< Esther 6 >

1 During that night, the sleep of the king fled, —and he commanded to bring in the book of remembrance, the chronicles, and they were read before the king.
Usiku umenewo mfumu inalephera kugona tulo; Choncho inayitanitsa buku limene amalembamo mbiri ya zamakedzana kuti amuwerengere.
2 And it was found written, how that Mordecai had told concerning Bigthana and Teresh, the two eunuchs of the king guarding the threshold, —who had sought to thrust forth a hand upon King Ahasuerus.
Anapeza kuti mʼbukumo munalembedwa zoti Mordekai anawulula kuti Bigitana ndi Teresi, awiri mwa adindo ofulidwa a mfumu amene ankalondera pa khomo la chipinda cha mfumu ndiwo anakonza chiwembu chofuna kupha mfumu Ahasiwero.
3 Then said the king, What honour and dignity hath been done unto Mordecai, for this? Then said the king’s young men, who were ministering unto him, Nothing hath been done for him.
Mfumu inafunsa kuti, “Kodi Mordekai anamupatsa ulemu ndi ukulu wotani chifukwa cha chinthu chimene anachitachi?” Atumiki ake anamuyankha kuti, “Palibe chimene chinachitika kwa iye.”
4 Then said the king, Who is in the court? Now, Haman, had come into the outer court of the kings house, to speak unto the king, to hang Mordecai, upon the gallows which he had prepared for him.
Mfumu inati, “Kodi ndani ali mʼbwalomo?” Tsono Hamani anali atangolowa kumene mʼbwalo lakunja la nyumba yaufumu kuti akawuze mfumu zomukhomera Mordekai pa mtanda umene anamukonzera.
5 So the king’s young men said unto him, Lo! Haman, standing in the court. And the king said, Let him come in.
Atumiki ake anamuyankha kuti, “Hamani ndiye wayima mu bwalo.” “Mulowetseni,” Mfumu inalamulira.
6 So Haman came in, and the king said unto him, What shall be done unto the man in whose honour, the king delighteth? Then said Haman, in his own heart, Unto whom will the king delight to do honour, more than unto me?
Hamani atalowa, mfumu inamufunsa kuti, “Kodi timuchitire ulemu otani munthu amene mfumu ikondweretsedwa naye?” Tsono Hamani anaganiza mu mtima kuti, “Kodi palinso ndani amene mfumu ingamulemekeze kuposa ine?”
7 So Haman said unto the king, —As touching the man in whose honour, the king, delighteth,
Choncho Hamani anayankha mfumuyo kuti, “Munthu amene mfumu ifuna kumuchitira ulemu, imuchitire izi:
8 let them bring in royal apparel wherewith the king hath clothed himself, —and the horse whereon the king hath ridden, and the royal crown which hath been set upon his own head;
Anthu abwere ndi chovala cha ufumu ndi kavalo amene mfumu imakwerapo wokhala ndi chizindikiro chaufumu pamutu pake.
9 and let the apparel and the horse be delivered unto the hand of one of the king’s rulers, one of the nobles, and so let them array the man, in whose honour, the king, delighteth, —and cause him to ride upon the horse through the broadway of the city, and let them proclaim before him, Thus and thus, shall it be done unto the man in whose honour, the king, delighteth!
Ndipo mupereke chovala cha ufumucho ndi kavalo kwa mmodzi wa akalonga a mfumu a ulemu kwambiri. Ameneyu amuveke chovalacho munthu amene mfumu yakondweretsedwa naye. Akavekedwa chovalachi amuyendetse mʼmisewu yonse ya mzinda atakwera pa kavalo wa mfumu. Kalongayu azifuwula patsogolo pa munthuyu kuti ‘Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!’”
10 Then said the king unto Haman, Haste, take the apparel and the horse, just as thou hast said, and do even so unto Mordecai the Jew, who is sitting in the kings gate, —do not let fail a thing, of all which thou hast spoken!
Mfumu inalamulira Hamani kuti, “Pita msanga, katenge chovala cha ufumu ndi kavalo ndipo uchite monga wanenera kwa Mordekai Myuda, amene amakhala pa chipata cha mfumu. Usasiyeko china chilichonse chimene wanena.”
11 So Haman took the apparel and the horse, and arrayed Mordecai, —and caused him to ride through the broadway of the city, and proclaimed before him, Thus and thus, shall it be done unto the man in whoso honour, the king, delighteth!
Choncho Hamani anatenga chovala ndi kavalo. Anamuveka Mordekai chovalacho ndipo anamuyendetsa mʼmisewu yonse ya mu mzinda atakwera pa kavalo, akufuwula kuti, “Ichi ndi chimene mfumu yachita kwa munthu amene yafuna kumuchitira ulemu!”
12 Then Mordecai returned unto the gate of the king, —but, Haman, hurried unto his own house, mourning, and with covered head.
Pambuyo pake Mordekai anabwerera ku chipata cha mfumu. Koma Hamani anapita msanga ku nyumba kwake, akulira, atafundira mutu wake.
13 And Haman recounted unto Zeresh his wife, and unto all his friends, everything that had befallen him. Then said his wise men, and Zeresh his wife, unto him, If, of the seed of the Jews, is Mordecai before whom thou hast begun to fall, thou shalt not prevail against him, but shalt, utterly fall, before him.
Hamani anawuza Zeresi mkazi wake ndi abwenzi ake onse zonse zinamuchitikira. Anthu ake anzeru ndi mkazi wake Zeresi anamuwuza kuti, “Popeza kuti Mordekai ndi Myuda amene mwayamba kale kugonja pamaso pake, ndiye kuti palibe chimene mungachitepo. Mudzagwa ndithu pamaso pake.”
14 While yet they were speaking with him, the eunuchs of the king, had come, —and they hastened to bring Haman, unto the banquet which Esther had prepared.
Pamene anthuwa amayankhula nayebe, adindo a mfumu ofulidwa anabwera kudzamutenga Hamani mofulumira kupita naye ku phwando limene Estere anakonza.

< Esther 6 >