< Isaiah 35 >
1 Wilderness and parched land, shall be glad for them, —And the waste plain, shall exult, and blossom as the lily:
Chipululu ndi dziko lopanda madzi zidzasangalala; dziko lowuma lidzakondwa ndi kuchita maluwa.
2 It shall, blossom abundantly, and exult, Yea with exultation and shouts of triumph, The glory of Lebanon, hath been given to it, The splendour of Carmel, and Sharon, —They, shall see the glory of Yahweh, the splendour of our God.
Dzikolo lidzakhala ndi maluwa ochuluka lidzasangalala kwambiri ndi kufuwula mwachimwemwe. Lidzakhala ndi ulemerero monga wa ku mapiri a ku Lebanoni, maonekedwe ake wokongola adzakhala ngati a ku Karimeli ndi a ku Saroni. Aliyense adzaona ulemerero wa Yehova, ukulu wa Mulungu wathu.
3 Strengthen ye the weak hands, —The trembling knees, make ye firm:
Limbitsani manja ofowoka, limbitsani mawondo agwedegwede;
4 Say to the hurried in heart, Be strong, Do not fear, —Lo! your God, with avenging, doth come, With the recompence of God, He, doth come to save you.
nenani kwa a mitima yamantha kuti; “Limbani mtima, musachite mantha; Mulungu wanu akubwera, akubwera kudzalipsira; ndi kudzabwezera chilango adani anu; akubwera kudzakupulumutsani.”
5 Then, shall be opened the eyes of the blind, —And, the ears of the deaf, be unstopped:
Pamenepo maso a anthu osaona adzapenyanso ndipo makutu a anthu osamva adzatsekuka.
6 Then, shall leap as a hart the lame, Then shall shout the tongue of the dumb, For, there have broken forth—In the desert—waters, And streams, in the waste plain:
Anthu olumala adzalumpha ngati mbawala, ndipo osayankhula adzayimba mokondwera. Akasupe adzatumphuka mʼchipululu ndipo mitsinje idzayenda mʼdziko lowuma,
7 Then shall the glowing sand, become a lake, And thirsty ground—springs of water, —In the home of the wild dog—its lair, Shall be an enclosure for cane and paper—reed.
mchenga wotentha udzasanduka dziwe, nthaka yowuma idzasanduka ya akasupe. Pamene panali mbuto ya ankhandwe padzamera udzu ndi bango.
8 And there shall be there, a raised way—even a high road, And the Highroad of Holiness, shall it be called, There shall not pass over it one who is unclean; But He Himself, shall be one of them travelling the road, And the perverse, shall not stray [thereinto].
Ndipo kumeneko kudzakhala msewu waukulu; ndipo udzatchedwa Msewu Wopatulika. Anthu odetsedwa sadzayendamo mʼmenemo; zitsiru sizidzasochera mʼmenemo.
9 There shall be, there, no lion, Nor shall ravenous beast, go up thereon, It shall not be found, there, —Thus, shall travel the redeemed;
Kumeneko sikudzakhala mkango, ngakhale nyama yolusa sidzafikako; sidzapezeka konse kumeneko. Koma okhawo amene Yehova anawapulumutsa adzayenda mu msewu umenewu.
10 And the ransomed of Yahweh! shall return, And shall enter Zion with shouting, With gladness age-abiding, upon their head, Joy and gladness shall overtake them, And sorrow and sighing, shall flee away.
Iwo amene Yehova anawawombola adzabwerera. Adzalowa mu mzinda wa Ziyoni akuyimba; kumeneko adzakondwa mpaka muyaya. Adzakutidwa ndi chisangalalo ndi chimwemwe, ndipo chisoni ndi kudandaula zidzatheratu.