< 2 Chronicles 18 >

1 And it came to pass, when Jehoshaphat had riches and honour, in abundance, that he contracted, by marriage, affinity with Ahab.
Tsono Yehosafati anali ndi chuma chambiri ndi ulemu, ndipo iye anachita mgwirizano wa ukwati ndi Ahabu.
2 So he went down, at the end of some years, unto Ahab, to Samaria, Ahab therefore sacrificed for him, sheep and oxen, in abundance, also for the people whom he had with him, -and then persuaded him to go up against Ramoth-gilead.
Patapita zaka zina, iye anapita kukacheza kwa Ahabu mu Samariya. Ahabu anaphera iye pamodzi ndi anthu amene anali naye, nkhosa zambiri ndi ngʼombe ndipo anamuwumiriza kuti akathire nawo nkhondo Ramoti Giliyadi
3 For Ahab king of Israel said unto Jehoshaphat king of Judah, Wilt thou go up with me to Ramoth-gilead? And he said unto him—So am I, even as thou, and, like thy people, are my people, and, with thee, in the war.
Ahabu mfumu ya Israeli anafunsa Yehosafati mfumu ya Yuda kuti, “Kodi mudzapita nane kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi?” Yehosafati anayankha kuti, “Ine ndili ngati inu nomwe, ndi anthu anga ngati anthu anu. Ife tikhala nanu limodzi pa nkhondoyi.”
4 Then said Jehoshaphat, unto the king of Israel, —Seek, I pray thee, some time to-day, the word of Yahweh.
Koma Yehosafati anatinso kwa mfumu ya Israeli, “Choyamba mupemphe nzeru kwa Yehova.”
5 So the king of Israel gathered together the prophets, four hundred men, and said unto them, Shall we go up against Ramoth-gilead to battle, or shall I forbear? And they said—Go up, and may God deliver it into the hand of the king!
Tsono mfumu ya Israeli inasonkhanitsa aneneri 400 ndipo inawafunsa kuti, “Kodi tipite kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iwo anayankha kuti, “Pitani, pakuti Mulungu adzawupereka mʼdzanja la mfumu.”
6 Then said Jehoshaphat, Is there not here a prophet of Yahweh, besides, —that we may seek, from him?
Koma Yehosafati anafunsanso kuti, “Kodi kuno kulibe mneneri wina wa Yehova amene ife tingafunsireko?”
7 Then said the king of Israel unto Jehoshaphat—There is yet one man, by whom to seek Yahweh, but, I, hate him, for he is never prophesying, concerning me, anything good—but—all his days—evil, the same, is Micaiah, son of Imla. Then said Jehoshaphat, Let not the king say, so!
Mfumu ya Israeli inayankha Yehosafati kuti, “Alipo munthu mmodzi amene ife kudzera mwa iye titha kufunsira kwa Yehova, koma ndimadana naye chifukwa sandilosera zabwino koma zoyipa nthawi zonse. Iyeyu ndi Mikaya mwana wa Imula.” Yehosafati anayankha kuti, “Mfumu isanene motero.”
8 And the king of Israel called for a certain officer, —and said, Haste, Micaiah son of Imla!
Choncho mfumu ya Israeli inayitana mmodzi mwa akuluakulu ake ndipo inati, “Kamutengeni Mikaya mwana wa Imula, abwere msanga.”
9 Now, the king of Israel, and Jehoshaphat king of Judah, were sitting, each upon his throne, clothed in robes, and they were sitting in an open space, at the entrance of the gate of Samaria, —and, all the prophets, were prophesying before them.
Mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda, atavala mikanjo yawo yaufumu anali atakhala pa mipando yawo yaufumu pabwalo lopunthira tirigu pa khomo la chipata cha Samariya, pamodzi ndi aneneri onse akunenera pamaso pawo.
10 Then did Zedekiah son of Chenaanah make him horns of iron, —and said—Thus, saith Yahweh, With these, shalt thou push Syria, until they are consumed.
Tsono Zedekiya mwana wa Kenaana anapanga nyanga zachitsulo ndipo analengeza kuti, “Yehova akuti, ‘Ndi nyanga izi udzagunda Aaramu mpaka atawonongedwa!’”
11 And, all the prophets, were prophesying, so, saying, -Go up to Ramoth-gilead, and prosper, and Yahweh will deliver [it] into the hand of the king.
Aneneri ena onse amanenera chimodzimodzi kuti, “Kathireni nkhondo Ramoti Giliyadi ndipo kapambaneni, pakuti Mulungu adzamupereka mʼdzanja la mfumu.”
12 And, the messenger who went to call Micaiah, spake unto him, saying, Lo! the words of the prophets, with one mouth, are good for the king, —be thy word then, I pray thee, like one of theirs, so wilt thou speak good.
Wauthenga amene anapita kukayitana Mikaya anati kwa iye, “Taonani aneneri ena onse ngati munthu mmodzi akulosera za chipambano cha mfumu. Mawu anunso agwirizane ndi awo ndipo muyankhule zabwino.”
13 Then said Micaiah, —By the life of Yahweh, whatsoever my God shall say, that, must I speak.
Koma Mikaya anati, “Pali Yehova wamoyo, ine ndidzanena zimene Mulungu wanga andiwuze.”
14 Now, when he came unto the king, the king said unto him, Micah, shall we go against Ramoth-gilead to battle, or shall I forbear? And he said, Go ye up and prosper, and may they be delivered into your hand.
Iye atafika mfumu inamufunsa kuti, “Mikaya, kodi tipite ku nkhondo kukalimbana ndi Ramoti Giliyadi kapena tileke?” Iye anayankha kuti, “Kathireni nkhondo ndipo kapambaneni, pakuti mzindawo udzaperekedwa mʼdzanja lanu.”
15 Then the king said unto him, How many times, must, I, be putting thee on oath, —that thou speak unto me nothing but the truth in the name of Yahweh?
Mfumu inati kwa iye, “Kodi ndikuwuze kangati kuti ulumbire kuti usandiwuze chilichonse koma zoonadi mʼdzina la Yehova?”
16 So he said, I saw all Israel, scattered upon the mountains, like sheep that have no shepherd, -and Yahweh said, No masters, have these! let them return every man unto his own house, in peace.
Ndipo Mikaya anayankha kuti, “Ine ndinaona Aisraeli atabalalika mʼmapiri monga nkhosa zopanda mʼbusa, ndipo Yehova anati, ‘Anthu awa alibe mbuye wawo. Aliyense apite kwawo mu mtendere!’”
17 Then said the king of Israel, unto Jehoshaphat, —Said I not unto thee, He wilt not prophesy concerning me anything good, but evil?
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Kodi ine sindinakuwuzeni kuti sandinenera zabwino koma zoyipa zokhazokha?”
18 Then said he, Therefore, hear ye the word of Yahweh, —I saw Yahweh, sitting upon his throne, and, all the host of the heavens, standing, on his right hand and his left.
Mikaya anapitiriza ndi kunena kuti, “Imvani tsono mawu a Yehova: Ine ndinaona Yehova atakhala pa mpando wake waufumu ndi gulu lonse lakumwamba litayima ku dzanja lake lamanja ndi lamanzere.
19 Then said Yahweh, Who will persuade Ahab king of Israel, that he may go up and fall in Ramoth-gilead? And one spake, saying after this manner, and another, saying after that manner.
Ndipo Yehova anati, ‘Ndani amene adzamunyengerere Ahabu mfumu ya Israeli kuti akathire nkhondo Ramoti Giliyadi ndi kukafera komweko?’ “Wina ananena zina, winanso ananena zina.”
20 Then came there forth a spirit and stood before Yahweh, and said, I, will persuade him. And Yahweh said unto him, Wherewith?
Pomaliza mzimu wina unatuluka ndi kuyima pamaso pa Yehova ndipo unati, “Ine ndikamunyengerera!” Yehova anafunsa kuti, “Ukagwiritsa ntchito njira yanji?”
21 And he said, I will go forth and become a spirit of falsehood, in the mouth of all his prophets. And he said—Thou mayest persuade, moreover also, thou shalt prevail, go forth, and do, so.
Mzimuwo unati, “Ine ndidzapita ndi kukhala mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri ake onse!” Yehova anati, “‘Iwe ukamunyengadi iyeyo. Pita kachite zimenezo.’
22 Now, therefore, lo! Yahweh hath suffered a spirit of falsehood to be put into the mouth of these thy prophets, —but, Yahweh, hath spoken concerning thee—evil.
“Choncho Yehova wayika mzimu wabodza mʼkamwa mwa aneneri anuwa. Yehova waneneratu kuti inu mukaona tsoka.”
23 Then drew near Zedekiah son of Chenaanah, and smote Micaiah upon the cheek, —and said, Which then is the way the spirit of Yahweh passed from me, to speak with thee?
Ndipo Zedekiya mwana wa Kenaana anapita pafupi ndi kumenya khofi Mikaya. Zedekiya anafunsa kuti, “Kodi mzimu wochokera kwa Yehova unadzera njira iti pamene unachoka kwa ine kupita kwa iwe?”
24 Then said Micaiah, Lo! thou shalt see, on that day when thou shalt enter into a chamber within a chamber, to hide thyself.
Mikaya anayankha kuti, “Udzadziwa pa tsiku limene uzikalowa mʼchipinda chamʼkati kuti ukabisale.”
25 Then said the king of Israel, Take ye Micaiah, and carry him back unto Amon ruler of the city, and unto Joash son of the king;
Pamenepo mfumu ya Israeli inalamula kuti, “Tengani Mikaya ndipo mupite naye kwa Amoni, wolamulira mzindawo ndi kwa Yowasi mwana wa mfumu,
26 and ye shall say, Thus, saith the king, Put ye this one into the prison, —and feed him with the bread of oppression, and with the water of oppression, until I return in peace.
ndipo mukanene kuti, ‘Chimene mfumu ikunena ndi ichi; Muyike munthu uyu mʼndende ndipo musamupatse kanthu kalikonse koma buledi ndi madzi pangʼono mpaka nditabwera mwamtendere.’”
27 Then said Micaiah, If thou do, at all return, in peace, Yahweh hath not spoken by me. And he said, Hear! ye peoples, all!
Mikaya anayankhula kuti, “Ngati inu mukabwera mwamtendere, Yehova sanayankhule kudzera mwa ine.” Ndipo anawonjeza kuti, “Anthu nonsenu, mumve zimene ndanenazi.”
28 Then went up the king of Israel, and Jehoshaphat king of Judah, against Ramothgilead.
Choncho mfumu ya Israeli ndi Yehosafati mfumu ya Yuda anapita ku Ramoti Giliyadi.
29 And the king of Israel said unto Jehoshaphat, [I am about] to disguise myself, and enter into the battle, but, thou, put on thy robes. So the king of Israel disguised himself, and entered into the battle.
Mfumu ya Israeli inati kwa Yehosafati, “Ine ndipita ku nkhondo modzibisa koma iwe uvale mikanjo yaufumu.” Kotero mfumu ya Israeli inadzibisa ndipo inapita ku nkhondoko.
30 Now, the king of Syria, had commanded the captains of chariots which he had, saying, Ye shall not fight, with small [or] with great, —save with the king of Israel, alone.
Tsono mfumu ya Aramu inalamulira olamulira magaleta kuti, “Musamenyane ndi wina aliyense, wamngʼono kapena wamkulu koma mfumu ya Israeli yokha.”
31 So it came to pass, when the chariot-captains saw Jehoshaphat, that, they, said, The king of Israel, it is. And they compassed him about, to fight, —but Jehoshaphat made outcry, and, Yahweh, helped him, yea God allured them away from him.
Olamulira magaleta ataona Yehosafati, iwo anaganiza kuti, “Mfumu ya Israeli ndi iyi.” Kotero anatembenuka kukamenyana naye koma Yehosafati anafuwula, ndipo Yehova anamuthandiza. Mulungu anawabweza mʼmbuyo,
32 And so it came to pass, when the chariot-captains saw that it was not the king of Israel, that they turned back from pursuing him;
pakuti olamulira magaleta ataona kuti sanali mfumu ya Israeli, anasiya kumuthamangitsa.
33 but, a certain man, drawing a bow in his innocence, smote the king of Israel between the shoulder-joints and the coat of mail, —wherefore he said to the charioteer, Turn thy hand, and convey me out of the host, for I am sore wounded.
Koma munthu wina anaponya muvi wake mwachiponyeponye ndipo analasa mfumu ya Israeli pakati polumikizira malaya achitsulo. Mfumu inawuza oyendetsa galeta kuti, “Bwerera, undichotse pa nkhondo pano. Ndavulazidwa.”
34 But the battle increased on that day, and, the king of Israel, was propping himself up in the chariot before the Syrians, until evening, -and died at the time of the going in of the sun.
Nkhondo inakula kwambiri tsiku lonse, ndipo mfumu ya Israeli inakhala tsonga mʼgaleta lake kuyangʼanana ndi Aaramu mpaka madzulo. Ndipo pamene dzuwa linkalowa inamwalira.

< 2 Chronicles 18 >