< Hosea 2 >

1 Say ye unto your brethren, O Ammi ["O my people"], and unto your sisters, O Ruhamah ["O compassionated one"]:
“Nena kwa abale ako kuti, ‘Ndinu anthu anga,’ kwa alongo ako kuti ‘Ndinu okondedwa anga.’”
2 Contend ye with your mother, contend, for she is no wife of mine, and I am no husband of hers, Let her then put away her paramours from before her, and her partners in adultery, from her embraces:
“Dzudzulani amayi anu, adzudzuleni iwo, pakuti si mkazi wanga, ndipo ine sindine mwamuna wake. Iyeyo achotse maonekedwe adama pa nkhope yake, ndi kusakhulupirika pa mawere ake.
3 Lest I strip off her under-clothing, and set her forth to view, as in the day she was born, —and make her like a wilderness, and render her like a land that is parched, and suffer her to die of thirst;
Akapanda kutero ndidzamuvula, ndipo adzakhala wamaliseche monga tsiku limene anabadwa; ndidzamuwumitsa ngati chipululu, adzakhala ngati dziko lopanda madzi, ndi kumupha ndi ludzu.
4 And, on her children, not have compassion, —because, the children of paramours, they are.
Sindidzaonetsa chikondi changa pa ana ake, chifukwa ndi ana a mʼchiwerewere.
5 For their mother, hath been unchaste, and she that conceived them, hath caused shame, —for she said, Let me go after my lovers! who used to give my bread, and my water, my wool, and my flax, mine oil, and my drink.
Amayi awo akhala akuchita zachiwerewere ndipo anawabereka anawo akuchita zinthu zochititsa manyazi. Iwo anati, ‘Ine ndidzatsatira zibwenzi zanga, zimene zimandipatsa chakudya ndi madzi, ubweya ndi thonje, mafuta ndi chakumwa.’
6 Therefore, behold me! hedging up her way, with thorns, —and I will wall her in, and, her footpaths, shall she not find.
Choncho njira yake ndidzayitseka ndi minga; ndidzamuzinga ndi khoma kotero kuti sadzapezanso njira yotulukira.
7 And, when she shall pursue her lovers, and not overtake them, and shall seek them and not find, then will she say, Let me go my way now! and return unto my first husband, for it was better with me, then, than, now!
Adzathamangira zibwenzi zake koma sadzazipeza; adzazifunafuna koma sadzazipeza. Pamenepo iye adzati, ‘Ndibwerera kwa mwamuna wanga woyamba uja, pakuti ndinali pabwino ndi iyeyo kusiyanitsa ndi pano.’
8 But, she, owneth not, that, I, gave her—the corn, and the new wine and the oil, —silver, also increased I unto her, and gold—[which] they offered to Baal!
Iye sanazindikire kuti ndine amene ndinkamupatsa tirigu, vinyo watsopano ndi mafuta. Ndine amene ndinkamukhuthulira siliva ndi golide, zimene ankapangira mafano a Baala.
9 Therefore, will I again take away my corn, in the time thereof, and my new wine, in the season thereof, —and will recover my wool and my flax [given] to hide her shame.
“Choncho Ine ndidzamulanda tirigu wanga pa nthawi yokolola, ndi vinyo wanga watsopano pa nthawi yopsinya mphesa. Ndidzamulanda ubweya ndi thonje langa, zomwe akanaphimba nazo umaliseche wake.
10 Now, therefore, will I expose her unseemliness, before the eyes of her lovers, —and no, man, shall deliver her out of my hand!
Motero tsopano ndidzaonetsa maliseche ake pamaso pa zibwenzi zake; palibe ndi mmodzi yemwe adzamupulumutse mʼmanja mwanga.
11 And I will cause to cease all her mirth, her pilgrim-festival, her new moon and her sabbath, —and her every appointed meeting;
Ndidzathetsa zikondwerero zake zonse: zikondwerero zake za chaka ndi chaka, za mwezi watsopano, za pa masiku a Sabata ndi maphwando ake onse a pa masiku okhazikitsidwa.
12 And will lay waste her vine and her fig- tree, as to which she hath said, A present, are they for myself, which my lovers, have given me, —and I will make of them a thicket, and the wild beasts of the field shall devour them.
Ndidzawononga mitengo yake ya mpesa ndi mitengo yake yamkuyu, imene iye ankanena kuti inali malipiro ake ochokera kwa zibwenzi zake. Ndidzayisandutsa chithukuluzi, ndipo zirombo zakuthengo zidzadya zipatsozo.
13 So will I visit upon her the days of the Baals, unto whom she used to burn incense, and decked herself with her nose-ring and her jewelry, and went her way after her lovers, —whereas, me, she forgat, Declareth Yahweh.
Ndidzamulanga chifukwa cha masiku amene anafukiza lubani kwa Abaala; anadzikongoletsa povala mphete ndi mikanda yamtengowapatali ndipo anathamangira zibwenzi zake, koma Ine anandiyiwala,” akutero Yehova.
14 Therefore, lo! I, am going to persuade her, and, though I conduct her forth into wilderness, yet will I speak unto her heart.
“Koma tsopano ndidzamukopa mkaziyo; ndidzapita naye ku chipululu ndipo ndidzamuyankhula mwachikondi.
15 Then will I give to her her vineyards from thence, and the vale of Achor ["trouble"] for a door of hope, —and she will respond there, as in the days of her youth, and as in the day when she came up out of the land of Egypt.
Kumeneko ndidzamubwezera minda yake ya mpesa, ndipo ndidzasandutsa Chigwa cha Akori kukhala khomo la chiyembekezo. Kumeneko iye adzayimba nyimbo monga mʼmasiku a ubwana wake, monga tsiku limene anatuluka ku Igupto.
16 And it shall come to pass, in that day, Declareth Yahweh, that she will call me Ishi ["My husband"], and will not call me any more, Baali ["Mine owner"].
“Tsiku limeneli,” Yehova akuti, “udzandiyitana kuti, ‘Amuna anga;’ sudzandiyitananso kuti, ‘Mbuye wanga.’
17 So will I take away the names of the Baals, out of her mouth, —and they shall not be called to mind any more, by their name.
Ndidzachotsa mayina a Abaala pakamwa pake; sadzatchulanso mayina awo popemphera.
18 And I will solemnize to them a covenant, in that day, with the wild-beast of the field, and with the bird of the heavens, and the creeping thing of the ground, —and, bow and sword and battle, will I break in pieces out of the land, so will I cause them to lie down, in security.
Tsiku limenelo ndidzachita pangano ndi zirombo zakuthengo ndi mbalame zamumlengalenga ndiponso zolengedwa zokwawa pansi kuti ziyanjane ndi anthu anga. Ndidzachotsa mʼdzikomo uta, lupanga ndi zida zonse zankhondo, kuti onse apumule mwamtendere.
19 And I will take thee unto myself, unto times age-abiding, —yea I will take thee unto myself, in righteousness and in justice, and in lovingkindness, and in abounding compassion:
Ndidzakutomera kuti ukhale mkazi wanga mpaka muyaya; ndidzakutomera mwachilungamo, mwaungwiro, mwachikondi ndi mwachifundo.
20 Yea I will take thee unto myself, in faithfulness, —So shalt thou know Yahweh.
Ndidzakutomera mokhulupirika ndipo udzadziwa Yehova.
21 And it shall come to pass in that day, that I will respond, Declareth Yahweh, I will respond to the heavens, —and, they, shall respond to the earth;
“Tsiku limenelo Ine ndidzayankha,” akutero Yehova. “Ndidzayankha mlengalenga pempho lake lofuna mitambo ndipo mvula idzagwa pa dziko lapansi;
22 And, the earth, shall respond to the corn, and to the new wine and to the oil, —and, they, shall respond to Jezreel ["Whom GOD scattereth," "Whom GOD soweth"].
ndipo nthaka idzamvera kupempha kwa tirigu, vinyo ndi mafuta, ndipo zidzamvera Yezireeli.
23 So will I sow her unto me in the land, and will have compassion upon the uncompassionated one ["Lo-ruhamah"], —and will say to him who was No-people-of-mine ["Lo-ammi"], My people, thou art, and, he, shall say, My God!
Ndidzadzala Israeli mʼdziko kuti akhale wanga: ndidzaonetsa chikondi changa kwa anthu amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Sakondedwa.’ Ndidzawawuza amene ndinkawatchula dzina loti, ‘Si anthu anga,’ kuti, ‘Ndinu anthu wanga;’ ndipo adzanena kuti, ‘ndinu Mulungu wathu,’”

< Hosea 2 >