< Isaiah 16 >

1 Send ye the lamb due to the ruler of the land, From Sela towards the desert, —Unto the mount of the daughter of Zion;
Anthu a ku Mowabu atumiza mphatso za ana ankhosa onenepa, kuchokera ku Sela kudutsa chipululu mpaka kukafika ku phiri la Ziyoni.
2 Yet shall it be that—Like wandering birds from a nest cast forth, Shall be the daughters of Moab, at the fords of Arnon.
Monga momwe mbalame zimawulukira uku ndi uku akazimwaza mʼchisa, momwemonso akazi a ku Mowabu akuyendayenda ku madooko a Arinoni.
3 Bring thou, in counsel, Execute thou judgment, Make as the night, thy shadow in the midst of high noon, —Hide thou the outcasts, The wanderer, do not thou reveal.
Amowabu aja anawuza a ku Yuda kuti, “Tiwuzeni chochita, gamulani zoti tichite. Inu mutiteteze kwa adani anthu. Mukhale ngati mthunzi wathu dzuwa lili pa liwombo. Mutibise, musatipereke ife othawa nkhondo kwa adani athu.
4 Let mine own outcasts, sojourn with thee, O Moab, become thou a covert to them from the face of the spoiler, —For vanished is the oppressor, At an end is extortion, They who tread down have ceased out of the land.
Lolani kuti anthu othawa nkhondo a ku Mowabu azikhala pakati panu; mukhale populumukira pawo kwa wowonongayo.” Nthawi idzafika ndipo wozunzayo sadzakhalaponso, kuwononga kudzaleka; waukaliyo adzachoka mʼdzikomo.
5 So shall be established, in lovingkindness, a throne, And one shall sit thereon, in truth, in the home of David, —Judging—and seeking justice and speeding righteousness.
Mpando waufumu udzakhazikitsidwa mwachikondi; mmodzi mwa zidzukulu za Davide adzakhalapo mokhulupirika. Iyeyo poweruza adzatsata chilungamo ndipo adzalimbikitsa kuchita zachilungamo.
6 We have heard of the arrogance of Moab, Proud exceedingly! His haughtiness and his arrogance and his passion, Not true, are his boastings.
Tinamva kuti Mowabu anadzikuza kwambiri. Kunyada kwawo ndi kunyogodola kwawo ndi kudzitama kwawo, zonse ndi zopanda phindu.
7 Therefore shall, Moab, howl for, Moab, All that belong to her, shall wail, —For the ruins of Kir-hareseth, shall they moan out Utterly stricken!
Nʼchifukwa chake Amowabu akulira kwambiri; iwo akulirira dziko lawo. Akubuma momvetsa chisoni chifukwa cha makeke a mphesa a ku Kiri Hareseti.
8 For, the fields of Heshbon are withered—The vine of Sibmah, the owners of nations, have broken off ruddy branches, Unto Jazer, had they reached, They had spread abroad to the desert, —Her boughs, had stretched forth, had gone over to the sea.
Minda ya ku Hesiboni yauma, minda ya mpesa ya ku Sibina yaguga. Atsogoleri a mitundu ina anapondaponda minda ya mpesa wabwino, imene nthambi zake zinakafika ku Yazeri, mpaka kutambalalira ku chipululu. Mizu yake inakafika mpaka ku tsidya la nyanja.
9 For this cause, will I bewail, in the wailing of Jazer, The vine of Sibmah, I will drench thee with my tears, O Heshbon and Elealeh, —For, upon thy fruit-harvest, and upon thy grain-harvest, the battle-shout, hath fallen.
Kotero Ine ndikulira, monga mmene akulirira anthu a ku Yazeri, chifukwa cha minda ya mpesa ya ku Sibima. Inu anthu a ku Hesiboni, inu anthu a ku Eleali, ndikukunyowetsani ndi misozi! Mwalephera kupeza zokolola, chifukwa cha nkhondo imene inawononga zokolola zonse.
10 Now shall be withdrawn rejoicing and exultation out of the garden-land, And, in the vineyards, shall be neither singing nor shouting, —Wine in the winepress, the treader, shall not tread, The vintage-shout, have I made to cease.
Chimwemwe ndi chisangalalo zalekeka ku minda yanu ya zipatso; palibe amene akuyimba kapena kufuwula mʼminda ya mpesa; palibe amene akupsinya vinyo ku malo opsinyira mphesa, pakuti ndathetsa kufuwula.
11 For this cause, mine inward parts—for Moab, like a lyre, shall make a plaintive sound, —Yea what is within me, for Kir-heres.
Chifukwa chake moyo wanga ukulira ngati pangwe kulirira Mowabu, mtima wanga ukubuwula chifukwa cha Kiri Hareseti.
12 And it shall be—When it is seen that Moab hath laboured in vain on the high place, He shall enter into his holy place to pray, and shall not prevail,
Ngakhale anthu a ku Mowabu apite ku malo awo achipembedzo koma amangodzitopetsa ndi kutaya nthawi chabe chifukwa sizidzatheka.
13 This, is the word which Yahweh spake concerning Moab in, time past;
Awa ndi mawu amene Yehova wayankhula kale zokhudza Mowabu.
14 But now, hath Yahweh spoken saying, In three years, —as the years of a hireling, shall the glory of Moab be diminished, with all the great multitude, —even a very small remnant, of no account.
Koma tsopano Yehova akuti, “Zisanathe zaka zitatu, potsata mʼmene munthu waganyu amawerengera, ulemerero wa Mowabu udzakhala utatheratu ndipo anthu ake ambiri adzakhala atawonongeka, ndipo opulumuka ake adzakhala ochepa ndi ofowoka.”

< Isaiah 16 >