< Genesis 22 >

1 And it came to pass after these things, that God, did prove Abraham, —and he said unto him, Abraham! And he said Behold me!
Nthawi ina zitatha izi, Mulungu anamuyesa Abrahamu. Iye anati, “Abrahamu!” Ndipo iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
2 And he said—Take, I pray thee, thy son, thine only one, whom thou lovest, even, Isaac, and get thee into the land of Moriah and cause him to ascend there as an ascending-sacrifice, on one of the mountains which I shall name unto thee.
Ndipo Mulungu anati, “Tenga Isake, mwana wako yekhayo amene umamukonda ndi kupita naye ku dziko la Moriya. Ukamupereke iye ngati nsembe yopsereza pa limodzi la mapiri a kumeneko limene ndidzakuwuza.”
3 So Abraham rose early in the morning, and saddled his ass, and took his two young men with him, and Isaac his son, and clave the pieces of wood for an ascending-sacrifice, and mounted and went his way unto the place which God had named to him.
Abrahamu anadzuka mmamawa wake namangirira chokhalira pa bulu. Atadula nkhuni zokwanira zowotchera nsembe yopsereza, Abrahamu, antchito ake awiri pamodzi ndi Isake ananyamuka kupita kumalo kumene Mulungu anamuwuza Abrahamu.
4 It was, on the third day, that Abraham lifted up his eyes, and saw the place afar off.
Pa tsiku lachitatu, Abrahamu anakweza maso ake ndipo anaona malowo chapatali.
5 And Abraham said unto his young men—Tarry by yourselves here with the ass, but I and the young man must go yonder, —that we may bow ourselves down and return unto you.
Ndipo Abrahamu anati kwa antchito ake aja, “Bakhalani pano ndi buluyu. Ine ndi mnyamatayu tipita uko kukapemphera, koma tibweranso.”
6 So Abraham took the pieces of wood for the ascending-sacrifice, and laid them on Isaac his son, and took in his own hand the fire and the knife, and they went on their way, both of them together.
Abrahamu anatenga nkhuni za nsembe yopsereza zija namusenzetsa mwana wake Isake, ndipo iye mwini anatenga moto ndi mpeni. Pamene awiriwo amayendera pamodzi,
7 Then said Isaac unto Abraham his father, then said he; My father! And he said, Behold me, my son, And he said, Behold the fire, and the pieces of wood, —but where is the lamb, for an ascending-sacrifice?
Isake anati kwa abambo ake Abrahamu, “Abambo?” Abrahamu anayankha, “Ee mwana wanga.” Isake anafunsa, “Moto ndi nkhuni zilipo, koma nanga mwana wankhosa wa nsembe yopsereza ali kuti?”
8 And Abraham said, God, will provide for himself the lamb for an ascending-sacrifice, my son! So they went on their way, both of them, together.
Abrahamu anayankha, “Mwana wanga, Mulungu adzipezera yekha mwana wankhosa wa nsembe yopsereza.” Ndipo awiriwo anapitiriza ulendo.
9 Then came they into the place which God had named to him, and Abraham built there the altar, and laid in order the pieces of wood, and bound Isaac his son, and laid him on the altar, above the pieces of wood.
Atafika pamalo pamene Mulungu anamuwuza paja, Abrahamu anamangapo guwa lansembe nayika nkhuni pamwamba pa guwapo. Kenaka anamumanga mwana wake Isake namugoneka paguwapo, pamwamba pa nkhuni paja.
10 And Abraham put forth his hand, and took the knife, —to slay his son.
Kenaka Abrahamu anatambasula dzanja lake natenga mpeni kuti aphe mwana wake.
11 Then called out unto him the messenger of Yahweh out of the heavens, and said. Abraham, Abraham! And he said Behold me!
Koma mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba nati, “Abrahamu! Abrahamu!” Iye anayankha kuti, “Ee Ambuye.”
12 Then he said, Do not put forth thy hand unto the young man, neither do to him—anything at all, —for, now, know I that one who reverest God, thou art, when thou hast not withheld thy son, thine only one, from me.
Mngeloyo anati, “Usatambasulire mwanayo dzanja lako kuti umuphe, pakuti tsopano ndadziwa kuti iwe umaopa Mulungu. Iwe sunandimane mwana wako mmodzi yekhayo.”
13 And Abraham lifted up his eyes and looked, and lo! a ram, behind, caught in a thicket by his horns, and Abraham went, and took the ram, and caused him to ascend as an ascending-sacrifice instead of his son.
Abrahamu anatukula maso ake ndipo anaona nkhosa yamphongo itakoledwa ndi nyanga zake mu ziyangoyango. Iye anapita nakatenga nkhosa ija ndikuyipha ngati nsembe yopsereza mʼmalo mwa mwana wake.
14 So Abraham called the name of that place Yahweh-yireh, —as to which it is still said to-day, In the mountain of Yahweh, will provision be made.
Choncho Abrahamu anatcha malo amenewa kuti Yehova-Yire (Wopereka). Ndipo mpaka lero amatchula malowo kuti ndi “Pa phiri la Yehova wopereka.”
15 Then called out the messenger of Yahweh unto Abraham, —a second time out of the heavens;
Mngelo wa Yehova anayitana Abrahamu kuchokera kumwamba kachiwiri
16 and said, By myself, have I sworn is the oracle of Yahweh, —Because thou hast done this thing, and hast not withheld thy son, thine only one,
ndipo anati, “Ndikulumbira mwa Ine ndekha kuti popeza wachita zimenezi, wosandikaniza mwana wako mmodzi yekhayu,
17 That I will, richly bless, thee, and, abundantly multiply, thy seed, as the stars of the heavens, and as the sand which is on the lip of the sea, —that thy seed may take possession of the gate of his foes:
ndidzakudalitsa ndithu ndipo ndidzakupatsa zidzukulu zochuluka ngati nyenyezi zamlengalenga komanso ngati mchenga wa mʼmphepete mwa nyanja. Zidzukulu zako zidzalanda mizinda ya adani awo,
18 So shall all the nations of the earth bless themselves in thy seed, —Because thou didst hearken unto my voice.
ndipo kudzera mwa chidzukulu chako, mitundu yonse ya anthu pa dziko lapansi idzadalitsika, chifukwa iwe wandimvera.”
19 So Abraham returned unto his young men, and they mounted, and went on their way together unto Beer-sheba, —and Abraham dwelt in Beer-sheba.
Kenaka Abrahamu anabwerera kumene anasiya antchito ake kuja nanyamukira nawo pamodzi kupita ku Beeriseba. Ndipo Abrahamu anakhala ku Beeriseba.
20 And it came to pass after these things, that it was told Abraham, saying, —Behold! Milcah—she also, hath borne sons, to Nahor thy brother:
Patapita nthawi, Abrahamu anamva kuti, “Milika nayenso anaberekera Nahori, mʼbale wake ana.
21 Uz his firstborn and Buz his brother, —and Kemuel, father of Aram—
Woyamba anali Huzi ndipo kenaka mʼbale wake Buzi. Anaberekanso Kemueli, amene anali abambo ake a Aramu.
22 and Chesed and Hazo, and Pildash, and Jidlaph, —and Bethuel;
Ana ena ndi Kesede Hazo, Pilidasi, Yidilafi ndi Betueli.”
23 And, Bethuel, hath begotten Rebekah, —These eight, hath Milcah borne to Nahor brother of Abraham.
Betueli anabereka Rebeka. Milika anaberekera Nahori, mʼbale wake wa Abrahamu, ana aamuna asanu ndi atatu amenewa.
24 And his concubine, whose name was Reumah, she also, hath borne Tebah and Gaham, and Tahash, and Maacah.
Mkazi wake wachiwiri, dzina lake Reuma, anamubaliranso Nahori ana awa: Teba, Gahamu, Tahasi ndi Maaka.

< Genesis 22 >