< Ezekiel 25 >

1 And the word of Yahweh came unto me, saying:
Yehova anandiyankhula kuti:
2 Son of man Set thy face against the sons of Ammon, — and prophesy against them.
“Iwe mwana wa munthu, tembenukira anthu a ku Amoni ndipo unenere mowadzudzula.
3 So then thou shalt say to the sons of Ammon, Hear ye the word of My Lord Yahweh: Thus, saith My Lord. Yahweh: Because thou saidst Aha! Against my sanctuary when it was profaned. And against the soil of Israel when it was laid waste, And against the house of Judah when they went into exile.
Awawuze kuti, ‘Inu anthu a ku Amoni, imvani zimene Ambuye Yehova akunena. Iye akuti: Inu munanena mawu onyoza pamene Nyumba yanga yopatulika inkayipitsidwa. Munanyozanso dziko la Israeli pamene linaguga ndiponso anthu a ku Yuda pamene anatengedwa ukapolo.
4 Therefore, behold me! delivering thee up to the Sons of the East for a possession And they shall set their encampments in thee, And place in thee their habitations, They, shall eat thy fruits, And they, shall drink thy milk;
Nʼchifukwa chake Ine ndidzakuperekani mʼmanja mwa anthu akummawa ngati cholowa chawo. Iwo adzamanga misasa yawo ndi kukhoma matenti awo pakati panu. Adzadya zipatso zanu ndi kumwa mkaka wanu.
5 And I will make of Rabbah a home for camels, And the sons of Ammon a couching-place for flocks, So shall ye know that, I, am Yahweh.
Ndidzasandutsa Raba kuti akhale busa la ngamira ndi mizinda ya Aamoni kuti ikhale makola a nkhosa. Pamenepo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
6 For, thus, saith My Lord Yahweh, Because thou didst clap thy hands and stamp with thy foot, —and didst rejoice with all thy contempt in thy soul, against the soil of Israel.
Zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Inu munawomba mʼmanja ndi kumalumphalumpha. Munkakondwa mu mtima mwanu pamene munkanyoza dziko la Israeli.
7 Therefore behold me! I have stretched out my hand over thee And will deliver thee for a prey to the nations, And will cut thee off from among the peoples, And will cause thee to perish from among the lands, — I will destroy thee, So shalt thou know that, I, am Yahweh.
Nʼchifukwa chake ndidzatambasula dzanja langa kuti ndikulangeni, ndipo ndidzakuperekani kuti mukhale chofunkha cha anthu a mitundu ina. Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukufafanizani mʼmayiko onse. Ndidzakuwonongani, ndipo inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova!’”
8 Thus saith My Lord Yahweh: Because Moab and Seir say, Lo! like all the nations, is the house of Judah.
“Ambuye Yehova akuti, ‘Anthu a ku Mowabu ndi a ku Seiri ananena kuti anthu a ku Yuda ali ngati mayiko ena onse.’
9 Therefore, behold me! laying open the side of Moab out of the cities, Out of his cities on his frontiers, The beauty of the land of Beth-jeshimoth, Baal-meon, and Kiriathaim:
Nʼchifukwa chake ndidzagumula mbali ina ya Mowabu, kuyambira ku mizinda yake ya kumalire; mizinda yokongola ya Beti-Yesimoti, Baala-Meoni ndi Kiriataimu.
10 To the Sons of the East [when they come] against the sons of Ammon, and I will deliver it up for possession, -to the end the sons of Ammon may not be remembered among the nations:
Ndidzapereka Amowabu pamodzi ndi Aamoni mʼmanja mwa anthu akummawa kotero kuti Aamoni adzayiwalikiratu pakati pa anthu a mitundu ina.
11 Also upon Moab, will I execute judgments, - So shall they know that I, am Yahweh.
Ndidzawalangadi Amowabuwo. Pamenepo iwo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.”
12 Thus, saith My Lord. Yahweh, Because of what Edom hath done, in taking vengeance on the house of Judah, so that they have become guilty again and again and have taken vengeance upon them,
“Ambuye Yehova akuti, ‘Pakuti Edomu analipsira Ayuda, ndiye kuti analakwa kwambiri pochita zimenezi.
13 Therefore, Thus, saith My Lord Yahweh, I will therefore stretch forth my hand over Edom, and will cut off therefrom man and beast, And will deliver it up as a desolation, from Teman, And they of Dedan, by the sword, shall fall,
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kulanga Edomu ndi kupha anthu ake ndiponso nyama zawo. Ndidzawonongeratu Edomu ndipo adzaphedwa ndi lupanga kuchokera ku Temani mpaka ku Dedani.
14 And I will put forth mine avenging against Edom, by the hand of my people Israel, And they shall deal with Edom, according to mine anger and according to mine indignation, - So shall they know mine avenging, Declareth My Lord. Yahweh,
Ndidzalanga Edomu ndi dzanja la anthu anga Aisraeli. Adzalanga anthu a ku Edomu molingana ndi mkwiyo ndi ukali wanga. Choncho adzaona kulipsira kwanga akutero Ambuye Yehova.’”
15 Thus saith My Lord Yahweh, Because of what the Philistines have done by way of vengeance, - In that they have taken vengeance with contempt in the soul, to destroy, with the enmity of age-past times.
“Ambuye Yehova akuti, ‘Afilisti analanga anthu anga mwankhanza ndi kuwalipsira.
16 Therefore, Thus, saith My Lord. Yahweh, Behold me! stretching forth my hand over the Philistines, And I will cut off the Cherethim, — And will cause to perish the remnant of the coast of the sea;
Nʼchifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: Ndidzatambasula dzanja langa kukantha Afilistiwo. Ndidzafafaniza Akereti ndi kuwononga iwo amene amakhala mʼmbali mwa nyanja.
17 And I will execute upon them great vengeance, with rebukes of indignation: shall they know that I am Yahweh, when I put forth mine avenging against them.
Ndidzawabwezera chilango choopsa ndipo ndidzawalanga mu mkwiyo wanga. Ndikadzawalipsira ndipo adzadziwa kuti Ine ndine Yehova.’”

< Ezekiel 25 >