< 2 Kings 14 >

1 In the second year of Joash son of Joahaz king of Israel, began Amaziah son of Joash king of Judah to reign.
Mʼchaka chachiwiri cha Yehowasi mwana wa Yowahazi mfumu ya Israeli, Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anayamba kulamulira.
2 Twenty-five years old, was he when he began to reign, and twenty-nine years, reigned he in Jerusalem, —and, his mother’s name, was Jehoaddan of Jerusalem.
Iye anali ndi zaka 25 pamene anakhala mfumu ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka 29. Amayi ake anali Yehoyadini wa ku Yerusalemu.
3 And he did that which was right in the eyes of Yahweh, only, not like David his father: according to all that Joash his father did, so he did;
Iye anachita zolungama pamaso pa Yehova, koma osafanana ndi zomwe anachita Davide kholo lake. Iye anatsatira zochita zonse za Yowasi abambo ake.
4 only, the high places, took they not away, —still were the people sacrificing and burning incense in the high places.
Komabe sanachotse malo opembedzerapo mafano. Anthu anapitiriza kupereka nsembe ndi kufukiza lubani kumeneko.
5 And it came to pass that, as soon as the kingdom was confirmed in his hand, he smote his servants who smote the king his father;
Atakhazikika mu ufumu wake, Amaziya anapha atumiki ake amene anapha abambo ake, mfumu ija.
6 but, the sons of them that smote him, slew he not, —as it is written in the book of the law of Moses, which Yahweh commanded, saying—Fathers, shall not be put to death, for sons, nor shall, sons, be put to death, for fathers, but every man, for his own sin, shall be put to death.
Komatu iye sanaphe ana a anthu amene anapha abambo ake potsatira zomwe zinalembedwa mʼbuku la Malamulo a Mose. Mʼmenemo Yehova analamula kuti, “Makolo asaphedwe chifukwa cha ana awo, ndipo ana asaphedwe chifukwa cha makolo awo, koma aliyense ayenera kufa chifukwa cha zolakwa zake.”
7 He, smote Edom, in the valley of salt, ten thousand, and seized Sela, in the war, —and called the name thereof Joktheel, [as it is] until this day.
Iye ndiye amene anapha Aedomu 10,000 mʼchigwa cha Mchere nalanda mzinda wa Sela pa nkhondo ndipo anawutcha Yokiteeli, dzina lake ndi lomwelo mpaka lero lino.
8 Then, sent Amaziah messengers unto Jehoash son of Jehoahaz son of Jehu, king of Israel, saying, —Come now, let us look one another in the face.
Tsono Amaziya anatuma amithenga kwa Yehowasi mwana wa Yehowahazi, mwana wa Yehu mfumu ya Israeli ndi kumuopseza kuti, “Bwera tidzaonane maso ndi maso.”
9 And Jehoash king of Israel sent unto Amaziah king of Judah, saying, A thistle that was in Lebanon, sent unto a cedar that was in Lebanon, saying—Give thy daughter to my son to wife, —and there passed by a beast of the field that was in Lebanon, and trampled down the thistle:
Koma Yehowasi mfumu ya Israeli anabweza mawu kwa Amaziya mfumu ya Yuda kuti, “Mtengo wa minga wa ku Lebanoni unatumiza uthenga kwa mkungudza wa ku Lebanoni. ‘Patse mwana wako wamkazi kuti ndimukwatire.’ Kenaka chirombo cha ku Lebanoni chinabwera ndi kupondaponda mtengo wa mingawo.
10 Thou hast, smitten, Edom, and, thy heart, would lift thee up, —Glory, and stay at home! Wherefore, then, shouldest thou contend with misfortune, and fall, thou, and Judah with thee?
Inde iwe wagonjetsa Edomu ndipo tsopano wayamba kudzikuza. Dzitamandire chifukwa cha kupambana kwako, koma khala kwanu konko! Nʼchifukwa chiyani ukuyamba dala mavuto amene adzakuwononga pamodzi ndi Yuda?”
11 But Amaziah hearkened not. So then Jehoash king of Israel came up, and they looked one another in the face, he and Amaziah king of Judah, —in Beth-shemesh, which belongeth unto Judah.
Koma Amaziya sanamvere zimenezi. Choncho Yehowasi mfumu ya Israeli anakamuthira nkhondo. Yehowasi ndi Amaziya anakumana maso ndi maso ku Beti-Semesi mʼdziko la Yuda.
12 Then was Judah defeated before Israel, —and they fled, every man to his own home;
Israeli anagonjetsa Yuda ndipo munthu aliyense anathawira kwawo.
13 and, upon Amaziah, king of Judah, son of Jehoash son of Ahaziah, did Jehoash king of Israel, seize, in Beth-shemesh, —and entered Jerusalem, and brake down the wall of Jerusalem, at the gate of Ephraim, as far as the corner gate, four hundred cubits;
Yehowasi mfumu ya Israeli anagwira Amaziya mfumu ya Yuda, mwana wa Yowasi, mwana wa Ahaziya ku Beti-Semesi. Ndipo anapita ku Yerusalemu nakagwetsa khoma la Yerusalemu kuyambira ku Chipata cha Efereimu mpaka ku Chipata Chapangodya, gawo lotalika mamita 180.
14 and took all the gold and the silver and all the vessels that were found in the house of Yahweh, and in the treasuries of the house of the king, and hostages, —and returned to Samaria.
Iye anatenga golide ndi siliva yense pamodzi ndi ziwiya zonse zimene zinali mʼNyumba ya Yehova ndi zimene zinali mosungira chuma cha nyumba ya mfumu. Iye anagwiranso anthu nabwerera ku Samariya.
15 Now, the rest of the story of Jehoash, what he did, and his might and how he fought with Amaziah king of Judah, are, they, not written in the book of the Chronicles of the Kings of Israel?
Ntchito zina za Yehowasi ndi zonse zimene anachita, kuwonjezera za nkhondo yake ndi Amaziya mfumu ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
16 And Jehoash slept with his fathers, and was buried in Samaria, with the kings of Israel, —and, Jeroboam his son, reigned, in his stead.
Yehowasi anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda mu Samariya pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo mwana wake Yeroboamu analowa ufumu mʼmalo mwake.
17 And Amaziah son of Joash king of Judah, lived, after the death of Jehoash son of Jehoahaz king of Israel, fifteen years.
Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda anakhala zaka khumi ndi zisanu atamwalira Yehowasi mwana wa Yehowahazi mfumu ya Israeli.
18 Now, the rest of the story of Amaziah, is, it, not written in the book of the Chronicles of the Kings of Judah?
Ntchito zina za Amaziya, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Yuda?
19 And, when they made against him a conspiracy in Jerusalem, he fled to Lachish, —but they sent after him to Lachish, and slew him, there.
Anthu anapangana zomuchita chiwembu mu Yerusalemu ndipo Amaziya anathawira ku Lakisi, koma anatumiza anthu ku Lakisiko nakamuphera komweko.
20 And they bare him on horses, —and he was buried in Jerusalem, with his fathers, in the city of David.
Anabwera naye ku pa kavalo ku Yerusalemu ndi kumuyika mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu Mzinda wa Davide.
21 And all the people of Judah took Azariah, he, being sixteen yearn old, —and made, him, king instead of his father Amaziah.
Ndipo anthu onse a ku Yuda anatenga Azariya, amene anali ndi zaka 16 namulonga ufumu mʼmalo mwa abambo ake Amaziya.
22 He, built Elath, and restored it to Judah, —after the king slept with his fathers.
Azariya anamanga mzinda wa Elati ndi kuwubwezeretsa ku Yuda, Amaziya atamwalira.
23 In the fifteenth year of Amaziah, son of Joash, king of Judah, began Jeroboam, son of Joash, king of Israel, to reign in Samaria, [and he reigned] forty-one years.
Mʼchaka cha khumi ndi chisanu cha Amaziya mwana wa Yowasi mfumu ya Yuda, Yeroboamu mwana wa Yehowasi mfumu ya Israeli analowa ufumu ku Samariya ndipo analamulira za 41.
24 And he did the thing that was wicked in the eyes of Yahweh, —he turned not away from any of the sins of Jeroboam son of Nebat, which he caused, Israel, to commit.
Iye anachita zoyipa pamaso pa Yehova ndipo sanasiye machimo a Yeroboamu mwana wa Nebati, amene anachimwitsa nawo Israeli.
25 He, restored the boundary of Israel, from the entering in of Hamath, unto the sea of the waste plain, —according to the word of Yahweh, God of Israel, which he spake by the hand of his servant Jonah, son of Amittai, the prophet, who was of Gath-hepher.
Iye ndi amene anabwezeretsanso malire a Israeli kuyambira ku Lebo Hamati mpaka ku Nyanja ya Araba, molingana ndi zimene ananena Yehova Mulungu wa Israeli, kudzera mwa mtumiki wake Yona mwana wa Amitai, mneneri wochokera ku Gati-Heferi.
26 For Yahweh saw the humiliation of Israel, that it was bitter, indeed, —and that there was no one shut up, nor any one left at large, no one indeed to help Israel.
Pakuti Yehova anaona masautso a Israeli amene anali owawa kwambiri, panalibe kapolo kapena mfulu ngakhale wina aliyense amene akanathandiza Israeli.
27 Neither had Yahweh spoken, to wipe out the name of Israel from under the heavens, —so he saved them, by the hand of Jeroboam son of Joash.
Pakuti Yehova anali asananene zofafaniza ufumu wa Israeli pa dziko lapansi, Iye anawapulumutsa kudzera mʼdzanja la Yeroboamu mwana wa Yowasi.
28 Now, the rest of the story of Jeroboam, and all that he did, and his might when he warred, and how he restored Damascus and Hamath to Judah in Israel, are, they, not written in the book of the Chronicles of the Kings of Israel?
Ntchito zina za Yeroboamu ndi zonse zimene anachita, za kupambana kwake pa nkhondo, za mmene anagonjetsera Damasiko ndi Hamati, imene inali mizinda ya Yuda, kodi sizinalembedwe mʼbuku la mbiri ya mafumu a Israeli?
29 And Jeroboam slept with his fathers, with the kings of Israel, —and, Zechariah his son, reigned, in his stead.
Yeroboamu anamwalira ndipo anayikidwa mʼmanda pamodzi ndi mafumu a Israeli. Ndipo Zekariya mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.

< 2 Kings 14 >