< Genesis 25 >
1 And Abraham took another wife and her name, was Keturah;
Abrahamu anakwatira mkazi wina dzina lake Ketura.
2 and she bare to him Zimran, and Yokshan, and Medan, and Midian, —and Ishbak, and Shuah.
Iyeyu anamubalira Zimurani, Yokisani, Medani, Midiyani, Isibaki ndi Suwa.
3 And, Yokshan, begat Sheba and Dedan, —and, the sons of Dedan, were Asshurim and Letushim, and Leummim.
Yokisani anabereka Seba ndi Dedani ndipo zidzukulu za Dedani ndiwo Aasuri, Aletusi, ndi Aleumi.
4 And the sons of Midian, Ephah and Epher and Hanoch, and Abida. and Eldaah, —all these, were the sons of Keturah.
Ana aamuna a Midiyani anali, Efai, Eferi, Hanoki, Abida ndi Elida. Onsewa anali zidzukulu za Ketura.
5 And Abraham gave all that he had to Isaac;
Abrahamu anasiyira Isake chilichonse anali nacho.
6 but, to the sons of the concubines whom Abraham had, Abraham gave gifts, —and then sent them away from Isaac his son while he himself yet lived, eastward unto the land of the east.
Koma pamene anali ndi moyo, Abrahamu anapereka mphatso kwa ana aakazi ake ena onse. Kenaka anawatumiza ku dziko la kummawa kuti akhale kutali ndi mwana wake Isake.
7 Now, these, are the days of the years of the life of Abraham which he lived—a hundred and seventy-five years.
Abrahamu anakhala ndi moyo zaka 175.
8 So Abraham breathed his last, and died in a fine old age, old and satisfied, —and was gathered unto his people,
Abrahamu anamwalira atakalamba kwambiri ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
9 And Isaac and Ishmael his sons buried him, in the cave of Machpelah, —in the field of Ephron son of Zohar the Hittite, which is over against Mamre;
Ana ake, Isake ndi Ismaeli anamuyika mʼphanga la Makipela pafupi ndi Mamre, mʼmunda umene kale unali wa Efroni mwana wa Zohari Mhiti,
10 the field which Abraham purchased of the sons of Heth, —there, was buried Abraham, with Sarah his wife.
uwu ndi munda umene Abrahamu anagula kwa Ahiti. Kumeneko Abrahamu anakayikidwa pamodzi ndi mkazi wake Sara.
11 And it came to pass after the death of Abraham, that God blessed Isaac his son, —and Isaac dwelt by Beer-lahai-roi.
Atamwalira Abrahamu, Mulungu anadalitsa mwana wake Isake, amene ankakhala pafupi ndi Beeri-lahai-roi (chitsime cha Wamoyo Wondipenya).
12 Now, these, are the generations of Ishmael son of Abraham, —whom hagar the Egyptian woman the handmaid of Sarah bare to Abraham;
Nazi zidzukulu za Ismaeli, mwana wa Abrahamu amene wantchito wa Sara, Hagara Mwigupto uja, anaberekera Abrahamu.
13 and these, are the names of the sons of Ishmael, by their names after their generations, —the firstborn of Ishmael, Nebaioth, and Kedar and Adbeel and Mibsam;
Awa ndi mayina a ana a Ismaeli monga mwa mndandanda wa mabadwidwe awo: Nebayoti ndiye anali mwana woyamba wa Ismaeli; kenaka Kedara, Adibeeli, Mibisamu,
14 and Mishma and Dumah, and Massa;
Misima, Duma, Masa,
15 Hadad, and Tema, Jetur, Naphish, and Kedemah:
Hadadi, Tema, Yeturi, Nafisi ndi Kedema;
16 these, same, are the sons of Ishmael and these, their names, by their villages and by their encampments, —twelve princes, after their tribes.
Amenewa ndi ana a Ismaeli ndi mayina awo monga mwa midzi ndi misasa yawo. Anali olamulira mafuko khumi ndi awiri.
17 And these, are the years of the life of Ishmael, a hundred and thirty-seven years, —and he breathed his last and died, and was gathered unto his people.
Ismaeli anakhala ndi moyo zaka 137. Iye anamwalira ndipo anakakhala ndi anthu a mtundu wake.
18 And they stretched their habitations from Havilah as far as to Shur, which is over against Egypt, as thou goest in towards Assyria, —over against all his brethren, he settled down.
Zidzukulu za Ismaeli zinkakhala mʼdera la pakati pa Havila ndi Suri, kummwera kwa Igupto, mukamapita cha ku Asuri. Choncho anakhala kummawa kwa abale awo.
19 And, these, are the generations of Isaac, son of Abraham, —Abraham, begat Isaac;
Iyi ndi mbiri ya Isake mwana wa Abrahamu. Abrahamu anabereka Isake
20 and it came to pass that, Isaac, was forty years old, when he took Rebekah daughter of Bethuel the Syrian, of the Plain of Syria, —sister of Laban the Syrian. to himself to wife.
ndipo Isake anali ndi zaka makumi anayi pamene anakwatira Rebeka mwana wa Betueli Mwaramu wa ku Padanaramu mlongo wa Labani Mwaramu.
21 So then Isaac made entreaty unto Yahweh in behalf of his wife, for she was, barren, —and Yahweh suffered himself to be entreated by him, and Rebekah his wife conceived.
Isake anapempherera mkazi wake kwa Yehova popeza iye anali wosabereka. Yehova anayankha pemphero lake ndipo mkazi wake Rebeka anatenga pathupi.
22 And the sons within her struggled together, so she said—If so, wherefore now am, I, [thus]? And she went to seek Yahweh.
Koma pamene anawo amalimbana mʼmimba mwake, iye anati, “Bwanji zikundichitikira zoterezi?” Choncho anapita kukafunsa kwa Yehova.
23 And Yahweh said to her. Two nations, are in thy womb, And two races, from thy body, shall be parted, —And, one race, shall be stronger, than the other race, And the elder, shall serve the younger.
Yehova anati kwa iye, “Udzabala mafuko awiri a anthu olimbana, ndipo magulu awiri a anthu ochokera mwa iwe adzasiyana; fuko limodzi lidzakhala la mphamvu kuposa linzake, ndipo wamkulu adzatumikira wamngʼono.”
24 Then were fulfilled her days to bring forth, —and lo! twins in her womb.
Pamene nthawi inakwana yakuti abeleke, Rebeka anaberekadi mapasa.
25 And the first came forth red, all over, as a mantle of hair, —so they called his name, Esau,
Woyamba kubadwa anali wofiira, ndipo thupi lake lonse linali ngati chovala cha ubweya; choncho anamutcha Esau.
26 And, after that, came forth his brother with his hand fast hold of the heel of Esau, so they called his name Jacob—Now, Isaac, was sixty years old when she bare them,
Kenaka mʼbale wake anabadwa atagwira chidendene cha Esau; choncho anamutcha Yakobo. Isake anali ndi zaka 60 pamene Rebeka anabereka mapasawa.
27 And when the youths grew up, it came to pass that Esau was a man skilled in game a man of the field, —but, Jacob, was a ready man, dwelling in tents.
Anyamatawo anakula ndipo Esau anakhala katswiri wosaka, munthu wamʼthengo, pamene Yakobo anali munthu wofatsa, wokonda kukhala pa nyumba.
28 And, Isaac, loved, Esau, because of the game he put in his mouth, —but, Rebekah, was a lover of Jacob!
Isake ankakonda Esau chifukwa cha nyama za kutchire zomwe ankakonda kudya, koma Rebeka ankakonda Yakobo.
29 And Jacob had boiled pottage, —when Esau came in from the field, he, being famished.
Tsiku lina pamene Yakobo ankaphika chakudya, Esau anabwera kuchokera kuthengo ali wolefuka ndi njala.
30 So Esau said unto Jacob. Do let me devour some of the red—this red, for, famished, I am. For this cause, was his name called Edom.
Iye anati kwa Yakobo, “Tandipatsako phala lofiiralo, ndimwe! Ndalefuka ndi njala.” (Nʼchifukwa chake amatchedwanso Edomu).
31 And Jacob said, —Come sell, just now, thy birthright unto me.
Yakobo anayankha, “Choyamba undigulitse ukulu wako.”
32 And Esau said, Here am I, on the point of dying, —wherefore, then, should I, have, a birthright?
Esau anati, “Chabwino, ine ndatsala pangʼono kufa, ukulu undithandiza chiyani?”
33 And Jacob said, Come swear to me just now! And he sware to him, —and sold his birthright to Jacob.
Koma Yakobo anati, “Lumbira kwa ine choyamba.” Kotero Esau analumbiradi, ndipo anagulitsa ukulu wake kwa Yakobo.
34 And Jacob, having given to Esau bread and a dish of lentils, he did eat and drink and rose up, and went his way, —thus Esau despised his birthright!
Choncho Yakobo anamupatsa Esau buledi ndi phala lofiira lija. Iye anadya ndi kumwa, nanyamuka kumapita. Motero Esau anapeputsa ukulu wake wachisamba uja.