< 2 Kings 25 >

1 And it came to pass, in the ninth year of his reign, in the tenth month, on the tenth day of the month, that Nebuchadnezzar king of Babylon came—he and all his force, against Jerusalem, and encamped against it, —and they built against it a siege wall, round about.
Choncho mʼchaka chachisanu ndi chinayi cha ulamuliro wa Zedekiya, mwezi wakhumi, pa tsiku lakhumi la mwezi, Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anabwera ndi gulu lake lonse la ankhondo, nadzathira nkhondo mzinda wa Yerusalemu. Iye anamanga misasa kunja kwa mzindawo ndipo anamanga mitumbira ya nkhondo kuzungulira mzindawo.
2 And the city came into the siege, —until the eleventh year of King Zedekiah.
Mzindawo anawuzinga mpaka chaka cha khumi ndi chimodzi cha Mfumu Zedekiya.
3 On the ninth of the month, when the famine had become severe in the city, —and there had come to be no bread for the people of the land,
Pa tsiku lachisanu ndi chinayi pa mwezi wachinayi, njala inakula kwambiri mu mzindamo kotero kuti anthu analibe chakudya.
4 then was the city broken up, and all the men of war [fled] by night by way of the gate between the two walls, which is by the garden of the king, the Chaldeans being near the city round about, —and he went the way of the Waste Plain;
Pamenepo khoma la mzindawo linabowoledwa ndipo gulu lonse la ankhondo linathawa usiku kudzera pa chipata cha pakati pa makoma awiri pafupi ndi munda wa mfumu, ngakhale kuti Ababuloni anali atazinga mzindawo. Iwo anathawira cha ku Araba,
5 and the force of the Chaldeans, pursued, the king, and overtook him in the Waste Plains of Jericho, —and, all his force, was scattered from him.
koma gulu la ankhondo la ku Babuloni linalondola mfumu Zedekiya ndi kumupeza mʼchigwa cha ku Yeriko. Ankhondo onse anamusiya yekha nabalalika.
6 So they seized the king, and brought him up unto the king of Babylon, at Riblah, —and they pronounced upon him sentence of judgment.
Anagwidwa napita naye kwa mfumu ya ku Babuloni ku Ribula, kumene anagamula mlandu wa Zedekiyayo.
7 And, the sons of Zedekiah, they slew before his eyes, —and, the eyes of Zedekiah, put they out, and then bound him with fetters of bronze, and brought him into Babylon.
Iwo anapha ana a Zedekiya iyeyo akuona. Kenaka anakolowola maso a Zedekiya namumanga ndi unyolo wamkuwa ndi kupita naye ku Babuloni.
8 And, in the fifth month, on the seventh of the month, the same, was the nineteenth year of King Nebuchadnezzar king of Babylon, came Nebuzaradan, chief of the royal executioners, servant of the king of Babylon, to Jerusalem;
Mwezi wachisanu, pa tsiku lachisanu ndi chiwiri la mwezi, mʼchaka cha 19 cha Nebukadinezara, mfumu ya Babuloni, Nebuzaradani, mkulu wa asilikali oteteza mfumu, nduna ya mfumu ya Babuloni, anabwera ku Yerusalemu.
9 and burned the house of Yahweh, and the house of the king, —yea, all the houses of Jerusalem, even every great man’s house, burned he with fire.
Iye anatentha Nyumba ya Yehova, nyumba ya mfumu pamodzi ndi nyumba zonse za mu Yerusalemu. Anatentha nyumba iliyonse yofunika.
10 And, the walls of Jerusalem round about, did all the force of the Chaldeans who were with the chief of the royal executioners, break down.
Gulu lonse la ankhondo la ku Babuloni limene linali ndi mkulu wa asilikali oteteza mfumu ija, linagumula malinga ozungulira Yerusalemu.
11 And, the residue of the people who were left in the city, and the disheartened who fell away unto the king of Babylon, and the residue of the multitude, did Nebuzaradan, chief of the royal executioners, carry away captive.
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anatenga anthu amene anatsala mu mzindamo, ndi ena amene anathawira kwa mfumu ya Babuloni, pamodzi ndi ena onse kupita nawo ku ukapolo ku Babuloni.
12 But, of the poorest of the land, did the chief of the royal executioners, leave, for vine-dressers and for husbandmen.
Koma mkulu wa asilikaliyo anasiya anthu ena osauka kwambiri mʼdzikomo kuti azisamalira minda ya mpesa ndi minda ina.
13 And, the pillars of bronze that were in the house of Yahweh, and the stands, and the sea of bronze which was in the house of Yahweh, the Chaldeans brake in pieces, and they carried away the bronze of them to Babylon;
Ababuloni anaphwanya zipilala zamkuwa, maphaka ndiponso mbiya ya mkuwa zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndipo anatenga mkuwawo napita nawo ku Babuloni.
14 and, the caldrons, and the shovels, and the snuffers, and the spoons, even all the utensils of bronze wherewith ministration used to be made, did they take away;
Iwo anatenganso miphika, mafosholo, mbaniro za nyale, mbale ndi ziwiya zonse zamkuwa zimene ankagwiritsa ntchito potumikira mʼNyumbayo.
15 and, the sprinkling pans and the dashing bowls which were of gold, in gold, and which were of silver, in silver, did, the chief of the royal executions, take away.
Mkulu wa asilikali uja anatenganso zofukizira lubani ndi mbale zowazira magazi. Zonsezi zinali zopangidwa ndi golide wabwino kwambiri kapena siliva.
16 As for the two pillars the one sea and the stands which Solomon made for the house of Yahweh, without weight, was the bronze of all these things.
Mkuwa wochokera ku zipilala ziwiri zija, mbiya ija ndi maphaka aja, zimene Solomoni anapanga mʼNyumba ya Yehova, kuchuluka kwake kunali kosawerengeka.
17 Eighteen cubits, was the height of each pillar, and, the capital thereupon was of bronze, and, the height of the capital, was three cubits, and, the lattice-work and pomegranates upon the capital round about, the whole, was of bronze; and, like these, had the second pillar, upon the lattice-work.
Chipilala chilichonse chinali chotalika mamita asanu ndi atatu. Mutu wa mkuwa umene unali pamwamba pa chipilalacho unali mita imodzi ndi theka ndipo unakongoletsedwa ndi ukonde wa makangadza a mkuwa amene anazungulira mutuwo. Chipilala chachiwiri chinali chofanana ndi chinacho, ndipo chinali ndi ukonde.
18 And the chief of the royal executioners took Seraiah the head priest, and Zephaniah the second priest, —and the three keepers of the entrance hall;
Mkulu wa asilikali uja anagwira ukapolo mkulu wa ansembe Seraya, Zefaniya wachiwiri wa mkulu wa ansembe ndi alonda atatu apakhomo.
19 and, out of the city, took he one courtier who himself was set over the men of war, and five men of them who were wont to see the face of the king, who were found in the city, and the scribe—general of the army, who used to muster the people of the land, —and sixty men of the people of the land, who were found in the city;
Mwa anthu amene anali mu mzindamo, anatenga mkulu amene ankalamulira ankhondo ndiponso alangizi asanu a mfumu. Anatenganso mlembi wa mtsogoleri wa ankhondo amene ankalemba anthu ntchito ya usilikali mʼdzikomo pamodzi ndi anthu ake 60 amene anali mu mzindamo.
20 and Nebuzaradan, chief of the royal executioners, took them, —and brought them unto the king of Babylon, at Riblah;
Nebuzaradani mkulu wa asilikali uja anawatenga onsewo napita nawo kwa mfumu ya Babuloni ku Ribula.
21 and the king of Babylon smote them and slew them in Riblah, in the land of Hamath, —and thus Judah disappeared from off their own soil.
Ku Ribulako, mʼdziko la Hamati, mfumu ya ku Babuloni inalamula kuti awakwapule ndi kuwapha. Choncho Ayuda anatengedwa ukapolo kuwachotsa mʼdziko lawo.
22 But, as for the people who were left in the land of Judah, whom Nebuchadnezzar king of Babylon left remaining, he set over them Gedaliah, son of Ahikam son of Shaphan.
Nebukadinezara mfumu ya Babuloni anasankha Gedaliya mwana wa Ahikamu, mwana wa Safani, kukhala woyangʼanira anthu amene anatsala ku Yuda.
23 And, when all the generals of the forces, they and the men, heard that the king of Babylon had given oversight unto Gedaliah, then came they in unto Gedaliah, at Mizpah, —even Ishmael son of Nethaniah, and Johanan son of Kareah, and Seraiah son of Tanhumeth the Netophathite, and Jaazaniah son of a Maacathite, they and their men.
Atsogoleri onse ankhondo ndi anthu awo atamva kuti mfumu ya Babuloni yasankha Gedaliya kukhala bwanamkubwa, anabwera kwa Gedaliya ku Mizipa. Atsogoleriwo mayina awo anali awa: Ismaeli mwana wa Netaniya, Yohanani mwana wa Kareya, Seraya mwana wa Tanihumeti wa ku Netofa ndi Yaazaniya mwana wa Maakati, pamodzi ndi anthu awo.
24 And Gedaliah sware unto them, and to their men, and said to them, Do not fear because of the servants of the Chaldeans, —dwell in the land, and serve the king of Babylon, and it shall be well with you.
Gedaliya analumbira powatsimikizira iwo ndi anthu awo. Iye anati, “Musachite mantha ndi atsogoleri Ababuloniwa. Khalani mʼdziko muno ndipo tumikirani mfumu ya Babuloni. Mukatero zinthu zidzakuyenderani bwino.”
25 And it came to pass, in the seventh month, that Ishmael son of Nethaniah a son of Elishama, of the seed royal, came, and ten men with him, and smote Gedaliah, that he died, —and the Jews and the Chaldeans who were with him at Mizpah.
Koma pa mwezi wachisanu ndi chiwiri, Ismaeli mwana wa Netaniya, mwana wa Elisama, wa banja laufumu, anabwera ndi anthu khumi ndipo anapha Gedaliya pamodzi ndi Ayuda ndi anthu a ku Babuloni amene anali naye limodzi ku Mizipa.
26 Then arose all the people, both small and great, and the generals of the forces, and came into Egypt, —for they were afraid of the Chaldeans.
Chifukwa cha zimenezi, anthu onse kuyambira wamngʼono mpaka wamkulu, pamodzi ndi atsogoleri a ankhondo anathawira ku Igupto chifukwa choopa Ababuloni.
27 And it came to pass, in the thirty-seventh year of the captivity of Jehoiachin king of Judah, in the twelfth month, on the twenty-seventh day of the month, —that Evil-merodach king of Babylon, in the year that he began to reign, did lift up the head of Jehoiachin king of Judah, out of prison;
Pa chaka cha 37 cha ukapolo wa Yehoyakini mfumu ya Yuda, chaka chimene Evili-Merodaki anakhala mfumu ya Babuloni, anamasula Yehoyakini mʼndende pa mwezi wa 12 pa tsiku la 27.
28 and he spake with him kind words, —and set his throne above the throne of the kings who were with him in Babylon;
Anamukomera mtima namukweza kupambana mafumu ena onse amene anali naye ku Babuloni.
29 and changed his prison garments, —and he did eat bread continually before him, all the days of his life.
Choncho Yoyakini anavula zovala zake za ku ndende, ndipo ankadya ndi mfumu masiku onse a moyo wake.
30 And, as his allowance, a continual portion, was given him, from the king, the provision of a day upon its own day, —all the days of his life.
Mfumu inkamupatsa Yehoyakini chakudya tsiku lililonse pa moyo wake wonse.

< 2 Kings 25 >