< Isaiah 46 >

1 Bel, hath crouched, Nebo, is cowering, Their images, are delivered up to beast and to cattle, —The things ye carried about, are become a load, A burden, to the weary!
Beli wagwada pansi, Nebo wawerama; nyama zonyamula katundu za nyamula milungu yawo. Mafano awo asanduka katundu wolemera pa msana pa ngʼombe. Asandukadi ngati katundu pa msana pa nyama zotopa.
2 They have cowered they have crouched at once, And they cannot rescue the burden, —But their own soul, into captivity, hath departed.
Nyamazo zikuwerama ndi kufuna kugwa ndi milunguyo; sizikutha kupulumutsa katunduyo, izo zomwe zikupita ku ukapolo.
3 Hearken unto me O house of Jacob, Even all the remnant of the house of Israel, —Who have been borne from birth, Who have been carried from nativity:
Mverani Ine, Inu nyumba ya Yakobo, inu nonse otsala a mʼnyumba ya Israeli, Ine ndakhala ndi kukusamalirani kuyambira mʼmimba ya amayi anu, ndakhala ndikukunyamulani chibadwire chanu.
4 Even unto old age, I, am, the same, And unto grey hairs, I, will bear the burden, —I have made and, I, will carry, Yea, I, will bear the burden and will deliver,
Mpaka pamene mudzakalambe ndi kumera imvi ndidzakusamalirani ndithu. Ndinakulengani ndipo ndidzakunyamulani, ndidzakusamalirani ndi kukulanditsani.
5 To whom can ye liken me or make me equal? Or compare me, and we be like?
“Kodi inu mudzandifanizira ndi yani, kapena mufananitsa ndi yani? Kodi mudzandiyerekeza kapena kundifanizitsa ndi yani?
6 They who pour gold out of a purse, And who weigh silver in a balance, —Who hire a goldsmith that he may make it into a GOD, They adore, yea they bow down;
Anthu ena amakhuthula golide mʼzikwama zawo ndipo amayeza siliva pa masikelo; amalemba ntchito mʼmisiri wosula kuti awapangire mulungu, kenaka iwo amagwada pansi ndikupembedza kamulunguko.
7 They carry him about on the shoulder They bear the burden of him—and set him in his place that he may stand, —Out of his place, will he not move, —Though one even make outcry unto him, he will not answer, Out of one’s trouble, he will not save him.
Amanyamula nʼkumayenda nayo milunguyo pa mapewa awo; amayikhazika pa malo pake ndipo imakhala pomwepo. Singathe kusuntha pamalo pakepo. Ngakhale wina apemphere kwa milunguyo singathe kuyankha; kapena kumupulumutsa ku mavuto ake.
8 Remember ye this and shew yourselves men, —Bring it back, ye transgressors, to your minds;
“Kumbukirani zimenezi ndipo muchite manyazi, Muzilingalire mu mtima, inu anthu owukira.
9 Remember ye the things named in advance from age-past times, —For, I, am, The Mighty One, and there is none else, The Adorable and there is none like me!
Kumbukirani zinthu zakale zinthu zamakedzana; chifukwa Ine ndine Mulungu ndipo palibe wina ofanana nane.
10 Declaring from the beginning, the latter end, And from olden time, that which had never been done, —Saying My purpose shall stand, and All my pleasure, will I perform;
Ndinaneneratu zakumathero kuchokera pachiyambi pomwe. Kuyambira nthawi yamakedzana ndinaloseratu zoti zidzachitike. Ndikanena zimene ndifuna kuchita ndipo zimachitikadi. Chilichonse chimene ndafuna ndimachichita.
11 Calling, From the East, a Bird of Prey, From a far country, the Man I intended, —Yea I have spoken I will also bring it to pass, I have planned, I will also do it.
Ndikuyitana chiwombankhanga kuchokera kummawa. Ndikuyitana kuchokera ku dziko lakutali munthu amene adzakwaniritsa cholinga changa. Zimene ndanena ndidzazikwaniritsadi; zimene ndafuna ndidzazichitadi.
12 Hearken unto me, Ye valiant of heart, —Who are far away from righteousness:
Ndimvereni, inu anthu owuma mtima, inu amene muli kutali ndi chipulumutso.
13 I have brought near my righteousness. It shall not be far away, And my deliverance, shall not linger, —But I will give In Zion, deliverance, To Israel, my glory.
Ndikubweretsa pafupi tsiku la chipulumutso changa; sichili kutali. Tsikulo layandikira ndipo sindidzachedwa kukupulumutsani ndi kupereka ulemerero wanga kwa Israeli.

< Isaiah 46 >