< Exodus 37 >

1 And Bezaleel made the ark, of acacia wood, two cubits and a half, the length thereof and, a cubit and a half, the breadth thereof, and, a cubit and a half, the height thereof;
Bezaleli anapanga Bokosi la Chipangano lamatabwa amtengo wa mkesha. Kutalika kwake kunali masentimita 114, mulifupi mwake munali masentimita 69, msinkhu wake masentimita 69.
2 and he overlaid it with pure gold within and without, -and made for it a rim of gold, round about;
Iye analikuta bokosilo ndi golide wabwino kwambiri mʼkati mwake ndi kunja komwe. Anapanganso mkombero wagolide kuzungulira bokosilo.
3 and he cast for it four rings of gold, upon the four feet thereof, —even, two rings, on the one side thereof and, two rings, on the other side thereof;
Iye anapanga mphete zinayi zagolide ndi kuzimangirira ku miyendo yake inayi ija, mbali ina ziwiri ndi mbali inanso ziwiri.
4 and he made staves of acacia wood, and overlaid them with gold;
Kenaka anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide.
5 and he brought the staves into the rings, upon the sides of the ark, for lifting the ark.
Ndipo analowetsa nsichizo mʼmphete zija za mbali zonse ziwiri za bokosilo kuti azinyamulira.
6 And he made a propitiatory of pure gold, —two cubits and a half, the length thereof, and, a cubit and a half, the breadth thereof:
Iye anapanga chivundikiro cha bokosilo cha golide wabwino kwambiri, kutalika kwake masentimita 114, mulifupi mwake masentimita 69.
7 and he made two cherubim, of gold, of beaten work, did he make them, out of the two ends of the propitiatory:
Ndipo anapanga Akerubi awiri agolide osula ndi nyundo ndi kuwayika mbali ziwiri za chivundikirocho.
8 one cherub, out of this end, and, one cherub, out of that end, out of the propitiatory itself, made he the cherubim, out of the two ends thereof:
Iye anapanga kerubi mmodzi mbali ina ndi wina mbali inayo. Akerubiwa anawapangira limodzi ndi chivundikirocho mʼmapeto mwa mbali ziwirizo.
9 and the cherubim were spreading out their wings on high making a shelter with their wings over the propitiatory, with, their faces, one towards the other, towards the propitiatory, were the faces of the cherubim,
Mapiko a Akerubiwo anatambasukira pamwamba pa chivundikiro cha bokosilo kuti achiphimbe. Akerubiwo anakhala choyangʼanana, aliyense kuyangʼana chivundikirocho.
10 And he made the table of acacia wood, two cubits, the length thereof and, a cubit, the breadth thereof, and a cubit and a half the height thereof,
Iwo anapanga tebulo la matabwa amtengo wa mkesha, mulitali mwake masentimita 91, mulifupi mwake masentimita 46, msinkhu wake masentimita 69.
11 And he overlaid it with pure gold, —and he made thereto a rim of gold round about:
Kenaka analikuta ndi golide wabwino kwambiri, ndipo anapanga mkombero wagolide mʼmbali mwake.
12 and he mane thereto a border of a handbreadth, round about, and he made a rim of gold to the border thereof round about:
Iwo anapanga feremu yozungulira tebulo, mulifupi mwake ngati chikhatho cha dzanja, ndipo anayika mkombero wagolide kuzungulira feremuyo.
13 and he cast for it, four rings of gold, and placed the rings upon the four corners, which pertained to the four feet thereof:
Iwo anapanga mphete zinayi zagolide ndipo anazilumikiza ku ngodya zake zinayi, kumene kunali miyendo yake inayi.
14 near to the border, were the rings, as receptacles for the staves, for lifting the table;
Mphetezo anaziyika kufupi ndi feremu kuti azikolowekamo nsichi zonyamulira tebuloyo.
15 and he made the staves of acacia wood, and overlaid them with gold, —for lifting the table;
Anapanga nsichi zamtengo wa mkesha ndi kuzikuta ndi golide kuti azinyamulira tebulolo.
16 and he made the utensils which were to be upon the table, its dishes and its pans and its bowls, and its basins for pouring out therewith, of pure gold.
Ndipo anapanga ziwiya za pa tebulolo zagolide wabwino, mbale ndi zipande, mitsuko ndi mabeseni zogwiritsa ntchito popereka nsembe za chakumwa.
17 And he made the lampstand, of pure gold, of beaten work, made he the lampstand, its base and its shafts, its cups, its apples and its blossoms were, of the same;
Iwo anapanga choyikapo nyale chagolide wabwino kwambiri. Tsinde lake ndi mphanda zake zinasulidwa ndi nyundo. Zikho zake zokhala ndi mphukira ndi maluwa ake zinapangidwa kumodzi.
18 with, six branches coming out of its sides, —three branches of the lampstand out of its one side and three branches of the lampstand out of its other side:
Mʼmbali mwake munali mphanda zisanu ndi imodzi, zitatu mbali iliyonse.
19 three cups like almond-flowers in the one branch—apple and blossom, and, three cups like almond-flowers, in the next branch, apple and blossom, so for the six branches coming out of the lampstand;
Zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa zinali pa mphanda yoyamba. Pa mphanda yachiwiri panalinso zikho zitatu zokhala ngati za maluwa amtowo, mphukira ndi duwa. Ndipo mphanda zonse zisanu ndi imodzi zinali chimodzimodzi ndipo zinatuluka mʼchoyikapo nyalecho.
20 and in the lampstand itself, four cups, like almond-flowers, its apples and its blossoms:
Pa choyikapo nyalecho panali zikho zinayi zokhala ngati maluwa amtowo, mphukira ndi maluwa ake.
21 with, an apple, under the two branches of the same, and, an apple, under the next two branches of the same, and, an apple, under the next two branches of the same, for the six branches coming out of the same:
Mphukira yoyamba inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zoyamba za pa choyikapo nyale. Mphukira yachiwiri inali mʼmunsi mwa nthambi ziwiri zinazo. Mphukira yachitatu inali mʼmunsi mwa nthambi zina ziwirinso. Zonse pamodzi zinali nthambi zisanu ndi imodzi
22 their apples and their brunches were of the same, all of it one beaten work, of pure gold.
Mphukira ndi nthambi zonse zinasulidwa kumodzi ndi choyikapo nyalecho ndi golide wabwino kwambiri.
23 And he made the lamps thereof seven, —with its snuffers and its snuff-trays, of pure gold.
Iwo anapanga nyale zisanu ndi ziwiri, mbaniro ndi zowolera phulusa, zonse zinali zagolide wabwino kwambiri.
24 Of a talent of pure gold, made he it, —and all the utensils thereof.
Iwo anapanga choyikapo nyale ndi zipangizo zake zonse zagolide wabwino kwambiri wolemera makilogalamu 34.
25 And he made the incense altar, of acacia wood, —a cubit, the length thereof, and, a cubit, the breadth thereof, foursquare, and two cubits the height thereof, of the same, were the horns thereof.
Iwo anapanga guwa lamatabwa amtengo wa mkesha lofukizirapo lubani. Linali lofanana mbali zonse, mulitali masentimita 46, mulifupi masentimita 46, ndipo msinkhu masentimita 91, ndipo nyanga zake zinapangidwa kumodzi ndi guwalo.
26 And he overlaid it with pure gold—the top thereof and the sides thereof round about, and the horns thereof, -and he made thereto a rim of gold, round about.
Iwo anakuta guwa lonse ndi golide wabwino kwambiri, pamwamba pake, mbali zonse ndi nyanga zake, ndipo anapanga mkombero wagolide kuzungulira guwalo.
27 And two rings of gold, made he thereto—beneath the rim thereof, upon the two corners thereof, upon the two sides thereof, —as receptacles for the staves, to lift it therewith.
Anapanga mphete ziwiri pansi pa mkomberowo ndi kulumikiza ku mbali zonse ziwiri kuti apisemo nsichi zonyamulira.
28 And he made the staves of acacia wood, —and overlaid them with gold.
Anapanga mizati yamtengo wa mkesha ndipo anayikuta ndi golide.
29 And he made the holy anointing oil, and the pure fragrant incense, —the work of a perfumer.
Iwo anapanganso mafuta opatulika odzozera ndi zofukiza za fungo lokoma kwambiri. Iyi inali ntchito ya mʼmisiri waluso lopanga zonunkhiritsa.

< Exodus 37 >