< Genesis 37 >

1 So Jacob dwelt in the land of the sojournings of his father, —in the land of Canaan.
Yakobo ankakhala mʼdziko la Kanaani kumene abambo ake ankakhala.
2 These, are the generations of Jacob—Joseph, when seventeen years old, was shepherding with his brethren among the flocks, and, he, being a youth, was with the sons of Bilhah and with the sons of Zilpah wives of his father, —so then Joseph brought in the talk about them—something bad, unto their father.
Mbiri ya banja la Yakobo ndi iyi: Yosefe, mnyamata wa zaka 17 ankaweta nkhosa ndi abale ake, pamodzi ndi ana a Biliha ndi Zilipa, akazi a abambo ake. Tsono Yosefe ankabwera kudzawuza abambo ake zoyipa za abale ake.
3 Now, Israel, loved Joseph more than any of his sons, because he was to him, the son of his old age, and he had made him, a long tunic.
Tsono Israeli ankakonda Yosefe koposa ana ake ena onse, chifukwa anali mwana wobadwa muukalamba wake. Ndipo anamusokera mkanjo wa manja aatali.
4 So his brethren saw that their father loved him, more than any of his brethren, and they hated him, and could not bid him prosper,
Pamene abale ake anaona kuti abambo awo ankakonda Yosefe kuposa aliyense wa iwo, anayamba kumuda Yosefe ndipo sankayankhula naye zamtendere.
5 And Joseph dreamed a dream, and told it to his brethren, and they went on yet more to hate him.
Tsiku lina Yosefe analota maloto ndipo pamene anawuza abale ake za malotowo, iwo anawonjeza kumuda.
6 And he said unto them, Hear ye I pray you, this dream which I have dreamed:
Iye anawawuza kuti, “Tamvani maloto amene ndinalota:
7 Lo! then, we, were binding sheaves in the midst of the field, when lo my sheaf rose up, yea and took its stand, —and lo! round about came your sheaves, and bowed themselves down to my sheaf.
Ife timamanga mitolo ya tirigu ku munda ndipo mwadzidzidzi mtolo wanga unayimirira chilili, pamene mitolo yanu inazungulira mtolo wangawo nʼkumawugwadira.”
8 And his brethren said to him, Shalt thou, reign, over us, shalt thou, have dominion over us? So they went on yet more to hate him, because of his dreams and because of his words.
Abale ake aja anamufunsa nati, “Kodi ukuyesa kuti ungakhale mfumu yathu? Ungadzatilamuliredi iweyo?” Ndipo anamuda kuposa kale chifukwa cha maloto ake ndi zimene ankakonda kunena kwa abambo awo.
9 Then dreamed he, yet another, dream, and related it to his brethren, and said: —Lo! I have dreamed a dream, yet again, Lo! then, the sun and the moon, and eleven stars, were bowing themselves down to me.
Tsiku lina analotanso maloto ena, ndipo anafotokozera abale ake za malotowo. Iye anati, “Tamverani, ndinalotanso maloto ena. Ulendo uno dzuwa ndi mwezi pamodzi ndi nyenyezi khumi ndi imodzi zimandigwadira.”
10 So he related it unto his father, and unto his brethren, —and his father rebuked him, and said unto him, What is this dream which thou hast dreamed? Shall we, indeed come in, I, and thy mother and thy brethren, to bow ourselves down to thee to the earth?
Atawuza abambo ake ndi abale ake malotowa, abambo ake anamukalipira nati, “Ndi maloto anji umalotawa? Kodi uganiza kuti ine, amayi ako pamodzi ndi abale ako onsewa tingadzabwere kudzakugwandira iwe?”
11 Then were his brethren jealous of him, but his father, marked the word.
Abale ake anamuchitira nsanje, koma abambo ake anasunga nkhaniyi mu mtima.
12 Now his brethren went their way, —to feed their father’s flock in Shechem.
Tsono abale ake anapita kukadyetsa ziweto za abambo awo ku Sekemu,
13 So Israel said unto Joseph Are not, thy brethren, feeding the flock in Shechem? Come on! and let me send thee unto them. And he said to him Behold me!
ndipo Israeli anati kwa Yosefe, “Tsono, ndikufuna kukutuma kwa abale ako.” Iye anayankha nati, “Chabwino.”
14 So he said to him—Go, I pray thee, look after the welfare of thy brethren, and the welfare of the flock, and bring me back word. And he sent him from the vale of Hebron, and he came in towards Shechem.
Choncho anati kwa iye, “Pita ukaone ngati abale ako ali bwino. Ukaonenso nkhosa ngati zili bwino. Kenaka ubwere udzandiwuze.” Choncho Israeli anatuma Yosefe kuchokera ku chigwa cha Hebroni. Yosefe atafika ku Sekemu,
15 And a man found him, and lo! he was wandering about in the field, so the man asked him saying—What seekest thou?
munthu wina anamupeza akungozungulirazungulira mʼmunda ndipo anamufunsa, “Ukufunafuna chiyani?”
16 And he said, My brethren, am, I, seeking, —do tell me, I pray thee, where they are feeding their flock.
Iye anayankha, “Ndikufuna abale anga. Mungandiwuze kumene akudyetsa ziweto zawo?”
17 And the man said, They have broken up from hence, for I heard them saying Let us go our way towards Dothan. So Joseph went after his brethren, and found them, in Dothan.
Munthuyo anayankha nati, “Anasamukako kuno. Ndinawamva akuti, ‘Tiyeni tipite ku Dotani.’” Choncho Yosefe analondola abale ake ndipo anakawapeza ku Dotani.
18 And they saw him afar off, —and, ere yet he drew near unto them, they conspired against him, to put him to death.
Abale ake aja anamuonera patali. Ndipo asanafike nʼkomwe kumene kunali iwo kuja, anayamba kale kumupangira chiwembu choti amuphe.
19 And they said each man unto his brother, Lo! that master of dreams yonder, coming in!
Iwo anawuzana nati, “Uyo akubwera apo wamaloto uja.
20 Now, therefore, come! let us slay him and cast him into one of the pits, and we will say A cruel beast, hath devoured him, —And let us see what will become of his dreams.
Tsono tiyeni timuphe ndi kuponya thupi lake mu chimodzi mwa zitsime izi ndipo tidzati anadyedwa ndi nyama zakuthengo zolusa. Tsono timuonera zomwe ziti zichitike ndi maloto ake aja.”
21 And Reuben heard it, and rescued him out of their hand, and said Let us not smite him, so as to take his life!
Koma Rubeni atamva izi, anapulumutsa Yosefe. Iye anati kwa abale ake, “Ayi, tisamuphe,
22 And Reuben said unto them Do not shed blood! Cast him into this pit, which is in the wilderness, but put not forth, a hand, against him! that he might rescue him out of their hand, to restore him unto his father.
tisakhetse magazi. Tiyeni timuponye mʼchitsime ku chipululu konkuno. Koma tisamuvulaze nʼkomwe. Rubeni ananena zonsezi kuti apulumutse Yosefe ndi kuti pambuyo pake akamupereke kwa abambo awo.”
23 So it came to pass, when Joseph had come in unto his brethren, that they stript Joseph of his tunic, the long tunic which was upon him,
Choncho Yosefe atafika kwa abale ake, iwo anamuvula mkanjo wake wamanja aatali uja umene anavala
24 and took him, and cast him into the pit, but the pit, was empty, there was in it no water.
ndipo anamutenga namuponya mʼchitsime chopanda madzi komanso mopanda chilichonse.
25 And when they had sat down to eat bread, they lifted up their eyes and looked, and lo! a caravan of Ishmaelites, coming in from Gilead, —and, their camels, were bearing tragacanth gum, and balsam and cistus-gum, they were going their way, to take them down to Egypt.
Atakhala pansi kuti adye chakudya, anatukula maso naona gulu la Aismaeli akubwera kuchokera ku Giliyadi. Ngamira zawo zinanyamula zonunkhiritsa bwino zakudya zamitundumitundu, ndipo zimenezi ankapita nazo ku Igupto.
26 So Judah said unto his brethren, —What profit that we slay our brother, and conceal his blood?
Yuda anafunsa abale ake nati, “Kodi tidzapindula chiyani tikapha mʼbale wathuyu ndi kuphimbitsa magazi ake?
27 Come and let us sell him to the Ishmaelites; but let not, our own hand, be upon him, for our own brother, our own flesh, is he And his brethren hearkened.
Bwanji timugulitse kwa Aismaeliwa, koma ife tisamuchite kanthu kalikonse. Ameneyu ndi mʼbale wathu thupi limodzi ndi ife.” Abale ake anavomereza zimenezi.
28 And there passed by certain Midianites travelling merchants, so they drew forth and uplifted Joseph out of the pit, and sold Joseph to the Ishmaelites, for twenty pieces of silver, —and they brought Joseph into Egypt.
Amalonda ena a ku Midiyani ankadutsa pomwepo. Tsono abale ake a Yosefe anamutulutsa Yosefe uja mu chitsime chija ndipo anamugulitsa kwa Aismaeli aja pamtengo wa masekeli makumi awiri. Choncho anapita naye Yosefe ku Igupto.
29 And Reuben returned unto the pit, and lo Joseph was not in the pit, so he rent his clothes;
Rubeni atabwerera ku chitsime kuja anapeza kuti Yosefe mulibe mʼchitsimemo. Pamenepo iye anangʼamba zovala zake
30 and returned unto his brethren, and said, —The, lad, is not! And, I, oh where can I, go?
nabwerera kwa abale ake nati, “Mnyamata uja mulibemo! Nanga ndilowere kuti ine tsopano?”
31 And they took Joseph’s tunic, —and slaughtered a buck of the goats, and dipped the tunic in the blood;
Tsono anapha kamwana ka mbuzi, natenga mkanjo wa Yosefe ndi kuwunyika mʼmagazi ake.
32 and sent the long tunic and brought it in unto their father, and said This, have we found! Examine, we pray thee, whether it is the tunic of thy son, or not!
Iwo anatenga mkanjo uja nabwerera nawo kwa abambo awo nati, “Ife tapeza mkanjowu. Tawuyangʼanitsitsani muone ngati uli wa mwana wanu.”
33 So he examined it, and said—The tunic of my son! A cruel beast hath devoured him, —torn in pieces—torn in pieces, is Joseph!
Iye anawuzindikira ndipo anati, “Ndi mkanjo wa mwana wanga umenewu! Nyama yakuthengo yolusa yamudya. Mosakayika, mwana wanga Yosefe wakhadzulidwa.”
34 And Jacob rent his garments, and put sackcloth upon his loins, —and mourned over his son many days.
Pamenepo Yakobo anangʼamba zovala zake, navala chisaka mʼchiwuno mwake. Iye analira maliro a mwana wake masiku ambiri.
35 And all his sons and all his daughters rose up to console him but he refused to be consoled, and said—Surely I will go down unto my son mourning to hades! And his father wept for him. (Sheol h7585)
Ngakhale kuti ana ake onse aamuna ndi aakazi anasonkhana kudzamutonthoza, iye anakana kutonthozedwa. Iye anati, “Ayi. Ndidzalira mpaka ndidzapite kwa mwana wanga ku manda.” Choncho Israeli anapitirirabe kulira mwana wake. (Sheol h7585)
36 Now, the Midianites, sold him into Egypt, —to Potiphar courtier of Pharaoh, chief of the royal executioners.
Amidiyani aja anagulitsa Yosefe kwa Potifara, mmodzi mwa nduna za Farao ku Igupto. Potifarayu anali mkulu wa asilikali olonda nyumba ya Farao.

< Genesis 37 >