< Ezekiel 20 >

1 And it came to pass in the seventh year in the fifth month, on the tent of the month, that there came in men of the elders of Israel to enquire of Yahweh, —and they sat before me.
Tsiku lakhumi la mwezi wachisanu, chaka chachisanu ndi chiwiri, ena mwa akuluakulu a Israeli anabwera kudzapempha nzeru kwa Yehova, ndipo anakhala pansi pamaso panga.
2 Then came the word of Yahweh unto me saying: -
Tsono Yehova anandiyankhula nati:
3 Son of man Speak thou with the elders of Israel and say unto them, Thus, saith My Lord Yahweh, To enquire of me, are ye coming in? As I live, verily I will not be enquired of by you, Declareth My Lord Yahweh.
“Iwe mwana wa munthu, ayankhule akuluakulu a Israeli ndi kuwawuza kuti, ‘Ambuye Yehova akuti: Kodi mwabwera kudzapempha nzeru kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, Ine sindidzakulolani kupempha nzeru kwa Ine, akutero Ambuye Yehova.’
4 Wilt thou judge them, wilt thou judge, O son of man? The abominations of their fathers, let them know:
“Kodi uwaweruza? Iwe mwana wa munthu, kodi ugamula mlandu wawo? Uwadziwitse tsono zonyansa zimene anachita makolo awo, uwawuze kuti,
5 So then thou shalt say unto them Thus, saith My Lord Yahweh, In the day when I made choice of Israel, then lifted I up my hand. to the seed of the house of Jacob, and made myself known to them, in the land of Egypt, - Yea I lifted up my hand to them, saying, I Yahweh, am your God.
‘Ambuye Yehova akuti: Pa tsiku limene ndinasankha Israeli, ndinalumbira kwa zidzukulu za nyumba ya Yakobo ndipo ndinadziwulula kwa iwo ku Igupto. Ndinalumbira ndi kuwawuza kuti: Ine ndine Yehova Mulungu wanu.
6 In that day, lifted I up my hand to them, to bring them forth out of the land of Egypt, —into a land that I had looked out for them flowing with milk and honey, The beauty, it was of all lands,
Pa tsiku limenelo ndinalumbira kwa iwo kuti ndidzawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kupita nawo ku dziko limene ndinawapezera, dziko la mwana alirenji, dziko lokongola kwambiri kupambana mayiko ena.
7 And I said unto them. Every one the abomination of his eyes, cast ye away, And with the manufactured gods of Egypt, let it not be that ye defile yourselves: I, Yahweh, am your God.
Ndipo ndinawawuza kuti, ‘Aliyense ataye zinthu zonse zonyansa zimene ankasangalala nazo, ndipo musadziyipitse ndi mafano a Igupto, Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
8 But they rebelled against me And were not willing to hearken unto me, Every man the abominations of their eyes, they cast not away, And the manufactured gods of Egypt, forsook they not; Therefore spake I of pouring out mine indignation upon them to bring mine anger to an end against them, in the midst of the land of Egypt.
“‘Koma iwo anandiwukira ndipo sanafune kundimvera. Palibe amene anataya zonyansa zonse zimene ankasangalala nazo. Panalibenso amene anasiya mafano a ku Igupto. Tsono ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwaonetsa mkwiyo wanga mʼdziko la Igupto momwemo.
9 Howbeit I wrought with effect, for the sake of mine own Name, that it might not be profaned—before the eyes of the nations in whose midst they were, —before whose eyes I made myself known unto them, by bringing them forth out of the land of Egypt.
Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene ankakhala pakati pawo. Paja ndinali nditaonetsa mphamvu zanga pamaso pa mitunduyo potulutsa Aisraeli mʼdziko la Igupto.
10 Therefore brought I them forth out of the land of Egypt, —and caused them to come into the desert.
Choncho ndinawatulutsa mʼdziko la Igupto ndi kubwera nawo mʼchipululu.
11 Then gave I unto them my statutes, And my regulations, caused I them to know, - By the which the man that doeth them shall live.
Ndinawapatsa malangizo anga ndi kuwadziwitsa malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo.
12 Moreover also my sabbaths, gave I unto them, to become a sign betwixt me and them, —that it might be known that, I, Yahweh, was hallowing them.
Ndinawapatsanso Masabata ngati chizindikiro pakati pathu, kuti adziwe kuti Ine Yehova ndinawapatula.
13 But the house of Israel, rebelled against me, in the desert, In my statutes, walked they not, And my regulations, they rejected By the which the man, that doeth them, shall live, My sabbaths also, they profaned exceedingly. Therefore spake I of pouring out mine indignation upon them in the desert, to make an end of them.
“‘Komabe anthu a Israeli anandiwukira mʼchipululu. Iwo sanatsatire malangizo anga koma anakana malamulo anga amene munthu aliyense akawamvera adzakhala ndi moyo. Ndipo anayipitsa kotheratu Masabata anga. Choncho, ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawononga mʼchipululu.
14 Howbeit I wrought with effect for the sake of mine own Name, —that it should not be profaned in the eyes of the nations, in whose eyes I had brought them forth.
Koma sindinachite zimenezi chifukwa cha dzina langa, kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Igupto.
15 Yet even I lifted up my hand to them. in the desert, — That I would not bring them into the land which I had given to them flowing with milk and honey, The beauty, it was. of all lands:
Ndinalumbiranso kwa iwo mʼchipululu muja, nditakweza dzanja, kuti sindidzawalowetsanso mʼdziko limene ndinawapatsa, dziko la mwana alirenji, lokoma kwambiri kuposa mayiko ena onse.
16 Because my regulations, they had rejected. And as for my statutes, they had not walked therein, My sabbaths also, had they profaned; For after their manufactured gods, their heart had been going.
Paja anakana malamulo anga, sanatsatire malangizo anga ndipo anayipitsa masabata anga. Mitima yawo inakonda mafano.
17 Nevertheless mine eye threw a shield over them that they should not be destroyed; So I made not of them a full end in the desert.
Komabe ndinawamvera chisoni ndipo sindinawawononge kapena kuwatheratu mʼchipululu.
18 But I said unto their children in the desert, In the statutes of your fathers, let it not be that ye walk, And their regulations, let it not be that ye observe, — And with their manufactured gods, let it not be that ye defile yourselves.
Tsono kwa ana awo mʼchipululu ndinati, ‘Musatsatire malangizo a makolo anu kapena kusunga malamulo awo kapena kudziyipitsa ndi mafano awo.
19 I, Yahweh, am your God, In my statutes, walk ye, — And my regulations, observe ye and do them;
Ine ndine Yehova Mulungu wanu; tsatirani malangizo anga ndipo sungani malamulo anga.
20 My sabbaths also, hallow ye, — And they shall become a sign betwixt me and you, That it may be known that I Yahweh am your God.
Masabata anga muziwasunga ngati opatulika kuti akhale chizindikiro pakati pa Ine ndi inu. Mukatero mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova Mulungu wanu.’
21 Notwithstanding the children rebelled against me, In my statutes, walked they not, And my regulations, observed they not to do them Wherein the man who shall do them shall live, My sabbaths, they profaned. Therefore spake I of pouring out mine indignation upon them to bring mine anger to an end against them. in the desert.
“‘Koma ana awo anandiwukira. Iwo sanatsatire malangizo anga, sanamvere malamulo anga, ngakhale kuti amapereka moyo kwa munthu amene amawamvera. Ndiponso anayipitsa Masabata anga. Choncho ndinaganiza zowakhuthulira ukali wanga ndi kuwawonongeratu mʼchipululu momwemo.
22 Howbeit I withdrew my hand, and wrought with effect for the sake of mine own Name, —that it should not be profaned before the eyes of the nations, before whose eyes I had brought them forth:
Koma sindinatero chifukwa cha dzina langa kuti lisayipitsidwe pakati pa anthu a mitundu ina amene anandiona ndikutulutsa Aisraeliwo mu Iguptomo.
23 Even, I, lifted up my hand to them in the desert, — That I would disperse them throughout the nations, And scatter them throughout the lands;
Choncho ndinalumbira mʼchipululu, nditakweza dzanja langa, kuti ndidzawabalalitsa pakati pa anthu a mitundu ina ndi kuwamwazira ku mayiko akutali,
24 Because my regulations, had they not done And my statutes, they had rejected, My sabbaths also, they had profaned, - And after the manufactured gods of their fathers, were their eyes turned.
chifukwa sanamvere malamulo anga, anakana malangizo anga, nayipitsa masabata anga, ndi kupembedza mafano a makolo awo.
25 I myself, indeed, suffered them to walk in statutes which were not good, — And regulations in which they could not live.
Ine ndinawapatsanso malangizo amene sanali abwino ndi malamulo amene sakanatha kupeza nawo moyo.
26 Yea I let them defile themselves with their gifts, when they caused every firstborn to pass through the fire, -. that I might make them desolate. To the end they might know that, I, am Yahweh.
Ndinawalekerera kuti adziyipitse ndi mphatso zawo zomwe, makamaka popereka ana awo oyamba kubadwa ngati nsembe zopsereza. Ndinatero kuti ndiwadetse nkhawa ndi kuti adziwe kuti Ine ndine Yehova.’
27 Therefore speak thou unto the house of Israel Son of man, and say unto them, Thus saith My Lord Yahweh, — Yet further in this, did your fathers insult me, by the treachery wherewith they dealt treacherously against me;
“Tsono iwe mwana wa munthu, yankhula nawo Aisraeli ndipo uwawuze kuti, ‘Ambuye Yehova akuti makolo anu anandinyozanso posaonetsa moyo wokhulupirika.
28 When I brought them into the land as to which I had lifted up mine hand to give it them, then beheld they every high hill and every tangled tree And offered there their sacrifices, And presented there, their provoking gift, And placed there, their satisfying odour, And poured out there, their drink- offerings.
Nditawalowetsa mʼdziko limene ndinachita kulumbirira kuti ndidzawapatsa, iwo tsono ankapita kulikonse kumene anaona chitunda chachitali ndi mtengo wa masamba ambiri kukapereka kumeneko nsembe ndi zopereka zawo zimene zinkandikwiyitsa. Kumeneko ankapereka nsembe za fungo lokoma ndiponso nsembe za zakumwa.
29 Therefore said I unto them, What! a high-place, whereinto ye are entering? And so the name thereof hath been called High-place, until this day.
Tsono ndinawafunsa kuti: Kodi chitunda chimene mukupitako nʼchotani? Chitundachi chakhala chikutchedwa mpaka lero kuti ‘Chitunda cha Chipembedzo.’
30 Therefore say thou unto the house of Israel. Thus saith My Lord Yahweh, Is it in the way of your fathers, ye are defiling yourselves, - And after their abominations, that ye are committing lewdness?
“Tsono uwawuze Aisraeli kuti, ‘Ine Ambuye Yehova ndikuti: Kodi mudzadziyipitsa nokha monga anachitira makolo anu ndi kuchita chigololo ndi milungu yawo yonyansa?
31 Yea when ye lift up your gifts When ye cause your children to pass through the fire, Ye are defiling yourselves unto all your manufactured gods unto this day, And shall, I, be enquired of by you O house of Israel? As I live, Declareth My Lord Yahweh, Surely I will not be enquired of by you.
Pamene mubwera kudzapereka mphatso zanu ndi kudzapereka ana kuti akhale ngati nsembe zopsereza mumadziyipitsa ndi mafano anu mpaka lero. Kodi Aisraeli, ndingathe kukulolani bwanji kuti mulandire malangizo kwa Ine? Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, sindidzalola kuti mupemphe nzeru kwa Ine.
32 And as for that which is rising up on your spirit, it shall, not at all come to pass, In that ye are saying Let us be like the nations Like the families of the lands, By ministering unto Wood and Stone!
“‘Inu munanena kuti, ‘Tikufuna tikhale ngati anthu a mitundu ina, ngati anthu adziko lapansi, amene amapembedza mtengo ndi mwala.’ Koma zimene mukuganizazo sizidzachitika.
33 As I live, Declareth My Lord Yahweh, Surely, with a strong hand and With an outstretched arm and With outpoured indignation, Will I be king over you;
Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, ndi dzanja langa lamphamvu, nditasamula mkono wanga mokwiya kwambiri, Ine ndidzakhala wokulamulani.
34 And I will bring you forth from among the peoples, And gather you together out of the lands, throughout which ye have been dispersed, With a strong hand and With an outstretched arm, and With outpoured indignation;
Ndidzakuchotsani pakati pa anthu a mitundu ina ndikukusonkhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munamwazikirako, ndi dzanja langa lamphamvu ndi lotambasuka ndili wokwiya kwambiri.
35 And I will bring you into the desert of the peoples, —and will contend with you there, face to face.
Ndidzakulowetsani mʼchipululu cha anthu a mitundu ina ndipo kumeneko, moonana maso ndi maso, ndidzakuzengani mlandu.
36 Just as I contended with your fathers in the desert of the land of Egypt, So will I contend with you, Declareth My Lord Yahweh;
Monga ndinawalangira makolo anu mʼchipululu cha dziko la Igupto, motero ndidzakulangani, akutero Ambuye Yehova.
37 And I will cause you to pass under the rod And will bring you into the bond of the covenant;
Ndidzakuwerengani ndi ndodo ya mʼbusa, kukulowetsani mʼchimango cha pangano langa.
38 And will sever from you those who are rebelling and those who are transgressing against me, Out of the land of their sojournings, will I bring them forth, Yet upon the soil of Israel, shall they not enter, So shall ye know that, I, am Yahweh.
Ndidzakuchotserani anthu amene anandigalukira ndi kundiwukira. Ngakhale ndidzawatulutsa mʼdziko limene akukhalamo, koma sadzalowamo mʼdziko la Israeli. Pamenepo mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova.
39 But as for you, O house of Israel Thus, saith my Lord. Yahweh, Go. serve every man his own manufactured gods, Yet afterwards, surely Ye shall be ready to hearken unto me, — And my holy name, shall ye profane no more, With your gifts, and With your manufactured gods.
“‘Koma inu Aisraeli, zimene ndikunena Ine Ambuye Yehova ndi izi: Pitani katumikireni mafano anu onse, aliyense wa inu! Koma mʼtsogolo mwake mudzandimvera ndithu ndipo simudzayipitsa dzina langa lopatulika popereka mphatso zanu kwa mafano.
40 For in my holy mountain. In the mountain of the height of Israel, Declareth, My Lord Yahweh, There shall all the house of Israel serve me, all of it, in the land, There will I accept them, and There, will I seek your heave-offerings and the firstfruits of your gifts, in all your holy things:
Pakuti pa phiri langa lopatulika, phiri lalitali la ku Israeli, akutero Ambuye Yehova, Aisraeli onse adzanditumikira, ndipo kumeneko Ine ndidzawalandira. Kumeneko ndidzayembekeza zopereka zanu ndi mphatso zanu zopambana, pamodzi ndi nsembe zanu zonse zopatulika.
41 As a satisfying odour, will I accept you, Through my bringing you forth from among the peoples, And gathering you out of the lands, throughout which ye have been dispersed; Thus will I hallow myself in you before the eyes of the nations.
Ndidzakulandirani ngati nsembe ya fungo lokoma ndikadzakutulutsani pakati pa anthu a mitundu ina ndi kukusokhanitsani kuchokera ku mayiko kumene munabalalitsidwirako. Motero ndidzadzionetsa pakati panu kuti ndine woyera ndipo mitundu ya anthu idzaona.
42 So shall ye know that I am Yahweh, Through my bringing you in unto the soil of Israel, Unto the land as to which I lifted up my hand, to give it unto your fathers.
Tsono mudzadziwa kuti ndine Yehova ndikadzabwera nanu ku dziko la Israeli, dziko limene ndinalumbira kuti ndidzapereka kwa makolo anu.
43 Then shall ye call to mind. there, your own ways and all your own doings, wherewith ye had defiled yourselves, - And ye shall become loathsome in your own sight, for all your wickednesses, which ye have done.
Kumeneko mudzakumbukira makhalidwe anu ndi machitidwe anu onse amene munadziyipitsa nawo, ndipo mudzanyansidwa nokha chifukwa cha zoyipa zimene munachita.
44 So shall ye know that, I, am Yahweh, Through my dealing effectively with you, for the sake of mine own Name, - Not according to your own wicked ways. Nor according to your corrupted doings. O house of Israel, Declareth My Lord Yahweh.
Inu mudzadziwa kuti Ine ndine Yehova, ndikadzakuchitirani zabwino chifukwa cha dzina langa koma osati molingana ndi njira zanu zoyipa ndi machitidwe anu okhota, inu Aisraeli, akutero Ambuye Yehova.’”
45 Then came the word of Yahweh unto me. saying:
Yehova anandiyankhula nati:
46 Son of man Set thy face the way towards Teman, And drop thy word against the land of the sun, And prophesy unto the forest of the field of the South;
“Iwe mwana wa munthu, tembenuka uyangʼane kummwera; ndipo lalika mawu odzudzula anthu akummwera ndipo unenere zodzudzula dziko la nkhalango ya kummwera.
47 And thou shalt say to the forest of the South Hear the word of Yahweh, — Thus saith My Lord Yahweh-Behold me! kindling in thee a fire. And it shall devour in thee every moist tree and every dry tree. The spreading flame shall not be quenched, Then shall be scorched thereby all faces from south to north;
Iwuze nkhalango yakummwera kuti, ‘Imvani mawu a Yehova! Ambuye Yehova akuti: Ndikuyatsa moto ndipo motowo udzapsereza mitengo yako yonse yayiwisi ndi yowuma yomwe. Malawi ake sadzazimitsika ndipo aliyense kuchokera kummwera mpaka kumpoto adzapsa nawo.
48 And all flesh shall see that I. Yahweh have kindled it, - It shall not be quenched.
Aliyense adzadziwa kuti Ine Yehova ndi amene ndayatsa motowo, ndipo sudzazimitsidwa.’”
49 Then said I, Ah! My Lord Yahweh: They are saying of me, Is not he a putter forth of parables?
Ndipo ine ndinati, “Aa, Ambuye Yehova! Anthu akungondinena kuti, ‘Kodi suja amangonena nthano chabe ameneyu!’”

< Ezekiel 20 >