< Isaiah 45 >

1 Thus, saith Yahweh, to his Anointed, to Cyrus—Whose right hand I have firmly grasped To subdue before him, nations, And the loins of kings, will I ungird, —To open, before him, the two-leaved doors, And, the gates, shall not be shut:
Yehova akuyankhula ndi wodzozedwa wake Koresi amene anamugwira dzanja lamanja kuti agonjetse mitundu ya anthu ndi kuwalanda mafumu zida zawo zankhondo, ndi kutsekula zitseko kuti zipatazo zisadzatsekedwenso ndi ichi:
2 I, before thee, will go, And the hills, will I level—The doors of bronze, will I break in pieces, And the bars of iron, will I cut asunder;
Ine ndidzayenda patsogolo pako, ndi kusalaza mapiri; ndidzaphwanya zitseko za mkuwa ndi kuthyola mipiringidzo ya chitsulo.
3 Then will I give thee The treasures of darkness, Even the hoards of hidden places, —That thou mayest get to know That I—Yahweh, who am calling thee by thy name, am the God of Israel.
Ndidzakupatsa chuma chobisika mu mdima, katundu wa pamalo obisika, kotero kuti udziwe kuti Ine ndine Yehova Mulungu wa Israeli, amene ndakuyitana pokutchula dzina.
4 For the sake of my servant Jacob, Even Israel my chosen Therefore have I called unto thee by thy name, I give thee a title though thou hast not known me, —
Chifukwa cha mtumiki wanga Yakobo, chifukwa cha wosankhidwa wanga Israeli, Ine ndakuyitana pokutchula dzina ndipo ndakupatsa dzina laulemu ngakhale iwe sukundidziwa Ine.
5 I, am Yahweh, and there is none else, Besides me, there is no God, —I gird thee, though thou hast not known me:
Ine ndine Yehova ndipo palibenso wina; kupatula Ine palibenso Mulungu wina. Ndidzakupatsa mphamvu, ngakhale sukundidziwa Ine,
6 That men may get to know. From the rising of the sun And from the west. That there is none besides me, —I, am Yahweh, and there is none else:
kotero kuti kuchokera kummawa mpaka kumadzulo anthu adzadziwa kuti palibe wina koma Ine ndekha. Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
7 Forming light and creating darkness, Making prosperity, and creating misfortune, —I—Yahweh, who doeth all these.
Ndimalenga kuwala ndi mdima, ndimabweretsa madalitso ndi tsoka; ndine Yehova, amene ndimachita zonsezi.
8 Let the drops fall ye heavens, from above, Yea, let, the skies, pour down righteousness, —Let the earth open and let them bear as their fruit—deliverance And let, justice, spring forth therewith, I—Yahweh, have created it.
“Iwe thambo gwetsa mvula kuchokera kumwamba; mitambo ivumbwe mivumbi ya chilungamo. Dziko lapansi litsekuke, ndipo chipulumutso chiphuke kuti chilungamo chimereponso; Ine Yehova, ndine ndalenga zimenezi.
9 Alas for him who contendeth with his Fashioner, —A potsherd, [should contend] with the potsherds of the ground! Shall it be said by the clay, unto him that is fashioning it, What wouldst thou make? Or, thy work say, of thee, He hath no hands?
“Tsoka kwa wokangana ndi mlengi wake, ngakhale kuti ali ngati phale chabe pakati pa mapale anzake. Kodi dongo lingafunse munthu wowumba kuti, ‘Kodi ukuwumba chiyani?’ Kodi ntchito yako inganene kuti, ‘Ulibe luso?’
10 Alas, for one who saith to a father, What begettest thou? Or to a woman What dost thou bring forth?
Tsoka kwa wofunsa abambo ake kuti, ‘Kodi munabereka chiyani?’ Kapena amayi ake kuti, ‘Kodi mufuna kubereka chiyani?’
11 Thus, saith, Yahweh, The Holy One of Israel And his Fashioner, As to things to come, they have asked me, Concerning my sons and concerning the work of my hands, they would command me!
“Yehova Woyerayo wa Israeli, ndiponso Mlengi wake akunena, zokhudza zinthu zimene zikubwera ndi izi: Kodi iwe ukundifunsa za ana anga, kapena kundilamula pa zokhudza ntchito zanga?
12 I, made the earth, And man upon it, I created, —I—mine own hands, stretched out the heavens, And all their host, I commanded:
Ndine amene ndinapanga dziko lapansi ndikulenga munthu kuti akhalemo. Ine ndi manja anga ndinayalika thambo; ndimalamulira zolengedwa zonse za mlengalenga.
13 I, have roused him up in righteousness, And all his roads, will I level, —He, shall build my city, And my captives, shall he let go, Not for price, nor for bribe, Saith Yahweh of hosts.
Ndine amene ndidzawutsa Koresi kuti chilungamo changa chikwaniritsidwe: ndipo ndidzawongolera njira zake zonse. Iye adzamanganso mzinda wanga ndi kumasula anthu anga amene ali mu ukapolo, wopanda kupereka ndalama kapena mphotho, akutero Yehova Wamphamvuzonse.”
14 Thus, saith Yahweh—The produce of Egypt and the gain of Ethiopia, and the Sabeans, men of great stature, Unto thee, shall come over, And thine, shall they become, After thee, shall they journey, In chains, shall they come over, —And unto thee, shall they bow down Unto thee, shall they pray [saying], —Surely, in thee, is a GOD And there is none else—no, God!
Yehova akuti, “Chuma cha ku Igupto ndi chuma cha malonda cha Kusi chidzakhala chanu. Anthu amphamvu zawo ndi athanzi a ku Seba adzabwera kwa inu ndipo adzakhala anthu anu; iwo adzidzakutsatani pambuyo panu ali mʼmaunyolo. Adzakugwadirani ndi kukupemphani, ponena kuti, ‘Ndithudi Mulungu ali ndi inu, ndipo palibenso wina; palibenso mulungu wina.’”
15 Surely, thou, art a GOD utterly hiding thyself, —O God of Israel, able to save!
Zoonadi inu muli ndi Mulungu wobisika amene ali Mulungu ndi Mpulumutsi wa Israeli.
16 They have turned pale and even been put to shame, all of them, —Together have they gone into disgrace, have the makers of images:
Onse amene amapanga mafano adzawachititsa manyazi ndi kuwanyozetsa. Adzakhala osokonezeka maganizo.
17 Israel, hath been delivered by Yahweh, with an age-abiding deliverance, —Ye shall neither turn pale nor he put to shame, unto the ages of futurity,
Koma Yehova adzapulumutsa Israeli ndi chipulumutso chamuyaya; simudzachitanso manyazi kapena kunyozeka mpaka kalekale.
18 For, Thus, saith Yahweh, Who created the heavens God himself! Who fashioned the earth—And made it Himself, established it, …Not a waste, created he it To be dwelt in, he fashioned it, …I, am Yahweh, and there is none else:
Yehova analenga zinthu zakumwamba, Iye ndiye Mulungu; amene akulenga dziko lapansi, ndi kulikhazikitsa, sanalipange kuti likhale lopanda kanthu, koma analipanga kuti anthu akhalemo. Iyeyu akunena kuti: Ine ndine Yehova, ndipo palibenso wina.
19 Not in secret, have I spoken In a place of the earth that is dark, —I have not said unto the seed of Jacob, In a waste, seek ye me, —I, am Yahweh, Speaking the thing that is right, Declaring the things that are just.
Ine sindinayankhule mwachinsinsi, pamalo ena a mdima; Ine sindinaziwuze zidzukulu za Yakobo kuti, “Ndifunefuneni ku malo kopanda kanthu.” Ine Yehova, ndimayankhula zoona; ndikunena zolungama.
20 Assemble yourselves and come Draw near together, ye escaped of the nations, —They know not Who carry the wood of their carved image, And pray unto a GOD who cannot save.
Yehova akuti, “Sonkhanani pamodzi ndipo mubwere; yandikirani, inu amene munapulumuka pothawa nkhondo kwa anthu a mitundu ina. Ndinu opanda nzeru amene mumanyamula mafano a mitengo, amene mumapemphera kwa milungu imene singathe kupulumutsa.
21 Tell ye—and bring near, Yea let them take counsel, together, —Who let this be known aforetime. In time past, declared it? Was it not, I—Yahweh? And there is none else that is God besides me, A GOD, righteous and ready to save, There is none, besides me!
Fotokozani mlandu wanu, mupatsane nzeru nonse pamodzi. Kodi ndani ananeneratu zimenezi kalekale? Ndani anazifotokozeratu zimenezi nthawi yamakedzana? Kodi si Ineyo Yehova? Ndipo palibenso Mulungu wina kupatula Ine, Mulungu wolungama ndi Wopulumutsa, palibenso wina kupatula Ine.
22 Turn unto me—and be ye saved, all ye ends of the earth, —For, I, am GOD, and there is none else.
“Tembenukirani kwa Ine kuti mupulumuke, inu anthu onse a pa dziko lapansi, pakuti Ine ndine Mulungu ndipo palibenso wina.
23 By myself, have I sworn, Gone forth out of my mouth, is righteousness as a decree And shall not turn back, —That, unto myself, Shall bow every knee, Shall swear every tongue:
Ndalumbira ndekha, pakamwa panga patulutsa mawu owona, mawu amene sadzasinthika konse akuti, bondo lililonse lidzagwada pamaso panga; anthu onse adzalumbira potchula dzina langa.
24 Only in Yahweh—for me, Hath one said, Is there righteousness and strength, Unto him, shall come and turn pale—All who have been incensed against him:
Iwo adzanene kwa Ine kuti, ‘Chilungamo ndi mphamvu zimapezeka mwa Yehova yekha.’” Onse amene anamuwukira Iye adzabwera kwa Iye ndipo adzachita manyazi.
25 In Yahweh, shall be justified and shall boast themselves—All the seed of Israel.
Koma mwa Yehova zidzukulu zonse za Israeli zidzapambana ndi kupeza ulemerero.

< Isaiah 45 >