< 2 Chronicles 10 >

1 And Rehoboam went to Shechem, —for, to Shechem, had all Israel come, to make him king.
Rehobowamu anapita ku Sekemu, pakuti Aisraeli onse anapita kumeneko kuti akamulonge ufumu.
2 And it came to pass, when Jeroboam son of Nebat, who was in Egypt-whither he had fled from the face of Solomon the king—heard of it, then returned Jeroboam out of Egypt.
Yeroboamu mwana wa Nebati atamva zimenezi (Iye anali ku Igupto, kumene anapita pothawa mfumu Solomoni) anabwerako kuchokera ku Igupto.
3 And they sent, and called him, so Jeroboam and all Israel came, —and spake unto Rehoboam, saying:
Kotero anthu anakayitana Yeroboamu ndipo iye ndi Aisraeli onse anapita kwa Rehobowamu ndi kumuwuza kuti,
4 Thy father, made our yoke oppressive, —now, therefore, lighten thou somewhat the oppressive servitude of thy father and his heavy yoke which he put upon us, and we will serve thee.
“Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma tsopano mutipeputsire ntchito yolemetsayi ndi goli lolemerali limene analiyika pa ife ndipo ifeyo tidzakutumikirani.”
5 And he said unto them, Yet three days, and then return unto me, —and the people departed.
Rehobowamu anayankha kuti, “Mukabwerenso pakapita masiku atatu.” Choncho anthuwo anachoka.
6 Then King Rehoboam took counsel with the old men who had been standing before Solomon his father, while he yet lived, saying, —How do, ye, counsel to return answer unto this people?
Kenaka mfumu Rehobowamu anafunsira nzeru kwa akuluakulu amene ankatumikira abambo ake, Solomoni, pamene anali moyo. Iye anafunsa kuti, “Kodi inu mungandilangize zotani kuti ndiwayankhe anthu awa?”
7 And they spake unto him saying, If thou wilt be kind to this people, and please them, and speak unto them kind words, then will they be thy servants, all the days.
Iwo anayankha kuti, “Ngati inu muwakomera mtima anthu awa ndi kuwasangalatsa ndiponso kuwayankha mawu abwino, iwo adzakutumikirani nthawi zonse.”
8 But he declined the counsel of the old men, which they gave him, —and took counsel with the young men who had grown up with him, who were standing before him.
Koma Rehobowamu anakana malangizo amene akuluakulu anamupatsa ndipo anakafunsira nzeru kwa anyamata amene anakula naye pamodzi komanso amamutumikira.
9 And he said unto them, What do, ye, counsel that we should return as answer, unto this people, —who have spoken unto me saying, Lighten thou somewhat the yoke, which thy father put upon us?
Iye anawafunsa kuti, “Kodi malangizo anu ndi otani? Kodi tiwayankhe chiyani anthu amene akunena kuti, ‘Peputsani goli limene abambo anu anayika pa ife?’”
10 Then spake with him the young men who had grown up with him, saying, Thus, shalt thou speak unto the people who have spoken unto thee saying, Thy father, made our yoke heavy, Thou, therefore, lighten somewhat our yoke, —Thus, shalt thou say unto them, My little finger, is thicker than my father’s loins;
Anyamata amene anakula pamodzi naye anamuyankha kuti, “Anthu amene anena kwa inu kuti, ‘Abambo anu anatisenzetsa goli lolemetsa koma inu mupeputse goli lathu,’ muwawuze kuti, ‘Chala changa chachingʼono ndi chachikulu kuposa chiwuno cha abambo anga.
11 Now, therefore, my father, laid upon you a heavy yoke, but, I, will add to your yoke, —My father, chastised you with whips, but, I, with scorpions,
Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.’”
12 So Jeroboam and all the people came unto Rehoboam, on the third day, —as the king spake, saying, Return unto me on the third day.
Tsiku lachitatu Yeroboamu ndi anthu onse anabwerera kwa Rehobowamu monga ananenera mfumu kuti, “Mukabwerenso kwa ine pakapita masiku atatu.”
13 And the king answered them harshly, —and King Rehoboam declined the counsel of the old men;
Mfumu inawayankha mwankhanza, pokana malangizo a akuluakulu aja.
14 and spake unto them according to the counsel of the young men, saying, My father, made your yoke heavy, but, I, will add thereunto, —My father, chastised you with whips, But, I, with scorpions.
Iye anatsatira malangizo a anyamata ndipo anati, “Abambo anga anakusenzetsani goli lolemetsa koma ine ndidzalichititsa kukhala lolemetsa kwambiri. Abambo anga anakukwapulani ndi zikoti wamba koma ine ndidzakukwapulani ndi zinkhanira.”
15 So the king hearkened not unto the people, —for there had come to be a turn from God, to the end Yahweh might establish his word which he had spoken by means of Ahijah the Shilonite, unto Jeroboam, son of Nebat.
Kotero mfumu sinamvere anthuwo, pakuti zinthu izi zinali zochokera kwa Mulungu, kukwaniritsa mawu amene Yehova ananena kwa Yeroboamu mwana wa Nebati kudzera mwa Ahiya wa ku Silo.
16 And, when, all Israel, [saw] that the king hearkened not unto them, the people answered the king, saying—What portion have, we, in David, or inheritance in the son of Jesse? Every man, to your homes, O Israel! Now, see to thine own house, O David! And all Israel departed to their homes.
Aisraeli onse ataona kuti mfumu yakana kuwamvera, iwo anayankha mfumu kuti, “Kodi ife tili ndi gawo lanji mwa Davide, gawo lanji mwa mwana wa Yese? Inu Aisraeli! Pitani kwanu. Iwe Davide! Yangʼana banja lako.” Kotero Aisraeli onse anapita kwawo.
17 But, as for the sons of Israel who were dwelling in the cities of Judah, Rehoboam reigned over them.
Koma Rehobowamu anakhala akulamulirabe Aisraeli amene amakhala mʼmizinda ya Yuda.
18 Then King Rehoboam sent Hadoram, who was over the tribute, and the sons of Israel stoned him with stones, that he died. So, King Rehoboam, hasted to mount his chariot, to flee to Jerusalem.
Mfumu Rehobowamu inatuma Hadoramu amene ankayangʼanira ntchito yathangata, koma Aisraeli anamugenda miyala ndi kumupha. Koma mfumu Rehobowamu anakwera galeta lake ndi kuthawira ku Yerusalemu.
19 Thus Israel rebelled against the house of David—unto this day.
Motero Israeli wakhala akuwukira banja la Davide mpaka lero lino.

< 2 Chronicles 10 >