< Isaiah 19 >

1 The oracle on Egypt: Lo! Yahweh, riding upon a swift cloud, and he will enter Egypt, And the idols of Egypt shall shake at his presence, And, the heart of Egypt, shall melt within him;
Uthenga onena za Igupto: Taonani, Yehova wakwera pa mtambo waliwiro, ndipo akupita ku Igupto. Mafano a ku Igupto akunjenjemera pamaso pake, ndipo mitima ya Aigupto yachokamo ndi mantha.
2 And I will stir up Egyptians against Egyptians, And they shall fight—Every one against his brother and Every one against his neighbour, —City against city, and Kingdom against kingdom.
“Ine ndidzadzutsa Aigupto kuti amenyane okhaokha; mʼbale adzamenyana ndi mʼbale wake, mnansi ndi mnansi wake, mzinda ndi mzinda unzake, ndiponso ufumu ndi ufumu unzake.
3 And the spirit of Egypt, shall vanish, within them, Yea the sagacity thereof, will I swallow up, —And they will seek Unto the idols and Unto them that mutter, and Unto them that have familiar spirits, and Unto the wizards;
Aigupto adzataya mtima popeza ndidzalepheretsa zolinga zawo; adzapempha nzeru kwa mafano awo ndiponso kwa woyankhula ndi mizimu ya anthu akufa, kwa amawula ndi kwa oyankhula ndi mizimu.
4 And I will deliver the Egyptians into the hand of a cruel lord, —And a fierce king shall rule over them, Declareth the Lord, Yahweh of hosts.
Ndidzawapereka Aigupto kwa olamulira ankhanza, ndipo mfumu yoopsa idzawalamulira,” akutero Ambuye Yehova Wamphamvuzonse.
5 And the waters shall be dried up from the great stream, —And the River, shall waste and be dry;
Madzi a mu mtsinje wa Nailo adzaphwa, ndipo mʼmbali mwa mtsinje mudzangʼaluka ndi kuwuma.
6 And rivers, shall stink, The canals of Egypt be shallow and waste, Reed and rush, be withered;
Ngalande zake zidzanunkha; ndipo mitsinje ya Igupto idzayamba kuchepa ndi kuwuma. Bango ndi dulu zidzafota,
7 The meadows by the Nile, by the mouth of the Nile. And all that is sown in the Nile, Shall be dry, driven away, and not be!
ndiponso zomera za mʼmphepete mwa Nailo ndi ku mathiriro a mtsinjewo. Zonse zodzalidwa mʼmbali mwa Nailo zidzawuma, zidzawuluzika ndipo sizidzaonekanso.
8 Then shall the fishers, lament, And all shall mourn who cast in the Nile a hook, —And they who spread nets on the face of the waters shall languish;
Asodzi adzabuwula ndi kudandaula, onse amene amaponya mbedza mu Nailo; onse amene amaponya makoka mʼmadzi adzalira.
9 Then shall turn pale The workers in combed flax, —and The weavers of white linen;
Amene amagwira ntchito yopota thonje adzataya mtima, anthu oluka nsalu zofewa zabafuta adzataya chiyembekezo.
10 Then shall her pillars be crushed, —All who make wages, be bowed down in soul.
Akatswiri opanga nsalu adzangoti kakasi, ndipo anthu onse ogwira ntchito yolipidwa adzatheratu mphamvu.
11 Surely, foolish, are the princes of Zoan, the wisest counsellors of Pharaoh, in counsel are brutish, —How can ye say unto Pharaoh, Son of the wise, am I Son of the kings of olden time?
Akuluakulu a ku Zowani ndi zitsiru; aphungu a nzeru a Farao amalangiza zopusa. Kodi mungathe kunena bwanji kwa Farao kuti, “Ine ndine mmodzi mwa anthu anzeru, wophunzira wa mafumu akale?”
12 Where then are thy wise men? Pray let them tell thee! And let them know what Yahweh of hosts hath purposed on Egypt!
Iwe Farao, anthu ako anzeru ali kuti? Abweretu kuti akuwuze ndi kukudziwitsa zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonza kuchitira dziko la Igupto.
13 Doting are the princes of Zoan, Deceived are the princes of Noph: They who are the corner-stone of her tribes, have led Egypt astray.
Akuluakulu a ku Zowani asanduka zitsiru, atsogoleri a ku Mefisi anamizidwa; atsogoleri a dziko la Igupto asocheretsa anthu a dzikolo.
14 Yahweh, hath infused in her midst, a spirit of perverseness, —And they have led Egypt astray into all his own doings, As a drunken man staggereth into his own vomit;
Yehova wasocheretsa anthu a ku Igupto. Iwo akuchita kudzandira pa zonse zimene akuchita, ngati chidakwa choterereka pa masanzi ake.
15 And Egypt shall have nothing which can be done, Which head or tail, palm-top or rush, can do!
Palibe chimene munthu wa mu Igupto angachite, mtsogoleri kapena wotsatira, nthambi ya kanjedza kapena bango.
16 In that day, shall Egypt be like unto women, —And shall start and tremble because of the brandishing of the hand of Yahweh of hosts, which he is about to brandish over it.
Tsiku limenelo Aigupto adzakhala ngati amayi. Adzanjenjemera ndi kuchita mantha akadzaona Yehova Wamphamvuzonse, atakweza dzanja lake kufuna kuwalanga.
17 Then shall the soil of Judah become, to Egypt, a terror; Every one to whom it is mentioned, will tremble, —Because of the purpose of Yahweh of hosts, which he is purposing against it.
Ndipo dziko la Yuda lidzaopsa dziko la Aigupto. Aliyense amene adzamve dzina la Yuda adzaopsedwa chifukwa cha zimene Yehova Wamphamvuzonse wakonzekera kuchitira dziko la Igupto.
18 In that day, shall there be five cities in the land of Egypt Speaking the language of Canaan, And swearing unto Yahweh of hosts, —The city of destruction, shall be the name of one!
Tsiku limenelo ku dziko la Igupto kudzakhala mizinda isanu yoyankhula chiyankhulo cha Akanaani, ndipo anthu ake adzalumbira kwa Yehova Wamphamvuzonse kuti adzamutumikira. Umodzi mwa mizindayo udzatchedwa Mzinda Wachilungamo.
19 In that day, shall there be An altar unto Yahweh, in the midst of the land of Egypt, —And a pillar near the boundary thereof unto Yahweh;
Tsiku limenelo mʼkati mwa dziko la Igupto mudzakhala guwa lansembe la Yehova, ndipo mʼmalire mwake adzayikira Yehova mwala wachikumbutso.
20 And it shall become a sign and a witness unto Yahweh of hosts in the land of Egypt, —For they will make outcry unto Yahweh, because of oppressors, That he would send them a saviour—and a great one Then will he deliver them.
Zimenezo zidzakhala umboni wozindikiritsa kuti Yehova Wamphamvuzonse alimo mʼdziko la Igupto. Pamene Aigupto adzalirira Yehova chifukwa cha owapondereza, Iye adzawatumizira mpulumutsi ndi mtetezi ndipo adzawalanditsa.
21 Then will, Yahweh, make himself known, to the Egyptians, So shall the Egyptians know, Yahweh, in that day, —And they will offer a sacrifice and a present And will vow a vow unto Yahweh and will perform.
Kotero Yehova adzadziulula yekha kwa Aigupto, ndipo tsiku limenelo adzadziwa Yehova. Adzapembedza Yehova popereka nsembe ndi popereka zopereka zachakudya; Adzalumbira kwa Yehova ndipo adzachita zimene alumbirazo.
22 And Yahweh, will plague Egypt, plague and heal, —And they will turn unto Yahweh And he will be entreated of them and will heal them.
Yehova adzakantha Aigupto ndi mliri. Iye adzawakanthadi ndipo kenaka adzawachiritsa. Aigupto adzatembenukira kwa Yehova ndipo Iye adzamva madandawulo awo ndi kuwachiritsa.
23 In that day, shall there be a highway. from Egypt to Assyria, And, the Assyrians, shall come into Egypt, And, the Egyptians, into Assyria; And, the Egyptians shall serve, with the Assyrians.
Tsiku limenelo kudzakhala msewu waukulu wochoka ku Igupto kupita ku Asiriya. Aasiriya adzapita ku Igupto ndi Aigupto ku Asiriya. Aigupto ndi Aasiriya adzapembedza pamodzi.
24 In that day, shall, Israel, be, a third, with Egypt and with Assyria, —A blessing in the midst of the earth:
Tsiku limenelo Israeli adzakhala pamodzi ndi Igupto ndi Asiriya, mayiko atatuwa adzakhala dalitso pa dziko lapansi.
25 Whom Yahweh of hosts hath blessed saying, —Blessed, be My people—the Egyptians, And the work of my hands—the Assyrians, And mine own inheritance—Israel.
Yehova Wamphamvuzonse adzawadalitsa, ndi mawu awa, “Adalitsike anthu anga Aigupto, Aasiriya, ntchito ya manja anga, ndi Aisraeli osankhidwa anga.”

< Isaiah 19 >