< Isaiah 29 >

1 Alas for Ariel, Ariel, The city against which, David encamped, —Add ye a year to a year. Let the festivals, come round;
Tsoka kwa iwe, Arieli, Arieli, mzinda umene Davide anakhazikitsamo zithando za nkhondo! Papite chaka chimodzi kapena ziwiri ndipo masiku a zikondwerero zanu azipitirirabe ndithu.
2 Yet will I bring Ariel into straits, —And she shall become a bewailing and wailing, Yea she shall become to me a veritable Hearth of God.
Komatu Ine ndidzathira nkhondo Arieli ndipo kudzakhala kulira ndi kudandaula, mzindawo udzasanduka ngati ngʼanjo ya guwa lansembe.
3 And I will encamp round about against thee, —And lay siege against thee with a fort, And raise against thee siege-works;
Ine ndidzamanga misasa ya nkhondo kulimbana ndi mzindawo; ndidzakuzungulira ndi nsanja za nkhondo ndi kumanga mitumbira yanga ya nkhondo kulimbana nawe.
4 And thou shalt be brought low—Out of the earth, shalt thou speak, And out of the dust, shalt thou lower thine utterance, —And as one that hath a familiar spirit, Out of the earth, shall come thy voice, And out of the dust, thy speech shall chirp;
Utagwetsedwa pansi, iwe udzayankhula kuchokera mʼnthaka, mawu ako adzatuluka uli mʼfumbi, adzamveka ngati a mzukwa. Mawu ako adzamveka ngati onongʼona kuchokera mʼfumbi.
5 Then shall be as fine dust the multitude of thy foreigners, —And as chaff that passeth away, the multitude of tyrants; And it shall come to pass, in a twinkling, Suddenly,
Koma chigulu cha adani ako chidzasanduka chifwirimbwiti. Chigulu cha ankhondo achilendo chidzabalalika ngati mungu wowuluzika ndi mphepo. Mwadzidzidzi ndi mosayembekezereka,
6 From Yahweh of hosts, shalt thou be visited, With thunder, and with earthquake and a great noise, hurricane and storm and flame of fire devouring;
Yehova Wamphamvuzonse adzabwera ndi mabingu ndi chivomerezi ndi phokoso lalikulu, kamvuluvulu ndi namondwe ndi malawi a moto wonyeketsa.
7 And it shall be like the dream of a night vision, With the multitude of all the nations who have been making war against Ariel, —Even with all who have been making war against her and her stronghold and who have been laying siege to her;
Tsono chigulu chankhondo cha mitundu ina yonse chimene chikulimbana ndi mzinda wa Arieli nʼkumathira nkhondo mzindawo, malinga ake ndi kuwuzinga, chigulu chonsecho chidzazimirira ngati maloto, gati zinthu zoziona mʼmasomphenya usiku.
8 Yea it shall be As when the hungry man dreameth and lo! he is eating, But he awaketh, and his soul, is empty, Or as when the thirsty man dreameth and lo! he is drinking, But he awaketh and lo! he is faint and his soul, is craving, So, shall it be with the multitude of all the nations, that have come forth to war against Mount Zion.
Chidzakhala ngati munthu wanjala wolota akudya, koma podzuka ali nayobe njala; kapena ngati munthu waludzu wolota akumwa, koma podzuka, ali nalobe ludzu, kummero kwake kuli gwaa. Izi zidzachitika pamene chigulu cha nkhondo cha mitundu ina yonse chikunthira nkhondo Phiri la Ziyoni.
9 Stand ye stock still and stare, Besmear your eyes and be blind, —They are drunken but not with wine, They reel, but not with strong drink;
Pitirizani kuledzera ndipo mudzakhala opusa. Dzitsekeni mʼmaso ndipo mukhale osapenya, ledzerani, koma osati ndi vinyo, dzandirani, koma osati ndi mowa.
10 For Yahweh, hath poured out upon you, a spirit of deep sleep, Yea hath tightly shut your eyes—the prophets, —And, your heads—the seers, hath he covered,
Yehova wakugonetsani tulo tofa nato. Watseka maso anu, inu aneneri; waphimba mitu yanu, inu alosi.
11 And so all vision hath become unto you as the words of a writing that is sealed, Which is delivered unto one acquainted with writing, saying, Pray thee read this, And he saith, I cannot, for it is sealed;
Kwa inu mawu onsewa ali ngati buku lotsekedwa, ndipo ngati lipatsidwa kwa wina wodziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde tawerengani bukuli,” iye adzati, “Sindingathe popeza ndi lomatidwa.”
12 And then the writing is delivered to one unacquainted with writing, saying, Pray thee read this, And he saith I am not acquainted with writing.
Kapena ngati lipatsidwa kwa amene sadziwa kuwerenga ndi kunena kuti, “Chonde werenga bukuli,” iye adzayankha kuti, “Ine sindidziwa kuwerenga.”
13 Wherefore My Lord hath said, —Because this people, hath drawn near with their mouth, And with their lips, have honoured me, But their heart, have they moved far from me, And so their reverence of me hath become A commandment of men in which they have been schooled,
Ambuye akuti, “Anthu awa amandipembedza Ine ndi pakamwa pawo, ndi kundilemekeza Ine ndi milomo yawo, koma mitima yawo ili kutali ndi Ine. Kundipembedza kwawo ndi kwa chiphamaso. Amandipembedza motsata malamulo a anthu amene anaphunzitsidwa.
14 Therefore, behold me! again dealing wonderfully with this people, doing wonderfully a wonderful thing, —So shall perish, the wisdom of their wise men, And the intelligence of their intelligent men, shall vanish!
Nʼchifukwa chakenso Ine ndidzapitirira kuwachitira ntchito zodabwitsa; nzeru za anthu anzeru zidzatha, luntha la anthu aluntha Ine ndidzalinyoza.”
15 Alas! for them who would fain have been too deep for Yahweh by giving secret counsel, —and therefore in the dark, have been their doings, and they have said Who can see us? and—Who can understand us?
Tsoka kwa amene amayesetsa kubisira Yehova maganizo awo, amene amachita ntchito zawo mu mdima nʼkumanena kuti, “Ndani amene akundiona kapena ndani akudziwa zimene ndikuchita?”
16 Your perverseness! As if like clay, the potter could be reckoned; For shall, the thing made say of him that made it, he made me not? Or hath the thing fashioned ever said of him that fashioned it, He hath no understanding.
Inu mumazondotsa zinthu ngati kuti dothi lasanduka wowumba mbiya. Kodi chinthu chopangidwa chingawuze wochipanga kuti “Sunandipange ndi iwe?” Kapena mʼphika kunena kwa amene anawuwumba kuti, “Iwe sudziwa chilichonse?”
17 Is it not yet a very little while, And Lebanon shall be turned, into garden land, —And garden land, for a forest, be reckoned?
Kodi Lebanoni posachedwapa sadzasanduka munda wachonde, ndipo kodi munda wachondewo ngati nkhalango?
18 Therefore, in that day, shall the deaf hear the words of a book, —And out of gloom and darkness, the eyes of the blind shall see;
Tsiku limenelo anthu osamva adzamva mawu a mʼbuku, ndipo anthu osaona amene ankakhala mu mdima adzapenya.
19 And again shall the humbled in Yahweh, have joy, —And the needy of mankind in the Holy One of Israel, exult;
Anthu odzichepetsa adzakhalanso ndi chimwemwe mwa Yehova; ndipo anthu osowa adzakondwa chifukwa cha Woyerayo wa Israeli.
20 For the tyrant, hath vanished, And the scoffer, is no more, Yea cut off are all who watch for iniquity: —
Koma anthu ankhanza adzazimirira, oseka anzawo sadzaonekanso, ndipo onse okopeka ndi zoyipa adzawonongedwa.
21 Who bring a man into condemnation with a rumour, And for him that decideth in the gate, lay a snare, —And have driven away, for a thing of nought, one who was righteous.
Yehova adzalanga amene amasinjirira munthu kuti apezeke wolakwa, kapena kuphophonyetsa anthu ozenga mlandu ndi umboni wonama kuti osalakwa asaweruzidwe mwachilungamo.
22 Therefore, Thus, saith Yahweh, concerning the house of Jacob, [even he saith it] who redeemed Abraham, —Not now, shall, Jacob turn pale, And, not now, shall their faces whiten;
Choncho Yehova amene anawombola Abrahamu, akunena kwa zidzukulu za Yakobo kuti, “Anthu anga sadzachitanso manyazi; nkhope zawo sizidzagwanso ndi manyazi.
23 For, when he seeth his children the work of my hands, in his midst, They will hallow my Name, —Yea they will hallow the Holy One of Jacob, And the God of Israel, will they regard with awe.
Akadzaona ana awo ndi ntchito ya manja anga pakati pawo, adzatamanda dzina langa loyera; adzazindikira kuyera kwa Woyerayo wa Yakobo, ndipo adzachita naye mantha Mulungu wa Israeli.
24 Then will they who erred in spirit comprehend, And the murmurers, accept instruction.
Anthu opusa adzapeza nzeru; onyinyirika adzalandira malangizo.”

< Isaiah 29 >