< Ezekiel 3 >
1 Then said he unto me, Son of man What thou findest, eat, —eat this roll, and go speak unto the house of Israel.
Tsono Mulungu anandiwuza kuti, “Mwana wa munthu, idya chimene ndikukupatsachi. Idya kenaka upite ukayankhule ndi Aisraeli.”
2 So I opened my mouth, —and he caused me to eat this roll.
Choncho ndinayasama ndipo anandipatsa mpukutuwo kuti ndidye.
3 Then said he unto me Son of man. Thy belly, cause thou to eat and thy bowels, fill thou with this roll which I am giving unto thee. So I did eat, and it became in my mouth, as honey for sweetness.
Kenaka Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, idya mpukutu umene ndikukupatsa kuti ukhute.” Choncho ndinadya, ndipo unkatsekemera ngati uchi mʼkamwa mwanga.
4 Then said he unto me, — Son of man Go get thee unto the house of Israel, and thou shalt speak with my words, unto them.
Pamenepo Iye anandiwuza kuti, “Iwe mwana wa munthu, pita tsopano kwa Aisraeli ndipo ukawawuze mawu anga.
5 For not unto a people deep of lip and heavy of tongue, art thou sent —[but] unto the house of Israel:
Sindikukutuma kwa anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, koma kwa Aisraeli.
6 not unto many peoples deep of lip and heavy of tongue, whose words thou couldst not understand, —surely if unto them I had sent thee, they would have hearkened unto thee.
Sindikukutuma kwa mitundu yambiri ya anthu oyankhula chiyankhulo chachilendo ndi chovuta, amene mawu ake sungawamvetse. Ndithu ndikanakutuma kwa iwowa, bwenzi iwo atakumvera.
7 But the house of Israel will not be willing to hearken unto thee, for they are not willing to hearken unto me, —for all the house of Israel are bold of forehead and hard of heart.
Koma Aisraeli sadzakumvera chifukwa iwo sakufuna kumvera Ine. Paja Aisraeli onse ndi okanika ndiponso a mtima wowuma.
8 Lo! I have made thy face bold like as their faces, and thy forehead bold like as their forehead.
Tsono ine ndakhwimitsa nkhope yako mofanana ndi nkhope zawo. Ndalimbitsanso mutu wako mofanana ndi mitu yawo.
9 As an adamant harder than flint, have I made thy forehead, —thou shalt not fear them neither shalt thou be dismayed at their faces, For a perverse house, they are!
Ine ndidzakusandutsa wolimba ngati mwala wa dayimondi umene uposa thanthwe lina lililonse kulimba kwake. Usachite nawo mantha kapena kuopsedwa nawo. Paja anthuwa ndi awupandu.”
10 Then said he unto me, — Son of man. All my words which I shall speak unto thee, receive thou into thy heart and in thine ears, hear thou:
Anatinso, “Iwe mwana wa munthu, umvetsetse bwino zimene ndikukuwuzazi ndipo mawu angawa uwasunge bwino mu mtima mwako.
11 then go get thee unto them of the captivity, unto the sons of thy people, and thou shalt speak unto them and say unto them, Thus saith My Lord Yahweh, whether they will hear or whether they will forbear.
Tsopano upite kwa Aisraeli anzako amene ali ku ukapolo ndipo ukayankhule nawo. ‘Kaya akamvera kaya sakamvera,’ koma uzikawawuza kuti, Ambuye Wamphamvuzonse akuti zakutizakuti.”
12 Then the Spirit lifted me up, and I heard behind me the sound of a great rushing, — Blessed be the glory of Yahweh. From his place!
Pamenepo Mzimu unandinyamula ndipo kumbuyo kwanga ndinamva liwu lamphamvu ngati chivomerezi chachikulu, lonena kuti, “Utamandike ulemerero wa Yehova kumene Iye amakhala!”
13 Yea the sound of the wings of the living ones, gently touching each other, and the sound of the wheels, along with them, even the sound of a great rushing.
Phokoso ndinkalimvalo linali la kugundana kwa mapiko a zamoyo ndiponso phokoso la mikombero ya pambali pake ija, limene linkamveka ngati chivomerezi chachikulu.
14 So the Spirit lifted me up, and took me away, —and I went bitterly, in the rage of my spirit, but the hand of Yahweh upon me was strong.
Mzimu wa Yehova unandikweza ndi kundinyamula ndipo ndinachokapo ndili wowawidwa ndi wonyuka mu mtima. Ndipo dzanja la Yehova linali pa ine mwa mphamvu.
15 Thus came I unto them of the captivity, at Tel-abib. who were dwelling towards he river Chebar and I dwelt where They were dwelling; yea I dwelt there seven days, stunned in their midst,
Choncho ndinafika kwa amene anali mu ukapolo ku Telabibu pafupi ndi mtsinje wa Kebara. Ndinakhala pansi pakati pawo masiku asanu ndi awiri, ndili wothedwa nzeru kwambiri.
16 And it came to pass at the end of seven days, that the word of Yahweh came unto me saying
Atatha masiku asanu ndi awiriwo, Yehova anandiwuza kuti,
17 Son of man, A watchman, have I appointed thee to the house of Israel, —and thou shalt hear, at my mouth a message, and shalt warn them from me.
“Iwe mwana wa munthu, Ine ndakuyika kuti ukhale mlonda wa Aisraeli. Uziti ukamva mawu anga, ndiye uzikawachenjeza.
18 When I say to the lawless man— Thou shalt surely die, and thou hast not given him warning, neither hast spoken to warn the lawless man from his lawless way, to save himself alive the same lawless man in his iniquity shall die, but his blood, at thy hand, will I require.
Ndikawuza munthu woyipa kuti, ‘Iwe udzafa ndithu,’ koma iwe osamuchenjeza kapena kumuyankhula kuti aleke njira zake zoyipa ndi kuti akhale ndi moyo, munthu woyipayo adzafa mu uchimo wake, koma Ine ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
19 Whereas when thou hast warned a lawless man, and he hath not turned from his lawlessness and from his lawless way he in his iniquity shall die, but Thou hast delivered thine own soul.
Koma ukamuchenjeza munthu woyipa koma iye osatembenuka mtima kuleka zoyipa zake kapena kusiya njira zake zoyipa, munthuyo adzafa chifukwa cha uchimo wake koma iwe udzapulumutsa moyo wako.
20 And when a righteous man hath turned from his righteousness, and committed perversity, and I have suffered a stumbling- block to be laid before him he shall die, —though thou hast not warned him, in his sin, shall he die, neither shall be remembered his righteous deeds which he hath done, but his blood, at thy hand will I require;
“Ngati munthu wolungama asiya chilungamo chake ndi kuchita uchimo ndipo Ine nʼkumuyika mʼzoopsa, munthuyo adzafa ndithu. Popeza iwe sunamuchenjeze, adzafadi chifukwa cha tchimo ndipo chilungamo chake sichidzakumbukiridwa, koma ndidzakuyimba mlandu chifukwa cha imfa yake.
21 whereas when Thou hast warned a righteous man. That a righteous man must not sin and he hath not sinned, he shall surely live in that he took warning, and thou hast delivered thine own soul.
Koma ngati umuchenjeza munthu wolungama kuti asachimwe ndipo iye nʼkuleka kuchimwa adzakhala ndi moyo ndithu chifukwa anamvera chenjezo, ndipo iwe udzapulumutsa moyo wako.”
22 Then came upon me there the hand of Yahweh, —and he said unto me, Arise go forth into the valley, and there, will I speak with thee.
Nthawi ina dzanja la Yehova linali pa ine ndipo anandiwuza kuti, “Nyamuka upite ku chigwa, kumeneko ndikayankhula nawe.”
23 So I arose and went forth into the valley, and lo! there the glory of Yahweh, standing, like the glory which I saw by the river Chebar, -and I fell upon my face.
Choncho ndinanyamuka kupita ku chigwa. Ndipo ndinaona ulemerero wa Yehova kumeneko, ngati ulemerero umene ndinaona mʼmbali mwa mtsinje wa Kebara ndipo ndinagwa pansi chafufumimba.
24 Then the Spirit entered into me, and caused me to stand upon my feet, —and he spake with me and said unto me, Go in shut thyself up, in the midst of thine own house,
Koma Mzimu wa Mulungu unalowa mwa ine ndipo unandiyimiritsa. Tsono Yehova anandiyankhula nati: “Pita, kadzitsekere mʼnyumba mwako.
25 And thou—O son of man, lo! they have put upon thee bands, and they will bind thee therewith, -. so that thou go not forth in their midst;
Ndipo iwe mwana wa munthu, adzakumanga ndi zingwe motero kuti sudzatha kuyendanso pakati pa anthu.
26 thy tongue also, will I cause to cleave unto the roof of thy mouth, so shalt thou be dumb and not be to them a reprover, — For a perverse house, they are!
Ndidzamatirira lilime lako kukhosi, kotero kuti udzakhala chete wosatha kuwadzudzula, chifukwa iwo ndi anthu aupandu.
27 But when I speak with thee, I will open thy mouth, and thou shalt say unto them. Thus saith My Lord Yahweh, —He that is minded to hear, let him hear, And he that is minded to forbear, let him forbear! For a perverse house, they are!
Koma pamene ndidzayankhula kwa iwe, ndidzatsekula pakamwa pako ndipo udzawawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti zakutizakuti.’ Aliyense wofuna kumva amve ndipo wokana kumva, muleke akane; pakuti iwo ndi anthu opanduka.”