< Ezekiel 18 >

1 And the word of Yahweh came unto me saying:
Yehova anandiyankhula nati:
2 What occasion have ye, to be using this proverb, concerning the soil of Israel, saying, —Fathers eat sour grapes, And the children’s teeth are blunted?
“Kodi anthu inu mumatanthauza chiyani mukamabwerezabwereza kunena mwambi uwu wokhudza dziko la Israeli kuti: “‘Nkhuyu zodya akulu zimapota ndi ana omwe?’”
3 As I live, Declareth My Lord, Yahweh, Surely ye shall have occasion no longer to use this proverb, in Israel.
“Ndithu pali Ine wamoyo, akutero Ambuye Yehova, simudzanenanso mwambi umenewu mu Israeli.
4 Lo! as for all persons, mine they are, As the person of the father, so also the person of the son, mine they are, —The person that sinneth, the same shall die.
Pakuti moyo uliwonse ndi wanga. Moyo wa abambo ndi wanga, wamwananso ndi wanga. Munthu wochimwa ndi amene adzafe.
5 But when, any man, shall be righteous, and do justice and righteousness:
“Tiyerekeze kuti pali munthu wolungama amene amachita zolungama ndi zolondola.
6 Upon the mountains, hath not eaten, And his eyes, hath not lifted up unto the manufactured gods of the house of Israel, And the wife of his neighbour, hath not defiled, And unto a woman during her removal, hath not approached;
Iye sadyera nawo pa mapiri a chipembedzo kapena kupembedza mafano a Aisraeli. Iye sayipitsa mkazi wa mnzake kapena kugonana ndi mkazi pamene akusamba.
7 And no man, hath treated with violence, But his debt-pledge, hath restored. Plunder, hath not seized, — His bread—to the famished, hath given, And the naked, hath covered with clothing;
Iye sapondereza munthu wina aliyense, koma amabwezera wangongole nʼchigwiriro chake. Iye salanda zinthu za osauka, koma amapereka chakudya kwa anthu anjala, ndipo amapereka zovala kwa anthu ausiwa.
8 Upon interest, hath not put out his money. And increase, hath not accepted, From dishonesty, hath turned back his hand, — Justice in truth, hath done, between man and man;
Iye sakongoletsa ndalama mwa katapira, kapena kulandira chiwongoladzanja chachikulu. Amadziletsa kuchita zoyipa ndipo sakondera poweruza milandu.
9 In my statutes, hath walked. And my regulations, hath observed to do them in truth, Righteous, he is, He shall surely live, Declareth My Lord. Yahweh.
Iye amatsatira malangizo anga, ndipo amasunga malamulo anga mokhulupirika. Munthu ameneyo ndi wolungama; iye adzakhala ndithu ndi moyo, akutero Ambuye Yehova.
10 But he hath begotten a son Who is a violent man A shedder of blood, - Who doeth the like of any of these things;
“Tiyerekeze kuti munthu wolungama chotere wabala mwana chimbalangondo amene amakhalira kupha anthu ndi kuchita zinthu zina zotere.
11 Whereas he, none of those other things, doeth, For indeed upon the mountains, he hath eaten, And the wife of his neighbour, hath defiled;
Iye nʼkumachita zinthu zimene ngakhale abambo ake sanachitepo. “Amadyera nawo ku mapiri achipembedzo. Amayipitsa mkazi wa mnzake.
12 The oppressed and the needy, hath treated with violence, Hath ruthlessly plundered, The pledge, hath not restored, But unto the manufactured gods, hath lifted up his eyes, Abomination, hath wrought;
Iye amapondereza munthu wosauka ndi wosowa. Amalanda zinthu za osauka. Sabweza chikole cha munthu wa ngongole. Iye amatembenukira ku mafano nachita zonyansa.
13 Upon interest, hath put out. And increase, hath accepted—, And shall he live? He shall not live All these abominations, he hath done, He shall surely be put to death, His blood, upon himself, shall be.
Iye amakongoletsa mwa katapira ndipo amalandira chiwongoladzanja chachikulu. Kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu! Chifukwa wachita zinthu zonyansa zonsezi, adzaphedwa ndipo adzalandira chilango chomuyenera.
14 But lo! he hath begotten a son, Who hath considered all the sins of his father which he hath done, - Yea he hath considered and not done like them:
“Tsono tiyerekeze kuti munthu woyipa uyu wabala mwana amene amaona machimo onse amene abambo ake ankachita. Ngakhale amaona koma osatsanzira ntchito zake zoyipazo.
15 Upon the mountains, hath not eaten, And his eyes, hath not lifted up unto the manufactured gods of the house of Israel, The wife of his neighbour, hath not defiled;
“Sadyera nawo pa mapiri achipembedzo. Sapembedza mafano a ku Israeli. Sayipitsa mkazi wa mnzake.
16 And no man, hath he treated with violence, Hath by no means withholden the pledge, And plunder, hath not seized, — His bread—to the famished, hath given And the naked, hath covered with clothing;
Sapondereza munthu wina aliyense. Satenga chikole akabwereketsa chinthu. Salanda zinthu za osauka. Salanda zinthu za munthu. Amapereka chakudya kwa anthu anjala. Amapereka zovala kwa anthu aumphawi.
17 From dishonesty, hath turned back his hand Neither interest nor increase, hath accepted, my regulations, hath executed, In my statutes, hath walked, — He shall not die for the iniquity of his father He shall surely live.
Amadziletsa kuchita zoyipa. Sakongoletsa kuti apezepo phindu. Salandira chiwongoladzanja. Amasunga malangizo anga ndi kumvera malamulo anga. Munthu wotereyo sadzafa chifukwa cha machimo a abambo ake. Adzakhala ndi moyo ndithu.
18 His father Because he exacted unjust gain Seized plunder of a brother, And that which was not good, had done in the midst of his people Therefore lo! he died, in his iniquity.
Koma abambo ake, popeza kuti anazunza anthu ena ndi kubera mʼbale wawo ndiponso popeza kuti sanachitire zabwino anansi ake, adzafera machimo ake omwe.
19 Will ye then say. Why hath not the son borne a part of the iniquity of the father? But the son hath done justice and righteousness, All my statutes, hath observed and done them He shall surely live.
“Mwina inu mukhoza kufunsa kuti, ‘Nʼchifukwa chiyani mwana salangidwa chifukwa cha kulakwa kwa abambo ake? Ayi, mwanayo adzakhala ndi moyo chifukwa ankachita zolungama ndi zolondola ndipo ankasamala kumvera malamulo anga onse.
20 The person that sinneth, the same, shall die, — A, son, shall not bear a part of the iniquity of, the father Neither shall, a father, bear a part of the iniquity of the son, the righteousness of the righteous, upon himself, shall be. And, the lawlessness of a lawless man, upon himself, shall be.
Munthu wochimwa ndiye amene adzafe. Mwana sadzapezeka wolakwa chifukwa cha abambo ake, kapena abambo kupezeka wolakwa chifukwa cha mwana wawo. Chilungamo cha munthu wolungama ndicho chidzamupulutse, ndipo kuyipa kwa munthu wochimwa ndiko kudzamuwonongetse.
21 But as for the lawless man— When he shall turn back from all his sins which he hath committed, And observe all my statutes, And do justice and righteousness He shall surely live. He shall not die:
“‘Munthu woyipa akatembenuka mtima ndi kusiya machimo amene ankachita ndi kuyamba kumvera malamulo anga ndi kumachita zolungama ndi zokhulupirika, ndiye kuti adzakhala ndi moyo. Sadzafa ayi.
22 None of his transgressions which he hath committed shall be remembered against him, —In his righteousness which he hath done, he shall live.
Zoyipa zake zonse zidzakhululukidwa. Chifukwa cha zinthu zolungama zimene anazichita adzakhala ndi moyo.
23 Could I take delight, in the death of the lawless? Demandeth My Lord. Yahweh. Must it not be in his turning from his ways in which case he shall live?
Kodi Ine ndimakondwera ndi imfa ya munthu woyipa? Ayi, ndimakondwera pamene woyipa watembenuka mtima kuti akhale ndi moyo. Akutero Ambuye Yehova.
24 But, when a righteous man, shall turn away, from his righteousness and do that which is perverse, Shall do, according to all the abominations which the lawless man hath done, Shall he live? None of his righteous acts which he hath done, shall be remembered, In his treachery wherein he hath been treacherous, And in his sin wherein he hath sinned, In them, shall he die.
“‘Koma ngati munthu wolungama apatuka kusiya zachilungamo ndi kuyamba kuchita tchimo ndi zonyansa za mtundu uliwonse zimene amachita anthu oyipa, kodi munthu wotereyu nʼkukhala ndi moyo? Ayi ndithu, zolungama zake zonse sizidzakumbukiridwa. Iye adzayenera kufa chifukwa cha machimo amene anachita.
25 Can ye then say— The way of My Lord will not be equal? Hear I pray you O house of Israel, Will my way, not be equal? Will not your ways be unequal?
“Komabe inu mukunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Tamvani tsono inu Aisraeli: Kodi zochita zanga ndizo zosalungama? Kodi si zochita zanu zimene ndi zosalungama?
26 When a righteous man shall turn away from his righteousness and do that which is perverse and die because of those things In his own perversity which he hath done, shall he die.
Ngati munthu wolungama atembenuka kusiya chilungamo chake ndi kuchita tchimo, iye adzafa chifukwa cha tchimolo.
27 But when a lawless man turneth away from his lawlessness which he hath done, And hath done justice and righteousness He, shall save his own soul, alive:
Koma ngati munthu woyipa aleka zoyipa zake zimene anazichita ndi kuyamba kuchita zimene ndi zolungama ndi zolondola, iye adzapulumutsa moyo wake.
28 When he considered, then he turned away from all his transgressions which he had committed, He shall surely live. He shall not die.
Popeza waganizira za zolakwa zonse ankachita ndipo wazileka, iye adzakhala ndi moyo ndithu; sadzafa.
29 Can the house of Israel then say- The way of My Lord will not be equal? Will my ways, not be equal O house of Israel? Will not your ways be unequal?
Komabe Aisraeli akunena kuti, ‘Zimene Ambuye amachita ndi zopanda chilungamo.’ Kodi zochita zanga ndizo zopanda chilungamo, inu Aisraeli? Kodi si zochita zanu zimene ndi zopanda chilungamo?
30 Therefore, Every man according to his own ways, will I judge you O house of Israel, Declareth My Lord Yahweh, Return ye—and make good your return—from all your transgressions, That they become not unto you a stumbling block of iniquity.
“Chifukwa chake Ine Ambuye Yehova ndikuti: inu Aisraeli, Ine ndidzakuweruzani aliyense wa inu molingana ndi ntchito zake. Lapani! Lekani zoyipa zanu kuti musawonongeke nazo.
31 Cast off from you all your transgressions which ye have committed against me, And make you a new heart; And a new spirit, - For why should ye die, O house of Israel?
Tayani zolakwa zanu zonse zimene munandichimwira nazo ndipo khalani ndi mtima watsopano ndi mzimu watsopano. Kodi muferanji inu Aisraeli?
32 For I cannot take delight in the death of him that dieth, Declareth My Lord Yahweh, Make good your return then and, live!
Ine sindikondwera ndi imfa ya munthu aliyense, akutero Ambuye Yehova. Chifukwa chake, lapani kuti mukhale ndi moyo.”

< Ezekiel 18 >