< Isaiah 31 >

1 Alas! for them who are going down to Egypt for help, On horses, would rely, —And have trusted—In chariots—because they are many, and In horsemen, because they are very bold, But have not looked unto the Holy One of Israel, And onto Yahweh, have not sought.
Tsoka kwa amene amapita ku Igupto kukapempha chithandizo, amene amadalira akavalo, nakhulupirira kuchuluka kwa magaleta awo ankhondo ndiponso mphamvu za asilikali awo okwera pa akavalo, koma sakhulupirira Woyerayo wa Israeli, kapena kupempha chithandizo kwa Yehova.
2 But, he also, is wise, and hath brought in calamity, And his own words, hath he not set aside, —Therefore will he rise up, Against the house of evil-doers, and Against the help of the workers of iniquity.
Komatu Yehovayo ndi wanzeru ndipo angathe kuwononga, ndipo sasintha chimene wanena. Adzalimbana ndi anthu ochita zoyipa, komanso ndi amene amathandiza anthu ochita zoyipa.
3 Now, the Egyptians, are, men, and not, GOD, And, their horses, flesh, and not, spirit; When, Yahweh, shall stretch out his hand, Then, he that is giving help, shall stumble And, he that is receiving help, shall fall, And, together, shall, all of them, vanish!
Aigupto ndi anthu chabe osati Mulungu; akavalo awo ndi nyama chabe osati mizimu. Yehova akangotambasula dzanja lake, amene amapereka chithandizo adzapunthwa, amene amalandira chithandizocho adzagwa; onsewo adzathera limodzi.
4 For Thus, hath Yahweh said unto me—Like as a lion or a young lion growleth over his prey. Who—though there be called out against him a multitude of shepherds—Will not at their voice, be dismayed, Nor, at their noise, be daunted, So, will Yahweh of hosts come down, to make war over Mount Zion, and over the hill thereof.
Zimene Yehova akunena kwa ine ndi izi: “Monga mkango kapena msona wamkango umabangula ukagwira nyama yake, ndipo suopsedwa kapena kusokonezeka ndi kufuwula kwa abusa amene akulimbana nayo, momwemonso palibe chingaletse Yehova Wamphamvuzonse kubwera kudzatchinjiriza phiri la Ziyoni ndi zitunda zake.
5 As little mother-birds hovering, so, will Yahweh of hosts throw a covering over Jerusalem, —Covering, so will he rescue, Passing over, so will he deliver!
Monga mbalame zowuluka pamwamba pa zisa zake, Yehova Wamphamvuzonse adzatchinjiriza Yerusalemu; ndi kumupulumutsa, iye adzawupitirira ndi kuwulanditsa.”
6 Return ye unto him against whom the sons of Israel have deeply revolted,
Inu Aisraeli, bwererani kwa Iye amene munamuwukira kwakukulu.
7 For in that day, will every man reject his idols of silver, and his idols of gold, —Which your hands had made for you as a sin!
Pakuti tsiku limenelo nonsenu mudzataya mafano anu a siliva ndi golide amene mumapanga ndi manja anu auchimo.
8 Then shall the Assyrian fall, by the sword, not of a great man, And the sword, not of a mean man, shall devour him, —Howbeit he shall take his flight from the face of a sword, And his young men, shall come under tribute;
“Aasiriya adzaphedwa ku nkhondo ndi mphamvu osati za munthu. Lupanga, osati la munthu, lidzawawononga. Adzathawa ku nkhondo ndipo anyamata awo adzagwira ntchito yathangata.
9 And his own Cliff, through terror, shall he pass by, And his princes shall be dismayed at an ensign, —Declareth Yahweh. Who hath a flame in Zion, And hath a furnace in Jerusalem.
Mfumu yawo idzamwalira ndi mantha, ndipo atsogoleri awo ankhondo adzathawa ndi mantha kusiya pambuyo mbendera yawo ya nkhondo.” Akutero Yehova, amene moto wake uli mu Ziyoni, ndipo ngʼanjo yake ili mu Yerusalemu.

< Isaiah 31 >