsiku la Sabatalo, monga ndinalamulira makolo anu.
23 Howbeit they hearkened not, neither inclined their ear, —but stiffened their neck, that they might not hearken, neither receive correction.
Komatu iwo sanandimvere kapena kulabadira. Ndi mitima yawo yowumayo sanamvere kapena kulandira malangizo anga.
24 And it shall come to pass, —If ye will, indeed hearken, unto me Declareth Yahweh, To bring in no burden through the gates of this city, on the sabbath day, —But to hallow the sabbath day, by not doing thereon any manner of work,
Yehova akuti, ‘Muzimvera Ine ndi kuleka kulowetsa kapena kutulutsa katundu pa zipata za mzinda pa tsiku la Sabata. Muzisunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika posachita ntchito iliyonse pa tsikuli.
25 Then shall enter in through the gates of this city, Kings and princes Sitting on the throne of David, Riding in chariots and on horses They, and their princes, The men of Judah and the inhabitants of Jerusalem, And this city shall remain unto times age-abiding.
Mukatero ndiye mafumu anu amene akukhala pa mpando wa Davide adzatulukira pa zipata za mzindawu pamodzi ndi nduna zawo. Iwo pamodzi ndi nduna zawo azidzalowa atakwera magaleta ndi akavalo, akuperekezedwa ndi anthu a ku Yuda ndi amene amakhala mu Yerusalemu, ndipo mu mzinda muno mudzakhala anthu mpaka muyaya.
26 And they shall come in—Out of the cities of Judah and Out of the places round about Jerusalem, and Out of the land of Benjamin, and Out of the lowlands, and out of the hill country, and Out of the South, Bringing in ascending-offering, and peace-offering, and meal-offering, and frankincense, —Even they who bring in a thank-offering into the house of Yahweh,
Anthu adzabwera kuchokera ku mizinda ya Yuda ndi ku midzi yozungulira Yerusalemu, kuchokera ku dziko la Benjamini ndi ku mapiri a kumadzulo, kuchokera ku dziko la mapiri ndi ku Negevi. Adzabwera ndi nsembe zopsereza, nsembe zaufa ndi za chakudya, nsembe za lubani ndi zopereka zachiyamiko ku nyumba ya Yehova.
27 But, if ye will not hearken unto me—To hallow the sabbath day, And to bear no burden and bring in through the gates of Jerusalem, on the sabbath day, Then will I kindle a fire within her gates, And it shall devour the palaces of Jerusalem, And shall not be quenched.
Koma ngati simundimvera; mukapanda kusunga tsiku la Sabata kuti likhale lopatulika ndi kumanyamula katundu nʼkumalowa naye pa zipata za Yerusalemu pa tsikuli, Ine ndidzabutsa moto pa zipata za Yerusalemu. Moto umenewo udzanyeketsa nyumba zaufumu za ku Yerusalemu ndipo moto wake sudzazima.’”