< 2 Chronicles 21 >

1 And Jehoshaphat slept with his fathers, and was buried with his fathers, in the city of David, —and Jehoram his son reigned in his steed.
Yehosafati anamwalira nayikidwa mʼmanda pamodzi ndi makolo ake mu mzinda wa Davide. Ndipo Yehoramu mwana wake analowa ufumu mʼmalo mwake.
2 Now, he, had brethren, sons of Jehoshaphat—Azariah and Jehiel and Zechariah and Azariah, and Michael and Shephatiah, —all these, were sons of Jehoshaphat king of Israel,
Abale ake a Yehoramu, ana aamuna a Yehosafati, anali Azariya, Yehieli, Zekariya, Azariyahu, Mikayeli ndi Sefatiya. Onsewa anali ana a Yehosafati mfumu ya Israeli.
3 and their father gave them large presents—of silver and of gold and of precious things, with cities of defence, in Judah, —but, the kingdom, gave he unto Jehoram, for, he, was the firstborn.
Abambo awo anawapatsa mphatso zambiri za siliva, golide ndi zinthu zina zamtengowapatali komanso mizinda yotetezedwa ya Yuda. Koma iye anapereka ufumu kwa Yehoramu chifukwa anali mwana wake woyamba kubadwa.
4 But, when Jehoram had arisen over the kingdom of his father, he strengthened himself, and slew all his brethren, with the sword, —moreover also some of the rulers of Israel.
Yehoramu atakhazikika pa ufumu wa abambo ake, iye anapha abale ake ndi lupanga pamodzi ndi atsogoleri ena a Israeli.
5 Thirty-two years old, was Jehoram when he began to reign, —and, eight years, reigned he in Jerusalem.
Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu, ndipo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu.
6 And he walked in the way of the kings of Israel, like as did the house of Ahab, for, the daughter of Ahab, had he, to wife, —so he wrought wickedness, in the eyes of Yahweh.
Iye anayenda mʼnjira za mafumu a Israeli, monga mmene linachitira banja la Ahabu, pakuti anakwatira mwana wa Ahabu. Ndipo anachita zoyipa pamaso pa Yehova.
7 Howbeit Yahweh was not willing to destroy the house of David, because of the covenant which he had solemnised, unto David, —and as he had promised to give unto him a lamp, and unto his sons, all the days.
Komabe, chifukwa cha pangano limene Yehova anachita ndi Davide, Yehova sanafune kuwononga banja la Davide. Iye analonjeza kusungira nyale Davide ndi zidzukulu zake mpaka muyaya.
8 In his days, revolted the Edomites, from under the hand of Judah, —and set over themselves a king.
Pa nthawi ya Yehoramu, Edomu anawukira Yuda ndipo anadzisankhira mfumu.
9 So Jehoram passed over, with his captains, and all his chariot, with him, -and it came to pass that he rose up by night, and smote the Edomites that were round about unto him, and the chariot-captains.
Choncho Yehoramu anapita kumeneko pamodzi ndi atsogoleri ake ndi magaleta ake onse. Aedomu anamuzungulira pamodzi ndi atsogoleri ake koma iye ananyamuka ndi kuthawa usiku.
10 So Edom revolted from under the hand of Judah—unto this day. Then, must Libnah needs revolt at the same time, from under his hand, —because he had forsaken Yahweh, the God of his fathers.
Mpaka lero lino Edomu ndi wowukira ulamuliro wa Yuda. Pa nthawi yomweyi, mzinda wa Libina unawukiranso chifukwa Yehoramu anasiya Yehova, Mulungu wa makolo ake.
11 He too, made high places among the mountains of Judah, —and caused the inhabitants of Jerusalem to be unchaste, and seduced Judah.
Iye anamanganso malo opembedzerapo mafano mʼmapiri a Yuda ndipo anachititsa anthu a mu Yerusalemu kukhala osakhulupirika. Choncho anasocheretsa anthu a ku Yuda.
12 Then came there unto him, a writing, from Elijah the prophet, saying, —Thus, saith Yahweh, God of David thy father, Because thou hast not walked in the ways of Jehoshaphat thy father, nor in the ways of Asa, king of Judah;
Yehoramu analandira kalata yochokera kwa mneneri Eliya yonena kuti, “Yehova Mulungu wa Davide abambo ako akuti, ‘Iwe sunayende mʼnjira ya Yehosafati abambo ako kapena Asa mfumu ya Yuda.
13 but hast walked in the way of the kings of Israel, and hast caused Judah and the inhabitants of Jerusalem to be unchaste, after the unchastities of the house of Ahab, —moreover also, thine own brethren of the house of thy father who were better than thou, hast thou slain,
Koma wayenda mʼnjira za mafumu a Israeli ndipo watsogolera anthu a ku Yuda ndi Yerusalemu kukhala osakhulupirika, monga linachitira banja la Ahabu. Waphanso abale ako, abale a banja la abambo ako, anthu amene anali abwino kuposa iweyo.
14 lo! Yahweh, is about to plague, with a great plague, thy people, -and thy children and thy wives, and all thy possessions;
Kotero tsono Yehova ali pafupi kukantha anthu ako, ana ako, akazi ako ndi zinthu zako zonse, ndi chilango chachikulu.
15 also, thyself, with sore diseases, with disease of thy bowels, -until thy bowels shall fall out, by reason of the disease, in a year added to a year.
Ndipo iwe udzadwala nthenda yoopsa yamʼmimba, mpaka nthendayo idzachititsa matumbo ako kutuluka.’”
16 And Yahweh stirred up against Jehoram the spirit of the Philistines, and the Arabians, who were under the direction of the Ethiopians;
Yehova anamuutsira Yehoramuyo mkwiyo wa Afilisti ndi Aarabu amene amakhala pafupi ndi Akusi.
17 and they came up against Judah, and forced their way into it, and carried off all the possessions that were found belonging to the house of the king, moreover also his sons and his wives, —so that there was left him never a son, save only Jehoahaz the youngest of his sons.
Iwo anathira nkhondo Yuda. Analowanso ndi kutenga katundu yense amene anamupeza mʼnyumba ya mfumu pamodzi ndi ana ake ndi akazi ake. Palibe mwana amene anatsala kupatula mwana wake wamngʼono kwambiri, Ahaziya.
18 And, after all this, Yahweh plagued him in his bowels with an incurable disease.
Izi zonse zitachitika, Yehova anakantha Yehoramu ndi nthenda yamʼmimba imene inali yosachiritsika.
19 And it came to pass, in a year beyond a year, even when the end of the days of two years had passed, that his bowels fell out by reason of his disease, so that he died, of, malignant disease, —and his people made him no burning, like the burning of his fathers.
Patapita nthawi, kumapeto kwa chaka chachiwiri, matumbo ake anatuluka chifukwa cha nthendayo, ndipo anafa imfa yopweteka kwambiri. Anthu ake sanasonkhe moto kumuchitira ulemu, monga anachitira ndi makolo ake.
20 Thirty-two years old, was he when he began to reign, and, eight years, reigned he in Jerusalem, —and went his way—unregretted, and, though they buried him in the city of David, yet, not in the sepulchres of the kings.
Yehoramu anali wa zaka 32 pamene anakhala mfumu. Iyeyo analamulira mu Yerusalemu zaka zisanu ndi zitatu. Ndipo anamwalira popanda odandawula, nayikidwa mʼmanda mu mzinda wa Davide, koma osati mʼmanda a mafumu.

< 2 Chronicles 21 >