< Ezekiel 5 >

1 Thou therefore son of man Take thee a sharp cutting instrument, a barber’s razor, shalt thou take thee, and shalt cause it to pass upon thy head and upon thy chin, —and shalt take the balances for weighing, and shalt divide the hair.
Tsiku lina Yehova anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, tsopano tenga lupanga lakuthwa ndipo uligwiritse ntchito ngati lumo lometera. Umete tsitsi ndi ndevu zako. Kenaka utenge sikelo ndipo ugawe tsitsilo patatu.
2 A third part in the fire, shalt thou burn in the midst of the city, when the days of the siege are fulfilled, —and thou shalt take a third part, thou shalt smite it with the cuting instrument round about it, and a third part, shalt thou scatter to the wind, and, a sword, will I, make bare after them;
Kuzinga mzinda kuja kukatha, chimodzi cha zigawo zitatu za tsitsilo uchitenthe pakati pa mzinda. Chigawo chachiwiri uchiduledule ndi lupanga, poyenda muzungulire mzinda wonsewo. Chigawo chachitatu uchimwazire ku mphepo, ndidzachitsata nditasolola lupanga.
3 and thou shalt take from thence, a few in number, —and shalt bind them in thy skirts;
Koma utengeko tsitsi pangʼono, ulimange mu mpindiro wa mkanjo wako.
4 and of them, again take, and cast them into the midst of the fire, and burn them in the fire, -therefrom, shall go forth a fire unto all the house of Israel.
Pa tsitsi limeneli utapepo lina, uliponye pa moto ndi kulitentha. Moto udzayambira pamenepo mpaka ku nyumba yonse ya Israeli.”
5 Thus, saith My Lord, Yahweh, This, is Jerusalem, In the midst of the nations, I placed her, — and of the countries round about her;
Ambuye Yehova akunena kuti, “Uyu ndi Yerusalemu amene ndamuyika pakati pa mitundu ya anthu, ndipo mayiko onse amuzungulira.
6 But she hath changed my regulations into lawlessness, more than the nations, And my statutes more than the countries which are round bout her, For my regulations, have they rejected, And in my statutes, have they not walked.
Koma anthu a Yerusalemu aphwanya malamulo anga pochita zoyipa kuposa anthu a mitundu ina. Iwo anandipandukira kupambana anthu ena amene awazungulira. Iwo anakana malamulo anga ndipo sanasunge malangizo anga.
7 Therefore, Thus saith My Lord, Yahweh. Because ye have become more rebellious than the nations who are round about you, In my statutes, have not walked. And my regulations, have not done, And according to the regulations of the nations which are round about you, have not done:
“Nʼchifukwa chake Ambuye Yehova akuti: Popeza mwakhala osamvera kupambana anthu a mitundu ina amene akuzungulirani, popeza simunatsate malamulo anga kapena kusunga malangizo anga, mʼmalo mwake mwakhala mukutsata makhalidwe a anthu a mitundu ina amene akuzungulirani.
8 Therefore, Thus, saith My Lord Yahweh, Lo! I am against thee, even I, Therefore will I, execute in thy midst, judgments, in the eyes of the nations;
“Tsono Ambuye Yehova akuti: Ine mwini ndikutsutsana nawe, Yerusalemu, choncho Ine ndidzakulangani. Ine ndidzakulangani anthu a mitundu ina akuona.
9 Yea I will execute upon thee that which I have not executed, And like unto which I will not execute again, - Because of all thine abominations.
Chifukwa cha ntchito zanu zonyansa ndidzakulangani ndi chilango chimene sindinakulangeni nacho nʼkale lomwe ndipo sindidzakulangani ndi chofanana nacho mʼtsogolomo.
10 Therefore, fathers will eat sons in thy midst, And sons will eat fathers, — And I will execute upon thee judgments, And will scatter the whole remnant of thee, to every wind.
Tsono pakati panu makolo adzadya ana awo, ndipo ana adzadya makolo awo. Ndidzakulanga ndipo otsala onse ndidzawabalalitsa ku mphepo zonse zinayi.
11 Therefore as I live, Declareth My Lord Yahweh, — Surely because my sanctuary, thou hast defiled, with all thy detestable things, and with all thine abominations Even I also, will cut off, and mine eye, shall not spare, Yea even I will not pity.
Ndithu, pali Ine, akutero Ambuye Yehova Wamoyo, pakuti mwayipitsa Nyumba yanga ndi mafano ano oyipa ndi miyambo yanu yonyansa, Inenso ndidzakulangani. Sindidzakulekererani kapena kukumverani chisoni.
12 The third part of thee by pestilence, shall die, and by famine, be consumed in thy midst And the third part by the sword, shall fall round about thee, - And the third part to every wind, will I scatter, and a sword, will I make bare after them.
Chimodzi mwa zigawo zitatu za anthu ako chidzafa ndi mliri, kapena chidzawonongeka ndi njala; chigawo china chidzaphedwa ndi lupanga kunja kwa mzinda, ndipo chigawo china ndidzachibalalitsira ku mphepo zonse zinayi pochita kuchithamangitsa.
13 So shall mine anger have an end, And I will cause mine indignation, to find rest, upon them, and will console myself, - And they shall know that, I, Yahweh, have spoken in my jealousy, when mine indignation hath come to an end, upon them.
“Ndi mmene udzachitire mkwiyo wanga. Ndikadzatsiriza kuwalanga, pamenepo mtima wanga udzakhala pansi. Adzadziwa kuti Ine Yehova ndinawayankhula mwa nsanje ndikadzawalanga.
14 And I will deliver thee up to desolation and reproach, among the nations that are round about thee, —in the eyes of every passer-by.
“Ndidzakusandutsa iwe bwinja ndi chinthu chonyozeka pakati pa anthu a mitundu ina amene akuzungulira, ndi kwa onse odutsapo
15 So shall it become a reproach and an insult a warning and an astonishment, to the nations that are round about thee, —in that I have executed upon thee judgments in anger and in indignation and in rebukes of indignation, I, Yahweh have spoken:
Udzakhala chinthu chonyozeka ndi chonyogodoledwa. Udzakhala chenjezo ndi chinthu choopsa kwa anthu a mitundu ina amene akuzungulira ndikadzakulanga mokwiya ndi mwaukali ndi kugamula mlandu wako mokwiya. Ine Yehova ndayankhula.
16 In that I have sent the malignant arrows of famine among them which were for destruction, which I will send to destroy you, —and famine, will I increase upon you, and will break for you the staff of bread.
Pamene ndidzakulasa ndi njala yolasa ngati mivi yoopsa ndi yosakaza ndidzatero nʼcholinga choti ndikuwonongeni. Ndidzagwetsa njalayo pa iwe mowirikiza pochepetsa chakudya chako cha tsiku ndi tsiku.
17 So will I send upon you famine and mischievous beast and they shall bereave thee, —and pestilence and blood, shall pass through thee, —and a sword, will I bring in upon thee, I Yahweh, have spoken.
Ndidzatumiza njala ndi zirombo za kuthengo, ndipo zidzakulanda ana ako. Mliri ndi kuphana zidzakhala pakati pako, ndipo ndidzakubweretsera nkhondo. Ine Yehova ndayankhula.”

< Ezekiel 5 >