< Exodus 13 >

1 And Yahweh spake unto Moses, saying:
Yehova anati kwa Mose,
2 Hallow to me every firstborn, that which any female first beareth among the sons of Israel, among men and among beasts, —mine! it is.
“Ana onse aamuna oyamba kubadwa uwapatule, ndi anga. Aliyense woyamba kubadwa pakati pa Aisraeli ndi wanga, kaya ndi wa munthu kapena wa chiweto.”
3 And Moses said unto the people—[Ye are] to remember this day, on which ye came forth out of Egypt out of the house of slaves, that with strength of hand, did Yahweh bring you forth from hence, —there shall not, therefore be eaten anything leavened.
Ndipo Mose anati kwa anthu, “Muzikumbukira tsiku lino, tsiku limene munatuluka mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo chifukwa Yehova anakutulutsani ndi dzanja lake lamphamvu. Musadye kalikonse kamene kali ndi yisiti.
4 To-day, are, ye, coming forth, —in the month Abib.
Pa tsiku la lero mwezi uno wa Abibu, mukutuluka mʼdziko la Igupto.
5 And it shall be, when Yahweh shall bring thee into the land of the Canaanite and the Hittite and the Amorite, and the Hivite and the Jebusite, which he sware to thy fathers to give thee, a land flowing with milk and honey, then shalt thou serve with this service, in this month.
Yehova akadzakulowetsani mʼdziko la Akanaani, Ahiti, Aamori, Ahivi ndi Ayebusi, dziko loyenda mkaka ndi uchi, muzikachita mwambo uwu mwezi uno.
6 Seven days, shalt thou eat unleavened cakes, —and on the seventh day, [shall be] a festival to Yahweh.
Muzidzadya buledi wopanda yisiti kwa masiku asanu ndi awiri ndipo tsiku lachisanu ndi chiwirilo muzichita chikondwerero cha Yehova.
7 Unleavened cakes, shall be eaten for the seven days, —neither shall there be seen with thee anything leavened, nor shall there be seen with thee leaven, within any of thy bounds,
Mudye buledi wopanda yisiti masiku asanu ndi awiri. Pasapezeke chinthu chilichonse chokhala ndi yisiti pakati panu, kapena paliponse mʼdziko lanu.
8 And thou shalt tell thy son, on that day, saying, —[This is] because, of that which Yahweh did for me, when he brought me forth out of Egypt.
Tsiku limenelo muzidzawuza ana anu kuti, ‘Ine ndimachita zimenezi chifukwa cha zimene Yehova anandichitira pamene ndimatuluka mʼdziko la Igupto.’
9 And it shall be to thee for a sign upon thy hand and for a memorial between thine eyes, in order that the law of Yahweh may be in thy mouth, —for with a strong hand, did Yahweh bring thee forth out of Egypt.
Lamulo ili lidzakhala ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi chikumbutso choyikidwa pamphumi panu kuti malamulo a Yehova asachoke pakamwa panu. Pakuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.
10 So shalt thou observe this statute in its appointed time, —from year to year.
Muzichita mwambo uwu pa nthawi yake chaka ndi chaka.
11 And it shall be when Yahweh shall bring thee into the land of the Canaanite, as he sware to thee and to thy fathers, —and shalt give it thee,
“Yehova akadzakulowetsani ndi kukupatsani dziko la Kanaani monga analonjezera kwa inu ndi makolo anu,
12 that thou shalt set apart whatsoever is born first, to Yahweh; and, of all firstlings of beasts which thou shalt have, the males, shall pertain to Yahweh.
muzikapereka kwa Ambuye ana onse oyamba kubadwa. Ziweto zonse zazimuna zoyamba kubadwa ndi za Ambuye.
13 But every firstling of an ass, shalt thou redeem with a lamb or if thou wilt not redeem it, then thou shalt break its neck, —but every firstborn of men among thy sons, shalt thou redeem.
Koma mwana woyamba kubadwa wa bulu muzikamuwombola ndi mwana wankhosa, koma ngati simukamuwombola, muzikamuthyola khosi. Mwana wamwamuna woyamba kubadwa muzikamuwombola.
14 And it shall be when thy son shall ask thee in time to come, saying, What is this? Then shalt thou say unto him: With strength of hand, did Yahweh bring us forth out of Egypt out of the house of slaves.
“Mʼtsogolomo mwana wanu akakafunsa kuti, ‘Zimenezi zikutanthauza chiyani?’ Mukamuwuze kuti, ‘Yehova anatitulutsa mʼdziko la Igupto, dziko la ukapolo ndi dzanja lamphamvu.
15 And it came to pass when Pharaoh had shown himself too hardened to let us go, then did Yahweh slay every firstborn in the land of Egypt, from the firstborn of men even unto the firstborn of beasts. For this cause, am, I, sacrificing to Yahweh whatsoever is born first, of the males, and every firstborn of my sons, must I redeem.
Farao atakanitsitsa kuti asatitulutse, Yehova anapha aliyense woyamba kubadwa mʼdziko la Igupto, kuyambira ana a anthu ndi ziweto zomwe. Nʼchifukwa chake ine ndimapereka nsembe kwa Yehova, chachimuna chilichonse choyamba kubadwa ndipo mwana wamwamuna woyamba kubadwa ndimamuwombola.’
16 And it shall be for a sign upon thy hand, and for frontlets between thine eyes, —that, with strength of hand, did Yahweh bring us forth out of Egypt.
Ndipo chidzakhala kwa inu ngati chizindikiro chomangidwa pa dzanja lanu ndi pamphumi panu kuonetsa kuti Yehova anakutulutsani mʼdziko la Igupto ndi dzanja lake lamphamvu.”
17 And it came to pass when Pharaoh had let the people go, that God did not lead by the land-way of the Philistines, although it was near, —for God said—Lest the people be dismayed when they see war and turn back to Egypt.
Farao atalola anthu aja kuti atuluke, Mulungu sanawadzeretse njira yodutsa dziko la Afilisti, ngakhale kuti inali yachidule popeza Mulungu anati, “Ngati anthuwa atadzakumana ndi nkhondo angadzakhumudwe ndi kubwerera ku Igupto.”
18 So God took the people round the desert-way of the Red Sea, —and the sons of Israel went up armed, out of the land of Egypt.
Choncho Mulungu anawadzeretsa anthuwo njira yozungulira ya mʼchipululu kulowera ku Nyanja Yofiira. Komabe Aisraeli anatuluka mʼdziko la Igupto atakonzekera nkhondo.
19 And Moses took the bones of Joseph, with him, —for he had, taken an oath, of the sons of Israel saying, God will, surely visit, you, so then ye shall carry up my bones from hence with you.
Mose ananyamula mafupa a Yosefe chifukwa Yosefe anawalumbiritsa ana a Israeli. Iye anawawuza kuti, “Mulungu adzabwera ndithu kudzakuthandizani, ndipo mudzanyamule mafupa anga pochoka ku malo ano.”
20 And they brake up from Succoth, —and encamped in Etham, at the edge of the desert.
Atachoka ku Sukoti anakagona ku Etamu mʼmphepete mwa chipululu.
21 Now, Yahweh, was going before them—by day, in a pillar of cloud to lead them the way, and by night, in a pillar of fire to give them light, —that they might journey day and night:
Nthawi yamasana Yehova amakhala patsogolo pa anthu kuwatsogolera njira ndi chipilala cha mtambo, ndipo usiku Yehova ankawatsogolera ndi chipilala cha moto, kuwawunikira njira kuti athe kuyenda masana ndi usiku.
22 the pillar of cloud by day ceased not, nor the pillar of fire by night, —from before the people.
Usana, chipilala cha mtambo ndi usiku, chipilala cha moto zinali patsogolo kuwatsogolera anthu aja.

< Exodus 13 >