< Hosea 5 >

1 Hear ye this—O priests, and attend, O house of Israel, and ye, House of the King, give ear, for, to you, pertaineth the sentence, —for, a snare, have ye been to Mizpah, and a net spread on Tabor.
“Ansembe inu, imvani izi! Inu Aisraeli, tcherani khutu! Inu nyumba yaufumu, mvetserani! Chiweruzo ichi ndi chotsutsa inu: Inu munali ngati msampha ku Mizipa, munali ngati ukonde woyalidwa pa phiri la Tabori.
2 And, a slaughter, have apostates deeply designed, —though, I, was a rebuker to them all.
Owukira azama mʼmoyo wakupha, Ine ndidzawalanga onsewo.
3 I, have known Ephraim, and, Israel, hath not been hidden from me, —for, now, hast thou committed unchastity, O Ephraim, Israel, hath made himself impure.
Ndimadziwa zonse za Efereimu; Aisraeli ndi osabisika kwa Ine. Efereimu wayamba tsopano kuchita zachiwerewere; Israeli wadziyipitsa.
4 Their doings, will not suffer, them to return unto their God, —for, the spirit of unchastity, is within them, and, Yahweh, have they not known.
“Ntchito zawo siziwalola kubwerera kwa Mulungu wawo. Mʼmitima mwawo muli mzimu wachiwerewere; Iwo sadziwa Yehova.
5 Therefore will the Excellency of Israel, answer, to his face, —and, Israel and Ephraim, shall stumble in their iniquity, even Judah with them, hath stumbled.
Kudzikuza kwa Israeli kwakhala umboni womutsutsa; Aisraeli, ngakhale Aefereimu, anagwa mʼmachimo awo; Yudanso anagwa nawo pamodzi.
6 With their flocks and with their herds, will they go to seek Yahweh, but shall not find him; he hath withdrawn himself from them.
Pamene adzapita ndi nkhosa zawo ndi ngʼombe zawo kukapereka nsembe kwa Yehova, iwo sadzamupeza; Iye wawachokera.
7 With Yahweh, have they dealt treacherously, for, to alien children, have they given birth, —now, a new moon, shall devour them, with their portions.
Iwo ndi osakhulupirika kwa Yehova; amabereka ana amʼchigololo ndipo chikondwerero chawo cha mwezi watsopano chidzawawononga pamodzi ndi minda yawo.
8 Blow ye a horn in Gibeah, a trumpet in Ramah, —sound an alarm at Beth-aven, behind thee, O Benjamin!
“Womba lipenga mu Gibeya, liza mbetete mu Rama. Fuwulani mfuwu wankhondo mu Beti-Aveni; iwe Benjamini tsogolera.
9 Ephraim, shall become, a desolation, in the day of rebuke: Throughout the tribes of Israel, have I hide known what is sure.
Efereimu adzasanduka bwinja pa tsiku la chilango. Ine ndikulengeza zomwe zidzachitikadi pakati pa mafuko a Israeli.
10 The rulers of Judah have become as they who remove a land-mark. Upon them, will I pour out, like water, my wrath.
Atsogoleri a Yuda ali ngati anthu amene amasuntha miyala ya mʼmalire. Ndidzawakhutulira ukali wanga ngati madzi a chigumula.
11 Oppressed, is Ephraim, crushed in judgment, —because he hath, wilfully, walked after falsehood.
Efereimu waponderezedwa, akulangidwa chifukwa chotsatira mafano.
12 But, I, was like a moth, to Ephraim, —and like rotten wood to the house of Judah.
Ine ndili ngati njenjete kwa Efereimu, ngati chinthu chowola kwa anthu a ku Yuda.
13 When Ephraim, saw, his injury, and Judah his wound, then went Ephraim unto Assyria, and [Judah] sent unto a hostile king, —yet, he, cannot heal you, nor will the wound, remove from you.
“Efereimu ataona nthenda yake, ndi Yuda ataona zilonda zake, pamenepo Efereimu anatembenukira kwa Asiriya, ndipo anawatumizira mfumu yayikulu kudzawathandiza. Koma mfumuyo singathe kukuchizani, singathe kuchiritsa mabala anu.
14 For, I, will be as a lion unto Ephraim, and as a young lion to the house of Judah, —I, I, will tear in pieces, and depart, I will carry off, and none be able to rescue.
Pakuti Ine ndidzakhala ngati mkango kwa Efereimu. Ngati mkango wamphamvu kwa Yuda. Ndidzawakhadzula nʼkuchokapo; ndidzawatenga ndipo palibe amene adzawalanditse.
15 I will depart, will return unto my place! till what time they acknowledge their guilt, and seek my face, —In their trouble, will they make for me diligent search.
Ndipo ndidzabwerera ku malo anga mpaka anthu anga atavomereza kulakwa kwawo. Ndipo iwo adzafunafuna nkhope yanga; mʼmasautso awo adzandifunitsitsa Ine.”

< Hosea 5 >